Eksodo 13 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Eksodo 13:1-22

Mwambo Wopatula Ana Oyamba Kubadwa

1Yehova anati kwa Mose, 2“Ana onse aamuna oyamba kubadwa uwapatule, ndi anga. Aliyense woyamba kubadwa pakati pa Aisraeli ndi wanga, kaya ndi wa munthu kapena wa chiweto.”

3Ndipo Mose anati kwa anthu, “Muzikumbukira tsiku lino, tsiku limene munatuluka mʼdziko la Igupto, dziko la ukapolo chifukwa Yehova anakutulutsani ndi dzanja lake lamphamvu. Musadye kalikonse kamene kali ndi yisiti. 4Pa tsiku la lero mwezi uno wa Abibu, mukutuluka mʼdziko la Igupto. 5Yehova akadzakulowetsani mʼdziko la Akanaani, Ahiti, Aamori, Ahivi ndi Ayebusi, dziko loyenda mkaka ndi uchi, muzikachita mwambo uwu mwezi uno. 6Muzidzadya buledi wopanda yisiti kwa masiku asanu ndi awiri ndipo tsiku lachisanu ndi chiwirilo muzichita chikondwerero cha Yehova. 7Mudye buledi wopanda yisiti masiku asanu ndi awiri. Pasapezeke chinthu chilichonse chokhala ndi yisiti pakati panu, kapena paliponse mʼdziko lanu. 8Tsiku limenelo muzidzawuza ana anu kuti, ‘Ine ndimachita zimenezi chifukwa cha zimene Yehova anandichitira pamene ndimatuluka mʼdziko la Igupto.’ 9Lamulo ili lidzakhala ngati chizindikiro chomangidwa pa dzanja lanu ndi chikumbutso choyikidwa pamphumi panu kuti malamulo a Yehova asachoke pakamwa panu. Pakuti Yehova anakutulutsani mʼdziko la Igupto ndi dzanja lake lamphamvu. 10Muzichita mwambo uwu pa nthawi yake chaka ndi chaka.

11“Yehova akadzakulowetsani ndi kukupatsani dziko la Kanaani monga analonjezera kwa inu ndi makolo anu, 12muzikapereka kwa Ambuye ana onse oyamba kubadwa. Ziweto zonse zazimuna zoyamba kubadwa ndi za Ambuye. 13Koma mwana woyamba kubadwa wa bulu muzikamuwombola ndi mwana wankhosa, koma ngati simukamuwombola, muzikamuthyola khosi. Mwana wamwamuna woyamba kubadwa muzikamuwombola.

14“Mʼtsogolomo mwana wanu akakafunsa kuti, ‘Zimenezi zikutanthauza chiyani?’ Mukamuwuze kuti, ‘Yehova anatitulutsa mʼdziko la Igupto, dziko la ukapolo ndi dzanja lamphamvu. 15Farao atakanitsitsa kuti asatitulutse, Yehova anapha aliyense woyamba kubadwa mʼdziko la Igupto, kuyambira ana a anthu ndi ziweto zomwe. Nʼchifukwa chake ine ndimapereka nsembe kwa Yehova, chachimuna chilichonse choyamba kubadwa ndipo mwana wamwamuna woyamba kubadwa ndimamuwombola.’ 16Ndipo chidzakhala kwa inu ngati chizindikiro chomangidwa pa dzanja lanu ndi pamphumi panu kuonetsa kuti Yehova anakutulutsani mʼdziko la Igupto ndi dzanja lake lamphamvu.”

Kuwoloka Nyanja

17Farao atalola anthu aja kuti atuluke, Mulungu sanawadzeretse njira yodutsa dziko la Afilisti, ngakhale kuti inali yachidule popeza Mulungu anati, “Ngati anthuwa atadzakumana ndi nkhondo angadzakhumudwe ndi kubwerera ku Igupto.” 18Choncho Mulungu anawadzeretsa anthuwo njira yozungulira ya mʼchipululu kulowera ku Nyanja Yofiira. Komabe Aisraeli anatuluka mʼdziko la Igupto atakonzekera nkhondo.

