Eksodo 12 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Eksodo 12:1-51

Kukhazikitsidwa kwa Paska

1Yehova anayankhula kwa Mose ndi Aaroni mʼdziko la Igupto kuti, 2“Mwezi uno uzikhala mwezi wanu woyamba wa chaka. 3Muliwuze khamu lonse la Israeli kuti pa tsiku la khumi la mwezi uno, munthu aliyense asankhire banja lake mwana wankhosa mmodzi. Banja lililonse litenge mwana wankhosa mmodzi. 4Ngati banja lili lochepa moti silingathe kudya nyama yonse ya nkhosa, ligawane ndi banja lomwe layandikana nalo nyumba. Mabanja adziwiretu chiwerengero cha anthu amene alipo pokonzekera zimenezi. Muwerengere kuchuluka kwa nyama imene anthu adzadye potengera mmene munthu mmodzi angadyere. 5Ziweto zimene musankhe ziyenera kukhala zazimuna za chaka chimodzi, zopanda chilema, ndipo zikhale nkhosa kapena mbuzi. 6Muzisunge mpaka tsiku la khumi ndi chinayi la mwezi, pamene gulu lonse la Aisraeli lidzaphe nyamazo madzulo. 7Ndipo adzatengeko magazi anyamazo ndi kuwaza pa mphuthu ziwiri za chitseko ndiponso pamwamba pa chitseko cha nyumba mmene adzadyeremo ana ankhosawo. 8Adzawotche nyamayo ndi kudya usiku womwewo, ndipo adzayidye ndi buledi wophikidwa popanda yisiti pamodzi ndi masamba wowawa. 9Musadzadye yayiwisi kapena yophika, koma mudzawotche yonse, mutu, miyendo ndi zamʼmimba. 10Musadzasiye nyama ina mpaka mmawa, ngati ina idzatsala mpaka mmawa, mudzayitenthe. 11Muzidzadya nyamayo mutavala chotere, pokonzekera ulendo: mudzazimangirire lamba mʼchiwuno, nsapato zanu kuphazi ndi ndodo yanu kumanja. Mudzadye mofulumira. Imeneyi ndi Paska ya Yehova.

12“Usiku umenewo Ine ndidzadutsa mʼdziko la Igupto ndipo ndidzapha chilichonse choyamba kubadwa kuyambira mwana wa munthu aliyense mpaka ana aziweto. Ndidzalanganso milungu yonse ya Igupto. Ine ndine Yehova. 13Magazi amene mudzawaze pa mphuthu za zitseko ndi pamwamba pa zitseko aja adzakhala ngati chizindikiro. Ine ndikadzaona magaziwo ndidzakudutsani, ndipo ndikadzamakantha anthu a Igupto, mliri wosakazawu sudzakukhudzani.

14“Ili ndi tsiku la chikumbutso. Tsiku limeneli muzidzachita chikondwerero, kupembedza Yehova. Mibado yonse imene ikubwera izidzakumbukira tsiku limeneli ngati lamulo lamuyaya ndi kuti pa tsikuli azidzachita chikondwerero cholemekeza Yehova. 15Kwa masiku asanu ndi awiri muzidya buledi wopanda yisiti. Tsiku loyamba muzichotsa yisiti mʼnyumba zanu, ngati aliyense adzadya kanthu kalikonse kali ndi yisiti kuyambira tsiku loyamba mpaka tsiku lachisanu ndi chiwiri, munthu ameneyo adzayenera kuchotsedwa mʼgulu la Israeli. 16Pa tsiku loyamba muzichita msonkhano wopatulika, ndipo winanso uzikhala pa tsiku lachisanu ndi chiwiri. Musamagwire ntchito masiku onsewa, koma ntchito yokonza chakudya yokha kuti aliyense adye. Izi ndi zimene muzichita.

