Ezekieli 28 – CCL & NSP

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ezekieli 28:1-26

Mawu Odzudzula Mfumu ya Turo

1Yehova anandiyankhula nati: 2“Iwe mwana wa munthu, iwuze mfumu ya ku Turo mawu a Ine Ambuye Yehova akuti,

“ ‘Iwe ndi mtima wako wodzikuza

umanena kuti, ‘Ine ndine mulungu;

ndimakhala pa mpando wa mulungu

pakati pa nyanja.’

Koma ndiwe munthu chabe osati mulungu,

ngakhale ukuganiza kuti ndiwe wanzeru ngati mulungu.

3Taona, ndiwedi wanzeru kupambana Danieli.

Ndipo palibe chinsinsi chobisika kwa iwe.

4Mwa nzeru zako ndi kumvetsa kwako

unadzipezera chuma

ndipo unasonkhanitsa golide ndi siliva

mʼnyumba zosungira chuma chako.

5Ndi nzeru zako zochitira malonda

unachulukitsa chuma chako

ndipo wayamba kunyada

chifukwa cha chuma chakocho.

6“ ‘Choncho Ine Ambuye Yehova ndikuti,

“ ‘Popeza umadziganizira

kuti ndiwe mulungu,

7Ine ndidzabwera ndi anthu achilendo, anthu ankhanza,

kuti adzalimbane nawe.

Adzakuthira nkhondo kuti awononge zonse zimene unazipeza ndi nzeru zako,

ndipo adzawononga kunyada kwakoko.

8Iwo adzakuponyera ku dzenje

ndipo udzafa imfa yoopsa

mʼnyanja yozama.

9Kodi udzanenabe kuti, ‘Ine ndine mulungu,’

pamaso pa iwo amene akukupha?

Iwe udzaoneka kuti ndiwe munthu chabe, osati mulungu,

mʼmanja mwa iwo amene akukuphawo.

10Udzafa imfa ya anthu osachita mdulidwe

mʼmanja mwa anthu achilendo.

Ine ndayankhula zimenezi, akutero Ambuye Yehova.’ ”

11Yehova anandiyankhula kuti: 12“Iwe mwana wa munthu, imba nyimbo yodandaulira mfumu ya Turo ndipo uyiwuze mawu a Ine Ambuye Yehova akuti,

“ ‘Iwe unali chitsanzo cha ungwiro weniweni,

wodzaza ndi nzeru ndi wokongola kwambiri.

13Iwe unkakhala ngati mu Edeni,

munda wa Mulungu.

Miyala yokongola ya mitundu yonse:

rubi, topazi ndi dayimondi,

kirisoliti, onikisi, yasipa,

safiro, kalineliyoni ndi berili ndiwo inali zofunda zako.

Ndipo zoyikamo miyalayo zinali zagolide.

Anakupangira zonsezi pa tsiku limene unalengedwa.

14Ndinayika kerubi kuti azikulondera.

Unkakhala pa phiri langa lopatulika,

ndipo unkayendayenda

pakati pa miyala ya moto.

15Makhalidwe ako anali abwino

kuyambira pamene unalengedwa

mpaka nthawi imene unayamba kuchita zoyipa.

16Unatanganidwa ndi zamalonda.

Zotsatira zake zinali zoti unachulukitsa zandewu

ndi kumachimwa.

Choncho ndinakuchotsa ku phiri langa lopatulika.

Mkerubi amene ankakulondera uja anakupirikitsa

kukuchotsa ku miyala yamoto.

17Unkadzikuza mu mtima mwako

chifukwa cha kukongola kwako,

ndipo unayipitsa nzeru zako

chifukwa chofuna kutchuka.

Kotero Ine ndinakugwetsa pansi

kuti ukhala chenjezo pamaso pa mafumu.

18Ndi malonda ako achinyengo unachulukitsa machimo ako.

Motero unayipitsa malo ako achipembedzo.

Choncho ndinabutsa moto pakati pako,

ndipo unakupsereza,

ndipo unasanduka phulusa pa dziko lapansi

pamaso pa anthu onse amene amakuona.

19Anthu onse amitundu amene ankakudziwa

akuchita mantha chifukwa cha iwe.

Watheratu mochititsa mantha

ndipo sudzakhalaponso mpaka muyaya.’ ”

Za Chilango cha Sidoni

20Yehova anandiyankhula nati: 21“Iwe mwana wa munthu, utembenukire ku mzinda wa Sidoni ndipo unenere mowudzudzula kuti, 22‘Ine Ambuye Yehova ndikuti,

“ ‘Ndine mdani wako, iwe Sidoni,

ndipo ndidzalemekezedwa chifukwa cha iwe.

Anthu adzadziwa kuti Ine ndine Yehova

ndikadzakulanga ndi kudzionetsa kuti

ndine woyera pakati pako.

23Ndidzatumiza mliri pa iwe

ndi kuchititsa magazi kuti ayende mʼmisewu yako.

Anthu ophedwa ndi lupanga

adzagwa mbali zonse.