19Mose ananyamula mafupa a Yosefe chifukwa Yosefe anawalumbiritsa ana a Israeli. Iye anawawuza kuti, “Mulungu adzabwera ndithu kudzakuthandizani, ndipo mudzanyamule mafupa anga pochoka ku malo ano.”

20Atachoka ku Sukoti anakagona ku Etamu mʼmphepete mwa chipululu. 21Nthawi yamasana Yehova amakhala patsogolo pa anthu kuwatsogolera njira ndi chipilala cha mtambo, ndipo usiku Yehova ankawatsogolera ndi chipilala cha moto, kuwawunikira njira kuti athe kuyenda masana ndi usiku. 22Usana, chipilala cha mtambo ndi usiku, chipilala cha moto zinali patsogolo kuwatsogolera anthu aja.

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

出埃及记 13:1-22

奉献头胎

1耶和华对摩西说: 2以色列人中的长子和头生的牲畜都属于我,因此要把他们分别出来,使他们圣洁,归给我。”

3摩西对百姓说:“你们要记住离开埃及的这一天,因为耶和华用大能的手把你们从受奴役的地方解救出来。不可吃带酵的食物。 4你们是在亚笔月13:4 亚笔月是犹太历的第一个月,约在阳历三月中旬到四月中旬,相当于中国的春分时节。的这一天从埃及出来的, 5将来耶和华带领你们进入迦南以后,你们每逢此月都要为祂守节期。那里现在住着迦南人、人、亚摩利人、希未人和耶布斯人。耶和华已经向你们祖先起誓,应许赐给你们那奶蜜之乡。 6在节期的七天之内,你们只可以吃无酵饼,到了第七天,你们要为耶和华守节期。 7七天之内要吃无酵饼,你们境内不得有酵或是带酵的东西。 8那时,要告诉你们的子孙,‘这节期是纪念我们离开埃及时耶和华为我们所做的一切。’ 9这节期就好像在你们手上或额上作的记号,叫你们记得耶和华的律法,祂曾经用大能的手把你们带出埃及10因此,每一年你们都要按时守这节期。

11“将来耶和华成就祂起誓给你们祖先的应许,领你们进入迦南人的土地,把那里赐给你们以后, 12你们要把所有长子和头生的公畜归给祂。 13所有头生的公驴必须用羊羔赎回,不然就要打断它的脖子。要赎回你们所有的长子。 14将来你们的子孙问起这件事的意义,你们就回答,‘耶和华曾经用大能的手把我们从受奴役之地——埃及领出来。 15当时法老硬着心不肯放我们走,所以耶和华就把埃及人的长子和头生的牲畜全都杀了。因此,我们把所有头生的公畜当作祭牲献给耶和华,只把长子赎回来。’ 16这事就像在你们手上作记号,额上作标记,以牢记耶和华曾用大能的手领我们离开埃及。”

云柱和火柱

17法老让以色列人离开埃及后,上帝没有带领他们穿越非利士地区,虽然那是条捷径。因为上帝说:“如果他们遇上战争,就会改变主意,返回埃及。” 18所以,上帝领他们绕道而行,走旷野的路,前往红海13:18 红海”或译“芦苇湖”,确切地点约在今红海北端苏伊士运河附近。以色列人离开埃及时都带着兵器。 19摩西约瑟的骸骨一起带走,因为约瑟曾叫以色列人郑重发誓,对他们说:“上帝必眷顾你们,把你们带出埃及,那时你们要把我的骸骨也一起带走。” 20以色列人从疏割启程,来到旷野边缘的以倘安营。 21耶和华走在他们前面,白天用云柱为他们指示道路,晚上用火柱照亮他们,这样他们可以日夜赶路。 22白天的云柱和晚上的火柱从不离开他们。