Deuteronomo 1 – CCL & PCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Deuteronomo 1:1-46

Mose Akumbutsa Aisraeli za ku Horebu

1Awa ndi mawu amene Mose anayankhula kwa Aisraeli onse mʼchipululu kummawa kwa Yorodani, ku Araba moyangʼanana ndi Sufi, pakati pa Parani ndi Tofeli, Labani, Heziroti ndi Dizahabu. 2(Kuyenda kuchokera ku Horebu kukafika ku Kadesi Barinea kudzera njira ya ku Phiri la Seiri ndi ulendo wa masiku khumi ndi limodzi).

3Mʼchaka cha makumi anayi, pa tsiku loyamba la mwezi 11, Mose anafotokozera Aisraeli zonse zimene Yehova anamulamula zokhudza iwowo. 4Apa nʼkuti atagonjetsa Sihoni mfumu ya Aamori, amene amalamulira ku Hesiboni, ndipo pa Ederi anagonjetsa Ogi mfumu ya ku Basani, amene amalamulira mu Asiteroti.

5Chakummawa kwa Yorodani mʼchigawo cha Mowabu, Mose anayamba kufotokozera lamulo ili kunena kuti:

6Ku Horebu, Yehova Mulungu wathu anati kwa ife, “Mwakhalitsa pa phiri lino. 7Sasulani msasa ndipo pitani ku dziko la mapiri la Aamori. Pitani kwa anthu onse oyandikana nawo ku Araba, ku mapiri, mʼmbali mwa mapiri a ku madzulo, ku Negevi ndiponso mʼmbali mwa nyanja, ku dziko la Akanaani ndi ku Lebanoni mpaka ku mtsinje waukulu wa Yufurate. 8Taonani, Ine ndakupatsani dziko ili. Lowani ndi kulilanda dziko limene Yehova analumbira kuti adzapereka kwa makolo anu, Abrahamu, Isake ndi Yakobo komanso kwa zidzukulu zawo.”

Kukhazikitsa Atsogoleri

9Pa nthawi imeneyi ine ndinati kwa inu, “Inu ndinu katundu olemera kwambiri woti sindingathe kumunyamula ndekha. 10Yehova Mulungu wanu wakuchulukitsani kotero kuti lero lino ndinu ochuluka ngati nyenyezi za kumwamba. 11Yehova Mulungu wa makolo anu wachulukitsa chiwerengero chanu ndipo wakudalitsani monga momwe analonjezera! 12Koma nanga ndekha ndidzasenza bwanji zovuta ndi zipsinjo zanu komanso milandu yanu? 13Sankhani amuna ena anzeru, ozindikira ndi amene mumawalemekeza kuchokera ku mtundu uliwonse wa mitundu yanu, ndipo ndidzawayika kuti akulamulireni.”

14Inu munandiyankha kuti, “Maganizo amenewa ndi abwino kuwachita.”

15Choncho ndinatenga anthu otsogolera mafuko anu, anzeru ndi omwe mumawalemekeza, ndipo ndinawayika kuti azikulamulirani mʼmagulu a 1,000, ena 100, ena makumi asanu ndi ena khumi, kuti akhalenso ngati akapitawo a mafuko. 16Ndipo pa nthawi imeneyo ndinawawuza olamula anu kuti, “Muzimva milandu ya pakati pa abale anu ndi kuweruza mosakondera, kaya mlanduwo uli pakati pa Aisraeli okhaokha kapena mmodzi wa iwo ndi mlendo. 17Osamayangʼana nkhope poweruza koma muzimvetsera aangʼono ndi aakulu omwe chimodzimodzi. Musamaope munthu aliyense, pakuti chiweruzo ndi cha Mulungu. Muzindibweretsera mlandu uliwonse wovuta ndipo ndidzaumva.” 18Ndipo nthawi imeneyo ndinakuwuzani chilichonse chimene munayenera kuchita.

Atumizidwa Kukazonda Dziko

19Tsono monga Yehova Mulungu wathu anatilamulira, tinanyamuka kuchoka ku Horebu ndi kupita cha ku dziko lamapiri la Aamori kudzera ku chipululu chachikulu ndi choopsa chija munachionachi, kotero kuti tinakafika ku Kadesi Barinea. 20Ndipo ndinati kwa inu, “Mwafika ku dziko la mapiri la Aamori, limene Yehova Mulungu wathu akutipatsa. 21Taonani, Yehova Mulungu wanu wakupatsani dzikoli. Pitani ndi kulitenga monga Yehova, Mulungu wa makolo anu anakuwuzirani. Musaope kapenanso kugwa mphwayi.”

