Eksodo 39 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Eksodo 39:1-43

Zovala za Ansembe

1Anapanga zovala za ansembe, zovala potumikira ku malo wopatulika pogwiritsa ntchito nsalu ya mtundu wa mtambo, yapepo ndi yofiira. Anapanganso zovala zopatulika za Aaroni monga momwe Yehova analamulira Mose.

Chovala cha Efodi

2Popanga efodi, iwo anagwiritsa ntchito golide, nsalu yamtundu wa mtambo, yapepo, yofiira, yosalala yofewa. 3Anasula golide wopyapyala ndi kumulezaleza kuti alumikize kumodzi ndi nsalu yamtundu wa mtambo, yapepo ndi yofiira yosalala yofewa yolukidwa mwaluso. 4Iwo anapanga efodi imene inali ndi timalamba tiwiri ta pa mapewa, tosokerera ku msonga zake ziwiri kuti azitha kumanga. 5Lamba womangira efodi anali wolukidwa mwaluso ngati efodiyo. Anali nsalu imodzi ndi efodiyo, wopangidwa ndi golide, nsalu yamtundu wa mtambo, yapepo, yofiira, yofewa yosalala, monga momwe Yehova analamulira Mose.

6Iwo anakonza miyala ya onikisi ndi kuyiika mu zoyikamo zake zagolide ndipo anazokota mayina a ana a Israeli monga amachitira pa chidindo. 7Kenaka anayimangirira pa tinsalu ta mʼmapewa ta efodi tija ngati miyala ya chikumbutso cha ana a Israeli monga momwe Yehova analamulira Mose.

Chovala Chapachifuwa

8Iwo anapanga chovala chapachifuwa mwaluso kwambiri. Anachipanga ngati efodi pogwiritsa ntchito golide, nsalu yamtundu wa mtambo, yapepo, yofiira, yofewa yosalala ndi yolukidwa bwino. 9Kutalika kwake kunali kofanana mbali zonse, mulitali masentimita 23, mulifupi masentimita 23, chinali chopinda pawiri. 10Kenaka anayikapo mizere inayi ya miyala yokongola kwambiri. Mzere woyamba anayika miyala ya rubi, topazi ndi berili; 11mzere wachiwiri anayikapo miyala ya emeradi, safiro ndi dayimondi; 12mzere wachitatu anayikapo miyala ya opera, agate ndi ametisiti; 13mzere wachinayi anayikapo miyala ya topazi, onikisi ndi yasipa. Miyalayi anayiyika mu zoyikamo zagolide. 14Miyalayo inalipo khumi ndi iwiri, uliwonse kuyimira dzina limodzi la ana a Israeli. Mwala uliwonse unazokotedwa ngati chidindo dzina limodzi la mafuko khumi ndi awiri a Israeli.

15Anapanga timaunyolo tagolide wabwino kwambiri ta pa chovala chapachifuwa, topota ngati chingwe. 16Anapanganso zoyikamo zake zagolide ndi mphete ziwiri zagolide, ndipo anamangirira mphetezo pa ngodya ziwiri za chovala chapachifuwa. 17Anamangirira timaunyolo tiwiri tagolide tija pa mphete za pa ngodya pa chovala chapachifuwacho. 18Ndipo mbali ina ya timaunyoloto anamangirira pa zoyikapo zake ziwiri zija, ndi kulumikiza pa tinsalu takutsogolo kwa mapewa a efodi. 19Anapanganso mphete ziwiri zagolide ndipo analumikiza ku ngodya ziwiri zamʼmunsi mwa chovala chapachifuwa, champhepete mwake, mʼkati pafupi ndi efodi ija. 20Kenaka anapanga mphete zina ziwiri zagolide ndi kuzilumikiza kumunsi kwa tinsalu takutsogolo kwa efodi, pafupi ndi msoko, pamwamba pangʼono pa lamba wamʼchiwuno wa efodi. 21Anamangirira mphete za pa chovala chapachifuwa zija ku mphete za efodi ndi chingwe chamtundu wa mtambo, kulumikiza lamba ndi chovala chapachifuwacho kuti chovala chapachifuwacho chisalekane ndi efodi ija monga Yehova analamulira Mose.

