1 Akorinto 1 – CCL & CRO

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Akorinto 1:1-31

1Paulo, woyitanidwa mwachifuniro cha Mulungu kuti akhale mtumwi wa Khristu Yesu ndi mʼbale wathu Sositene.

2Kupita ku mpingo wa Mulungu ku Korinto, kwa oyeretsedwa mwa Khristu Yesu ndi oyitanidwa kukhala opatulika ndiponso kwa onse amene amapemphera mʼdzina la Ambuye athu Yesu Khristu mʼdziko lonse lapansi, amene ndi Ambuye wawo ndi wathunso.

3Landirani chisomo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate athu ndi Ambuye athu Yesu Khristu.

Kuthokoza

4Nthawi zonse ndimayamika Mulungu chifukwa cha inu chifukwa cha chisomo chake chopatsidwa kwa inu mwa Khristu Yesu. 5Pakuti mwa Iye mwalemekezedwa mʼnjira iliyonse, mʼkuyankhula kwanu konse ndi mʼkudziwa kwanu konse, 6chifukwa umboni wathu pa za Khristu unatsimikizidwa mwa inu. 7Choncho inu simusowa mphatso yauzimu iliyonse pamene mukudikira mofunitsitsa kuti Ambuye athu Yesu Khristu avumbulutsidwe. 8Adzakulimbikitsani mpaka kumapeto kuti mudzakhale wopanda mlandu pa tsiku lobwera Ambuye athu Yesu Khristu. 9Mulungu amene wakuyitanani inu mu chiyanjano ndi Mwana wake Yesu Khristu Ambuye athu ngokhulupirika.

Kugawikana mu Mpingo

10Ndidandaulira inu, abale, mʼdzina la Ambuye athu Yesu Khristu kuti nonsenu muvomerezane wina ndi mnzake kuti pasakhale kugawikana pakati panu ndi kuti mukhale amodzi kwenikweni mu nzeru ndi mʼmaganizo. 11Abale anga, ena a ku nyumba ya Kloe andidziwitsa kuti pali mkangano pakati panu. 12Chimene ndikutanthauza ndi ichi: wina amati, “Ndimatsatira Paulo,” wina, “Ndimatsatira Apolo,” wina, “Ndimatsatira Kefa,” winanso, “Ndimatsatira Khristu.”

13Kodi Khristu wagawikana? Kodi Paulo anapachikidwa pa mtanda chifukwa cha inu? Kodi munabatizidwa mʼdzina la Paulo? 14Ine ndikuyamika kuti sindinabatizepo mmodzi mwa inu kupatula Krispo ndi Gayo, 15mwakuti palibe amene anganene kuti anabatizidwa mʼdzina langa. 16(Inde, ine ndinabatizanso a mʼbanja la Stefano, koma sindikumbukira ngati ndinabatizanso wina aliyense). 17Pakuti Khristu sananditume ine kudzabatiza, koma kudzalalikira Uthenga Wabwino, osati ndi mawu anzeru za umunthu, kuopa kuti mtanda wa Khristu ungakhale wopanda mphamvu.

Khristu ndiye Nzeru ndi Mphamvu za Mulungu

18Pakuti uthenga wa mtanda ndi chopusa kwa iwo amene akuwonongeka, koma kwa ife amene tikupulumutsidwa uthengawu ndi mphamvu ya Mulungu. 19Pakuti kwalembedwa kuti,

“Ine ndidzawononga nzeru za anthu anzeru;

luntha la anthu aluntha Ine ndidzalinyoza.”

20Munthu wanzeru ali kuti? Munthu wozama ndi maphunziro ali kuti? Munthu wodziwa zakuya zamakono ali kuti? Kodi Mulungu sanazipusitse nzeru za dziko lapansi? 21Tsono poti mwa nzeru za Mulungu dziko lapansi mu nzeru zake silinamudziwe Iye, Mulungu amakondweretsedwa kuti kudzera mu chopusa cha zomwe zinalalikidwa apulumutse iwo amene akhulupirira. 22Ayuda amafuna zizindikiro zodabwitsa ndipo Agriki amafunafuna nzeru, 23koma ife timalalikira Khristu wopachikidwa. Chitsa chokhumudwitsa kwa Ayuda ndi chopusa kwa a mitundu ina. 24Koma kwa iwo amene Mulungu anawayitana, Ayuda ndi Agriki omwe, Khristu ndi mphamvu ya Mulungu ndi nzeru za Mulungu. 25Pakuti za Mulungu zooneka ngati zopusa, ndi za nzeru kuposa nzeru za munthu, ndipo za Mulungu zooneka ngati zofowoka, zili ndi mphamvu kuposa mphamvu za munthu.

26Abale taganizirani mmene munalili musanayitanidwe. Si ambiri a inu munali a nzeru, si ambiri a inu munali a mphamvu zamakopedwe. Si ambiri a inu munali obadwa pa ulemerero. 27Koma Mulungu anasankha zinthu zopusa za dziko lapansi kuti achititse manyazi anzeru. Mulungu anasankha zinthu zofowoka za dziko lapansi kuti achititse manyazi amphamvu. 28Anasankha zinthu zapansipansi ndi zopeputsidwa za dziko la pansi lino, zinthu zimene kulibe, kuti asukulutse zimene zilipo, 29kuti munthu asanyade pamaso pa Mulungu. 30Nʼchifukwa cha Iye kuti inu muli mwa Khristu Yesu, amene wakhala nzeru ya kwa Mulungu, kwa ife, kunena kuti kulungama kwathu, chiyero ndi chipulumutso. 31Choncho poti zinalembedwa kuti, “Ngati munthu akufuna kunyadira, anyadire mwa Ambuye.”

