Ezekieli 30 – CCL & BDS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ezekieli 30:1-26

Za Kulangidwa kwa Igupto

1Yehova anandiyankhula kuti: 2“Iwe mwana wa munthu, nenera ndipo ulengeze zimene Ine Ambuye Yehova ndikunena.

“ ‘Ufuwule mawu awa akuti,

‘Kalanga, tsiku lafika!’

3Pakuti tsiku layandikira,

tsiku la Yehova lili pafupi,

tsiku la mitambo yakuda,

tsiku lachiwonongeko cha mitundu ya anthu.

4Lupanga lidzabwera kudzalimbana ndi Igupto

ndipo mavuto adzafika pa Kusi.

Pamene anthu ambiri adzaphedwa mu Igupto,

chuma chake chidzatengedwa

ndipo maziko ake adzagumuka.

5Kusi, Puti, Ludi ndi Arabiya yense, Libiya ndiponso anthu a mʼdziko logwirizana naye adzaphedwa ndi lupanga pamodzi ndi Igupto.

6“ ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti:

“ ‘Onse othandiza Igupto adzaphedwa

ndipo kunyadira mphamvu zake kudzatheratu.

Adzaphedwa ndi lupanga

kuyambira ku Migidoli mpaka ku mzinda wa Asiwani,’ ”

ndikutero Ine Ambuye Yehova.

7“ ‘Dziko la Igupto lidzasanduka bwinja

kupambana mabwinja ena onse opasuka,

ndipo mizinda yake idzakhala yopasuka

kupambana mizinda ina yonse.

8Nditatha kutentha Igupto

ndi kupha onse omuthandiza,

pamenepo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.

9“ ‘Nthawi imeneyo ikadzafika, amithenga adzapita mofulumira kuchokera kwa Ine kukaopseza Kusi, iwowo osadziwako kanthu. Ndipo adzada nkhawa pa tsiku limene Igupto adzawonongedwa, chifukwa tsikulo lidzafika ndithu.

10“ ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti,

“ ‘Ndidzagwiritsa ntchito Nebukadinezara, mfumu ya ku Babuloni

kuti ndithetse gulu lankhondo la Igupto.

11Iye ndi gulu lake lankhondo, mtundu wa anthu ankhanza kwambiri aja

adzabwera kudzawononga dzikolo.

Adzasolola malupanga awo kulimbana ndi Igupto

ndipo dziko lidzadzaza ndi mitembo.

12Ndidzawumitsa mtsinje wa Nailo

ndi kugulitsa dziko la Igupto kwa anthu oyipa.

Ndidzagwiritsa ntchito anthu achilendo kuti ndiwononge dzikolo

pamodzi ndi zonse zili mʼmenemo.

Ine Yehova ndayankhula.

13“ ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti,

“ ‘Ndidzawononga mafano

ndi kuthetsa milungu yosema ya ku Mefisi.

Simudzakhalanso mfumu mu Igupto,

ndipo ndidzaopseza dziko lonse.

14Ndidzasandutsa chipululu mzinda wa Patirosi,

ndi kutentha mzinda wa Zowani.

Ndidzalanga mzinda wa Thebesi.

15Ndidzakhuthulira ukali wanga pa mzinda wa Peluziumu,

linga lolimba la Igupto,

ndi kuwononga gulu lankhondo la Thebesi.

16Ndidzatentha ndi moto dziko la Igupto;

Peluziumu adzazunzika ndi ululu.

Malinga a Thebesi adzagumuka,

ndipo mzindawo udzasefukira ndi madzi.

17Anyamata a ku Oni ndi ku Pibeseti

adzaphedwa ndi lupanga

ndipo okhala mʼmizinda yake adzatengedwa ukapolo.

18Ku Tehafinehezi kudzakhala mdima

pamene ndidzathyola goli la Igupto;

motero kunyada kwake kudzatha.

Iye adzaphimbidwa ndi mitambo yakuda,

ndipo okhala mʼmizinda yake adzapita ku ukapolo.