Zovala zina za Unsembe

22Anayipangira efodiyo mkanjo wamtundu wa mtambo, wolukidwa ndi mmisiri waluso. 23Mkanjowo unali ndi malo opisapo mutu pakati pakepo. Pa chibowopo panali chibandi chosokedwa mochita ngati kuluka monga muja akhalira malaya kuti chibowocho chilimbe, chisangʼambike. 24Pa mpendero wamʼmunsi wa mkanjowo, analumikiza mphonje zokhala ngati makangadza za nsalu yamtundu wa mtambo, yapepo ndi yofiira yofewa yosalala ndi yopetedwa bwino yomwe inazungulira mkanjo. 25Ndipo anapanga maberu agolide wabwino kwambiri ndipo analumikiza mozungulira mpendero pakati pa makangadzawo. 26Kotero panali mphonje imodzi ndi belu limodzi kuzungulira mpendero wa mkanjo wovala potumikira monga momwe Yehova analamulira Mose.

27Kwa Aaroni ndi ana ake anawapangira minjiro ya nsalu yofewa yosalala, yolukidwa bwino ndi munthu waluso, 28nduwira ya nsalu yofewa yosalala, lamba wa nsalu yofewa yosalala, womanga mʼmutu, ndi makabudula amʼkati a nsalu yofewa yosalala olukidwa bwino. 29Anapanga lamba wolukidwa bwino wa nsalu yofewa ndi yosalala ya mtundu wa mtambo yapepo ndi yofiira. Ili linaliluso la munthu wopanga zokometsera monga Yehova analamulira Mose.

30Iwo anapanga duwa lagolide wabwino kwambiri ngati chidindo ndipo anazokotapo mawu akuti, wopatulikira Yehova. 31Kenaka analimangira ndi chingwe cha nsalu yamtundu wa mtambo pa nduwira, monga momwe Yehova analamulira Mose.

Mose Ayendera Chihema

32Tsopano ntchito yonse ya tenti ya msonkhano inatha. Aisraeli anachita zonse monga momwe Yehova analamulira Mose. 33Kenaka anabweretsa chihema kwa Mose. Tenti ndi zipangizo zake, ngowe zake, maferemu ake, mitanda yake, mizati yake ndi matsinde ake; 34chophimba cha chikopa cha nkhosa yayimuna chonyikidwa mu utoto ofiira, chophimba cha chikopa cha akatumbu ndi nsalu zophimba; 35bokosi la umboni pamodzi ndi mitengo yake yonyamulira ndiponso chovundikira chake; 36tebulo pamodzi ndi zipangizo zake ndiponso buledi wokhala pamaso pa Yehova; 37choyikapo nyale chagolide wabwino kwambiri pamodzi ndi nyale zake ndi zipangizo zake zonse, ndiponso mafuta anyalezo; 38guwa lagolide, mafuta odzozera, lubani onunkhira ndi nsalu yotchinga pa khomo lolowera mu tenti; 39guwa lamkuwa ndi sefa yamkuwa, mitengo yake yonyamulira ndi zipangizo zake zonse; beseni ndi miyendo yake; 40nsalu yotchingira bwalo pamodzi ndi mizati yake ndi matsinde ake ndiponso nsalu yotchingira pa khomo lolowera ku bwalo; zingwe zake ndi zikhomo za tenti; zipangizo zonse za chihema, tenti ya msonkhano; 41ndiponso zovala zolukidwa zovala potumikira kumalo opatulika, zovala zopatulika za wansembe, Aaroni pamodzi ndi za ana ake aamuna pamene akutumikira monga ansembe.

42Aisraeli anagwira ntchito yonse monga momwe Yehova analamulira Mose. 43Mose anayendera ntchitoyo ndipo anaona kuti anayichita monga momwe Yehova analamulira. Kotero Mose anawadalitsa.

New International Reader’s Version

Exodus 39:1-43

The Clothes for the Priests

1The workers made clothes from the blue, purple and bright red yarn. The clothes were worn by the priests who served in the holy tent. The workers also made sacred clothes for Aaron. They made them just as the Lord had commanded Moses.

The Linen Apron

2The workers made the linen apron. They made it out of thin gold wire, and of blue, purple and bright red yarn, and of finely twisted linen. 3They hammered out thin sheets of gold. They cut it into thin wire. Then they sewed it into the blue, purple and bright red yarn and fine linen. Skilled workers made it. 4The workers made shoulder straps for the apron. The straps were joined to two of its corners. 5Its skillfully made waistband was made like the apron. The waistband was part of the apron itself. It was made out of thin gold wire, and out of blue, purple and bright red yarn, and out of finely twisted linen. The workers made it just as the Lord had commanded Moses.

