Eksodo 38 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Eksodo 38:1-31

Guwa Lansembe Yopsereza

1Anapanga guwa lansembe zopsereza lamatabwa amtengo wa mkesha. Linali lofanana mbali zonse. Msinkhu wake masentimita 137, mulitali mwake masentimita 229, mulifupi masentimita 229. 2Anapanga nyanga imodziimodzi pa ngodya zake zinayizo, kotero kuti nyangazo ndi guwalo zinali chinthu chimodzi, ndipo anakuta guwalo ndi mkuwa. 3Anapanganso ziwiya zamkuwa izi zogwirira ntchito pa guwalo: miphika, mafosholo, mabeseni owazira magazi, ngowe zokowera nyama ndi zosonkhezera moto. 4Anapanga sefa yachitsulo chamkuwa ya guwa lansembelo kuti ikhale mmunsi mwa khoma la guwa lansembelo, kuchokera pansi mpaka pakati pa khoma la guwalo. 5Anapanga mphete zamkuwa zinayi ndipo anazilumikiza ku ngodya zinayi za sefa ija kuti zigwire nsichi zonyamulira. 6Anapanga nsichi zamtengo wa mkesha ndipo anazikuta ndi mkuwa. 7Iwo analowetsa nsichizo mʼmphetemo mbali zonse ziwiri za guwalo kuti azinyamulira. Guwalo linali lamatabwa ndi logoba mʼkati mwake.

Beseni Losambira

8Anapanga beseni lamkuwa lokhala ndi miyendo yamkuwanso kuchokera ku magalasi oyangʼanira nkhope a amayi amene ankatumikira pa chipata cha tenti ya msonkhano.

Bwalo la Chihema

9Kenaka anapanga bwalo la chihema. Mbali yakummwera inali yotalika mamita 46 ndipo kunali nsalu yotchinga yofewa yosalala yolukidwa bwino. 10Anapanganso mizati makumi awiri, matsinde makumi awiri amkuwa ndi ngowe zasiliva ndi zingwe za mizatiyo. 11Mbali yakumpoto inalinso yotalika mamita 46 ndipo inali ndi mizati makumi awiri, matsinde amkuwa makumi awiri, ngowe zasiliva ndi zingwe za mizatiyo.

12Mbali yakumadzulo inali yotalika mamita 23 ndipo inali ndi nsalu yotchinga, mizati khumi ndi matsinde khumi. Inalinso ndi ngowe zasiliva ndi zingwe za mizatiyo. 13Mbali yakummawa, kotulukira dzuwa, inalinso yotalika mamita 23. 14Mbali imodzi yachipata kunali nsalu yotchinga yotalika mamita asanu ndi awiri, mizati itatu ndi matsinde atatu, 15polowera mʼbwalo panali nsalu yotchinga ya mamita asanu ndi awiri pamodzi ndi mizati itatu ndi matsinde atatu. 16Katani yonse yotchinga kuzungulira chihema inali yofewa, yosalala ndi yolukidwa bwino. 17Matsinde amizati anali amkuwa. Ngowe ndi zingwe za mizati zinali zasiliva, ndipo pamwamba pa mizatiyo anakutapo siliva. Choncho mizati yonse ya bwalolo inalumikizidwa ndi zingwe zasiliva.

18Nsalu yotchinga ya pa chipata inali yamtundu wa mtambo, yapepo ndi yofiira, yofewa yosalala ndi yopangidwa ndi anthu aluso. Nsaluyo inali yotalika mamita asanu ndi anayi, molingana ndi nsalu zotchinga bwalo. Msinkhu wake unali masentimita 229, 19pamodzi ndi mizati yake inayi ndi matsinde amkuwa anayi. Ngowe ndi zingwe zake zinali za siliva, ndipo pamwamba pake pa mzati anakutapo ndi siliva. 20Zikhomo za chihema ndi zina zonse zozungulira chihemacho zinali zamkuwa.

Zipangizo Zachitsulo za ku Malo Opatulika

21Chiwerengero cha zipangizo zimene anagwiritsa ntchito popanga chihema, chihema chaumboni, zimene Mose analamulira Alevi kuti alembe motsogozedwa ndi Itamara mwana wa Aaroni, wansembe, chinali ichi: 22Bezaleli mwana wa Uri, mwana wa Huzi wa fuko la Yuda anapanga chilichonse Yehova analamulira Mose, 23pamodzi ndi Oholiabu mwana wa Ahisamaki, wa fuko la Dani, wa luso la zopangapanga ndi kulemba mapulani, ndi wopanga nsalu zolukidwa bwino za mtundu wa mtambo, yapepo ndi zofiira, zofewa ndi zosalala. 24Golide yense wochokera ku nsembe yoweyula amene anagwiritsa ntchito pa ntchito yonse yopanga malo wopatulika anali wolemera makilogalamu 1,000 potsata miyeso ya kumalo wopatulika.

