Amosi 5 – CCL & NSP

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Amosi 5:1-27

Mawu Odandawulira Aisraeli

1Israeli, imva mawu awa, nyimbo ya maliro imene ndikuyimba za iweyo:

2“Namwali Israeli wagwa,

moti sadzadzukanso,

wasiyidwa mʼdziko lake lomwe,

popanda woti ndi kumudzutsa.”

3Ambuye Yehova akuti,

“Mzinda umene udzapite ku nkhondo ndi anthu 1,000 amphamvu

udzatsala ndi anthu 100 okha;

mzinda umene udzapite ku nkhondo ndi anthu 100 amphamvu

udzatsala ndi anthu khumi okha basi.”

4Zimene Yehova akunena kwa nyumba ya Israeli ndi izi:

“Mundifunefune kuti mukhale ndi moyo;

5musafunefune Beteli,

musapite ku Giligala,

musapite ku Beeriseba.

Pakuti Giligala adzatengedwa ndithu kupita ku ukapolo,

ndipo Beteli adzawonongekeratu.”

6Funani Yehova kuti mukhale ndi moyo,

mukapanda kutero Iye adzatentha nyumba ya Yosefe ngati moto;

motowo udzawononga,

ndipo sipadzakhala wina wozimitsa motowo ku Beteli.

7Inu amene mumasandutsa chiweruzo cholungama kukhala chowawa

ndi kunyoza chilungamo.

8(Iye amene analenga nyenyezi za Nsangwe ndi Akamwiniatsatana,

amene amasandutsa mdima kuti ukhale mmawa

ndi kudetsa usana kuti ukhale usiku,

amene amayitana madzi a mʼnyanja

ndi kuwathira pa dziko lapansi,

Yehova ndiye dzina lake.

9Iyeyo amabweretsa chiwonongeko modzidzimutsa pa anthu amphamvu

ndi kuwononga mizinda yotetezedwa),

10inu mumadana ndi amene amadzudzula mʼbwalo la milandu

ndi kunyoza amene amanena zoona.

11Mumapondereza munthu wosauka

ndi kumukakamiza kuti akupatseni tirigu.

Nʼchifukwa chake, ngakhale mwamanga nyumba zamiyala yosema,

inuyo simudzakhalamo.

Ngakhale mwalima minda yabwino ya mphesa,

inu simudzamwa vinyo wake.

12Pakuti Ine ndikudziwa kuchuluka kwa zolakwa zanu

ndi kukula kwa machimo anu.

Inu mumapondereza anthu olungama ndi kulandira ziphuphu

ndipo anthu osauka simuwaweruza mwachilungamo mʼmabwalo anu amilandu.

13Nʼchifukwa chake pa nthawi yotere munthu wanzeru sayankhulapo kanthu,

popeza ndi nthawi yoyipa.

14Muyike mtima wanu pa zabwino osati pa zoyipa,

kuti mukhale ndi moyo.

Mukatero Yehova Mulungu Wamphamvuzonse adzakhala nanu,

monga mmene mumanenera kuti ali nanu.

15Mudane ndi zoyipa, mukonde zabwino;

mukhazikitse chiweruzo cholungama mʼmabwalo anu amilandu.

Mwina mwake Yehova Mulungu Wamphamvuzonse adzachitira chifundo

anthu otsala a mʼbanja la Yosefe.

16Choncho izi ndi zimene Ambuye, Yehova Mulungu Wamphamvuzonse, akunena:

“Mʼmisewu monse mudzakhala kulira mofuwula,

ndi kulira chifukwa cha kuwawa kwa masautso kudzakhala paliponse.

Adzayitana alimi kuti adzalire,

ndipo anthu odziwa maliridwe anthetemya adzalira mofuwula.

17Mʼminda yonse ya mpesa mudzakhala kulira kokhakokha,

pakuti Ine ndidzadutsa pakati panu,”

akutero Yehova.

Tsiku la Yehova

18Tsoka kwa inu amene mumalakalaka

tsiku la Yehova!

Chifukwa chiyani mumalakalaka tsiku la Yehova?

Tsikulo kudzakhala mdima osati kuwala.

19Lidzakhala ngati tsiku limene munthu pothawa mkango

amakumana ndi chimbalangondo,

ngati pamene munthu walowa mʼnyumba,

natsamira dzanja lake pa khoma

ndipo njoka nʼkuluma.

20Kodi tsiku la Yehova silidzakhala mdima osati kuwala,

mdima wandiweyani, popanda powala pena paliponse?

