Kuyendayenda Mʼchipululu
1Kenaka tinabwerera ndi kuyamba ulendo wolowera ku chipululu motsatira njira ya ku Nyanja Yofiira, monga mmene Yehova anatilamulira. Kwa nthawi yayitali tinayendayenda cha ku dziko la mapiri la Seiri.
2Ndipo Yehova anati kwa ine, 3“Mwazungulira mokwanira dziko la mapiri, tsopano tembenukirani kumpoto. 4Apatse anthu malamulo awa: ‘Muli pafupi kudutsa mʼchigawo cha abale anu adzukulu a Esau okhala ku Seiri. Iwowa adzachita nanu mantha koma musamale kwambiri. 5Musayambane nawo popeza sindidzakupatsani gawo lina lililonse la dziko lawo ngakhale poti mungoyika phazi. Ndamupatsa Esau dziko lamapiri la Seiri kuti likhale lakelake. 6Inu muyenera kuwalipira ndi siliva pa chakudya chimene mudye ndi madzi amene mumwe.’ ”
7Yehova Mulungu wanu wakudalitsani mʼntchito zonse za manja anu. Iye wakuyangʼanirani pa ulendo wanu wodutsa mʼchipululu chachikulu. Yehova Mulungu wanu wakhala nanu mʼzaka makumi anayi, ndipo simunasowe kalikonse.
8Choncho tinapitiriza ulendo modutsa abale athu, adzukulu a Esau okhala ku Seiri. Tinapatukira njira ya ku Araba imene imachokera ku Elati ndi Ezioni Geberi ndipo tinayenda njira ya ku chipululu cha Mowabu.
9Ndipo Yehova anati kwa ine, “Musawavutitse Amowabu kapena kuwaputa kuti muchite nawo nkhondo popeza sindidzakupatsani gawo lina lililonse la dziko lawo. Ndinapereka Ari kwa adzukulu a Loti ngati chuma chawo.”
10(Aemi, anthu amphamvu ndi ochuluka komanso ataliatali ngati Aanaki amakhala kumeneko. 11Ngati Aanaki, nawonso ankawayesa kuti anali Arefai, koma Amowabu ankawatcha iwo Aemi. 12Ahori amakhala ku Seiri koma adzukulu a Esau anawapirikitsa. Iwo anawononga Ahori pamaso pawo nawakhalira pamalo pawo monga Aisraeli anachitira mʼdziko limene Yehova anawapatsa ngati chuma chawo).
13Ndipo Yehova anati, “Tsopano nyamukani ndipo muwoloke Chigwa cha Zeredi.” Choncho tinawoloka chigwacho.
14Panapita zaka 38 kuchokera pa nthawi imene tinachoka ku Kadesi Barinea mpaka pamene tinawoloka Chigwa cha Zeredi. Pa nthawi imeneyi nʼkuti mʼbado wonse wa anthu ankhondowo utawonongeka ku msasa monga Yehova anawalumbirira. 15Dzanja la Yehova linatsutsana nawo mpaka wonse anathera ku msasa.
16Tsono atafa munthu wotsiriza mwa anthu ankhondowo, 17Yehova anati kwa ine, 18“Lero mudutsa malire a Mowabu ku Ari podzera ku Ari. 19Mukafika kwa Aamoni, musawavutitse kapena kuwaputa, popeza sindidzakupatsani gawo lililonse la dziko la Aamoni. Ine ndalipereka dzikoli ngati chuma kwa adzukulu a Loti.”
20(Ilinso ankaliyesa dziko la Arefai amene ankakhala kumeneko. Koma Aamoni ankawatcha iwo Azamuzumi. 21Iwo anali anthu amphamvu ndiponso ochuluka, ataliatali ngati Aanaki. Yehova anawawononga ndi kuwachotsa pamaso pa Aamoni, amene anawapirikitsa nawakhalira pa malo pawo. 22Yehova anachitanso chimodzimodzi ndi adzukulu a Esau omwe anakhazikika ku Seiri atawononga Ahori powachotsa pamaso pawo. Iwo anawapirikitsa Ahoriwo ndi kuwakhalira pamalo pawo mpaka lero. 23Ndipo za Aavi omwe ankakhala mʼmidzi yofika mpaka ku Gaza, anagonjetsedwa ndi Akafitori wochokera ku Akafitori nakhala pamalo pawo).
Kugonjetsedwa kwa Sihoni Mfumu ya ku Hesiboni
24“Tsopano nyamukani, muwoloke khwawa la Arinoni. Taona ndapereka mʼmanja mwako Sihoni Mwamori mfumu ya Hesiboni ndi dziko lake lonse. Yambapo kutenga chuma chake ndi kumenyana naye nkhondo. 25Lero lomwe lino ndidzayamba kuyika chiopsezo ndi mantha pa mitundu yonse pansi pa thambo kuti akuope. Iwowo adzamva zambiri yako ndipo adzanjenjemera ndi kuwawidwa mtima chifukwa cha iwe.”
