Amosi 1 – CCL & KJV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Amosi 1:1-15

1Mawu a Amosi, mmodzi mwa anthu oweta nkhosa ku Tekowa. Zimene iye anaona mʼmasomphenya zokhudza Israeli patatsala zaka ziwiri kuti chivomerezi chichitike, nthawi imene Uziya anali mfumu ya Yuda ndipo Yeroboamu mwana wa Yowasi anali mfumu ya Israeli.

2Amosi anati:

“Yehova akubangula mu Ziyoni

ndipo akumveka ngati bingu mu Yerusalemu;

msipu wa abusa ukulira,

ndipo pamwamba pa Karimeli pakuwuma.”

Chiweruzo pa Anthu Oyandikana ndi Israeli

3Yehova akuti,

“Chifukwa anthu a ku Damasiko akunka nachimwirachimwira,

Ine sindileka kuwalanga.

Popeza anapuntha Giliyadi

ndi zopunthira za mano achitsulo,

4Ine ndidzatumiza moto pa nyumba ya Hazaeli

umene udzanyeketsa nyumba zaufumu za Beni-Hadadi.

5Ndidzathyola chipata cha Damasiko;

ndidzawononga mfumu yokhala ku Chigwa cha Aveni,

ndiponso iye amene akugwira ndodo yaufumu mu Beti-Edeni.

Anthu a ku Aramu adzapita ku ukapolo ku Kiri,”

akutero Yehova.

6Yehova akuti,

“Chifukwa anthu a ku Gaza akunka nachimwirachimwira,

Ine sindileka kuwalanga.

Popeza anatenga ukapolo mtundu wathunthu

ndi kuwugulitsa ku Edomu,

7ndidzatumiza moto pa makoma a Gaza

umene udzanyeketsa nyumba zake zaufumu.

8Ndidzawononga mfumu ya ku Asidodi

komanso amene akugwira ndodo yaufumu ku Asikeloni.

Ndidzalanga Ekroni,

mpaka wotsala mwa Afilisti atafa,”

akutero Ambuye Yehova.

9Yehova akuti,

“Chifukwa anthu a ku Turo akunka nachimwirachimwira,

Ine sindileka kuwalanga.

Popeza iwo anagulitsa mtundu wathunthu ku ukapolo ku Edomu,

osasunga pangano laubale lija,

10Ine ndidzatumiza moto pa makoma a Turo

umene udzanyeketsa nyumba zake zaufumu.”

11Yehova akuti,

“Chifukwa anthu a ku Edomu akunka nachimwirachimwira,

Ine sindileka kuwalanga.

Popeza anathamangitsa mʼbale wake ndi lupanga,

popanda nʼchifundo chomwe.

Popeza mkwiyo wake unakulabe

ndipo ukali wake sunatonthozeke,

12Ine ndidzatumiza moto pa Temani

umene udzanyeketsa nyumba zaufumu za Bozira.”

13Yehova akuti,

“Chifukwa anthu a ku Amoni akunka nachimwirachimwira,

Ine sindileka kuwalanga.

Popeza anatumbula akazi oyembekezera a ku Giliyadi

nʼcholinga choti akuze malire awo,

14Ine ndidzayatsa moto pa makoma a ku Raba

umene udzanyeketsa nyumba zake zaufumu.

Padzakhala kulira kwakukulu pa tsiku la nkhondoyo,

kumenyana kudzakhala kwafumbi ngati mkuntho wa kamvuluvulu.

15Mfumu yawo idzatengedwa kupita ku ukapolo,

iyo pamodzi ndi akuluakulu ake,”

akutero Yehova.

King James Version

Amos 1:1-15

1The words of Amos, who was among the herdmen of Tekoa, which he saw concerning Israel in the days of Uzziah king of Judah, and in the days of Jeroboam the son of Joash king of Israel, two years before the earthquake. 2And he said, The LORD will roar from Zion, and utter his voice from Jerusalem; and the habitations of the shepherds shall mourn, and the top of Carmel shall wither.

3Thus saith the LORD; For three transgressions of Damascus, and for four, I will not turn away the punishment thereof; because they have threshed Gilead with threshing instruments of iron:1.3 and…: or, yea, for four1.3 turn…: or, convert it, or, let it be quiet 4But I will send a fire into the house of Hazael, which shall devour the palaces of Ben-hadad. 5I will break also the bar of Damascus, and cut off the inhabitant from the plain of Aven, and him that holdeth the sceptre from the house of Eden: and the people of Syria shall go into captivity unto Kir, saith the LORD.1.5 the plain…: or, Bikathaven1.5 the house…: or, Beth-eden

6¶ Thus saith the LORD; For three transgressions of Gaza, and for four, I will not turn away the punishment thereof; because they carried away captive the whole captivity, to deliver them up to Edom:1.6 away captive…: or, them away with an entire 7But I will send a fire on the wall of Gaza, which shall devour the palaces thereof: 8And I will cut off the inhabitant from Ashdod, and him that holdeth the sceptre from Ashkelon, and I will turn mine hand against Ekron: and the remnant of the Philistines shall perish, saith the Lord GOD.

9¶ Thus saith the LORD; For three transgressions of Tyrus, and for four, I will not turn away the punishment thereof; because they delivered up the whole captivity to Edom, and remembered not the brotherly covenant:1.9 the brotherly…: Heb. the covenant of brethren 10But I will send a fire on the wall of Tyrus, which shall devour the palaces thereof.

11¶ Thus saith the LORD; For three transgressions of Edom, and for four, I will not turn away the punishment thereof; because he did pursue his brother with the sword, and did cast off all pity, and his anger did tear perpetually, and he kept his wrath for ever:1.11 did cast…: Heb. corrupted his compassions 12But I will send a fire upon Teman, which shall devour the palaces of Bozrah.

13¶ Thus saith the LORD; For three transgressions of the children of Ammon, and for four, I will not turn away the punishment thereof; because they have ripped up the women with child of Gilead, that they might enlarge their border:1.13 ripped…: or, divided the mountains 14But I will kindle a fire in the wall of Rabbah, and it shall devour the palaces thereof, with shouting in the day of battle, with a tempest in the day of the whirlwind: 15And their king shall go into captivity, he and his princes together, saith the LORD.