Knijga O Kristu

1 Korinćanima 1:1-31

Pavlovi pozdravi

1Od Pavla, pozvanoga po Božjoj volji za apostola Isusa Krista, i od brata Sostena,

2Božjoj crkvi u Korintu, vama koje je Bog pozvao da budete njegov sveti narod. Posvetio vas je u Kristu Isusu, kao i sve ostale koji bilo gdje prizivlju ime njihova i našega Gospodina Isusa Krista.

3Neka vam je milost i mir od našega Boga Oca i Gospodina Isusa Krista.

Pavao zahvaljuje Bogu

4Uvijek zahvaljujem Bogu na milosti kojom vas je obdario sada kad pripadate Kristu Isusu. 5U njemu ste obogaćeni u svemu—u svakovrsnoj riječi i spoznaji. 6Svjedočanstvo o Kristu utvrdilo se među vama 7pa sada ne oskudijevate ni u jednome duhovnom daru iščekujući povratak našega Gospodina Isusa Krista. 8On će vas učiniti postojanima sve do konca i sačuvat će vas neporočnima sve do svojega povratka, 9jer Bog vjerno ispunjava obećanja, a on vas je sam pozvao da imate zajedništvo s našim Gospodinom Isusom Kristom.

Podjele u Crkvi

10Draga braćo i sestre, zaklinjem vas imenom našega Gospodina Isusa Krista da se prestanete međusobno prepirati. Neka među vama vlada sloga i neka ne bude razdora u Crkvi. Molim vas da budete jedinstveni u mislima iu osjećajima. 11Klojini su mi ukućani rekli da se međusobno prepirete. 12Neki od vas, naime, kažu: “Ja sam Pavlov sljedbenik”, a drugi: “Ja sam Apolonov”, ili “Ja sam Petrov”1:12 U grčkome: Kefin., ili “Ja slijedim samo Krista.” 13Zar je Krist razdijeljen?

Jesam li ja, Pavao, raspet za vas? Je li tko od vas kršten u Pavlovo ime? 14Hvala Bogu što ja nisam krstio nikoga od vas osim Krispa i Gaja 15da sada nitko ne može reći kako je kršten u moje ime. 16A da, krstio sam i Stefanine ukućane. Ne sjećam se da sam osim njih ikoga više krstio. 17Jer Krist me nije poslao krstiti, nego propovijedati Radosnu vijest, i to ne mudrim riječima da Kristov križ ne izgubi snagu.

Božja mudrost

18Govor o križu zvuči kao ludost onima koji su na putu propasti, ali mi koji smo spašeni prepoznajemo u toj poruci Božju silu. 19U Svetome pismu stoji da je Bog rekao:

“Učinit ću da propadne mudrost mudraca

i da se pomrači umnost umnika.”1:19 Izaija 29:14.

20Ali što je s učenim glavama, s ljudima vičnim raspravama, znanstvenicima? Bog je učinio da se njihova mudrost čini beskorisnom ludošću. 21Bog je u svojoj mudrosti znao da ga svijet nikada neće pronaći ljudskom mudrošću, pa je odlučio one koji vjeruju spasiti ludošću propovijedanja. 22U taj Božji način spasenja Židovi odbijaju povjerovati jer za dokaz traže znak s neba, a Grci zato što vjeruju samo u ono što ne proturječi njihovoj vlastitoj mudrosti. 23Zato naše propovijedanje raspetoga Krista Židove sablažnjava, a pogani ga smatraju ludošću. 24Ali onima koje je Bog pozvao na spasenje, i Židovima i poganima, Krist je Božja sila i Božja mudrost. 25Taj “budalast” Božji plan mnogo je mudriji od najmudrijih ljudskih planova, a Božja je “slabost” mnogo jača od najjače ljudske snage.

26Možete vidjeti, draga braćo, kako među vama koji ste izabrani nema mnogo onih koji ste po tjelesnom podrijetlu mudri, moćni ili plemenita roda. 27Bog je, naprotiv, izabrao one koje svijet smatra budalastima da posrami njegove mudrace, i slabe u očima svijeta da posrami njegove moćnike. 28Ono što je neplemenito i prezreno u očima svijeta, pa čak i ono čega nema, Bog je izabrao da obezvrijedi ono što svijet smatra vrijednim, 29zato da se nijedan smrtnik ne može hvaliti pred Bogom.

30Sam vam je Bog omogućio da budete u Kristu Isusu. Za našu je dobrobit Bog učinio Krista mudrošću. On nas opravdava pred Bogom. Čini nas svetima. Otkupio nas je. 31Kao što piše u Svetome pismu:

“Ako se tko hvali, neka se hvali jedino time

što je Gospodin učinio.”1:31 Vidjeti: Jeremija 9:24.