26Ine ndinatuma amithenga kuchokera ku chipululu cha Kedemoti kupita kwa Sihoni mfumu ya Hesiboni kukanena mawu ofuna mtendere ndipo ndinati, 27“Tiloleni tidutse mʼdziko mwanu. Ife tidzangodutsa ndi msewu waukulu, ndipo sitidzapatukira kumanja kapena kumanzere. 28Mutigulitse chakudya kuti tidye ndi madzi kuti timwe pa mtengo wa siliva. Mungotilola kuti tidutse, tikuyenda pansi 29monga mmene anatichitira adzukulu a Esau okhala ku Seiri ndi Amowabu okhala ku Ari mpaka titawoloka Yorodani kufika ku dziko limene Yehova Mulungu wathu akutipatsa.” 30Koma Sihoni mfumu ya Hesiboni sanalole kuti tidutse. Popeza Yehova Mulungu wanu analimbitsa mzimu wake, nawumitsa mtima wake kuti amupereke mʼmanja mwanu monga wachitira lero lino.
31Yehova anati kwa ine, “Taona ndayamba kumupereka Sihoni ndi dziko lake kwa iwe. Tsopano yamba kugonjetsa ndi kulanda dziko lake.”
32Sihoni ndi ankhondo ake atabwera kudzakumana nafe mwankhondo pa Yahazi, 33Yehova Mulungu anamupereka iye kwa ife ndipo tinankantha, pamodzi ndi ana ake aamuna ndi gulu lake lonse lankhondo. 34Pa nthawi imeneyi tinamulanda mizinda yake yonse ndi kuyiwononga kwathunthu, amuna, akazi ndi ana. Palibe amene anapulumuka. 35Koma ziweto ndi zinthu zonse zimene tinalanda mʼmizinda imene tinagonjetsayo, tinazitenga kukhala zathu. 36Kuchokera ku Aroeri mʼmphepete mwa mtsinje wa Arinoni ndi ku mzinda wa ku mtsinjeko mpaka kukafika ku Giliyadi, panalibe ndi mzinda ndi umodzi omwe umene unatikanika kuwugonjetsa. Yehova Mulungu wathu anatipatsa onsewo. 37Molingana ndi lamulo la Yehova Mulungu wathu, simunalowerere dziko lililonse la Aamoni, ngakhale dera lonse la ku mtsinje wa Yaboki kapena dera lozungulira dera la ku mizinda ya ku mapiri.
سالهای آوارگی در بيابان
1-2آنگاه طبق دستور خداوند بازگشتيم و از راهی كه به سوی دريای سرخ میرود به بيابان رفتيم. سالهای زيادی در اطراف ناحيهٔ كوه سعير سرگردان بوديم. سرانجام خداوند فرمود:
3«به اندازهٔ كافی در اين كوهستان سرگردان بودهايد. حال به سمت شمال برويد. 4به قوم بگو كه ايشان از مرز سرزمينی خواهند گذشت كه به برادرانشان ادومیها تعلق دارد. (ادومیها از نسل عيسو هستند و در سعير زندگی میكنند.) آنها از شما خواهند ترسيد، 5ولی شما با ايشان نجنگيد، چون من تمام سرزمين كوهستانی سعير را به عنوان ملک دائمی به ايشان دادهام و حتی يک وجب از زمين ايشان را به شما نخواهم داد. 6در آنجا به ازای آب و غذايی كه مصرف میكنيد، پول بپردازيد. 7خداوند، خدايتان در تمام چهل سالی كه در اين بيابان بزرگ سرگردان بودهايد با شما بوده و قدم به قدم از شما مراقبت نموده است. او در تمام كارهايتان به شما بركت داده و شما هيچوقت محتاج به چيزی نبودهايد.»
8بنابراين ما از كنار سعير كه برادرانمان در آنجا زندگی میكردند گذشتيم و جادهای را كه به سمت جنوب به اِيلَت و عصيون جابر میرود قطع نموده، رو به شمال به طرف بيابان موآب كوچ كرديم.
9آنگاه خداوند به ما چنين هشدار داد: «با موآبیها كه از نسل لوط هستند كاری نداشته باشيد و با ايشان وارد جنگ نشويد. من شهر عار را به ايشان دادهام و هيچ زمينی را از سرزمين ايشان به شما نخواهم داد.»
10(ايمیها كه قبيلهٔ بسيار بزرگی بودند قبلاً در آن ناحيه سكونت داشتند و مثل غولهای عناقی بلند قد بودند. 11ايمیها و عناقیها غالباً رفائی خوانده میشوند، ولی موآبیها ايشان را ايمی میخوانند. 12در روزگار پيشين حوریها در سعير سكونت داشتند، ولی ادومیها يعنی اعقاب عيسو آنها را بيرون رانده، جايشان را گرفتند، همانطور كه اسرائيل جای مردم كنعان را كه خداوند سرزمينشان را به اسرائيل بخشيده بود، گرفتند.)
