Ezekieli 30 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ezekieli 30:1-26

Za Kulangidwa kwa Igupto

1Yehova anandiyankhula kuti: 2“Iwe mwana wa munthu, nenera ndipo ulengeze zimene Ine Ambuye Yehova ndikunena.

“ ‘Ufuwule mawu awa akuti,

‘Kalanga, tsiku lafika!’

3Pakuti tsiku layandikira,

tsiku la Yehova lili pafupi,

tsiku la mitambo yakuda,

tsiku lachiwonongeko cha mitundu ya anthu.

4Lupanga lidzabwera kudzalimbana ndi Igupto

ndipo mavuto adzafika pa Kusi.

Pamene anthu ambiri adzaphedwa mu Igupto,

chuma chake chidzatengedwa

ndipo maziko ake adzagumuka.

5Kusi, Puti, Ludi ndi Arabiya yense, Libiya ndiponso anthu a mʼdziko logwirizana naye adzaphedwa ndi lupanga pamodzi ndi Igupto.

6“ ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti:

“ ‘Onse othandiza Igupto adzaphedwa

ndipo kunyadira mphamvu zake kudzatheratu.

Adzaphedwa ndi lupanga

kuyambira ku Migidoli mpaka ku mzinda wa Asiwani,’ ”

ndikutero Ine Ambuye Yehova.

7“ ‘Dziko la Igupto lidzasanduka bwinja

kupambana mabwinja ena onse opasuka,

ndipo mizinda yake idzakhala yopasuka

kupambana mizinda ina yonse.

8Nditatha kutentha Igupto

ndi kupha onse omuthandiza,

pamenepo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.

9“ ‘Nthawi imeneyo ikadzafika, amithenga adzapita mofulumira kuchokera kwa Ine kukaopseza Kusi, iwowo osadziwako kanthu. Ndipo adzada nkhawa pa tsiku limene Igupto adzawonongedwa, chifukwa tsikulo lidzafika ndithu.

10“ ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti,

“ ‘Ndidzagwiritsa ntchito Nebukadinezara, mfumu ya ku Babuloni

kuti ndithetse gulu lankhondo la Igupto.

11Iye ndi gulu lake lankhondo, mtundu wa anthu ankhanza kwambiri aja

adzabwera kudzawononga dzikolo.

Adzasolola malupanga awo kulimbana ndi Igupto

ndipo dziko lidzadzaza ndi mitembo.

12Ndidzawumitsa mtsinje wa Nailo

ndi kugulitsa dziko la Igupto kwa anthu oyipa.

Ndidzagwiritsa ntchito anthu achilendo kuti ndiwononge dzikolo

pamodzi ndi zonse zili mʼmenemo.

Ine Yehova ndayankhula.

13“ ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti,

“ ‘Ndidzawononga mafano

ndi kuthetsa milungu yosema ya ku Mefisi.

Simudzakhalanso mfumu mu Igupto,

ndipo ndidzaopseza dziko lonse.

14Ndidzasandutsa chipululu mzinda wa Patirosi,

ndi kutentha mzinda wa Zowani.

Ndidzalanga mzinda wa Thebesi.

15Ndidzakhuthulira ukali wanga pa mzinda wa Peluziumu,

linga lolimba la Igupto,

ndi kuwononga gulu lankhondo la Thebesi.

16Ndidzatentha ndi moto dziko la Igupto;

Peluziumu adzazunzika ndi ululu.

Malinga a Thebesi adzagumuka,

ndipo mzindawo udzasefukira ndi madzi.

17Anyamata a ku Oni ndi ku Pibeseti

adzaphedwa ndi lupanga

ndipo okhala mʼmizinda yake adzatengedwa ukapolo.

18Ku Tehafinehezi kudzakhala mdima

pamene ndidzathyola goli la Igupto;

motero kunyada kwake kudzatha.

Iye adzaphimbidwa ndi mitambo yakuda,

ndipo okhala mʼmizinda yake adzapita ku ukapolo.