Pamenepo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.

24“ ‘Nthawi imeneyo Aisraeli sadzakhalanso ndi anthu pafupi achipongwe amene ali ngati nthula zowawa ndi ngati minga zopweteka. Pamenepo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Ambuye Yehova.

25“ ‘Ine Ambuye Yehova mawu anga ndi awa: Nditasonkhanitsa Aisraeli kuchoka ku mayiko kumene anamwazikira, ndidzadzionetsa kuti ndine woyera pakati pawo pamaso pa anthu a mitundu ina. Adzakhala mʼdziko lawo, limene ndinalipereka kwa mtumiki wanga Yakobo. 26Adzakhala kumeneko mwamtendere ndipo adzamanga nyumba ndi kulima minda ya mpesa. Adzakhala kumeneko mwamtendere pamene ndidzalange anthu oyandikana nawo, amene ankawanyoza. Motero iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova Mulungu wawo.’ ”

New Serbian Translation

Књига пророка Језекиља 28:1-26

Пророштво против тирског кнеза

1Дође ми реч Господња: 2„Сине човечији, реци тирском владару: ’Говори Господ Бог:

Узохолио си се у срцу говорећи:

„Ја сам бог;

седим на Божијем престолу28,2 Или: седим на престолу богова.

у срцу мора.“

Ипак, ти си само човек, а не Бог,

иако свој ум изједначаваш с Божијим умом.

3Ето, мудрији си од Данила;

ниједна тајна ти није скривена.

4Стекао си себи богатство

мудрошћу и разумом,

накупио си сребро и злато

у својим ризницама.

5Умножио си своје богатство

великом својом мудрошћу у трговини,

али си се узохолио у срцу

због свог богатства.

6Зато говори Господ Бог:

Зато што изједначаваш свој ум

с Божијим умом,

7ево, довешћу на тебе туђинце,

најнемилосрдније међу народима,

а они ће исукати мачеве

на лепоту твоје мудрости

и окаљати твој сјај.

8Бациће те у јаму

и умрећеш смрћу посечених усред мора.

9Хоћеш ли пред својим погубитељем да кажеш: „Ја сам Бог“?

Ти си човек, а не Бог,

кад паднеш у руке својих погубитеља!

10Умрећеш смрћу необрезаних руком туђинаца,

јер сам ја то рекао – говори Господ Бог.’“

11Опет ми дође реч Господња: 12„Сине човечији, испевај тужбалицу против тирског цара. Реци му: ’Говори Господ Бог:

Ти си печат савршенства,

пун мудрости и савршен у лепоти.

13Био си у Едену, врту Божијем,

сав окићен драгим камењем:

рубином, топазом, дијамантом,

хрисолитом, ониксом, јасписом,

сафиром, малахитом и смарагдом;

златом те уоквирили и извезли,

учврстили их у дан кад си био створен.

14Учиних те херувимом заштитником,

поставих те на свету гору Божију,

ходио си посред огњеног камења.

15Беспрекоран беше на путевима својим,

од дана кад си створен,

до дана кад се неправда нашла на теби.

16Због обиља твоје трговине

напунило се насиље у теби; згрешио си.

Зато те збацих нечистог с горе Божије

и уклоних те, херувиме заштитниче,

исред огњеног камења.

17Понело се срце твоје због твоје лепоте,

упропасти мудрост своју због свог сјаја.

И бацио сам те на земљу,

пред цареве те земаљске поставио

да те они гледају с презрењем.

18Због многих твојих кривица,

због трговине твоје непоштене,

светилиште си своје оскрнавио.

Зато сам запалио огањ посред тебе,

и огањ те је прогутао;

у пепео сам те претворио

на очи свима што те гледају.

19Сви који су те знали међу народима,

згражају се сад над тобом,

постао си призором ужаса,

и више те никада неће бити.’“

Пророштво против Сидона

20Дође ми реч Господња: 21„Сине човечији, окрени се лицем према Сидону и пророкуј против њега. 22Реци: ’Говори Господ Бог:

Ево ме против тебе, Сидоне,

да се прославим усред тебе.

И знаћете да сам ја Господ,

када над њим извршим суд,

и када покажем своју светост у њему.

23Послаћу на њега пошаст,

и крви ће бити на његовим улицама.

Посечени ће гинути усред њега од мача,

који ће их стизати са свих страна.

Тада ће знати да сам ја Господ.

24Дом Израиљев неће више имати трн који убада, ни бодљу која наноси бол; ниоткуда више неће бити оних који их презиру. Тада ће знати да сам ја Господ Бог.

25Зато говори Господ: када скупим дом Израиљев из народа где су били расејани, и покажем на њима своју светост пред пуцима, тада ће живети на земљи, коју сам ја дао своме слузи Јакову. 26И живеће спокојно на њој: градиће куће, садиће винограде и живеће безбедно, када извршим суд над свима који их презиру са свих страна. Тада ће знати да сам ја, Господ, њихов Бог.’“