Aroma 10 – CCL & CRO

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Aroma 10:1-21

1Abale, chokhumba cha mtima wanga ndi pemphero langa kwa Mulungu ndi chakuti Aisraeli apulumutsidwe. 2Popeza ndiwachitira umboni kuti ndi achangu pa zinthu za Mulungu koma osati mwachidziwitso. 3Pakuti sanadziwe chilungamo chochokera kwa Mulungu ndipo anafuna kukhazikitsa chawochawo. Iwo sanagonjere chilungamo cha Mulungu. 4Khristu ndiye mathero amalamulo kuti aliyense amene akhulupirira akhale olungama pamaso pa Mulungu.

5Mose akulemba motere zachilungamo cha malamulo, “Munthu amene achita zinthu izi adzakhala ndi moyo pozichita.” 6Koma chilungamo cha chikhulupiriro chikuti, “Usanene mu mtima mwako kuti, ‘Kodi ndani amene akwere kumwamba?’ ” (ndiko, kukatsitsa Khristu) 7“kapena ‘Ndani adzatsikira ku dziko la anthu akufa?’ ” (ndiko, kukamutenga Khristu kwa akufa). 8Nanga akuti chiyani? “Mawu ali pafupi ndi inu. Ali mʼkamwa mwanu ndi mu mtima mwanu.” Ndiwo mawu achikhulupiriro amene ife tikuwalalikira, 9kuti ngati udzavomereza ndi pakamwa pako kuti, “Yesu ndiye Ambuye,” ndi kukhulupirira mu mtima mwako kuti Mulungu anamuukitsa kwa akufa, udzapulumuka. 10Pakuti ndi mtima wanu mukhulupirira ndi kulungamitsidwa, ndipo ndi pakamwa panu muvomereza ndi kupulumutsidwa. 11Pakuti Malemba akuti, “Aliyense amene akhulupirira Iye, sadzachititsidwa manyazi.” 12Pakuti palibe kusiyana pakati pa Myuda ndi a mitundu ina, pakuti Ambuye mmodzi yemweyo ndi Ambuye wa onse ndipo amadalitsa mochuluka onse amene ayitana pa Iye 13pakuti, “Aliyense amene adzayitana pa dzina la Ambuye adzapulumuka.”

14Kodi adzayitana bwanji amene sanamukhulupirire? Ndipo adzakhulupirira bwanji asanamve za Iye? Ndipo adzamva bwanji popanda wina kulalikira kwa iwo? 15Ndipo iwo adzalalikira bwanji osatumidwa? Kwalembedwa kuti, “Akongoladi mapazi a iwo amene amabweretsa Uthenga Wabwino!”

16Koma si onse amene anavomereza Uthenga Wabwino. Pakuti Yesaya akuti, “Ambuye, ndani amene wakhulupirira uthenga wathu?” 17Motero, chikhulupiriro chimabwera pamene timva uthenga ndipo uthenga umamveka kuchokera ku mawu a Khristu. 18Koma ndikufunsa kuti kodi iwo anamva? Inde, iwo anamva kuti,

“Liwu lawo linamveka ponseponse pa dziko lapansi.

Mawu awo anafika ku malekezero a dziko lonse.”

19Ine ndifunsanso kuti, kodi Israeli sanazindikire? Poyamba Mose akuti,

“Ine ndidzawachititsa kuti achite nsanje ndi mtundu wina wopandapake.

Ine ndidzawakwiyitsa ndi mtundu wina wachabechabe.”

20Ndipo Yesaya molimba mtima akuti,

“Anandipeza anthu amene sanali kundifunafuna.

Ndinadzionetsera kwa amene sanafunse za Ine.”

21Koma zokhudzana ndi Aisraeli akuti,

“Tsiku lonse ndinatambasulira manja anga

kwa anthu osandimvera ndi okanika.”

Knijga O Kristu

Rimljanima 10:1-21

1Draga braćo, želja je mojega srca i moja molitva Bogu da se svi Židovi spase. 2Svjedok sam njihova revnovanja za Boga, ali ono se ne temelji na pravom razumijevanju 3jer ne shvaćaju na koji način Bog opravdava ljude. Umjesto toga drže se vlastitih običaja i nastoje se pred Bogom opravdati vršeći Zakon—te se tako odbijaju podložiti Božjoj volji. 4Jer Krist je u potpunosti ispunio svrhu Zakona. Tko vjeruje u njega, opravdan je pred Bogom.

Spasenje je za svakoga

5O pravednosti koja dolazi po Zakonu Mojsije piše: “Tko je vrši, u njoj će naći život.”10:5 Levitski zakonik 18:5.

6A o pravednosti koja dolazi po vjeri kaže: “Nemoj se u srcu upitati: ‘Tko će uzići na nebo’” (da dovede Krista), 7“niti: ‘Tko će sići u bezdan’” (da dovede Krista od mrtvih)?10:6-8 Ponovljeni zakon 30:12-14. 8Što to zapravo znači?

“Riječ je sasvim blizu tebe,

u tvojim ustima i u tvojem srcu.”

To je riječ vjere koju propovijedamo.

9Jer ako ustima priznaješ da je Isus Krist Gospodin i ako u srcu vjeruješ da ga je Bog uskrisio od mrtvih, bit ćeš spašen. 10Naime, vjera u srcu nas opravdava, a priznanje usnama spašava. 11Jer u Svetome pismu piše: “Tko u njega vjeruje, neće se postidjeti.” 12To vrijedi za Židove, kao i za ostale ljude: svi imaju istoga Gospodina, koji izobilno daje svoja bogatstva svima koji ga zazivaju. 13Jer “Tko god zazove ime Gospodnje, bit će spašen.”10:13 Joel 3:5.

14Ali kako će ga zazvati da ih spasi ako u njega ne vjeruju? A kako će u njega vjerovati ako nikada nisu za njega čuli? A kako će čuti za njega ako im nitko o njemu ne propovijeda? 15A kako će im tko propovijedati ako nije poslan da propovijeda? O tomu Sveto pismo kaže:

“Kako su divne noge onih

koji donose Radosnu vijest!”10:15 Izaija 52:7.

16Ali svatko tko čuje Radosnu vijest neće ju i prihvatiti. Izaija je o tome rekao: “Gospodine, tko je povjerovao našoj poruci?”10:16 Izaija 53:1. 17Vjera dakle dolazi upravo slušanjem Radosne vijesti o Kristu.

18Ali što je sa Židovima? Jesu li oni zapravo čuli tu poruku? Jesu:

“Poruka o Božjemu stvaranju

raširila se po svoj zemlji,

a njezine riječi sežu do kraja svijeta.”10:18 Psalam 19:5.

19Ali, ja pitam: Jesu li Izraelci zaista razumjeli? Jesu, jer je još u Mojsijevo vrijeme Bog rekao:

“Učinit ću vas ljubomornima

blagoslivljajući druge narode.

Razgnjevit ću vas blagoslivljajući

nerazumne pogane.”

20Poslije je Izaija u Božje ime hrabro rekao:

“Našli su me oni

koji me nisu tražili.

Objavio sam se onima

koji me to nisu molili.”10:20 Izaija 65:1.

21A za Izrael je Bog rekao:

“Svagda sam pružao ruke

nepokornom i buntovnom narodu.”10:21 Izaija 65:2.