Mboni Zotsutsa Israeli
1Inu Aisraeli, imvani mawu awa amene Yehova wayankhula kutsutsana nanu, kutsutsana ndi banja lonse limene analitulutsa mu Igupto:
2“Inu nokha ndi amene ndinakusankhani
pakati pa mabanja onse a dziko lapansi;
nʼchifukwa chake ndidzakulangani
chifukwa cha machimo anu onse.”
3Kodi anthu awiri nʼkuyendera limodzi
asanapangane?
4Kodi mkango umabangula mʼnkhalango
usanagwire nyama?
Kodi msona wamkango umalira mʼphanga mwake
pamene sunagwire kanthu?
5Kodi mbalame nʼkutera pa msampha
pamene palibe nyambo yake?
Kodi msampha umafwamphuka
usanakole kanthu?
6Kodi pamene lipenga la nkhondo lalira mu mzinda,
anthu sanjenjemera?
Pamene tsoka lafika mu mzinda,
kodi si Yehova amene wachititsa zimenezo?
7Zoonadi Ambuye Yehova sachita kanthu
asanawulule zimene akufuna kuchita
kwa atumiki ake, aneneri.
8Mkango wabangula,
ndani amene sachita mantha?
Ambuye Yehova wayankhula,
ndani amene sanganenere?
9Lengezani zimenezi ku nyumba zaufumu za ku Asidodi
ndiponso ku nyumba zaufumu za ku Igupto:
“Sonkhanani ku mapiri a ku Samariya;
onani chisokonezo pakati pake
ndiponso kuponderezana pakati pa anthu ake.”
10“Iwo sadziwa kuchita zolungama,
ndipo amadzaza malo awo otetezedwa ndi zinthu zolanda ku nkhondo ndi zakuba,” akutero Yehova.
11Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akunena izi:
“Mdani adzalizungulira dzikoli;
iye adzagwetsa malinga ako,
ndi kufunkha nyumba zako zaufumu.”
12Yehova akuti,
“Monga mʼbusa amalanditsa mʼkamwa mwa mkango
miyendo iwiri yokha kapena msonga yokha ya khutu,
moteronso ndimo mmene adzapulumukire Aisraeli
amene amakhala mu Samariya
pa msonga za mabedi awo,
ndi ku Damasiko pa akakhutagona awo.”
13“Imvani izi ndipo mupereke umboni wotsutsa nyumba ya Yakobo,” akutero Ambuye, Yehova Mulungu Wamphamvuzonse.
14“Pa tsiku limene ndidzalange Israeli chifukwa cha machimo ake,
ndidzagumula maguwa ansembe a ku Beteli;
nyanga za guwa zidzathyoka
ndipo zidzagwa pansi.
15Ndidzagwetsa nyumba ya pa nthawi yozizira
pamodzi ndi nyumba ya pa nthawi yotentha;
nyumba zokongoletsedwa ndi minyanga ya njovu zidzawonongedwa
ndipo nyumba zikuluzikulu zidzaphwasulidwa,”
akutero Yehova.
በእስራኤል ላይ የተጠሩ ምስክሮች
1የእስራኤል ልጆች ሆይ፤ እግዚአብሔር በእናንተ ከግብፅ ባወጣሁት ሕዝብ ሁሉ ላይ የተናገረውን ይህን ቃል ስሙ፤
2“ከምድር ወገን ሁሉ፣
እናንተን ብቻ መረጥሁ፤
ስለዚህ ስለ ሠራችሁት ኀጢአት ሁሉ፣
እኔ እቀጣችኋለሁ።”
3በውኑ ሁለት ሰዎች ሳይስማሙ፣
አብረው መጓዝ ይችላሉን?
4አንበሳ የሚበላውን ሳያገኝ፣
በጫካ ውስጥ ይጮኻልን?
ምንም ነገርስ ሳይዝ፣
በዋሻው ውስጥ ያገሣልን?
5ወጥመድ ሳይዘረጋ፣
ወፍ በምድር ላይ ይጠመዳልን?
የሚይዘው ነገር ሳይኖርስ፣
ወጥመዱ ከምድር ይፈነጠራልን?
6የመለከት ድምፅ በከተማ ውስጥ ሲሰማ፣
ሰዎች አይደነግጡምን?
ጥፋትስ በከተማ ላይ ቢደርስ፣
ያደረገው እግዚአብሔር አይደለምን?
7በእውነት ጌታ እግዚአብሔር ምስጢሩን
ለአገልጋዮቹ ለነቢያት ሳይገልጥ፣
ምንም ነገር አያደርግም።
8አንበሳ አገሣ፤
የማይፈራ ማን ነው?
ጌታ እግዚአብሔር ተናገረ፤
ትንቢት የማይናገር ማን ነው?
9ለአዛጦን ምሽግ፣
ለግብፅም ምሽግ እንዲህ ብላችሁ ዐውጁ፤
“በሰማርያ ተራሮች ላይ ተሰብሰቡ፤
በውስጧ ያለውን ታላቅ ሁከት፣
በሕዝቧም መካከል ያለውን ግፍ እዩ።”
10“ቅሚያንና ዝርፊያን በምሽጋቸው ውስጥ የሚያከማቹ፣
በጎ ነገር ማድረግን አያውቁም፤”
ይላል እግዚአብሔር።
11ስለዚህ ጌታ እግዚአብሔር እንዲህ ይላል፤
“ጠላት ምድሪቱን ይወርራል፤
ምሽጎቻችሁን ያፈርሳል፤ ድንኳኖቻችሁን
ይዘርፋል።”
12እግዚአብሔር እንዲህ ይላል፤
“እረኛ ከአንበሳ መንጋጋ፣
ሁለት የእግር ዐጥንት ወይም የጆሮ ቍራጭ እንደሚያድን፣
እንዲሁም በሰማርያ በዐልጋቸው3፥12 በዕብራይስጡ ለዚህ ዐረፍተ ነገር የተሰጠው ትርጕም አይታወቅም ጫፍ ላይ፣
በደማስቆም በምንጣፋቸው ላይ የተቀመጡ፣
እስራኤላውያን ይድናሉ።”
13“ይህን ስሙ፤ በያዕቆብም ቤት ላይ መስክሩ” ይላል ጌታ፣ ሁሉን የሚገዛ አምላክ እግዚአብሔር።
14“እስራኤልን ስለ ኀጢአቷ በምቀጣበት ቀን፣
የቤቴልን መሠዊያዎች አፈርሳለሁ፤
የመሠዊያው ቀንዶች ይቈረጣሉ፤
ወደ ምድርም ይወድቃሉ።
15የክረምቱን ቤት፣
ከበጋው ቤት ጋር እመታለሁ፤
በዝኆን ጥርስ ያጌጡ ቤቶችም ይደመሰሳሉ፤
ታላላቅ አዳራሾችም ይፈርሳሉ፤”
ይላል እግዚአብሔር።