Ezekieli 31 – CCL & BDS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ezekieli 31:1-18

Mkungudza mu Lebanoni

1Pa tsiku loyamba la mwezi wachitatu, chaka cha khumi ndi chimodzi, Yehova anandiyankhula kuti: 2“Iwe mwana wa munthu, unene kwa Farao mfumu ya Igupto ndi gulu lake lankhondo. Awawuze kuti,

“ ‘Kodi mu ukulu wanu ndani angafanane ndi inu?

3Taonani, ndidzakufanizirani ndi mtengo wa mkungudza wa ku Lebanoni,

wa nthambi zokongola zochititsa mthunzi mʼnkhalango.

Unali wautali,

msonga zake zooneka pamwamba pa nkhalango.

4Madzi ndiwo ankawukulitsa mkungudzawo,

akasupe ozama ankawutalikitsa.

Mitsinje yake inkayenda

mozungulira malo amene unaliwo

ndipo ngalande zake zinkafika

ku mitengo yonse ya mʼmunda.

5Choncho unatalika kwambiri

kupambana mitengo yonse ya mʼmunda.

Nthambi zake zinachuluka

ndi kutalika kwambiri,

chifukwa inkalandira madzi ambiri.

6Mbalame zonse zamlengalenga

zinkamanga zisa zake mʼnthambi za mtengowo.

Nyama zakuthengo zonse

zinkaswanirana mʼmunsi mwa nthambi zake.

Mitundu yotchuka ya anthu

inkakhala mu mthunzi wake.

7Unali wokongola kwambiri,

wa nthambi zake zotambalala,

chifukwa mizu yake inazama pansi

kumene kunali madzi ochuluka.

8Mʼmunda wa Mulungu munalibe

mkungudza wofanana nawo,

kapena mitengo ya payini

ya nthambi zofanafana ndi nthambi zake.

Munalibenso mtengo wa mkuyu

nthambi zofanafana ndi zake.

Mʼmunda wa Mulungu munalibe mtengo wina uliwonse

wofanana ndi iwo kukongola kwake.

9Ine ndinawupanga wokongola

wa nthambi zochuluka.

Mitengo yonse ya mu Edeni, mʼmunda wa

Mulungu inawuchitira nsanje.

10“ ‘Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Chifukwa kuti mtengowo unatalika kwambiri, unatulutsa songa zake mpaka ku thambo, ndipo unadzikweza chifukwa cha msinkhu wake, 11ndinawupereka mʼdzanja la mfumu ya mitundu ya anthu kuti awulange molingana ndi kuyipa kwake. 12Anthu ankhanza kwambiri amitundu ya anthu achilendo adzawudula ndi kuwusiya. Nthambi zake zidzagwera pa mapiri ndi mu zigwa zonse. Nthambi zake zidzathyokera mʼmitsinje ya mʼdzikomo. Motero mitundu yonse ya anthu a dziko lapansi amene ankasangalala mu mthunzi wake idzawusiya. 13Mbalame zonse zamlengalenga zidzakhala pa mtengo wakugwawo, ndipo nyama zakuthengo zonse zidzakhala pa nthambi zake. 14Zidzakutero kuti pasakhalenso mitengo inanso ya mʼmbali mwa madzi yotalika kwambiri, imene idzatalike kwambiri ndi songa zake kufika mpaka ku mitambo. Komanso kuti pasadzakhalenso mitengo yolandira bwino madzi, imene idzatalika motero. Paja yonseyo kutha kwake ndi kufa, kupita ku dziko lapansi kukhala ndi anthu akufa amene analowa mʼmanda kale.

15“ ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pa nthawi imene mkungudzawo unatsikira ku manda, ndinawuza nyanja kuti iwulire maliro pakuwuphimba. Ndinawumitsa mitsinje ndipo madzi ambiri anaphwa. Ndinabweretsa mdima pa Lebanoni chifukwa cha mtengowo ndipo mitengo yonse ya mʼdzikomo inawuma. 16Mitundu ya anthu inagwedezeka pakumva mkokomo wa kugwa kwake, pamene ndinawutsitsira ku manda pamodzi ndi iwo amene anafa. Pamenepo ku dziko la akufa mitengo yonse ya ku Edeni pamodzi ndi ya ku Lebanoni yosankhidwa bwino inasangalatsidwa chifukwa cha zimenezi. 17Amene ankakhala mu mthunzi wake, amene ankayanjana nawo, iwonso anapita nawo pamodzi ku manda, kukakhala pamodzi ndi amene anaphedwa ndi lupanga pakati pa mitundu ya anthu.

18“ ‘Ndi mitengo iti ya mu Edeni imene ingafanane ndi kukongola kwako ndi ulemerero wako? Komabe iwenso, udzatsikira ku dziko la anthu akufa pamodzi ndi mitengo ya mu Edeni. Udzagona pamodzi ndi anthu osachita mdulidwe, anthu amene anaphedwa pa nkhondo.