22Tsono nonse munabwera kwa ine ndi kuti, “Tiyeni titumize anthu ayambe apita kuti akazonde dzikolo ndi kutibweretsera mawu pa za njira yomwe tidzere ndi za mizinda imene tikafikireko.”

23Ndinaona kuti maganizo amenewa anali abwino, choncho ndinasankha anthu khumi ndi awiri, mmodzi ku fuko lililonse. 24Iwo ananyamuka napita mʼdziko la mapiri, ndipo anafika ku Chigwa cha Esikolo ndi kukazonda dzikolo. 25Pobwerera anatitengerako zipatso za mʼdzikomo ndipo anatipatsa mawu akuti, “Dziko limene Yehova Mulungu wathu akutipatsa ndi labwino.”

Awukira Yehova

26Koma inu simunafune kupitako ndipo munawukira lamulo la Yehova Mulungu wanu. 27Inu munanyinyirika mʼmatenti anu nʼkumati, “Mulungu amatida nʼchifukwa chake anatitulutsa ku Igupto kuti atipereke mʼmanja mwa Aamori kuti atiwononge. 28Tigwire mtengo wanji? Abale athu anatitayitsa mtima. Iwo akuti, ‘Anthuwo ndi amphamvu ndi aatali kuposa ife, mizindayo ndi yayikulu ndipo mipanda yake ndi yayitali yofika kumwamba. Ife tinaonanso Aanaki kumeneko.’ ”

29Ndipo ine ndinati kwa inu, “Musachite mantha kapena kuwaopa. 30Yehova Mulungu wanu, amene akukutsogolerani, adzakumenyerani nkhondo monga muja anachitira ku Igupto inu mukuona, 31ndi mʼchipululu muja. Kumeneko munaona mmene Yehova Mulungu wanu anakunyamulirani monga abambo anyamulira mwana wawo, njira yonse yomwe munayenda mpaka munafika pamalo ano.”

32Ngakhale zinali choncho, simunadalire Yehova Mulungu wanu 33amene anakutsogolerani pa ulendo wanu, ndi moto nthawi ya usiku ndi mtambo nthawi ya masana, kukufunirani malo woti mumange msasa ndi kukuonetsani njira yoti muyendemo.

34Yehova atamva zimene munanena anakwiya nalumbira kuti, 35“Palibe ndi mmodzi yemwe mwa mʼbado woyipawu amene adzaona dziko labwino limene ndinalumbira kupatsa makolo anu, 36kupatula Kalebe mwana wa Yefune. Iye adzaliona, ndipo ndidzamupatsa iye ndi adzukulu ake, dziko limene adzapondamo popeza anatsata Yehova ndi mtima wake wonse.”

37Chifukwa cha inu, Yehova anakwiyiranso ine ndipo anati, “Iwenso sudzalowa mʼdzikomo. 38Koma Yoswa mwana wa Nuni amene amakuthandiza, adzalowa mʼdzikomo. Umulimbikitse chifukwa adzatsogolera Israeli kukalandira dzikolo. 39Ndipo angʼonoangʼono amene munati adzagwidwa ukapolo, ana anu amene sanadziwe kusiyanitsa chabwino ndi choyipa, amenewo adzalowa mʼdzikolo. Ndidzalipereka kwa iwo ndipo lidzakhala lawo. 40Koma inu, tembenukani nyamukani kulowera cha ku chipululu kutsatira njira ya ku Nyanja Yofiira.”

41Ndipo inuyo munati, “Tachimwa pamaso pa Yehova. Tipita ndi kukachita nkhondo monga Yehova Mulungu wathu watilamulira.” Choncho aliyense wa inu anavala zankhondo, ndi kuganiza kuti nʼkosavuta kupita mʼdziko la mapiri lija.

42Koma Yehova anandiwuza kuti, “Awuze anthuwa kuti, ‘Musapite kukachita nkhondo chifukwa Ine sindidzakhala nanu. Mudzagonjetsedwa ndi adani anu.’ ”

43Choncho ndinakuwuzani koma simunamve. Inu munawukira lamulo la Yehova ndipo mwamwano munayenda kulowa mʼdziko la mapiri. 44Aamori amene ankakhala mʼmapiriwo anatuluka kukakumana nanu ndipo anakuthamangitsani ngati gulu la njuchi ndipo anakukanthani kuchokera ku Seiri, njira yonse mpaka ku Horima. 45Munabwererako mukulira pamaso pa Yehova, koma Iye sanalabadire kulira kwanuko ndipo sanakumvetsereni. 46Pamenepo munakhala ku Kadesi masiku ambiri kwa nthawi yayitali ndithu.

