Amosi 2 – CCL & NASV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Amosi 2:1-16

1Yehova akuti,

“Chifukwa anthu a ku Mowabu akunka nachimwirachimwira,

Ine sindileka kuwalanga.

Popeza anatentha mafupa a mfumu ya ku Edomu,

mpaka kuwasandutsa phulusa,

2Ine ndidzatumiza moto pa Mowabu,

umene udzanyeketsa nyumba zaufumu za ku Keriyoti.

Mowabu adzafera pakati pa nkhondo yoopsa,

mʼkati mwa mfuwu wa nkhondo ndi kuliza malipenga.

3Ndidzawononga wolamulira wake

ndi kupha akuluakulu onse amene ali pamodzi ndi iye,”

akutero Yehova.

4Yehova akuti,

“Chifukwa anthu a ku Yuda akunka nachimwirachimwira,

Ine sindileka kuwalanga.

Popeza iwo akana lamulo la Yehova

ndipo sanasunge malangizo ake,

popeza asocheretsedwa ndi milungu yabodza,

milungu imene makolo awo ankayitsatira,

5Ine ndidzatumiza moto pa Yuda,

umene udzanyeketsa nyumba zaufumu za ku Yerusalemu.”

Chilango cha Anthu a ku Israeli

6Yehova akuti,

“Chifukwa anthu a ku Israeli akunka nachimwirachimwira,

Ine sindileka kuwalanga.

Iwo amagulitsa anthu olungama ndi siliva,

ndi osauka ndi nsapato.

7Amapondereza anthu osauka

ngati akuponda fumbi,

ndipo sawaweruza mwachilungamo anthu oponderezedwa.

Abambo ndi mwana wawo amagonana ndi mtsikana mmodzi yemweyo,

ndipo potero amanyozetsa dzina langa loyera.

8Anthuwo amakagonana mʼmbali mwa guwa lililonse la nsembe

pa zovala zimene anatenga ngati chikole.

Mʼnyumba ya mulungu wawo

amamweramo vinyo amene analipiritsa anthu pa milandu.

9“Ine ndinawononga Aamori pamaso pawo,

ngakhale iwo anali anthu ataliatali ngati mikungudza

ndiponso amphamvu ngati mitengo ya thundu.

Ndinawononga zipatso zawo

ndiponso mizu yawo.

10“Ine ndinakutulutsani ku Igupto,

ndipo ndinakutsogolerani mʼchipululu kwa zaka makumi anayi,

kudzakupatsani dziko la Aamori.

11Ine ndinawutsanso ena mwa ana ako kuti akhale aneneri,

ndi ena mwa anyamata ako kuti akhale anaziri.

Kodi si choncho, inu Aisraeli?”

akutero Yehova.

12“Koma inu munawamwetsa vinyo anaziri aja,

ndipo munalamula aneneri kuti asanenere.

13“Tsono Ine ndidzakupsinjani

monga imapsinjikira ngolo imene yadzaza ndi tirigu.

14Munthu waliwiro sadzatha kuthawa,

munthu wamphamvu sadzakhalanso ndi nyonga,

wankhondo sadzapulumutsa moyo wake.

15Munthu wa uta sadzalimbika,

msilikali wothamanga kwambiri sadzapulumuka,

ndipo wokwera pa akavalo sadzapulumutsa moyo wake.

16Ngakhale asilikali olimba mtima kwambiri

adzathawa ali maliseche pa tsikulo,”

akutero Yehova.

