Machitidwe a Atumwi 1 – CCL & CRO

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Machitidwe a Atumwi 1:1-26

Lonjezo la Mzimu Woyera

1Mʼbuku langa loyamba, ndinakulembera iwe Teofilo zonse zimene Yesu anayamba kuchita ndi kuphunzitsa, 2mpaka tsiku limene anatengedwa kupita kumwamba, mwamphamvu ya Mzimu Woyera, atawalangiza atumwi amene anawasankha. 3Zitatha zowawa zake Yesu anadzionetsa kwa ophunzira ake, ndi kuonetsanso maumboni ambiri kuti anali wamoyo. Iye anadzionetsera kwa iwo ndi kuwaphunzitsa za ufumu wa Mulungu pa masiku makumi anayi. 4Nthawi ina atasonkhana nawo pamodzi, Yesu analamulira ophunzira ake kuti, “Musachoke mu Yerusalemu, koma mudikire mphatso imene Atate anga analonjeza yomwe ndinakuwuzani. 5Pakuti Yohane anakubatizani ndi madzi, koma posachedwapa inu mudzabatizidwa ndi Mzimu Woyera.”

Yesu Akwera Kumwamba

6Atumwi atasonkhana pamodzi, iwo anamufunsa Iye kuti, “Ambuye, kodi nthawi ino mubwezeretsa ufumu kwa Israeli?”

7Yesu anawawuza kuti, “Sikofunika kuti mudziwe za nthawi kapena masiku amene Atate ayika mwa ulamuliro wawo. 8Koma mudzalandira mphamvu Mzimu Woyera akadzafika pa inu; ndipo mudzakhala mboni zanga mu Yerusalemu, ku Yudeya konse ndi ku Samariya, mpaka ku malekezero a dziko lapansi.”

9Atatha kuyankhula zimenezi, Yesu anatengedwa kupita kumwamba ophunzira ake akuona, ndipo anabisika mʼmitambo.

10Yesu akukwera kumwamba, ophunzira ake anayangʼanitsitsa ndi chidwi mʼmitambo. Mwadzidzidzi anaona anthu awiri ovala zoyera atayimirira pambali pawo. 11Iwo anati, “Inu, anthu a ku Galileya, chifukwa chiyani mukuyima ndi kumayangʼana mʼmitambo? Yesu amene wachotsedwa pakati panu ndi kupita kumwamba, adzabweranso mʼnjira yomweyi mwamuona akupita kumwamba.”

Matiyasi Alowa Mʼmalo mwa Yudasi Isikarioti

12Pamenepo atumwi anabwerera ku Yerusalemu kuchokera ku phiri la Olivi, mtunda wosakwana kilomita kuchokera mu mzindamo. 13Atafika mu mzindamo, analowa mʼchipinda chammwamba kumene amakhala. Amene analipo anali awa: Petro, Yohane, Yakobo ndi Andreya; Filipo ndi Tomasi, Bartumeyu ndi Mateyu; Yakobo mwana wa Alifeyo ndi Simoni Zelote ndi Yuda mwana wa Yakobo. 14Onsewa ndi mtima umodzi anapitiriza kupemphera pamodzi ndi amayi, ndi Mariya amayi ake a Yesu, ndiponso abale ake a Yesu.

15Pa nthawi imeneyo Petro anayimirira pakati pa okhulupirira (gulu la anthu pafupifupi 120). 16Iye anati, “Abale anga, Malemba anayenera kukwaniritsidwa omwe Mzimu Woyera anayankhula kalekale kudzera mwa Davide za Yudasi, amene anatsogolera amene anamugwira Yesu. 17Iye anali mmodzi wa gulu lathu ndipo anatumikira pamodzi ndi ife.”

18(Yudasi anagula munda ndi ndalama zimene anazipeza pochita zoyipa zija; kumeneko, iye anagwa chamutu, naphulika pakati ndipo matumbo ake wonse anakhuthuka. 19Aliyense mu Yerusalemu anamva zimenezi, kotero anatcha mundawo mʼchiyankhulo chawo kuti Akeledama, kutanthauza, Munda wa Magazi).

20Petro anati, “Pakuti kwalembedwa mʼbuku la Masalimo kuti,

“Nyumba yake isanduke bwinja,

ndipo pasakhale wogonamo.

Ndiponso,

“Wina atenge ntchito yake yautsogoleri.

21Chifukwa chake ndi kofunika kusankha mmodzi wa anthu amene akhala nafe nthawi yonse imene Ambuye Yesu ankayenda nafe, 22kuyambira pa nthawi ya ubatizo wa Yohane mpaka nthawi imene Yesu anatengedwa pakati pathu. Pakuti mmodzi wa anthu awa ayenera kukhala mboni pamodzi ndi ife zakuuka kwake.”