Persian Contemporary Bible

تثنيه 1:1‏-46

1‏-5در اين كتاب، سخنرانی موسی خطاب به قوم اسرائيل، زمانی كه آنها در بيابان عربه (واقع در صحرای موآب) در شرق رود اردن بودند، ثبت شده است. شهرهای اين ناحيه عبارت بودند از: سوف، فاران، توفل، لابان، حضيروت و دی ذهب. (فاصلهٔ كوه حوريب تا قادش برنيع از طريق كوه سعير يازده روز است1‏:1‏-5 ولی بنی‌اسرائيل اين فاصله کوتاه را در مدت چهل سال طی کردند. قادش برنيع در مرز جنوبی سرزمين موعود قرار داشت.‏.) اين سخنرانی در روز اول ماه يازدهم سال چهلم بعد از خروج بنی‌اسرائيل از مصر ايراد شد. در آن زمان، سيحون، پادشاه اموری‌ها كه در حشبون حكومت می‌كرد شكست خورده بود و عوج، پادشاه سرزمين باشان كه در عشتاروت حكومت می‌كرد، در اَدَرعی مغلوب شده بود. موسی در اين سخنرانی به شرح قوانين و دستورات خداوند می‌پردازد:

دستور به ترک حوريب

6وقتی ما در كوه حوريب بوديم خداوند، خدايمان به ما فرمود: «به اندازه كافی در اينجا مانده‌ايد. 7اكنون برويد و سرزمين كوهستانی اموری‌ها، نواحی درهٔ اردن، دشتها و كوهستانها، صحرای نِگِب و تمامی سرزمين كنعان و لبنان يعنی همهٔ نواحی سواحل مديترانه تا رود فرات را اشغال نماييد. 8تمامی آن را به شما می‌دهم. داخل شده، آن را تصرف كنيد، چون اين سرزمينی است كه من به نياكان شما ابراهيم و اسحاق و يعقوب و تمامی نسلهای آيندهٔ ايشان وعده داده‌ام.»

موسی قضات تعيين می‌كند

(خروج 18‏:13‏-27)

9در آن روزها به مردم گفتم: «شما برای من بار سنگينی هستيد و من نمی‌توانم به تنهايی اين بار را به دوش بكشم، 10چون خداوند شما را مثل ستارگان زياد كرده است. 11خداوند، خدای نياكانتان، شما را هزار برابر افزايش دهد و طبق وعده‌اش شما را بركت دهد. 12ولی من چگونه می‌توانم به تنهايی تمامی دعواها و گرفتاريهايتان را حل و فصل نمايم؟ 13بنابراين از هر قبيله چند مرد دانا و مجرب و فهميده انتخاب كنيد و من آنها را به رهبری شما منصوب خواهم كرد.» 14ايشان با اين امر موافقت كردند 15و من افرادی را كه آنها از هر قبيله انتخاب كرده بودند برايشان گماردم تا مسئوليت گروه‌های هزار، صد، پنجاه و ده نفری را به عهده گرفته، به حل دعواهای آنان بپردازند. 16به آنها دستور دادم كه در همه حال، عدالت را كاملاً رعايت كنند، حتی نسبت به غريبه‌ها. 17به آنها گوشزد كردم: «هنگام داوری از كسی جانبداری نكنيد، بلكه نسبت به بزرگ و كوچک يكسان قضاوت نماييد. از مردم نترسيد، چون شما از طرف خداوند داوری می‌كنيد. هر مسئله‌ای كه حل آن برايتان مشكل است نزد من بياوريد تا من آن را فيصله دهم.» 18در همان وقت دستورات ديگری را هم كه قوم می‌بايست انجام دهند، به ايشان دادم.

بررسی سرزمين كنعان

(اعداد 13‏:1‏-33)

19‏-21آنگاه طبق دستور خداوند، خدايمان كوه حوريب را ترک گفته، از بيابان بزرگ و ترسناک گذشتيم و سرانجام به ميان كوهستانهای اموری‌ها رسيديم. بعد به قادش برنيع رسيديم و من به قوم گفتم: «خداوند، خدايمان اين سرزمين را به ما داده است. برويد و همچنانكه به ما امر فرموده آن را تصرف كنيد. نترسيد و هراس به دلتان راه ندهيد.»

22ولی آنها جواب دادند: «بياييد افرادی به آنجا بفرستيم تا آن سرزمين را بررسی كنند و گزارشی از شهرهای آنجا به ما بدهند تا ما بدانيم از چه راهی می‌توانيم به آنجا رخنه كنيم.»

