Amosi 6 – CCL & NSP

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Amosi 6:1-14

Tsoka kwa Osalabadira Kanthu

1Tsoka kwa amene simukulabadira kanthu ku Ziyoni,

ndiponso kwa inu amene mukukhala mwamtendere pa Phiri la Samariya,

inu anthu otchuka ochokera ku mtundu wa anthu omveka,

kumene Aisraeli amafikako!

2Pitani ku mzinda wa Kaline mukawuyangʼane;

mukapitenso ku Hamati-raba mzinda waukulu uja,

ndipo mukatsikirenso ku Gati kwa Afilisti.

Kodi mizinda imeneyi ndi yopambana maufumu anu awiriwa?

Kodi dziko lawo ndi lalikulu kupambana lanu?

3Inu simulabadirako kuti tsiku loyipa lidzafika,

zochita zanu zimafulumizitsa ulamuliro wankhanza.

4Mumagona pa mabedi owakongoletsa ndi minyanga ya njovu,

mumagona pa mipando yanu ya wofuwofu.

Mumadya ana ankhosa onona

ndi ana angʼombe onenepa.

5Mumayimba azeze anu ndi kumangopeka

nyimbo pa zingʼwenyengʼwenye ngati Davide.

6Mumamwera vinyo mʼzipanda zodzaza

ndipo mumadzola mafuta abwino kwambiri,

koma simumva chisoni ndi kuwonongeka kwa Yosefe.

7Nʼchifukwa chake inu mudzakhala mʼgulu la anthu oyamba kupita ku ukapolo;

maphwando ndi zikondwerero zanu zidzatheratu.

Yehova Amanyansidwa ndi Kunyada kwa Israeli

8Ambuye Yehova walumbira mʼdzina lake. Yehova Mulungu Wamphamvuzonse walengeza kuti,

“Ndimanyansidwa ndi kunyada kwa Yakobo,

ndimadana ndi nyumba zake zaufumu;

Ine ndidzawupereka mzindawu

pamodzi ndi zonse zili mʼmenemo.”

9Ngati anthu khumi otsala adzabisala mʼnyumba imodzi, nawonso adzafa ndithu. 10Ndipo ngati mʼbale wake wa wina wakufayo, woyenera kusamala za maliro, adzafika kudzatulutsa mitembo mʼnyumbamo nʼkufunsa aliyense amene akubisalabe mʼnyumbamo kuti, “Kodi uli ndi wina wamoyo mʼmenemo?” Ndipo munthu wobisalayo ndi kuyankha kuti, “Ayi,” mʼbaleyo adzanena kuti, “Khala chete! Ife tisayerekeze kutchula dzina la Yehova.”

11Pakuti Yehova walamula kuti

nyumba zikuluzikulu Iye adzazigamulagamula,

ndipo nyumba zazingʼono zidzasanduka maduka okhaokha.

12Kodi akavalo amathamanga pa thanthwe?

Kodi wina amatipula ndi ngʼombe mʼnyanja?

Koma chiweruzo cholungama mwachisandutsa kukhala zinthu zakupha

ndipo chipatso cha chilungamo mwachisandutsa kukhala chowawa.

13Inu amene mukunyadira kuti munagonjetsa Lo Debara

ndipo mukunena kuti, “Kodi sitinatenge Karinaimu ndi mphamvu zathu zokha?”

14Koma Yehova Mulungu Wamphamvuzonse akulengeza kuti,

“Inu nyumba ya Israeli, ndidzakudzutsirani mtundu wina wa anthu

umene udzakuzunzani

kuchokera ku Lebo Hamati mpaka ku Chigwa cha Araba.”

New Serbian Translation

Књига пророка Амоса 6:1-14

Јао лакомисленима!

1Јао лакомисленима на Сиону,

онима што су безбрижни на гори Самарији,

онима што се зову угледнима најбољих народа,

а којима долази дом Израиљев!

2Пређите у Халани, разгледајте,

па оданде идите у Амат-Рабу

и спустите се у Гат филистејски.

Јесу ли та царства боља од ових

и да ли су им пространије међе од ваших међа?

3Ви одгурујете долазак дана зла,

а примичете владавину насиља.

4Башкарите се на лежајима од слоноваче,

протежете на диванима својим

и једете јагњад из стада

и телад из штале.

5Дрндате по харфи,

као Давид себи измишљате инструменте.

6Ви пехарима пијете вино,

мажете се најбољим уљима

и не боле вас Јосифове развалине.

7Зато ћете сада отићи у изгнанство на челу изгнаника,

умукнуће славље оних што се протежу.

Бог се гнуша Јаковљевог поноса

8Собом се заклео Господ Бог, овако говори Господ, Бог над војскама:

„Гнушам се Јаковљевог поноса

и мрзим његова утврђења.

Зато ћу да предам град

и све у њему.“

9Ако и десеторо људи преостане у једној кући и они ће помрети. 10Њихов рођак, најближи њихов ће их узети да их спали, да изнесе кости њихове из куће. И рећи ће ономе у ћошку куће: „Је ли још неко са тобом?“ А он ће му одговорити: „Није.“ И додаће: „Тише само! Не спомињи Господње име!“

11Јер, ево, Господ заповеда

и удариће велику кућу и развалиће је,

а мања ће кућа пући.

12Трче ли коњи по литицама?

Оре ли се море воловима?

Јер, правду сте у отров преокренули

и у пелен плод праведности.

13Радујете се Ло-Девару и говорите:

„Нисмо ли својом снагом освојили Карнајим!“

14„Јер, ево, подижем против вас, о, доме Израиљев

– говори Господ Бог над војскама –

народ који ће вас тлачити

од Лево-Амата до пустињског потока.“