Numeri 36 – CCL & PCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Numeri 36:1-13

Cholowa cha Ana Aakazi a Zelofehadi

1Atsogoleri a mabanja a fuko la Giliyadi, mwana wa Makiri, mwana wa Manase omwe anali ochokera ku fuko la ana a Yosefe anabwera ndi kuyankhula ndi Mose, atsogoleri ndi akuluakulu a mabanja a Aisraeli. 2Iwo anati, “Pamene Yehova analamula mbuye wanga kuti apereke dziko ngati cholowa kwa Aisraeli mwa maere, anakulamulani inu kupereka cholowa cha mʼbale wathu Zelofehadi kwa ana ake aakazi. 3Tsopano ngati akwatiwa ndi aamuna ochokera ku mafuko ena a mitundu ya Aisraeli, cholowa chawo chidzatengedwa kuchoka pa cholowa cha makolo athu ndipo adzachiwonjezera ku fuko limene akwatiwakolo. Ndipo gawo lina la cholowacho, lopatsidwa kwa ife lidzatengedwa. 4Pamene chaka cha chikondwerero cha zaka makumi asanu, cha Aisraeli chafika, cholowa chawo chidzawonjezeredwa ku fuko limene iwo akwatiwako. Ndipo katundu wawo adzachotsedwa pa cholowa cha fuko la makolo athu.”

5Tsono mwa lamulo la Yehova, Mose anapereka lamulo ili kwa Aisraeli: “Zimene ana a Yosefe akunena ndi zoona. 6Izi ndi zimene Yehova akulamula kwa ana aakazi a Zelofehadi: Atha kukwatiwa ndi aliyense amene angakondweretsedwe naye koma zingakhale bwino atakwatiwa mʼfuko la abambo awo 7kuti cholowa cha Israeli chisapite ku fuko lina, pakuti Mwisraeli aliyense ayenera kusunga cholowa cha fuko la makolo ake. 8Mwana wamkazi aliyense amene adzalandira cholowa cha dziko la fuko lililonse la Israeli ayenera kukwatiwa ndi munthu wa fuko la abambo ake. 9Cholowa chilichonse mu Israeli sichiyenera kupita ku fuko lina, popeza fuko lililonse la Israeli liyenera kusunga cholowa chimene linalandira.”

10Choncho ana aakazi a Zelofehadi anachita monga Yehova analamulira Mose. 11Ana aakazi a Zelofehadi amene ndi Mahila, Tiriza, Hogila, Milika ndi Nowa, anakwatiwa ndi asuweni awo a ku mbali ya abambo awo. 12Anakwatiwa mʼmafuko a zidzukulu za Manase mwana wa Yosefe, ndipo cholowa chawo chinakhalabe mʼfuko la abambo awo.

13Awa ndi malamulo ndi malangizo amene Yehova anapereka kwa Aisraeli kupyolera mwa Mose ku chigwa cha Mowabu mʼmbali mwa Yorodani, ku Yeriko.

Persian Contemporary Bible

اعداد 36:1‏-13

ارث دختران صَلُفحاد

1‏-2سران طوايف جلعاد (جلعاد پسر ماخير، ماخير پسر منسی و منسی پسر يوسف بود) با درخواستی نزد موسی و رهبران اسرائيل آمدند و به موسی يادآوری كرده، گفتند: «خداوند به تو دستور داد كه زمين را به قيد قرعه بين قوم اسرائيل تقسيم كنی و ارث برادرمان صَلُفحاد را به دخترانش بدهی. 3ولی اگر آنها با مردان قبيلهٔ ديگری ازدواج كنند، زمينشان هم با خودشان به آن قبيله انتقال خواهد يافت و بدين‌سان از كل زمين قبيلهٔ ما كاسته خواهد گرديد 4و در سال يوبيل بازگردانده نخواهد شد.»

5آنگاه موسی در حضور مردم اين دستورات را از جانب خداوند به ايشان داد: «شكايت مردان قبيلهٔ يوسف بجاست، 6آنچه خداوند دربارهٔ دختران صلفحاد امر فرموده اين است: بگذاريد با مردان دلخواه خود ازدواج كنند، ولی فقط به شرط آنكه اين مردان از قبيلهٔ خودشان باشند. 7به اين طريق هيچ قسمتی از زمينهای قبيلهٔ يوسف به قبيلهٔ ديگری منتقل نخواهد شد، زيرا ميراث هر قبيله بايستی همانطور كه در اول تقسيم شد برای هميشه همانطور باقی بماند. 8دخترانی كه در تمامی قبايل اسرائيل وارث زمين هستند بايستی با مردان قبيلهٔ خودشان ازدواج كنند تا زمين ايشان از آن قبيله، جدا نشود. 9به اين طريق هيچ ميراثی از قبيله‌ای به قبيلهٔ ديگر منتقل نخواهد شد.»

10دختران صلفحاد همانطور كه خداوند به موسی دستور داده بود عمل كردند. 11‏-12اين دختران، يعنی محله، تِرصه، حُجله، مِلكه و نوعه با پسر عموهای خود ازدواج كردند. بدين ترتيب آنها با مردانی از قبيلهٔ خود يعنی قبيلهٔ منسی (پسر يوسف) ازدواج كردند و ميراث آنان در قبيلهٔ خودشان باقی ماند.

13اين است احكام و اوامری كه خداوند توسط موسی به قوم اسرائيل داد، هنگامی كه آنها در دشت موآب كنار رود اردن و در مقابل اريحا اردو زده بودند.