19Kotero ndidzalanga dziko la Igupto,

ndipo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’ ”

Farao Watha Mphamvu

20Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri la mwezi woyamba wa chaka chakhumi ndi chimodzi, Yehova anandiyankhula kuti: 21“Iwe mwana wa munthu, ndathyola dzanja la Farao mfumu ya Igupto. Taona, silinamangidwe kuti lipole, ngakhale kulilimbitsa ndi nsalu kuti lithe kugwiranso lupanga. 22Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti, Ine ndikudana ndi Farao mfumu ya Igupto. Ndidzathyola manja ake onse; dzanja labwino pamodzi ndi lothyokalo, ndipo lupanga lidzagwa mʼmanja mwake. 23Ndidzamwaza Aigupto pakati pa mitundu ya anthu ndikuwabalalitsira ku mayiko ambiri. 24Ndidzalimbitsa manja a mfumu ya ku Babuloni, ndipo mʼmanja mwake ndidzayikamo lupanga langa. Koma ndidzathyola manja a Farao, ndipo adzabuwula ngati wolasidwa koopsa pamaso pa mfumu ya ku Babuloniyo. 25Ndidzalimbitsa manja a mfumu ya ku Babuloni, koma manja a Farao adzafowoka. Motero anthu adzadziwa kuti Ine ndine Yehova, ndikadzayika lupanga langa mʼmanja mwa mfumu ya ku Babuloni. Ndipo adzaligwiritsa ntchito pothira nkhondo dziko la Igupto. 26Ndidzamwaza Aigupto pakati pa mitundu ya anthu, ndikuwabalalitsira ku mayiko ambiri. Motero adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”

La Bible du Semeur

Ezéchiel 30:1-26

Le jugement de Dieu plane sur l’Egypte

1L’Eternel m’adressa la parole en ces termes :

2Fils d’homme, prophétise.

Tu diras : « Le Seigneur, ╵l’Eternel, dit ceci :

Poussez des hurlements, ╵criez : “Hélas ! Quel jour !”

3Oui, car le jour est proche,

il approche à grands pas, ╵le jour de l’Eternel,

et ce sera un jour ╵tout chargé de nuages, ╵un temps de jugement ╵réservé pour les peuples.

4Car l’épée va s’abattre ╵sur le pays d’Egypte

et l’effroi régnera ╵jusque dans l’Ethiopie

lorsqu’au pays d’Egypte ╵tomberont les tués

et qu’on s’emparera ╵de toutes ses richesses,

et qu’on renversera ╵jusqu’à ses fondations.

5L’Ethiopie, Pouth et Loud30.5 Pouth et Loud: voir Gn 10.6, 22 et notes., ╵et toute l’Arabie30.5 toute l’Arabie: selon une orthographe très voisine du mot hébreu et plusieurs versions anciennes. Le texte hébreu traditionnel a : tout ce mélange. ╵ainsi que la Libye30.5 En hébreu : Koub.

et les gens du pays de l’alliance,

tomberont par l’épée ╵avec les Egyptiens.

6L’Eternel dit ceci :

Les soutiens de l’Egypte ╵tomberont tous ensemble

et sa puissance, ╵dont elle était si fière, ╵s’écroulera.

Ils tomberont ╵sous les coups de l’épée ╵de Migdol à Assouan30.6 Voir 29.10 et note..

C’est là ce que déclare ╵le Seigneur, l’Eternel.

7L’Egypte ne sera plus qu’une terre désolée ╵parmi les terres désolées,

ses villes seront parmi les villes en ruine.

8Et l’on reconnaîtra ╵que je suis l’Eternel

lorsque je mettrai le feu à l’Egypte

et que tous ses soutiens ╵auront été brisés.

