Aroma 5 – CCL & CRO

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Aroma 5:1-21

Mtendere ndi Chimwemwe

1Tsopano popeza tayesedwa olungama mwa chikhulupiriro, tili ndi mtendere ndi Mulungu kudzera mwa Ambuye athu Yesu Khristu. 2Iyeyo ndiye amene anatsekulira njira mwachikhulupiriro yolowera mʼchisomo mʼmene takhazikikamo. Ndipo tikukondwerera chiyembekezo cha ulemerero wa Mulungu. 3Koma si pokhapo ayi, koma ife tikukondweranso mʼmasautso athu chifukwa tikudziwa kuti masautso amatiphunzitsa kupirira. 4Ndipo kupirira kumabweretsa makhalidwe, makhalidwe amabweretsa chiyembekezo. 5Ndipo chiyembekezo chimenechi sichitikhumudwitsa chifukwa Mulungu mwa Mzimu Woyera, amene Iye anatipatsa, wadzaza mʼmitima mwathu ndi chikondi chake.

6Pakuti pa nthawi yake, tikanali ochimwa, Khristu anatifera anthu osapembedzafe. 7Sizichitika kawirikawiri kuti munthu wina afere munthu wolungama, ngakhale kuti chifukwa cha munthu wabwino wina atha kulimba mtima kumufera. 8Koma Mulungu anaonetsa chikondi chake kwa ife chifukwa pamene tinali ochimwabe, Khristu anatifera.

9Popeza chifukwa cha magazi ake ife tapezeka olungama pamaso pa Mulungu, Iyeyo adzatipulumutsa koposa kotani ku mkwiyo wa Mulungu. 10Pakuti pamene tinali adani a Mulungu, tinayanjanitsidwa ndi Iye kudzera mu imfa ya Mwana wake. Nanga tidzapulumutsidwa bwanji kudzera mʼmoyo wake, titayanjanitsidwa naye? 11Sikuti izi zili chomwechi chabe, koma timakondweranso mwa Mulungu kudzera mwa Ambuye athu Yesu Khristu. Kudzera mwa Iye, ife tsopano tayanjanitsidwa ndi Mulungu.

Imfa Kudzera mwa Adamu, Moyo Kudzera mwa Yesu

12Choncho monga momwe tchimo linalowa mʼdziko lapansi kudzera mwa munthu mmodzi, ndi imfa kudzera mu tchimo, mʼnjirayi imfa inafika kwa anthu onse pakuti onse anachimwa. 13Pakuti Malamulo asanaperekedwe, tchimo linali mʼdziko lapansi. Koma pamene palibe Malamulo, tchimo silitengedwa kukhala tchimo. 14Komabe, imfa inalamulira kuyambira nthawi ya Adamu mpaka nthawi ya Mose. Inalamulira ngakhalenso pa iwo amene sanachimwe posamvera Malamulo monga anachitira Adamu. Adamuyo amene anali chifaniziro cha wina amene ankabwera.

15Koma sitingafananitse mphatso yaulereyo ndi kuchimwa kwa anthu. Pakuti ngati anthu ambiri anafa chifukwa cha kuchimwa kwa munthu mmodziyo, kuli koposa bwanji nanga chisomo cha Mulungu ndi mphatso zomwe zinabwera ndi chisomo cha munthu mmodzi, Yesu Khristu, ndi kusefukira kwa ambiri! 16Ndiponso, mphatso ya Mulungu sifanana ndi zotsatira za kuchimwa kwa munthu mmodzi. Chiweruzo chinatsatira tchimo la munthu mmodzi ndi kubweretsa kutsutsidwa koma mphatso inatsatira zolakwa zambiri ndi kubweretsa kulungamitsidwa. 17Pakuti ngati, chifukwa cha kulakwa kwa munthu mmodziyo, imfa inalamulira kudzera mwa munthu mmodziyo, kuli koposa bwanji nanga kwa iwo amene adzalandira chisomo chochuluka ndi mphatso yachilungamo, adzalamulira mʼmoyo kudzera mwa munthu mmodzi, Yesu Khristu.

18Choncho monga tchimo limodzi linabweretsa kutsutsika pa anthu onse, chimodzimodzinso ntchito imodzi yolungama inabweretsa chilungamo kwa anthu onse ndi kuwapatsa moyo. 19Pakuti kusamvera kwa munthu mmodzi kunasandutsa anthu ambiri kukhala ochimwa, chimodzimodzinso anthu ambiri adzasanduka olungama kudzera mwa munthu mmodzinso.