“ ‘Mtengowo ndi Farao ndi gulu lake lankhondo, akutero Ambuye Yehova.’ ”

La Bible du Semeur

Ezéchiel 31:1-18

La chute du grand cèdre

1Le premier jour du troisième mois de la onzième année31.1 C’est-à-dire en juin 587 av J.-C., l’Eternel m’adressa la parole en ces termes :

2Fils d’homme,

dis au pharaon, roi d’Egypte, ╵et à son nombreux peuple :

A qui ressembles-tu ╵dans ta grandeur ?

3L’Assyrie était comme un cèdre ╵sur le Liban,

à la belle ramure,

au feuillage touffu ╵donnant de l’ombre,

à la haute stature ;

sa cime s’élançait ╵jusque dans les nuages.

4Les eaux l’avaient fait croître,

les sources de l’abîme ╵l’avaient fait s’élever bien haut,

répandant leurs rivières

tout alentour du lieu ╵où il était planté,

puis dirigeant leur cours

vers tous les arbres des campagnes.

5Voilà pourquoi sa taille ╵était plus élevée que celle

de tous les arbres des campagnes ;

ses rameaux se multipliaient,

ses branches s’allongeaient,

grâce à l’eau abondante ╵qui l’abreuvait.

6Tous les oiseaux du ciel

nichaient dans ses rameaux ╵et sous ses branches,

les animaux des champs ╵mettaient bas leurs petits,

de nombreux peuples ╵habitaient à son ombre.

7Par sa taille imposante

et l’ampleur de ses branches, ╵c’était le plus bel arbre :

ses racines plongeaient

dans un sol gorgé d’eau.

8Il n’était pas de cèdre ╵qui lui fût comparable ╵dans le jardin de Dieu.

Les cyprès n’étaient pas ╵comparables à ses branches,

ni les platanes à ses rameaux ;

il n’était aucun arbre ╵dans le jardin de Dieu

qui lui fût égal en beauté.

9Je l’avais embelli ╵d’une riche ramure.

Tous les arbres d’Eden,

dans le jardin de Dieu,

étaient jaloux de lui.

10C’est pourquoi le Seigneur, l’Eternel, dit ceci : Parce qu’il s’est dressé de toute sa hauteur, parce qu’il a porté sa cime jusque dans les nuages, parce que dans son cœur il s’est enorgueilli de sa très haute taille, 11je l’ai livré au puissant dominateur des peuples31.11 Il s’agit du roi de Babylone., afin qu’il lui inflige le traitement que sa méchanceté mérite ; je l’ai chassé. 12Des étrangers, parmi les plus violents des peuples, l’ont abattu et laissé là, ses branches sont tombées sur les montagnes et dans toutes les vallées ; ses rameaux ont été brisés dans tous les cours d’eau du pays, et tous les peuples de la terre ont fui loin de son ombre et l’ont abandonné. 13Tous les oiseaux du ciel sont venus pour s’établir sur son tronc abattu, et les bêtes sauvages s’abritent dans ses branches. 14Et tout cela arrive afin qu’aucun autre arbre croissant au bord de l’eau ne devienne orgueilleux à cause de sa taille et n’élève sa cime jusque dans les nuages, et afin qu’aucun arbre arrosé par les eaux ne se dresse en hauteur poussé par son orgueil. Car ils sont tous voués à la mort, pour descendre au séjour souterrain, au milieu des humains avec ceux qui descendent dans la fosse.

Dans la fosse

15Voici ce que déclare le Seigneur, l’Eternel : Le jour où il est descendu dans le séjour des morts, j’ai fait mener le deuil et, à cause de lui, j’ai recouvert l’abîme31.15 j’ai fait mener le deuil… l’abîme. Autre traduction : et, à cause de lui, j’ai recouvert l’abîme pour lui faire mener le deuil., j’ai retenu ses fleuves, et ses puissantes eaux ont cessé de couler. Oui, à cause de lui, j’ai obscurci la forêt du Liban et, à cause de lui, tous les arbres des champs ont été desséchés. 16Par le bruit de sa chute, j’ai fait trembler les autres peuples, quand je l’ai fait descendre dans le séjour des morts avec ceux qui descendent dans la fosse ; dans les lieux souterrains, tous les arbres d’Eden, tous les arbres de choix, les plus beaux du Liban qui s’abreuvaient aux eaux, ont été consolés. 17Eux aussi, avec lui, ils sont tous descendus dans le séjour des morts vers les victimes de l’épée. Ils étaient son appui et vivaient à son ombre au milieu des peuples. 18Qui t’était comparable en gloire et en grandeur parmi tous les arbres d’Eden ? Et pourtant, te voici descendu avec eux au séjour souterrain pour être couché là au milieu des incirconcis, avec ceux qui ont été tués par l’épée. Tel sera le destin du pharaon et de son nombreux peuple, c’est là ce que déclare le Seigneur, l’Eternel.