Yoweli 1 – CCL & NASV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yoweli 1:1-20

1Yehova anayankhula ndi Yoweli mwana wa Petueli.

Kubwera kwa Dzombe

2Inu akuluakulu, imvani izi;

mvetserani, nonse amene mumakhala mʼdziko.

Kodi zinthu zokhala ngati izi zinayamba zaonekapo mʼnthawi yanu,

kapena mʼnthawi ya makolo anu?

3Muwafotokozere ana anu,

ndipo ana anuwo afotokozere ana awo,

ndipo ana awo adzafotokozere mʼbado winawo.

4Chimene dzombe losamera mapiko lasiya

dzombe lowuluka ladya;

chimene dzombe lowuluka lasiya

dzombe lalingʼono ladya;

chimene dzombe lalingʼono lasiya

chilimamine wadya.

5Dzukani, inu zidakwa ndipo mulire!

Lirani mofuwula, inu nonse amene mumamwa vinyo;

lirani mofuwula chifukwa cha vinyo watsopano,

pakuti wachotsedwa pakamwa panu.

6Mtundu wa anthu wathira nkhondo dziko langa,

wamphamvu ndi wosawerengeka;

uli ndi mano a mkango,

zibwano za mkango waukazi.

7Wawononga mphesa zanga

ndipo wathyola mitengo yanga ya mkuyu.

Wakungunula makungwa ake

ndi kuwataya,

kusiya nthambi zake zili mbee.

8Lirani ngati namwali wovala chiguduli,

chifukwa cha mwamuna wa utsikana wake.

9Chopereka cha chakudya ndi cha chakumwa

sizikuperekedwa ku nyumba ya Yehova.

Ansembe akulira,

amene amatumikira pamaso pa Yehova.

10Minda yaguga,

nthaka yauma;

tirigu wawonongeka,

vinyo watsopano watha,

mitengo ya mafuta yauma.

11Khalani ndi nkhawa, inu alimi,

lirani mofuwula inu alimi a mphesa;

imvani chisoni chifukwa cha tirigu ndi barele,

pakuti zokolola za mʼmunda zawonongeka.

12Mpesa wauma

ndipo mtengo wamkuyu wafota;

makangadza, kanjedza ndi mitengo ya apulosi,

mitengo yonse ya mʼmunda yauma.

Ndithudi chimwemwe cha anthu

chatheratu.

Mulungu Ayitana Anthu kuti Atembenuke

13Inu ansembe, valani ziguduli ndipo lirani;

lirani mofuwula, inu amene mumatumikira pa guwa lansembe.

Bwerani, fundani ziguduli usiku wonse,

inu amene mumatumikira pamaso pa Mulungu wanga;

pakuti chopereka cha chakudya ndi cha chakumwa

sizikupezekanso mʼnyumba ya Mulungu wanu.

14Lengezani tsiku lopatulika losala zakudya,

itanani msonkhano wopatulika.

Sonkhanitsani akuluakulu

ndi anthu onse okhala mʼdziko

ku nyumba ya Yehova Mulungu wanu

ndipo alirire Yehova.

15Kalanga ine tsikulo!

Pakuti tsiku la Yehova layandikira;

lidzabwera ngati chiwonongeko chochokera kwa Wamphamvuzonse.

16Kodi chakudya chathu sichachotsedwa

ife tikuona?

Kodi mʼnyumba ya Mulungu wathu

simulibe chimwemwe ndi chisangalalo?

17Mbewu zikunyala

poti pansi ndi powuma.

Nyumba zosungiramo zinthu zawonongeka;

nkhokwe zapasuka

popeza tirigu wauma.

18Taonani mmene zikulirira ziweto;

ngʼombe zikungoyenda uku ndi uku

chifukwa zilibe msipu;

ngakhalenso nkhosa zikusauka.

19Kwa Inu Yehova ndilirira,

pakuti moto wapsereza msipu wakuthengo,

malawi amoto apsereza mitengo yonse ya mʼtchire.

20Ngakhale nyama zakuthengo zikulirira Inu;

timitsinje tonse taphwa

ndipo moto wapsereza msipu wa kuthengo.

New Amharic Standard Version

ኢዩኤል 1:1-20

1ወደ ባቱኤል ልጅ ወደ ኢዩኤል የመጣው የእግዚአብሔር ቃል ይህ ነው፤

የአንበጣ ወረራ

2እናንት ሽማግሌዎች፣ ይህን ስሙ፤

በምድሪቱም የምትኖሩ ሁላችሁ፣ አድምጡ፤

በእናንተ ዘመንም ሆነ በአባቶቻችሁ ዘመን፣

እንዲህ ዐይነት ነገር ሆኖ ያውቃልን?