9En ce jour-là, des messagers que j’enverrai s’en iront en bateau pour faire trembler l’Ethiopie dans sa sécurité. Elle sera saisie d’angoisse au jour où l’Egypte sera châtiée, et ce jour est sur le point d’arriver. 10Le Seigneur, l’Eternel, le déclare : Je ferai disparaître la population nombreuse de l’Egypte, et c’est Nabuchodonosor, le roi de Babylone, qui le fera. 11Lui et ses gens de guerre, parmi les plus violents des peuples, seront amenés là pour dévaster le pays ; ils tireront l’épée contre l’Egypte qu’ils couvriront de morts. 12Je changerai les fleuves30.12 Voir 29.3 et note. en terres desséchées et j’abandonnerai le pays aux méchants. Je le dévasterai, lui et ce qu’il contient, par la main d’étrangers. Oui, moi, l’Eternel, j’ai parlé !

13Voici ce que déclare le Seigneur, l’Eternel : Je ferai disparaître les idoles, je supprimerai les faux dieux de Memphis30.13 Au sud du Caire. et il n’y aura plus de chef en Egypte. Dans tout le pays, je répandrai l’effroi. 14Oui, je dévasterai Patros, j’incendierai Tsoân, et j’exécuterai les jugements contre Thèbes30.14 Patros: la Haute-Egypte. Tsoân: une ville du delta. Thèbes: la capitale de la Haute-Egypte.. 15Je déverserai ma colère sur la ville de Sîn30.15 Ville non identifiée dans le delta du Nil, peut-être la Péluse actuelle vers l’est du delta., forteresse de l’Egypte, et j’exterminerai les nombreux habitants de Thèbes. 16J’incendierai l’Egypte et Sîn se tordra de douleur, on fera une brèche dans les remparts de Thèbes, et Memphis sera dans la détresse30.16 sera dans la détresse, autre traduction : devra faire face à l’ennemi. en plein jour. 17Les jeunes gens d’Héliopolis et ceux de Pi-Béseth30.17 Deux villes de la Basse-Egypte. tomberont par l’épée, et les femmes s’en iront en exil30.17 Autre traduction : et ces villes s’en iront en exil.. 18A Daphné30.18 Autre ville de la Basse-Egypte, forteresse frontière à l’est du delta., le jour s’obscurcira quand je romprai les jougs imposés par l’Egypte et que disparaîtra la force dont elle est si fière. Une sombre nuée recouvrira la ville, et ses habitantes30.18 Autre traduction : ses villages. s’en iront en exil. 19J’exécuterai ainsi les jugements sur l’Egypte et l’on reconnaîtra que je suis l’Eternel. »

La puissance du pharaon sera brisée

20Le septième jour du premier mois de la onzième année30.20 C’est-à-dire en avril 587 av. J.-C., l’Eternel m’adressa la parole en ces termes :

21Fils d’homme, vois, j’ai cassé le bras du pharaon, du roi d’Egypte, et il n’a pas été pansé, on ne l’a pas soigné en y posant des ligatures, on ne l’a pas bandé pour qu’il retrouve assez de forces pour manier une épée. 22C’est pourquoi le Seigneur, l’Eternel, dit ceci : Voici, je vais m’en prendre au pharaon, au roi d’Egypte, et lui casser les bras, celui qui est valide aussi bien que celui qui est déjà rompu, et je ferai tomber l’épée de sa main, 23je disperserai les Egyptiens parmi les autres peuples et je les répandrai dans divers pays. 24Mais je fortifierai les bras du roi de Babylone, je mettrai dans sa main ma propre épée et je casserai les deux bras du pharaon qui gémira devant son ennemi comme gémit un homme blessé à mort.

25Oui, je fortifierai les bras du roi de Babylone, mais quant aux bras du pharaon ils tomberont, et l’on reconnaîtra que je suis l’Eternel lorsque je mettrai mon épée dans la main du roi de Babylone et qu’il la brandira contre l’Egypte. 26Oui, je disperserai les Egyptiens parmi les autres peuples, et je les répandrai dans divers pays, et l’on reconnaîtra que je suis l’Eternel.