17“Muzichita chikondwerero cha buledi wopanda yisiti, chifukwa ndi pa tsiku limeneli ndinatulutsa magulu anu mʼdziko la Igupto. Muzikondwerera tsiku limeneli pa mibado yonse ngati lamulo lamuyaya. 18Mwezi woyamba muzidzadya buledi wopanda yisiti kuyambira madzulo tsiku la 14 la mweziwo mpaka tsiku la 21 mwezi womwewo. 19Yisiti asamapezeka mʼnyumba zanu kwa masiku asanu ndi awiri. Ndipo aliyense amene adya chakudya chimene muli yisiti, munthu ameneyo ayenera kuchotsedwa mʼgulu la Aisraeli, kaya iyeyo ndi mlendo kapena mbadwa. 20Musadye chilichonse chokhala ndi yisiti. Kulikonse kumene mukukhala, muyenera kudya buledi wopanda yisiti.”

21Ndipo Mose anasonkhanitsa akuluakulu onse a Israeli nati, “Pitani msanga kukasankha nkhosa zokwanira pa mabanja anu, ndipo muziphe ngati Paska. 22Mutengenso nthambi ya chitsamba cha hisope, muchiviyike mʼmagazi amene mwawayika mʼbeseni ndipo muwaze ena mwa magaziwo pamwamba ndi mʼmbali mwa mphuthu za chitseko. Palibe aliyense wa inu amene adzatuluke mʼnyumba yake mpaka mmawa. 23Pamene Yehova adzadutsa mʼdziko kudzakantha Aigupto, nʼkuona magazi pamwamba ndi mʼmbali mwa mphuthu za chitseko, Iye adzadutsa khomo limenelo ndipo sadzalola woonongayo kuti alowe mʼnyumba zanu kuti akukantheni.

24“Muzimvera malamulo amenewa kwa muyaya, inu ndi zidzukulu zanu. 25Mukakalowa mʼdziko limene Yehova adzakupatseni monga analonjeza, mukasunge mwambo umenewu. 26Ndipo ana anu akakakufunsani kuti, ‘Mwambo umenewu ukutanthauza chiyani?’ 27Inu mukawawuze kuti, ‘Ndi nsembe ya Paska ya Yehova, popeza pamene ankakantha nyumba za Aigupto anasiya nyumba zathu.’ ” Kenaka anthu anawerama napembedza. 28Aisraeli anachita monga momwe Yehova analamulira Mose ndi Aaroni.

29Pakati pa usiku Yehova anakantha ana onse oyamba kubadwa mʼdziko la Igupto, kuyambira woyamba kubadwa wa Farao, amene amakhala pa mpando waufumu wa Faraoyo, mpaka mwana woyamba kubadwa wa munthu amene anali mʼdzenje, pamodzinso ndi ana oyamba kubadwa a ziweto zawo. 30Farao ndi nduna zake zonse ndiponso Aigupto onse anadzuka pakati pa usiku, ndipo kunali kulira kwakukulu mʼdziko lonse la Igupto, pakuti panalibe nyumba imene munalibe munthu wakufa.

Kutuluka kwa Aisraeli

31Pakati pa usiku Farao anayitanitsa Mose ndi Aaroni ndipo anati, “Nyamukani! Asiyeni anthu anga, inu ndi Aisraeli! Pitani, kapembedzeni Yehova monga munapempha. 32Tengani ziweto ndi ngʼombe zanu ndipo pitani kapembedzeni Mulungu wanu monga munanenera kuti ine ndidalitsike.”

33Aigupto anawawumiriza anthuwo kuti atuluke mofulumira ndi kusiya dziko lawo. Iwo anati, “Ngati sitiwalola kutero, tonse tidzafa.” 34Motero anthuwo ananyamula ufa wawo wopangira buledi asanathiremo yisiti ndipo anasenza pa mapewa awo pamodzi ndi zokandiramo buledi atazikulunga mu nsalu. 35Aisraeli anachita monga anawawuzira Mose kuti apemphe kwa Aigupto zozikongoletsera zasiliva ndi zagolide ndi zovala. 36Yehova anafewetsa mtima Aigupto kuti akomere mtima Aisraeliwo ndipo anawapatsa zimene anawapempha. Motero Aisraeli anawalanda zinthu Aigupto.