20Malamulo a Mulungu anaperekedwa ndi cholinga chakuti anthu onse azindikire kuchuluka kwa machimo awo. Koma pamene machimo anachuluka, chisomo chinachuluka koposa. 21Choncho monga momwe tchimo linkalamulira anthu ndi kubweretsa imfa pa iwo, chomwecho kunali koyenera kuti chisomo chilamulire pobweretsa chilungamo kwa anthu, ndi kuwafikitsa ku moyo wosatha mwa Yesu Khristu Ambuye athu.

Knijga O Kristu

Rimljanima 5:1-21

Vjera donosi radost

1Opravdani smo dakle u Božjim očima vjerom te pomireni s Bogom zbog onoga što je naš Gospodin Isus Krist za nas učinio. 2Zbog vjere u njega možemo pristupiti najvećoj milosti i radujemo se nadi Božje slave.

3Možemo se radovati i kad smo u nevolji jer znamo da je to za naše dobro—jača našu strpljivost. 4Strpljivost donosi prokušanost, a prokušanost nadu. 5Zbog tog se očekivanja nećemo postidjeti. Jer znamo da nas Bog silno ljubi—ulio je tu ljubav u naša srca po Svetom Duhu.

6Kad smo bili potpuno bespomoćni, Krist je došao u pravo vrijeme i umro za nas grešnike. 7Za dobra čovjeka malo bi tko bio voljan umrijeti, iako bi se za izvanredno dobra čovjeka možda i našao tko da za njega dade život. 8No Bog je pokazao svoju veliku ljubav prema nama time što je poslao Krista da umre za nas dok smo još bili grešnici. 9A kako smo mi u Božjim očima opravdani Kristovom krvlju, on će nas sigurno spasiti od Božjega suda. 10Jer kako nas je, dok smo još bili Božji neprijatelji, s njime pomirila smrt njegova Sina, tako će nas život njegova Sina sigurno osloboditi vječne kazne. 11Zato se sada možemo radovati svojemu novom odnosu prema Bogu—zato što nas je naš Gospodin Isus Krist pomirio s Bogom.

Adam je donio smrt, a Krist život

12Kad je Adam zgriješio, grijeh je ušao u sav ljudski rod. A budući da je taj Adamov grijeh donio smrt, smrt je prešla na sve ljude jer su svi zgriješili. 13Doista, ljudi su griješili i prije nego što su dobili Zakon. Ali iako još nije bilo Zakona koji bi kršili, 14svi su oni—od Adama do Mojsija—umrli iako nisu prekršili jasnu Božju zapovijed kao što je to Adam učinio. Kakve li razlike između Adama i Krista koji je tek trebao doći! 15Kako su različiti naši grijesi od Božjega milostivog dara! Jer taj jedan čovjek, Adam, svojim je grijehom mnogima donio smrt. Ali zato se na mnoge obilno izlila Božja milost oproštenja grijeha, darovana po jednome čovjeku—Isusu Kristu. 16S darom Božje milosti nije kao s posljedicama grijeha jednoga čovjeka—jer presuda nad Adamovim grijehom postala je osudom nad svima, a dar Božjega oproštenja nam je—nakon mnogih grijeha koje smo počinili—postao opravdanjem. 17Jer Adamovim je grijehom kroz jednog čovjeka nad nama zakraljila smrt, ali koji prime izobilni milosni dar pravednosti, živjet će u pobjedi nad grijehom i smrću—po jednome Čovjeku, Isusu Kristu. 18Prema tome, kao što je grijehom jednoga došla osuda na sve ljude, tako su pravednošću Jednoga na sve došli opravdanje i život. 19Baš kao što su zbog neposluha jednoga čovjeka mnogi postali grešnicima, tako će i zbog poslušnosti Jednoga mnogi postati pravednicima u Božjim očima. 20Božji je Zakon dan ljudima da se umnoži grijeh. Ali kako su ljudi sve više i više griješili, Božja divna milost sve se obilnije izlijevala. 21Baš kao što je grijeh nekada vladao nad svim ljudima i vodio ih u smrt, tako sada nad njima kraljuje Božja milost i opravdava ih pred Bogom da bi mogli imati vječni život po našemu Gospodinu Isusu Kristu.