23اين پيشنهاد را پسنديدم و دوازده نفر، يعنی از هر قبيله يک نفر، انتخاب كردم. 24‏-25آنها از ميان كوهستانها گذشته، به وادی اشكول رسيده، آنجا را بررسی كردند و با نمونه‌هايی از ميوه‌های آن سرزمين مراجعت نموده، گفتند: «سرزمينی كه خداوند، خدايمان به ما داده است سرزمين حاصلخيزی است.» 26ولی قوم از ورود به آنجا خودداری نموده، عليه دستور خداوند قيام كردند. 27آنها در خيمه‌هايشان غرغر و شكايت كرده، گفتند: «لابد خداوند از ما بيزار است كه ما را از مصر به اينجا آورده تا به دست اموری‌ها كشته شويم. 28كار ما به كجا خواهد كشيد؟ برادران ما كه آن سرزمين را بررسی كرده‌اند با خبرهايشان ما را ترسانده‌اند. آنها می‌گويند كه مردم آن سرزمين بلند قد و قوی هيكل هستند و ديوار شهرهايشان سر به فلک می‌كشد. آنها غولهايی از بنی‌عناق نيز در آنجا ديده‌اند.»

29ولی من به ايشان گفتم: «نترسيد و هراس به دلتان راه ندهيد. 30‏-31خداوند، خدای شما هادی شماست و برای شما جنگ خواهد كرد، همانطور كه قبلاً در مصر و در اين بيابان اين كار را برای شما كرد. ديده‌ايد كه در تمام طول راه از شما مراقبت كرده است همانطور كه يک پدر از بچه‌اش مواظبت می‌كند.» 32ولی با اين همه به خداوند اعتماد نكردند، 33هر چند خداوند در طول راه آنها را هدايت می‌نمود و پيشاپيش آنها حركت می‌كرد تا مكانی برای بر پا كردن اردويشان پيدا كند، و شبها با ستونی از آتش و روزها با ستونی از ابر آنها را راهنمايی می‌نمود.

خداوند قوم اسرائيل را تنبيه می‌كند

(اعداد 14‏:20‏-45)

34‏-35آری، خداوند شكوه‌هايشان را شنيد و بسيار غضبناک شد و قسم خورده، گفت: «حتی يک نفر از تمامی اين نسل شرير زنده نخواهد ماند تا سرزمين حاصلخيزی را كه به پدرانشان وعده داده بودم ببيند 36مگر كاليب پسر يَفُنه. من زمينی را كه او بررسی كرده است به او و به نسلش خواهم داد، زيرا از من اطاعت كامل نمود.»

37خداوند به خاطر آنها بر من نيز خشمناک شد و به من فرمود: «تو به سرزمين موعود داخل نخواهی شد. 38به جای تو، دستيارت يوشع (پسر نون) قوم را هدايت خواهد كرد. او را تشويق كن تا برای به عهده گرفتن رهبری آماده شود.»

39سپس خداوند خطاب به همهٔ ما فرمود: «من سرزمين موعود را به همان اطفالی كه می‌گفتيد دشمنان، آنها را به اسارت خواهند برد، به ملكيت خواهم داد. 40اما شما اكنون برگرديد و از راهی كه به سوی دريای سرخ می‌رود به بيابان برويد.»

41آنگاه قوم اسرائيل اعتراف نموده، به من گفتند: «ما گناه كرده‌ايم؛ اما اينک به آن سرزمين می‌رويم و همانطور كه خداوند، خدايمان به ما امر فرموده است برای تصاحب آن خواهيم جنگيد.» پس اسلحه‌هايشان را به كمر بستند و گمان كردند كه غلبه بر تمامی آن ناحيه آسان خواهد بود.

42ولی خداوند به من گفت: «به ايشان بگو كه اين كار را نكنند، زيرا من با ايشان نخواهم رفت و دشمنانشان آنها را مغلوب خواهند كرد.»

43من به ايشان گفتم، ولی گوش ندادند. آنها مغرور شده، فرمان خداوند را اطاعت نكردند و برای جنگيدن به كوهستان برآمدند. 44ولی اموری‌هايی كه در آنجا ساكن بودند برای مقابله با آنها بيرون آمده، مثل زنبور ايشان را دنبال كردند و از سعير تا حرمه آنها را كشتند. 45آنگاه قوم اسرائيل بازگشته، در حضور خداوند گريستند، ولی خداوند گوش نداد. 46سپس آنها مدت مديدی در قادش ماندند.