37Aisraeli anayenda ulendo kuchokera ku Ramesesi mpaka kukafika ku Sukoti. Anthu aamuna oyenda pansi analipo 600,000 osawerengera akazi ndi ana. 38Anthu enanso ambiri anapita nawo, kuphatikizanso gulu lalikulu la ziweto, mbuzi, nkhosa pamodzi ndi ngʼombe. 39Iwo anapanga buledi wopanda yisiti ndi ufa umene anachoka nawo ku Igupto. Ufawo unalibe yisiti chifukwa anachita kuthamangitsidwa ku Igupto ndipo analibe nthawi yokonzera chakudya chawo.

40Ndipo Aisraeli anakhala ku Igupto kwa zaka 430. 41Pa tsiku lomwelo limene anakwanitsa zaka 430, magulu onse a Yehova anatuluka mʼdziko la Igupto. 42Usiku wonse Yehova anachezera kutulutsa ana a Israeli mʼdziko la Igupto. Nʼchifukwa chake pa tsiku limeneli Aisraeli onse azichezera usiku wonse kulemekeza Mulungu kamba ka mibado yonse ya mʼtsogolo.

Lamulo la Paska

43Yehova anati kwa Mose ndi Aaroni, “Malamulo a Paska ndi awa:

“Mlendo asadye Paska. 44Kapolo aliyense amene munagula angadye ngati atayamba wachita mdulidwe. 45Koma amene mukukhala naye kwa kanthawi kapena waganyu asadye Paska.

46“Muzidyera Paska mʼnyumba imodzi. Musatulutse nyama iliyonse kunja kwa nyumba. Musaswe mafupa aliwonse. 47Gulu lonse la Israeli lizichita mwambo wachikondwererochi.

48“Ngati mlendo wokhala pakati panu angafune kuchita nawo mwambo wa chikondwerero cha Paska, cha Yehovachi, amuna onse a mʼnyumba mwake ayenera kuchita mdulidwe. Akatero muzimutenga ngati mbadwa pakati panu. Koma aliyense wosachita mdulidwe asadye Paska. 49Lamulo limeneli likhudza mbadwa ngakhalenso alendo wochita mdulidwe wokhala pakati panu.

50“Aisraeli onse anachita monga momwe Yehova analamulira Mose ndi Aaroni. 51Ndipo tsiku lomwelo Yehova anatulutsa gulu lonse la ana a Israeli mʼdziko la Igupto.”

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

出埃及记 12:1-51

逾越节

1耶和华在埃及摩西亚伦说: 2“从现在开始,你们要以这个月为一月,为一年之首。 3你要向以色列全体会众宣布,本月的第十日,每家都要预备一只羊羔,一家一只。 4倘若家人太少,吃不了一只,可以跟最近的邻居共享一只,你们要按人数和各人的食量预备羊羔。 5羊羔必须是毫无残疾、一岁的公绵羊或公山羊。 6全体会众要把羊留到本月十四日,在黄昏时分宰杀, 7然后取点血涂在房子的门框和门楣上,全家要在房子里吃羊肉。 8当晚,你们要用火把羊肉烤熟,与无酵饼和苦菜一起吃。 9不可吃生羊肉,也不可煮着吃,要把整只羊,连头带腿和内脏一并烤着吃。 10不可把肉留到早晨,留到早晨的肉要烧掉。 11你们吃的时候,要束腰、穿鞋、手中拿杖,要赶快吃,这是耶和华的逾越节。

12“因为那一夜我要巡遍埃及,把境内所有长子和头生的牲畜全都杀掉,也要严惩埃及所有的神明。我是耶和华。 13涂在你们房屋上的血是一个记号,我见到这血就会越过你们。我击打埃及的时候,那灾祸不会落到你们身上。 14你们要记住这一天,守为耶和华的节期,作为世世代代永远的定例。