19Kotero ndidzalanga dziko la Igupto,

ndipo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’ ”

Farao Watha Mphamvu

20Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri la mwezi woyamba wa chaka chakhumi ndi chimodzi, Yehova anandiyankhula kuti: 21“Iwe mwana wa munthu, ndathyola dzanja la Farao mfumu ya Igupto. Taona, silinamangidwe kuti lipole, ngakhale kulilimbitsa ndi nsalu kuti lithe kugwiranso lupanga. 22Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti, Ine ndikudana ndi Farao mfumu ya Igupto. Ndidzathyola manja ake onse; dzanja labwino pamodzi ndi lothyokalo, ndipo lupanga lidzagwa mʼmanja mwake. 23Ndidzamwaza Aigupto pakati pa mitundu ya anthu ndikuwabalalitsira ku mayiko ambiri. 24Ndidzalimbitsa manja a mfumu ya ku Babuloni, ndipo mʼmanja mwake ndidzayikamo lupanga langa. Koma ndidzathyola manja a Farao, ndipo adzabuwula ngati wolasidwa koopsa pamaso pa mfumu ya ku Babuloniyo. 25Ndidzalimbitsa manja a mfumu ya ku Babuloni, koma manja a Farao adzafowoka. Motero anthu adzadziwa kuti Ine ndine Yehova, ndikadzayika lupanga langa mʼmanja mwa mfumu ya ku Babuloni. Ndipo adzaligwiritsa ntchito pothira nkhondo dziko la Igupto. 26Ndidzamwaza Aigupto pakati pa mitundu ya anthu, ndikuwabalalitsira ku mayiko ambiri. Motero adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

以西结书 30:1-26

为埃及唱哀歌

1耶和华对我说: 2“人子啊,你要说预言,这样宣告主耶和华的话,

“‘哀号吧!你们要为那日悲伤。

3因为日子近了,耶和华的日子近了,

那是乌云密布的日子,

列国沦亡的时候。

4必有刀剑攻击埃及

埃及必尸横遍野,

古实必痛苦不堪。

敌人要掳掠埃及的财富,

摧毁她的根基。

5古实路德阿拉伯利比亚以及她的其他盟友都必与她一同死于刀下。’

6“耶和华说,

埃及的盟友都要覆灭,

埃及的傲气必荡然无存,

密夺色弗尼的居民都要丧身刀下。

这是主耶和华说的。

7埃及要变成荒地中的荒地,

她的城邑要沦为废墟中的废墟。

8我要点火烧埃及

埃及的所有盟友都要灭亡。

那时,他们就知道我是耶和华。

9“‘在那日,我要差遣使者乘船出去惊吓安逸的古实人,在埃及遭难的日子,他们必痛苦不堪。看啊,这日子快到了。’

10“主耶和华说,

“‘我要借巴比伦尼布甲尼撒的手消灭埃及的百姓。

11他和追随他的都是万民中最残暴的人。

我要差他们去毁灭埃及

大肆杀戮,

使埃及尸骨遍野。

12我要使尼罗河干涸,

把土地卖给恶人,

我要借外族人的手使地和地上的一切都荒废,

这是我耶和华说的。’

13“主耶和华说,

‘我要毁灭偶像,

铲除挪弗的神像。

埃及再没有君王,

国内到处充满恐惧。

14我要使巴特罗荒废,

放火焚烧琐安

审判底比斯

15把我的烈怒倾倒在埃及的堡垒——

消灭底比斯的百姓。

16我要放火烧埃及

要受痛苦的折磨,

底比斯要被攻破,

挪弗终日惶恐不已,

17亚文比伯实的壮丁必死于刀下,

众城都要遭受掳掠。

18我粉碎埃及势力的那天,

答比匿日月无光,

她的锐气全消。

乌云要笼罩她,

她城邑的居民要被掳去。

19我必这样审判埃及

他们就知道我是耶和华。’”

20第十一年一月七日,耶和华对我说: 21“人子啊,我打断了埃及王法老的臂膀,没有人替他敷药包扎,以致他无力拿刀。 22主耶和华说,‘我要与埃及王法老为敌,我要把他那强壮的臂膀和曾经受伤的臂膀一起打断,使刀从他手中掉落。 23我要把埃及人驱散到列国,分散到列邦。 24我要使巴比伦王的臂膀强壮有力,把我的刀交在他手中。我要打断法老的臂膀,使法老在他面前像受了致命伤的人一样呻吟。 25我要使巴比伦王的臂膀强壮有力,而法老的双臂必软弱无力。我要把我的刀交在巴比伦王手中,让他挥刀攻击埃及。那时他们就知道我是耶和华。 26我要把埃及人驱散到列国,分散到列邦,这样他们就知道我是耶和华。’”