25Siliva wochokera ku gulu lonse la anthu anali wolemerera makilogalamu 3,430, potsata miyeso ya ku malo wopatulika. 26Munthu aliyense amapereka beka imodzi, kufanana ngati makilogalamu 6, potsata muyeso wa ku malo wopatulika. Kuchokera kwa aliyense amene anawerengedwa kuyambira zaka 20 kapena kuposerapo, amuna onse analipo 603,550. 27Anagwiritsa ntchito siliva wolemera makilogalamu 3,400 kupanga matsinde 100 a ku malo wopatulika ndi makatani, ndipo makilogalamu 34 kupanga tsinde limodzi. 28Makilogalamu otsalawo anagwiritsa ntchito popanga ngowe zamzati kukutira pamwamba pa mizati ndiponso kupanga zingwe zake.

29Mkuwa ochokera ku nsembe yoweyula unali makilogalamu 2,425. 30Iwo anawugwiritsa ntchito popanga matsinde a pa chipata cha tenti ya msonkhano, guwa la mkuwa pamodzi ndi sefa yake ndiponso ziwiya zonse, 31matsinde ozungulira bwalo ndiponso a pa chipata pake, ndi zikhomo zonse za tentiyo ndi matsinde a malo wozungulirapo.

New International Reader’s Version

Exodus 38:1-31

The Altar for Burnt Offerings

1The workers built the altar for burnt offerings out of acacia wood. It was four feet six inches high and seven feet six inches square. 2They made a horn stick out from each of its four upper corners. They covered the altar with bronze. 3They made all its tools out of bronze. They made its pots, shovels, sprinkling bowls, meat forks, and pans for carrying ashes. 4They made a bronze grate for the altar. They put the grate halfway up the altar on the inside. 5They made a bronze ring for each of the four corners of the grate. 6They made poles out of acacia wood. They covered them with bronze. 7They put the poles through the rings. The poles were on two sides of the altar for carrying it. The workers made the altar out of boards. They left it hollow.

The Large Bowl for Washing

8The workers made the large bronze bowl and its bronze stand. They made them out of bronze mirrors. The mirrors belonged to the women who served at the entrance to the tent of meeting.

The Courtyard

9Next, the workers made the courtyard. The south side was 150 feet long. It had curtains made out of finely twisted linen. 10The curtains had 20 posts and 20 bronze bases. The posts had silver hooks and bands on them. 11The north side was also 150 feet long. Its curtains had 20 posts and 20 bronze bases. The posts had silver hooks and bands on them.

12The west end was 75 feet wide. It had curtains with ten posts and ten bases. The posts had silver hooks and bands on them. 13The east end, toward the sunrise, was also 75 feet wide. 14Curtains 22 feet six inches long were on one side of the entrance to the courtyard. They were hung on three posts. Each post had a base. 15Curtains 22 feet six inches long were also on the other side of the entrance. They were hung on three posts. Each post had a base. 16All the curtains around the courtyard were made out of finely twisted linen. 17The bases for the posts were made out of bronze. The hooks and bands on the posts were made out of silver. Their tops were covered with silver. So all the posts of the courtyard had silver bands.

18The curtain for the courtyard entrance was made out of blue, purple and bright red yarn and finely twisted linen. A person who sewed skillfully made it. It was 30 feet long. Like the curtains of the courtyard, it was seven feet six inches high. 19It had four posts and four bronze bases. Their hooks and bands were made out of silver. Their tops were covered with silver. 20All the tent stakes of the holy tent were made out of bronze. So were all the stakes of the courtyard around it.

The Amounts of the Metals Used

21Here are the amounts of the metals used for the holy tent, where the tablets of the covenant law were kept. Moses commanded the Levites to record the amounts. The Levites did the work under the direction of Ithamar. Ithamar was the son of Aaron the priest. 22Bezalel, the son of Uri, made everything the Lord had commanded Moses. Uri was the son of Hur. Bezalel was from the tribe of Judah. 23Oholiab, the son of Ahisamak, helped Bezalel. Oholiab was from the tribe of Dan. He could carve things and make patterns. And he could sew skillfully with blue, purple and bright red yarn and on fine linen. 24The total weight of the gold from the wave offering was more than a ton. It was weighed out in keeping with the standard weights used in the sacred tent. The gold was used for all the work done in connection with the sacred tent.

25The silver received from the men in the community who were listed and counted weighed almost four tons. It was weighed out in keeping with the weights used in the sacred tent. 26It amounted to a fifth of an ounce for each person. It was weighed out in keeping with the weights used in the sacred tent. The silver was received from the men who had been listed and counted. All of them were 20 years old or more. Their total number was 603,550. 27The four tons of silver were used to make the bases for the holy tent and for the curtain. The 100 bases were made from the four tons. Each base used more than 75 pounds of silver. 28The workers used 45 pounds to make the hooks for the posts, to cover the tops of the posts, and to make their bands.

29The bronze from the wave offering weighed two and a half tons. 30The workers used some of it to make the bases for the entrance to the tent of meeting. They used some for the bronze altar for burnt offerings and its bronze grate and all its tools. 31They used some for the bases for the courtyard around the holy tent. They used some for the bases for the courtyard entrance. And they used the rest to make all the tent stakes for the holy tent and the courtyard around it.