13خداوند فرمود: «اكنون برخيزيد و از رود زارَد بگذريد.» ما چنين كرديم. 14سی و هشت سال پيش، ما قادش را ترک گفته بوديم. همانطور كه خداوند فرموده بود، در اين مدت تمام جنگجويان ما از بين رفتند. 15خداوند بر ضد آنها بود و سرانجام همهٔ آنها را از بين برد. 16پس از اينكه تمام جنگجويان مردند 17خداوند به من فرمود: 18«امروز بايد از شهر عار كه در مرز موآب است بگذريد. 19وقتی به سرزمين عمونیها كه از نسل لوط هستند نزديک شديد با آنها كاری نداشته باشيد و با ايشان وارد جنگ نشويد، زيرا هيچ زمينی را از سرزمينی كه به ايشان بخشيدهام، به شما نخواهم داد.»
20(آن ناحيه نيز زمانی محل سكونت رفائیها كه عمونیها ايشان را زَمزُمی میخوانند، بود. 21آنها قبيلهٔ بسيار بزرگی بودند و مثل عناقیها قد بلندی داشتند، ولی خداوند ايشان را هنگام ورود عمونیها از بين برد و عمونیها به جای ايشان در آنجا سكونت كردند. 22خداوند به همين نحو به اعقاب عيسو در كوه سعير كمک كرده بود و آنها حوریها را كه قبل از ايشان در آنجا سكونت داشتند از بين برده و تا امروز به جای ايشان ساكن شدهاند. 23وضع مشابه ديگر، زمانی اتفاق افتاد كه مردم كفتور به قبيلهٔ عِویها كه تا حدود غزه در دهكدههای پراكندهای سكونت داشتند حمله نموده، آنها را هلاک كردند و به جای ايشان ساكن شدند.)
24آنگاه خداوند فرمود: «از رود ارنون گذشته، به سرزمين سيحونِ اموری، پادشاه حشبون داخل شويد. من او را و سرزمينش را به شما دادهام. با او بجنگيد و سرزمين او را به تصرف خود درآوريد. 25از امروز ترس شما را بر دل مردم سراسر جهان میگذارم. آنها آوازهٔ شما را میشنوند و به وحشت میافتند.»
شكست سيحون پادشاه
(اعداد 21:21-30)
26سپس از صحرای قديموت سفيرانی با پيشنهاد صلح نزد سيحون، پادشاه حشبون فرستادم. 27پيشنهاد ما اين بود: «اجازه دهيد از سرزمين شما عبور كنيم. از جادهٔ اصلی خارج نخواهيم شد و به طرف مزارع اطراف آن نخواهيم رفت. 28هنگام عبور برای هر لقمه نانی كه بخوريم و هر جرعه آبی كه بنوشيم، پول خواهيم داد. تنها چيزی كه میخواهيم، اجازهٔ عبور از سرزمين شماست. 29ادومیهای ساكن سعير اجازهٔ عبور از سرزمين خود را به ما دادند. موآبیها هم كه پايتختشان در عار است همين كار را كردند. ما از راه اردن به سرزمينی كه خداوند، خدايمان به ما داده است میرويم.»
30ولی سيحون پادشاه موافقت نكرد، زيرا خداوند، خدای شما او را سختدل گردانيد تا او را به دست اسرائيل نابود كند، همچنانكه الان شده است.
31آنگاه خداوند به من فرمود: «اكنون به تدريج سرزمين سيحون پادشاه را به شما میدهم. پس از اينكه آنجا را تصرف كرديد، اين سرزمين از آن شما خواهد بود.»
32آنگاه سيحون پادشاه به ما اعلان جنگ داد و نيروهايش را در ياهص بسيج كرد. 33-34ولی خداوند، خدايمان او را به ما تسليم نمود و ما او را با تمام پسران و افرادش كشتيم و تمامی شهرهايش را به تصرف خود درآورده، همهٔ مردان و زنان و اطفال را از بين برديم. 35به غير از گلههايشان، موجود ديگری را زنده نگذاشتيم. اين گلهها را هم با غنايمی كه از تسخير شهرها به چنگ آورده بوديم با خود برديم. 36ما از عروعير كه در كنارهٔ درهٔ ارنون است تا جلعاد، همهٔ شهرها را به تصرف خود درآورديم. حتی يک شهر هم در برابر ما قادر به مقاومت نبود، زيرا خداوند، خدايمان تمامی آنها را به ما داده بود. 37ولی ما به سرزمين بنیعمون و به رود يبوق و شهرهای كوهستانی يعنی جاهايی كه خداوند، خدايمان قدغن فرموده بود، نزديک نشديم.