Ezekieli 29 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ezekieli 29:1-21

Za Chilango cha Igupto

1Pa tsiku lakhumi ndi chiwiri la mwezi wakhumi, chaka chakhumi, Yehova anandiyankhula kuti: 2“Iwe mwana wa munthu, tembenukira kwa Farao, mfumu ya Igupto, ndipo unenere modzudzula mfumuyo pamodzi ndi dziko lake. 3Uyiwuze mfumuyo kuti, ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti,

“ ‘Ndine mdani wako, iwe Farao mfumu ya Igupto,

iwe ngʼona yayikulu yogona pakati pa mitsinje yako.

Umanena kuti, ‘Mtsinje wa Nailo ndi wanga;

ndinadzipangira ndekha.’

4Koma ndidzakukola ndi mbedza mʼkamwa mwako

ndipo nsomba za mʼmitsinje yako zidzakangamira ku mamba ako.

Tsono ndidzakutulutsa mu mtsinje mwakomo

pamodzi ndi nsomba zimene zakangamira ku mamba ako.

5Ndidzakutaya ku chipululu,

iwe pamodzi ndi nsomba zonse za mʼmitsinje yako.

Udzagwera pamtetete kuthengo

popanda munthu woti akutole kuti akayike maliro ako.

Ndidzakusandutsa chakudya

cha zirombo za pa dziko lapansi ndi mbalame za mlengalenga.

6Motero aliyense amene amakhala mu Igupto adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.

“ ‘Iwe unakhala ngati ndodo yabango ku Aisraeli. 7Pamene anakugwira unathethekera mʼmanja mwawo ndi kucheka mapewa awo. Pamene anakutsamira, unathyoka ndipo misana yawo inagwedezeka.

8“ ‘Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti, ndikubweretsera lupanga kuti lidzaphe anthu pamodzi ndi nyama zomwe. 9Dziko la Igupto lidzasanduka lopanda anthu. Pamenepo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.

“ ‘Popeza iwe unati, ‘Mtsinje wa Nailo ndi wanga; ndinawupanga ndine,’ 10nʼchifukwa chake Ine ndikudana nawe pamodzi ndi mitsinje yakoyo, ndipo ndidzasandutsa dziko la Igupto bwinja kuyambira chipululu cha Migidoli mpaka ku mzinda wa Asiwani, kukafika ku malire a Kusi. 11Palibe phazi la munthu kapena la nyama limene lidzapondepo. Kudzakhala kopanda anthu kwa zaka makumi anayi. 12Ndidzasandutsa dziko la Igupto kukhala chipululu ngati zipululu za mayiko ena. Kwa zaka makumi anayi mizinda yakenso idzakhala yopasuka pakati pa mizinda yopasuka. Ndipo ndidzathamangitsira Aigupto pakati pa mitundu ya anthu ndi kuwabalalitsira mʼmayiko.

13“ ‘Komabe Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pakutha pa zaka makumi anayi ndidzasonkhanitsa Aigupto onse kuchokera ku mayiko amene ndinawabalalitsirako. 14Ndidzachotsa Aiguptowo ku ukapolo ndipo ndidzawabwezera ku Patirosi kumene anachokera. Kumeneko iwo adzakhala ufumu wotsika. 15Udzakhala ufumu wotsika kwambiri kupambana maufumu ena onse ndipo sudzadzitukumula pakati pa mitundu ina. Ndidzawufowoketsa kwambiri kotero kuti sudzathanso kulamulira mitundu ya anthu. 16Aisraeli sadzadaliranso Aigupto. Koma kuti chilango chawo chidzawakumbutsa tchimo lawo lija lofunafuna thandizo kuchokera ku Igupto. Pamenepo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Ambuye Yehova.’ ”

Mphotho ya Nebukadinezara

17Pa tsiku loyamba la mwezi woyamba, chaka cha 27, Yehova anandiyankhula kuti: 18“Iwe mwana wa munthu, kale Nebukadinezara mfumu ya Babuloni inagwiritsa ntchito ankhondo ake kukathira nkhondo mzinda wa Turo, mpaka munthu aliyense anachita dazi chifukwa chosenza katundu, ndipo ananyuka pa phewa. Komabe ngakhale iyeyo, kapena gulu lake lankhondo sanaphulepo kanthu pa ntchito yonse imene anayigwira polimbana ndi mzindawo. 19Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti, Ine ndidzapereka Igupto kwa Nebukadinezara mfumu ya Babuloni, ndipo iyo idzatenga chuma chake ndi kuchifunkha ngati malipiro a gulu lake lankhondo. 20Ndamupatsa Nebukadinezara Igupto ngati mphotho ya kulimbika kwake chifukwa iyo ndi gulu lake lankhondo anandigwirira ntchito, akutero Ambuye Yehova.