3ይህን ለልጆቻችሁ ተናገሩ፤

ልጆቻችሁ ለልጆቻቸው ይንገሩ፤

ልጆቻቸውም ለሚቀጥለው ትውልድ ይንገሩ።

4ከአንበጣ መንጋ1፥4 በዚህ ክፍል፣ ስለ አንበጦች የሚገልጹት አራት የዕብራይስጥ ቃላት፣ ትክክለኛ ትርጕም አይታወቅም። የተረፈውን፣

ትልልቁ አንበጣ በላው፤

ከትልልቁ አንበጣ የተረፈውን፣

ኵብኵባ በላው፤

ከኵብኵባ የተረፈውን፣

ሌሎች አንበጦች በሉት።

5እናንት ሰካራሞች፤ ተነሡ፤ አልቅሱ፤

እናንት የወይን ጠጅ ጠጪዎች ሁሉ፤ ዋይ በሉ፤

ስለ አዲሱ የወይን ጠጅ ዋይ ብላችሁ አልቅሱ፤

አፋችሁ ላይ እንዳለ ተነጥቃችኋልና።

6ኀያልና ቍጥር ስፍር የሌለው ሕዝብ፣

ምድሬን ወሯታልና፤

ጥርሱ እንደ አንበሳ ጥርስ፣

መንጋጋውም እንደ እንስት አንበሳ መንጋጋ ነው።

7የወይን ቦታዬን ባድማ አደረገው፤

የበለስ ዛፎቼንም ቈራረጠ፤

ቅርንጫፎቻቸው ነጭ ሆነው እስኪታዩ ድረስ፣

ቅርፊታቸውን ልጦ፣

ወዲያ ጣላቸው።

8የልጅነት ዕጮኛዋን1፥8 ወይም የልጅነት ባሏ እንዳጣች ድንግል1፥8 ወይም ወጣት ሴት

ማቅ ለብሳችሁ አልቅሱ።

9የእህል ቍርባንና የመጠጥ ቍርባን፣

ከእግዚአብሔር ቤት ተቋርጧል፤

በእግዚአብሔርም ፊት የሚያገለግሉ፣

ካህናት ያለቅሳሉ።

10ዕርሻዎች ባዷቸውን ቀርተዋል፤

ምድሩም ደርቋል1፥10 ወይም መሬቱ ያዝናል

እህሉ ጠፍቷል፤

አዲሱ የወይን ጠጅ ዐልቋል፤

ዘይቱም ተሟጧል።

11እናንት ገበሬዎች፣ ዕዘኑ፤

እናንት የወይን ገበሬዎች፣ ዋይ በሉ፤

ስለ ገብሱና ስለ ስንዴው አልቅሱ፤

የዕርሻው መከር ጠፍቷልና።

12ወይኑ ደርቋል፤

የበለስ ዛፉም ጠውልጓል፤

ሮማኑ፣ ተምሩና እንኮዩ፣

የዕርሻው ዛፎች ሁሉ ደርቀዋል፤

ስለዚህ ደስታ፣

ከሰው ልጆች ርቋል።

የንስሓ ጥሪ

13ካህናት ሆይ፤ ማቅ ለብሳችሁ አልቅሱ፤

እናንተ በመሠዊያው ፊት የምታገለግሉ፣ ዋይ በሉ፤

እናንት በአምላኬ ፊት የምታገለግሉ፣

ኑ፤ ማቅ ለብሳችሁ ዕደሩ፤

የእህል ቍርባኑና የመጠጥ ቍርባኑ፣

ከአምላካችሁ ቤት ተቋርጧልና።

14ቅዱስ ጾምን ዐውጁ፤

የተቀደሰንም ጉባኤ ጥሩ፤

ሽማግሌዎችን ሰብስቡ፤

በምድሪቱ የሚኖሩትን ሁሉ፣

ወደ አምላካችሁ ወደ እግዚአብሔር ቤት ጥሩ፤

ወደ እግዚአብሔርም ጩኹ።

15ወዮ ለዚያ ቀን፤

የእግዚአብሔር ቀን ቀርቧልና፤

ሁሉን ከሚችል1፥15 ዕብራይስጡ ሻደይ ይለዋል። አምላክ እንደ ጥፋት ይመጣል።

16የሚበላ ምግብ፣

ከዐይናችን ፊት፣

ደስታና ተድላ፣

ከአምላካችን ቤት አልተቋረጠብንምን?

17ዘሩ በዐፈር ውስጥ1፥17 ለዚህ የገባው የዕብራይስጡ ቃል ትርጕም አይታወቅም።

በስብሶ ቀርቷል፤

ግምጃ ቤቶቹ ፈራርሰዋል፤

ጐተራዎቹም ተሰባብረዋል፤

እህሉ ደርቋልና።

18መንጎች እንደ ምን ጮኹ፣

ከብቶቹ ተደናግጠዋል፤

መሰማሪያ የላቸውምና፤

የበግ መንጎች እንኳ ተቸግረዋል።

19አቤቱ እግዚአብሔር ሆይ፤ ወደ አንተ እጣራለሁ፤

ያልተነካውን መሰማሪያ እሳት በልቶታልና፤

የዱሩን ዛፍ ሁሉ ነበልባል አቃጥሎታል።

20የዱር አራዊት እንኳ ወደ አንተ አለኸለኹ፤

ወራጁ ውሃ ደርቋል፤

ያልተነካውንም መሰማሪያ እሳት በልቶታል።