Ezekieli 27 – CCL & NSP

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ezekieli 27:1-36

Nyimbo Yodandaulira Turo

1Yehova anandiyankhula kuti: 2“Iwe mwana wa munthu, imba nyimbo yodandaulira Turo. 3Uza Turo, mzinda wokhala pa dooko la nyanja, wochita malonda ndi anthu ambiri a mʼmbali mwa nyanja kuti: Ambuye Yehova akuti,

“Iwe Turo, umanena kuti,

‘Ndine wokongola kwambiri.’

4Malire ako anali mʼkati mwenimweni mwa nyanja;

amisiri ako anakukongoletsa kwambiri.

5Anakupanga ndi matabwa

a payini ochokera ku Seniri;

anatenga mikungudza ya ku Lebanoni

kupangira mlongoti wako.

6Ndi mitengo ya thundu ya ku Basani

anapanga zopalasira zako;

ndi matabwa a mitengo ya payini yochokera ku zilumba za Kitimu.

Pakuti anapanga thandala lako pakati pa matabwawo panali minyanga ya njovu.

7Nsalu yabafuta yopeta yochokera ku Igupto inali thanga yako,

ndipo inakhala ngati mbendera.

Nsalu zophimba matenti ako zinali za mtundu wamtambo ndi pepo

zochokera ku zilumba za Elisa.

8Anthu a ku Sidoni ndi Arivadi ndi amene anali opalasa ako.

Anthu aluso ako, iwe Turo, anali mwa iwe ndiwo amene ankakuyendetsa.

9Akuluakulu ndi eni luso a ku Gebala anali mʼkati mwako,

ngati okonza zibowo zako.

Sitima za pa nyanja zonse, ndi oyendetsa ake

ankabwera pamodzi ndi katundu kudzachita nawe malonda.

10“Anthu a ku Perisiya, a ku Ludi ndi Puti

anali asilikali mʼgulu lako la nkhondo.

Iwo ankapachika zishango ndi zipewa zawo zankhondo pa makoma ako,

kubweretsa kwa iwe ulemerero.

11Anthu a ku Arivadi ndi Heleki

ankalondera mbali zonse za mpanda wako;

anthu a ku Gamadi

anali mu nsanja zako,

Iwo ankapachika zishango zawo pa makoma ako onse.

Amenewo ndiwo anakukongoletsa kwambiri.

12“Dziko la Tarisisi linachita nawe malonda chifukwa cha kuchuluka kwa katundu wako wamtundumtundu. Iwo ankapereka siliva, chitsulo, chitini ndi mtovu mosinthanitsa ndi katundu wako.

13“Yavani, Tubala ndi Mesaki ankachita nawe malonda; iwo ankapereka akapolo ndi ziwiya za mtovu mosinthanitsa ndi katundu wako.

14“Anthu a ku Beti Togarima ankapereka akavalo antchito, akavalo ankhondo ndi abulu mosinthanitsa ndi katundu wako.

15“Anthu a ku Dedani ankachita nawe malonda, ndipo anthu ambiri a mʼmbali mwa nyanja anali ogula malonda ako. Ankakupatsa minyanga ya njovu ndi phingo.

16“Anthu a ku Aramu ankachita nawe malonda chifukwa cha kuchuluka kwa zinthu zako. Iwo ankapereka miyala ya emeradi, nsalu zapepo, nsalu zopetapeta, nsalu zabafuta, korali ndi miyala ya rubi mosinthanitsa ndi katundu wako.

17“Yuda ndi Israeli ankachita nawe malonda. Iwo ankapereka tirigu ochokera ku Miniti ndi zokometsera zakudya, uchi, mafuta ndi mankhwala mosinthanitsa ndi katundu wako.