6They put the onyx stones in fancy gold settings. They carved the names of the sons of Israel on the stones. They did it the way a jewel cutter would carve them. 7Then they connected them to the shoulder straps of the linen apron. The stones stood for the sons of Israel and were a constant reminder for them. The workers did those things just as the Lord had commanded Moses.

The Chest Cloth

8Skilled workers made the chest cloth. They made it like the linen apron. They used thin gold wire, and blue, purple and bright red yarn, and finely twisted linen. 9The chest cloth was nine inches square. It was folded in half. 10The workers put four rows of valuable jewels on it. Carnelian, chrysolite and beryl were in the first row. 11Turquoise, lapis lazuli and emerald were in the second row. 12Jacinth, agate and amethyst were in the third row. 13And topaz, onyx and jasper were in the fourth row. The workers put them in fancy gold settings. 14They used a total of 12 stones. There was one stone for each of the names of the sons of Israel. Each stone was carved with the name of one of the 12 tribes.

15The workers made braided chains out of pure gold for the chest cloth. They made them like ropes. 16They made two fancy gold settings and two gold rings. They connected them to two corners of the chest cloth. 17They joined the two gold chains to the rings at the corners of the chest cloth. 18They joined the other ends of the chains to the two settings. They joined them to the shoulder straps on the front of the linen apron. 19The workers made two gold rings. They connected them to the other two corners of the chest cloth. They put them on the inside edge next to the apron. 20Then they made two more gold rings. They connected them to the bottom of the shoulder straps on the front of the apron. They put them close to the seam. They put them right above the waistband of the apron. 21They tied the rings of the chest cloth to the rings of the apron with blue cord. That connected it to the waistband. Then the chest cloth would not swing out from the linen apron. The workers did those things just as the Lord had commanded Moses.

More Clothes for the Priests

22The workers made the outer robe of the linen apron completely out of blue cloth. The cloth was made by a skillful person. 23The workers made an opening in the center of the robe. They made an edge like a collar around the opening. Then it couldn’t tear. 24They made pomegranates out of blue, purple and bright red yarn and finely twisted linen. They sewed them around the hem of the robe. 25They made bells out of pure gold. They sewed them around the hem between the pomegranates. 26They sewed a bell between every two pomegranates all around the hem of the robe. Aaron had to wear the robe when he served as priest. That’s what the Lord commanded Moses.

27The workers made inner robes out of fine linen for Aaron and his sons. The linen cloth was made by a skillful person. 28The workers also made the turban out of fine linen. And they made the caps and the underwear out of finely twisted linen. 29The belt was made out of finely twisted linen and blue, purple and bright red yarn. A person who sewed skillfully made it. The workers did those things just as the Lord had commanded Moses.

30They made the plate out of pure gold. It was a sacred crown. On the plate, they carved the words

Set Apart for the Lord.

31Then they tied the plate to the turban with a blue cord. They did those things just as the Lord had commanded Moses.

The Holy Tent Is Completed

32So all the work on the holy tent, the tent of meeting, was completed. The Israelites did everything just as the Lord had commanded Moses. 33Then they brought the holy tent to Moses along with everything that belonged to it. Here are the things they brought:

hooks, frames, crossbars, posts and bases

34the covering of ram skins dyed red, the covering of another kind of strong leather and the curtain that hides the ark

35the ark where the tablets of the covenant law are kept, the poles and the cover for the ark

36the table for the holy bread with all its things and the holy bread

37the pure gold lampstand with its row of lamps and everything used with it, and the olive oil that gives light

38the gold altar for burning incense, the anointing oil and the sweet-smelling incense

the curtain for the entrance to the tent

39the bronze altar for burnt offerings with its bronze grate, its poles and all its tools

the large bowl with its stand

40the curtains of the courtyard with their posts and bases, and the curtain for the entrance to the courtyard

the ropes and tent stakes for the courtyard

everything that belongs to the holy tent, the tent of meeting

41and the sacred clothes for Aaron the priest and the clothes for his sons when they serve as priests

42The Israelites had done all the work just as the Lord had commanded Moses. 43Moses looked over the work carefully. He saw that the workers had done it just as the Lord had commanded. So Moses gave them his blessing.