23Pamenepo anasankha anthu awiri, Yosefe wotchedwa Barsaba (wodziwikanso kuti Yusto) ndi Matiyasi. 24Kenaka iwo anapemphera nati, “Ambuye mukudziwa mtima wa aliyense. Tionetseni amene mwamusankha mwa awiri awa 25kuti atenge ntchito iyi ya utumwi, imene Yudasi anasiya napita kumalo womuyenera.” 26Tsono anachita maere, ndipo maerewo anagwera Matiyasi. Tsono iye anawonjezedwa pa gulu la atumwi khumi ndi mmodziwo.

Knijga O Kristu

Djela Apostolska 1:1-26

Obećanje Svetoga Duha

1Dragi Teofile, u prvoj knjizi koju sam ti napisao iznio sam sve što je Isus počeo da djeluje i poučava 2do dana kad je uznesen na nebo, pošto je odabranim apostolima dao upute Svetoga Duha. 3Još četrdeset dana nakon raspeća ukazivao se apostolima i na mnoge im načine dokazao da je živ. Govorio im je o Božjemu kraljevstvu.

4Dok je tako s njima blagovao, reče im: “Ne idite iz Jeruzalema, nego ostanite ondje dok vam Otac ne pošalje što je obećao. Sjetite se, već sam vam o tomu govorio. 5Ivan je krstio vodom, ali vi ćete uskoro biti kršteni Svetim Duhom.”

Isusovo uzašašće

6Apostoli koji su bili s njim upitaju ga: “Gospodine, hoćeš li sada obnoviti izraelsko kraljevstvo?”

7“Ta vremena i prigode određuje Otac svojom vlasti”, odgovori im on, “i nije na vama da ih znate. 8Ali kad na vas siđe Sveti Duh, primit ćete snagu da o meni svjedočite ljudima posvuda—u Jeruzalemu, po svoj Judeji i Samariji i do kraja zemlje.”

9Tek što je to rekao, uznesen je na nebo pred njihovim očima i nestao u oblaku. 10Dok su očiju uprtih u nebo gledali kako odlazi, odjednom se među njima pojave dvojica ljudi u bijeloj odjeći. 11“Galilejci, što tu stojite i gledate u nebo?” rekli su. “Isus je od vas uznesen na nebo, ali jednoga dana će se vratiti jednako tako kao što ste ga vidjeli da odlazi!”

Umjesto Jude izabran Matija

12Bilo je to na Maslinskoj gori. Vrate se zatim do Jeruzalema udaljenoga otprilike kilometar.1:12 U grčkome: jedan subotni hod. 13Čim uđu u grad, odu u kuću u kojoj su boravili, u sobu na katu. Bili su ondje Petar, Ivan, Jakov, Andrija, Filip, Toma, Bartolomej, Matej, Jakov (Alfejev sin), Šimun (zelot) i Juda (Jakovljev sin).

14Svi su se ustrajno i jednodušno sastajali na molitvu s Isusovom majkom Marijom, još nekoliko drugih žena i s Isusovom braćom.

15Kad ih je jednom tako bilo okupljeno sto dvadeset, Petar ustane i reče:

16“Braćo, moralo se ispuniti ono što piše u Svetome pismu za Judu, koji je doveo hramsku policiju da uhiti Isusa. To je odavno, kroz Davida, pretkazao Sveti Duh.

17Juda je bio jedan od nas, dionik naše službe.

18Novcem koji je dobio za svoje zlodjelo Juda je kupio polje. Ondje je pao i rasprsnuo se tako da mu se prosula sva utroba. 19Vijest o njegovoj smrti brzo se pronijela među stanovnicima Jeruzalema pa su to polje prozvali Akeldama, što na aramejskome znači ‘Krvavo polje’.

20To je pretkazano u Knjizi psalama. Ondje piše:

‘Neka njegov dom opusti,

neka nitko u njemu ne stanuje!’

i

‘Neka njegovu službu dobije drugi!’1:20 Psalam 69:26; Psalam 109:8.

21Moramo zato odabrati nekoga da zamijeni Judu—nekoga tko je bio s nama cijelo vrijeme dok smo bili s Gospodinom Isusom 22otkad ga je Ivan krstio pa do uznesenja u nebo. Taj će s nama biti svjedokom Isusova uskrsnuća.”

23Predlože dvojicu: Josipa Barsabu (kojega su zvali i Just) i Matiju. 24Svi se pomole: “Gospodine, ti poznaješ svako srce. Pokaži nam kojega si od ove dvojice izabrao 25da kao apostol zamijeni izdajnika Judu koji nas je napustio i otišao onamo kamo pripada.” 26Zatim bace kocke i kocka padne na Matiju. Tako je on postao dvanaestim apostolom.