New Amharic Standard Version

አሞጽ 2:1-16

1እግዚአብሔር እንዲህ ይላል፤

“ስለ ሦስቱ የሞዓብ ኀጢአት፣

ይልቁንም ስለ አራቱ፣ ቍጣዬን አልመልስም፤

የኤዶምን ንጉሥ ዐጥንት፣

ዐመድ እስኪሆን ድረስ አቃጥሏልና፤

2የቂርዮትን ምሽጎች2፥2 ወይም ከተሞቿ እንዲበላ፣

በሞዓብ ላይ እሳት እሰድዳለሁ፤

ሞዓብ በጦርነት ጩኸትና በመለከት ድምፅ መሐል፣

በታላቅ ሁካታ ውስጥ ይሞታል።

3ገዧን እደመስሳለሁ፣

አለቆቿንም ሁሉ ከንጉሧ ጋር እገድላለሁ፤”

ይላል እግዚአብሔር

4እግዚአብሔር እንዲህ ይላል፤

“ስለ ሦስቱ የይሁዳ ኀጢአት፣

ይልቁን ስለ አራቱ፣ ቍጣዬን አልመልስም፤

የእግዚአብሔርን ሕግ ንቀዋል፤

ትእዛዙንም አልጠበቁምና፤

አባቶቻቸው በተከተሏቸው2፥4 ወይም በውሸት አማልክት፣

በሐሰት2፥4 ወይም ውሸት አማልክት በመመራት ስተዋልና።

5የኢየሩሳሌምን ምሽጎች እንዲበላ፣

በይሁዳ ላይ እሳት እሰድዳለሁ።”

በእስራኤል ላይ የተሰጠ ፍርድ

6እግዚአብሔር እንዲህ ይላል፤

“ስለ ሦስቱ የእስራኤል ኀጢአት፣

ይልቁንም ስለ አራቱ፣ ቍጣዬን አልመልስም፤

ጻድቁን ስለ ጥሬ ብር፣

ችግረኛውንም ስለ ጥንድ ጫማ ይሸጡታልና።

7የድኾችን ራስ፣

በምድር ትቢያ ላይ ይረግጣሉ፤

ፍትሕንም ከጭቍኖች ይነጥቃሉ፤

አባትና ልጅ ከአንዲት ሴት ጋር ይተኛሉ፤

እንዲህም እያደረጉ ቅዱስ ስሜን ያረክሳሉ።

8በመያዣነት በተወሰደው ልብስ ላይ፣

በየመሠዊያው ሥር ይተኛሉ፤

በአምላካቸው ቤት፣

በመቀጫነት የተወሰደውን የወይን ጠጅ ይጠጣሉ።

9“ቁመቱ እንደ ዝግባ፣

ጥንካሬውም እንደ ባሉጥ ዛፍ የነበረ ቢሆንም፣

አሞራዊውን ከፊታቸው አጠፋሁት፣

ከላይ ፍሬውን፣

ከታችም ሥሩን አጠፋሁ።

10የአሞራውያንን ምድር ልሰጣችሁ፣

ከግብፅ አወጣኋችሁ፤

አርባ ዓመትም በምድረ በዳ መራኋችሁ።

11“ደግሞም ነቢያትን ከወንዶች ልጆቻችሁ መካከል፣

ናዝራውያንንም ከጕልማሶቻችሁ መካከል አስነሣሁ፤

የእስራኤል ሕዝብ ሆይ፤ ይህ እውነት አይደለምን?”

ይላል እግዚአብሔር

12“እናንተ ግን ናዝራውያኑን የወይን ጠጅ አጠጣችኋቸው፤

ነቢያቱንም ትንቢት እንዳይናገሩ አዘዛችኋቸው።

13“እነሆ፤ በእህል የተሞላ ጋሪ እንደሚያደቅቅ፣

እኔም አደቅቃችኋለሁ።

14ፈጣኑ አያመልጥም፤

ብርቱውንም ብርታቱ አይረዳውም፤

ኀያሉም ነፍሱን አያድንም።

15ቀስተኛው በቦታው ጸንቶ አይቆምም፤

ፈጣኑም ተዋጊ ሮጦ አያመልጥም፤

ፈረሰኛውም ነፍሱን አያድንም።

16ጐበዞቹ ተዋጊዎች እንኳ፣

በዚያ ቀን ዕራቁታቸውን ይሸሻሉ፤”

ይላል እግዚአብሔር