21“Ndimadana nawo masiku anu achikondwerero ndipo ndimawanyoza;

sindikondwera nayo misonkhano yanu.

22Ngakhale mupereke nsembe zopsereza ndi nsembe zachakudya,

Ine sindidzazilandira.

Ngakhale mupereke nsembe zabwino zachiyanjano,

Ine sindidzaziyangʼana nʼkomwe.

23Musandisokose nazo nyimbo zanu!

Sindidzamvetsera kulira kwa azeze anu.

24Koma chiweruzo cholungama chiyende ngati madzi,

chilungamo ngati mtsinje wosaphwa!

25“Kodi pa zaka makumi anayi zimene munakhala mʼchipululu muja

munkandibweretsera nsembe ndi zopereka, inu nyumba ya Israeli?

26Inu mwanyamula kachisi wa mfumu yanu,

ndi nyenyezi ija Kaiwani,

mulungu wanu,

mafano amene munadzipangira.

27Nʼchifukwa chake Ine ndidzakupititsani ku ukapolo, kutali kupitirira ku Damasiko,”

akutero Yehova, amene dzina lake ndi Mulungu Wamphamvuzonse.

New Serbian Translation

Књига пророка Амоса 5:1-27

Јадиковка и позив на покајање

1Чујте ову реч, нарицаљку коју о вама износим, о, доме Израиљев!

2„Пала је девица израиљска

и више устати неће.

Напуштена је на својој земљи

и никога нема да је подигне.“

3Јер овако каже Господ Бог:

„У граду из ког је отишла хиљада

остаће њих стотину,

из ког је отишло њих стотину

остаће десеторо дому израиљском.“

4Јер овако каже Господ дому израиљском:

„Тражите ме и живећете!

5Не тражите Ветиљ!

Не идите у Галгал!

Не прелазите у Вир-Савеју!

Јер, Галгал ће сигурно у изгнанство,

а и Ветиљ ће аветиња постати.“

6Тражите Господа и живећете,

да се не би обрушио као огањ на дом Јосифов

и спалио га,

а нико га не гаси у Ветиљу.

7Ви у пелен правду изокрећете

и праведност на тле обарате.

8А он је створио Влашиће и Орион,

претвара мрак у јутро

и окреће дан у ноћ.

Он дозива морске воде

и излива их по земљином лицу.

Господ је име његово.

9Он сукне пустош на моћника

и пустош ће на утврђење доћи.

10А они мрзе онога који на вратима прекорева,

гаде се онога који честито говори.

11Зато што газите убогога

и узимате му данак у житу,

саградили сте куће од клесаног камена

али нећете пребивати у њима.

Нећете пити вино

ваших родних винограда које сте засадили.

12Јер ја знам мноштво ваших преступа

и ваше многобројне грехе.

Тлачите праведника, мито узимате,

на вратима убогоме правду изврћете.

13Зато мудар ћути у овом времену

јер је зло време.

14Добро тражите, а не зло,

да живи будете,

да са вама буде Господ, Бог над војскама,

како и кажете.

15Зло мрзите, а волите добро,

на вратима правду заступајте,

па се можда Господ, Бог над војскама,

смилује остатку Јосифовом.

16Зато овако каже Господ, Бог над војскама, Господ:

„Јадиковка је по свим трговима

и улицама свим: ’Јао! Јао!’

И зваће ратара да жали,

да жале они који знају нарицаљку.

17Јадиковаће по свим виноградима,

јер посред тебе ја ћу проћи

– говори Господ.“

Дан Господњи

18Јао онима што прижељкују

дан Господњи!

Шта ће вама дан Господњи?

Тад је тама, а не светло.

19Као човек кад од лава бежи,

а дочека га медвед,

или у кућу уђе

и руку своју на зид стави

да га уједе змија.

20Неће ли дан Господњи бити тама, а не светло

и помрчина без сјаја?

21„Ја мрзим, ја презирем ваше светковине!

Светим саборима вашим ни да примиришем!

22И ако ми приносите свеспалнице

и ваше житне жртве,

нећу да их прихватим.

Не обазирем се на жртве мира

ваших утовљених јунаца.

23Склоните од мене буку својих песама

и мелодију харфи својих.

Не желим да их чујем.

24Нека правда као вода потече

и праведност као поток непресушни.

25Мени ли сте приносили житне жртве

и приносе у пустињи четрдесет година,

о, доме Израиљев?!

26Носили сте своје идоле –

Сикута, цара свога

и Кијуна, звезду својих богова –

које сте себи начинили.

27Изагнаћу вас још даље од Дамаска,

каже Господ, а његово је име Бог над војскама.“