18“Anthu a ku Damasiko, chifukwa cha zinthu zako za malonda zambiri ndi katundu wako wosiyanasiyana, ankachita nawe malonda a vinyo wochokera ku Heliboni ndi ubweya wankhosa ochokera ku Zahari. 19Adani ndi Agriki ochokera ku Uzala ankagula katundu wako. Iwo ankapereka chitsulo chosalala, kasiya ndi bango lonunkhira mosinthanitsa ndi katundu wako.

20“Anthu a ku Dedani ankakugulitsa nsalu zoyika pa zishalo za akavalo.

21“Arabiya ndi mafumu onse a ku Kedara anali ogula malonda ako. Iwo ankachita nawe malonda a ana ankhosa onenepa, nkhosa zazimuna ndi mbuzi.

22“Anthu amalonda a ku Seba ndi Raama ankachita nawe malonda. Iwo ankapereka zonunkhira zosiyanasiyana zabwino kwambiri, miyala yokongola ndi golide mosinthanitsa ndi katundu wako.

23“Amalonda a ku Harani, Kane, Edeni, Seba, Asuri ndi Kilimadi ankachita nawe malonda. 24Iwowa ankasinthanitsana nawe zovala zokongola, nsalu zopetapeta, zoyala pansi za mawangamawanga, atazimanga bwino ndi zingwe zolimba.

25“Sitima za pa madzi za ku Tarisisi zinali

zonyamula malonda ako.

Motero iwe uli ngati sitima yapamadzi

yodzaza ndi katundu wolemera.

26Anthu opalasa ako amakupititsa

pa nyanja yozama.

Koma mphepo yakummawa idzakuthyolathyola

pakati pa nyanja.

27Chuma chako, katundu wako, malonda ako,

okuyendetsa ako, okuwongolera ako ndi opanga sitima za pa madzi,

anthu ako amalonda ndi asilikali ako onse

ndiponso aliyense amene ali mʼmenemo

adzamira mʼnyanja

tsiku limene udzawonongeka.

28Madera a mʼmbali mwa nyanja adzagwedezeka

chifukwa cha kufuwula kwa oyendetsa sitimawo.

29Onse amene amapalasa sitima zapamadzi,

adzatuluka mʼsitima zawo;

oyendetsa ndi onse owongolera sitima zapamadzi

adzayimirira mʼmbali mwa nyanja.

30Iwo akufuwula,

kukulira iwe kwambiri;

akudzithira fumbi kumutu,

ndi kudzigubuduza pa phulusa.

31Akumeta mpala mitu yawo chifukwa cha iwe

ndipo akuvala ziguduli.

Akukulira iweyo

ndi mitima yowawa kwambiri.

32Akuyimba nyimbo

yokudandaulira nʼkumati:

‘Ndani anawonongedwapo ngati Turo

pakati pa nyanja?’

33Pamene malonda ako ankawoloka nyanja

unakhutitsa mitundu yambiri ya anthu.

Mafumu a dziko lapansi analemera ndi chuma chako

komanso ndi malonda ako.

34Koma tsopano wathyokera mʼnyanja,

pansi penipeni pa nyanja.

Katundu wako ndi onse amene anali nawe

amira pamodzi nawe.

35Onse amene amakhala mʼmbali mwa nyanja

aopsedwa ndi zimene zakuchitikira.

Mafumu awo akuchita mantha

ndipo nkhope zangoti khululu.

36Anthu amalonda a mitundu ina akukunyogodola.

Watha mochititsa mantha

ndipo sudzakhalaponso mpaka muyaya.”

New Serbian Translation

Књига пророка Језекиља 27:1-36

1И дође ми реч Господња: 2„Сине човечији, запевај тужбалицу о Тиру! 3Реци Тиру:

’О, ти што столујеш на вратима морским,

што тргујеш с народима на многим острвима,

Говори Господ Бог: о, Тире, ти рече:

„Ја сам савршенство лепоте!“

4Границе твоје у срцу су мора,

савршена твоја лепота твојих је зидара дело.