21“Pa nthawi imeneyo ndidzapereka mphamvu yatsopano pa Aisraeli, ndipo ndidzatsekula pakamwa pako, iwe, Ezekieli kuti uthe kuyankhula pakati pawo. Pamenepo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”

New International Reader’s Version

Ezekiel 29:1-21

A Prophecy Against Egypt

1It was the tenth year since King Jehoiachin had been brought to Babylon as a prisoner. On the 12th day of the tenth month, a message from the Lord came to me. The Lord said, 2“Son of man, turn your attention to Pharaoh Hophra. He is king of Egypt. Prophesy against him and the whole land of Egypt. 3Tell him, ‘The Lord and King says,

“ ‘ “Pharaoh Hophra, I am against you.

King of Egypt, you are like a huge monster

lying among your streams.

You say, ‘The Nile River belongs to me.

I made it for myself.’

4But I will put hooks in your jaws.

I will make the fish in your streams

stick to your scales.

I will pull you out from among your streams.

All the fish will stick to your scales.

5I will leave you out in the desert.

All the fish in your streams

will be there with you.

You will fall down in an open field.

You will not be picked up.

I will feed you to the wild animals

and to the birds in the sky.

6Then everyone who lives in Egypt will know that I am the Lord.

“ ‘ “You have been like a walking stick made out of a papyrus stem. The people of Israel tried to lean on you. 7They took hold of you. But you broke under their weight. You tore open their shoulders. The people of Israel leaned on you. But you snapped in two. And their backs were broken.” ’ ”

8So the Lord and King says, “I will send Nebuchadnezzar’s sword against you. He will kill people and animals alike. 9Egypt will become a dry and empty desert. Then your people will know that I am the Lord.

“You said, ‘The Nile River belongs to me. I made it for myself.’ 10So I am against you and your streams. I will destroy the land of Egypt. I will turn it into a dry and empty desert from Migdol all the way to Aswan. I will destroy everything as far as the border of Cush. 11No people or animals will travel through Egypt. No one will even live there for 40 years. 12Egypt will be more empty than any other land. Its destroyed cities will lie empty for 40 years. I will scatter the people of Egypt among the nations. I will send them to other countries.”

13But here is what the Lord and King says. “At the end of 40 years I will gather the Egyptians together. I will bring them back from the nations where they were scattered. 14I will bring them back from where they were taken as prisoners. I will return them to Upper Egypt. That is where their families came from. There they will be an unimportant kingdom. 15Egypt will be the least important kingdom of all. It will never place itself above the other nations again. I will make it very weak. Then it will never again rule over the nations. 16The people of Israel will no longer trust in Egypt. Instead, Egypt will remind them of how they sinned when they turned to it for help. Then they will know that I am the Lord and King.”

17It was the 27th year since King Jehoiachin had been brought to Babylon as a prisoner. On the first day of the first month, a message from the Lord came to me. Here is what the Lord said. 18“Son of man, King Nebuchadnezzar drove his army in a hard military campaign. The campaign was against Tyre. Their helmets rubbed their heads bare. The heavy loads they carried made their shoulders raw. But he and his army did not gain anything from the campaign he led against Tyre. 19So I am going to give Egypt to Nebuchadnezzar, the king of Babylon. He will carry off its wealth. He will take away anything else they have. He will give it to his army. 20I have given Egypt to him as a reward for his efforts. After all, he and his army attacked Egypt because I told them to,” announces the Lord and King.

21“When Nebuchadnezzar wins the battle over Egypt, I will make the Israelites strong again. Ezekiel, I will open your mouth. And you will be able to speak to them. Then they will know that I am the Lord.”