除酵节

15“七天之内你们都要吃无酵饼。第一天,要清除家中所有的酵。任何人若在这七天当中吃有酵的饼,要将他从以色列人中铲除。 16在节期的第一天和第七天,你们都要招聚百姓举行圣会。这两天所有人都不得工作,除了预备各人要吃的以外,不可做任何工。 17你们要守这无酵节,因为我在这天把你们大队人马从埃及领了出来。你们要守这节期,作为世世代代永远的定例。 18从一月十四日晚上开始,直到二十一日晚上,你们都要吃无酵饼。 19在这七天内,你们屋里不能有酵。任何人若吃了有酵的东西,不论他是寄居者还是本地人,要将他从以色列会众中铲除。 20无论你们住在哪里都要吃无酵饼,不能吃有酵的食物。”

21于是,摩西召集以色列的众长老,对他们说:“你们家家户户都要挑选羊羔,把这逾越节的羊羔宰了。 22拿一把牛膝草蘸盆里的血,把血涂在门框和门楣上。天亮前,你们不可踏出门外。 23因为耶和华要巡行各地,击杀埃及人,祂看见你们的门框和门楣上有血,就必越过你们的家门,不让灭命者进你们家杀人。 24这是你们世世代代都要遵守的定例。 25你们进入耶和华应许给你们的地方以后,要守这逾越节。 26你们的儿女问你们守这节期的意义时, 27你们就说,‘这是献给耶和华逾越节的祭,因为我们从前在埃及时,祂击杀埃及人,却越过以色列人所住的房子,救了我们各家。’”百姓听了摩西这番话,都低头下拜。 28耶和华怎么吩咐摩西亚伦以色列人就照样遵行。

29到了半夜,耶和华把所有埃及人的长子都杀了,包括坐王位的法老的长子、牢中囚犯的长子和一切头生的牲畜。 30晚上,法老及其臣仆和所有埃及人都惊醒了,到处都是哭号声,因为没有一家不死人的。 31法老连夜召见摩西亚伦,对他们说:“你们和以色列人走吧,离开我的人民。就照你们的要求,去事奉耶和华吧! 32照你们的要求,把所有的牛羊都带走吧!也要为我祝福。” 33埃及人催促以色列人赶快离开埃及,因为他们说:“我们都要死了。” 34于是,以色列百姓就把没有酵的面团放在揉面盆里,用衣服包起来扛在肩上, 35又遵照摩西的吩咐向埃及人索取金器、银器和衣服。 36耶和华使埃及人恩待以色列人,他们要什么,埃及人就给什么。这样,以色列人夺取了埃及人的财富。

37以色列百姓从埃及兰塞启行,前往疏割,妇女孩童不算在内,单是步行的男子就有六十万, 38同行的还有许多外族人和大群的牛羊。 39他们用从埃及带出来的面团烤成无酵饼,面团没有酵,因为他们被催促离开埃及,没有时间准备食物。 40以色列人在埃及共住了四百三十年, 41正好满了四百三十年的那一天,耶和华带领以色列大队人马离开了埃及42那天晚上是耶和华把祂的子民带出埃及之夜,因此以后世世代代的以色列人都要在那日守夜,以尊崇耶和华。

43耶和华对摩西亚伦说:“以下是逾越节的条例。

“所有外族人都不可吃逾越节的羊羔, 44但那些买来的奴隶若接受了割礼,就可以吃。 45寄居的外族人和雇用的工人不可吃。 46你们吃的时候,应当在房子里吃,不得把肉带到外面去,也不可折断羊羔的一根骨头。 47以色列全体会众都要守这节期。 48跟你们住在一起的外族人如果想为耶和华守逾越节,他全家的男子都必须接受割礼,这样才可以像以色列人一样守逾越节,但没有接受割礼的人绝不可吃逾越节的羊羔。 49本地人和在你们中间寄居的外族人都要遵守这规矩。”

50耶和华怎样吩咐摩西亚伦以色列百姓都遵命而行。 51就在那一天,耶和华带领以色列大队人马离开了埃及