5Од чемпреса сенирских

све су ти даске начинили,

с Ливана кедар узеше,

да ти јарбол начине,

6од храстова васанских,

весла су ти направили,

а палубу од борова с китимских острва;

слонову кост у њу су уметнули.

7Једро ти је било од лана везеног, египатског,

а застори од гримиза и скерлета с острва елиских.

8Мештани Сидона и Арвада били су ти веслачи,

мудраци твоји, Тире, били су ти кормилари.

9Старешине гевалске и мудраци његови

пукотине су твоје поправљали;

све лађе на мору и посада њихова

долазили су да од тебе робу купују.

10Људи из Персије, Луда и Фута,

твоји су били ратници.

О твоје су зидове штитове и шлемове качили,

и китили те сјајем.

11Арвађани и војска твоја на твојим зидовима,

куле су твоје Гамадити чували унаоколо.

Штитове су своје качили на твоје зидове

да дотерају твоју лепоту.

12Тарсис је трговао с тобом; због твог силног богатства свакојаког плаћао је твоју робу сребром и гвожђем, калајем и оловом.

13Јаван, Тувал и Месех су трговали с тобом размењујући робље и бронзано посуђе за твоју робу.

14Они из дома Тогарминог размењивали су коње, јахаће коње и мазге за твоју робу.

15Синови Деданови су трговали с тобом. И многа су острва трговала за тебе; доносили су ти као накнаду слонову кост и ебоново дрво.

16Арам је трговао с тобом због обиља твојих производа; плаћали су за твоју робу малахитима, скерлетом, везеним платном и финим ланом, коралима и рубинима.

17Јуда и земља Израиљева су трговали с тобом; плаћали су за твоју робу пшеницом из Минита, брашном, медом, уљем и мелемом.

18Дамаск је, због обиља твојих производа сваке врсте, трговао с тобом хелвонским вином и вуном из Сахара. 19Дан и Јаван из Узала за твоју су робу давали обрађено гвожђе, касију и трску.

20Дедан је трговао с тобом с јахачким простиркама.

21Арабљани и сви кнезови кедарски трговали су с тобом и плаћали ти јагањцима, овновима и јарцима.

22Трговци из Саве и Регме су трговали с тобом. За твоју робу плаћали су најбољим зачинима сваке врсте, свакојаким драгуљима и златом.

23Харан, Кана, Еден, савски трговци, Асирија и Хилмад, су трговали с тобом. 24Трговали су с тобом на твојој пијаци у замену за најбоље рухо од везене пурпурне тканине, и разнобојне тепихе од чврсто уплетених нити.

25Тарсиске лађе превозиле су твоју робу. Био си пун и веома натоварен на морској пучини. 26Твоји веслачи су те извели на пучину, али источни ветар те је разбио усред мора. 27Твоје богатство, твоја роба, твоји морепловци, твоји морнари, кормилари и мајстори за твоје пукотине, твоји трговци, сви ратници у теби, и сви који су на палуби, пашће у морске дубине у дан твога пада. 28Кад се зачује вапај твојих кормилара затрешће се обала. 29Тада ће сви веслачи, морнари и сви морски кормилари напустити своје лађе и искрцати се на земљу. 30Они ће подићи свој глас и горко завапити над тобом. Прашином ће посути своју главу и ваљати се у пепелу, 31обријаће главу за тобом, припасаће кострет, па ће, огорчене душе, плакати за тобом и горко нарицати.

32Закукаће и запевати нарицаљку над тобом:

„Ко је као Тир

ућуткан усред мора?“

33Кад су ти робу довозили с мора,

њом си ситио многе народе;

обиљем блага и робом својом,

ти си богатио цареве земаљске.

34А сада те море разби у води дубокој,

роба твоја пропаде, и сав народ у теби.

35Сви су житељи острвски запањени над тобом;

цареве им подилази језа, од страха им се лице грчи.

36Трговци народа звижде над тобом;

постао си ругло

и више те неће бити.’“