Yoweli 3 – CCL & KJV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yoweli 3:1-21

Kuweruzidwa kwa Mitundu ya Anthu

1“Masiku amenewo ndiponso nthawi imeneyo,

nditadzabwezeretsanso Yerusalemu ndi Yuda mʼchimake,

2ndidzasonkhanitsa anthu a mitundu yonse

ndipo ndidzawabweretsa ku Chigwa cha Yehosafati.

Kumeneko ndidzawaweruza

chifukwa cha cholowa changa, anthu anga Aisraeli,

pakuti anabalalitsa anthu anga pakati pa mitundu ya anthu

ndikugawa dziko langa.

3Anagawana anthu anga pochita maere

ndipo anyamata anawasinthanitsa ndi akazi achiwerewere;

anagulitsa atsikana chifukwa cha vinyo

kuti iwo amwe.

4“Kodi tsopano inu a ku Turo ndi Sidoni ndi madera onse a Filisitiya, muli ndi chiyani chotsutsana nane? Kodi mukundibwezera pa zinthu zimene ndakuchitirani? Ngati inu mukundibwezera, Ine ndidzabwezera zochita zanu mofulumira ndi mwachangu pa mitu yanu. 5Pakuti munatenga siliva ndi golide wanga ndi kupita nacho chuma changa chamtengowapatali ku nyumba zanu zopembedzera mafano. 6Inu munagulitsa anthu a ku Yuda ndi Yerusalemu kwa Agriki, kuti apite kutali ndi malire a dziko lawo.

7“Taonani, Ine ndidzawachotsa kumalo kumene munawagulitsako, ndipo ndidzabwezera zimene mwachita pa mitu yanu. 8Ndidzagulitsa ana anu aamuna ndi ana anu aakazi kwa anthu a ku Yuda, ndipo iwo adzawagulitsa kwa Aseba, mtundu wa anthu okhala kutali.” Yehova wayankhula.

9Lengezani izi pakati pa anthu a mitundu ina:

Konzekerani nkhondo!

Dzutsani ankhondo amphamvu!

Asilikali onse afike pafupi ndipo ayambe nkhondo.

10Sulani makasu anu kuti akhale malupanga

ndipo zikwanje zanu zikhale mikondo.

Munthu wofowoka anene kuti,

“Ndine wamphamvu!”

11Bwerani msanga, inu anthu a mitundu yonse kuchokera ku mbali zonse,

ndipo musonkhane kumeneko.

Tumizani ankhondo anu Yehova!

12“Mitundu ya anthu idzuke;

ipite ku Chigwa cha Yehosafati,

pakuti kumeneko Ine ndidzakhala

ndikuweruza anthu a mitundu yonse yozungulira.

13Tengani chikwakwa chodulira tirigu,

pakuti mbewu zakhwima.

Bwerani dzapondeni mphesa,

pakuti mopsinyira mphesa mwadzaza

ndipo mitsuko ikusefukira;

kuyipa kwa anthuwa nʼkwakukulu kwambiri!”

14Chigulu cha anthu, chigulu cha anthu,

mʼchigwa cha chiweruzo!

Pakuti tsiku la Yehova layandikira

mʼchigwa cha chiweruzo.

15Dzuwa ndi mwezi zidzadetsedwa,

ndipo nyenyezi sizidzawalanso.

16Yehova adzabangula kuchokera mu Ziyoni

ndipo mawu ake adzamveka ngati bingu kuchokera mu Yerusalemu;

dziko lapansi ndi thambo zidzagwedezeka.

Koma Yehova adzakhala pothawira pa anthu ake,

linga la anthu a ku Israeli.

Madalitso a Anthu a Mulungu

17“Pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine Yehova Mulungu wanu,

ndimakhala mu Ziyoni, phiri langa lopatulika.

Yerusalemu adzakhala wopatulika;

alendo sadzamuthiranso nkhondo.

18“Tsiku limenelo mapiri adzachucha vinyo watsopano,

ndipo zitunda zidzayenderera mkaka;

mitsinje yonse ya ku Yuda idzadzaza ndi madzi.

Kasupe adzatumphuka mʼnyumba ya Yehova

ndipo adzathirira Chigwa cha Sitimu.

19Koma Igupto adzasanduka bwinja,

Edomu adzasanduka chipululu,

chifukwa cha nkhondo imene anathira anthu a ku Yuda

mʼdziko limene anakhetsa magazi a anthu osalakwa.

20Koma Yuda adzakhala ndi anthu mpaka muyaya

ndi Yerusalemu ku mibadomibado.

21Kukhetsa magazi kwawo kumene Ine sindinakhululuke

ndidzakhululuka.”

Yehova amakhala mu Ziyoni!

King James Version

Joel 3:1-21

1For, behold, in those days, and in that time, when I shall bring again the captivity of Judah and Jerusalem, 2I will also gather all nations, and will bring them down into the valley of Jehoshaphat, and will plead with them there for my people and for my heritage Israel, whom they have scattered among the nations, and parted my land. 3And they have cast lots for my people; and have given a boy for an harlot, and sold a girl for wine, that they might drink. 4Yea, and what have ye to do with me, O Tyre, and Zidon, and all the coasts of Palestine? will ye render me a recompence? and if ye recompense me, swiftly and speedily will I return your recompence upon your own head; 5Because ye have taken my silver and my gold, and have carried into your temples my goodly pleasant things:3.5 pleasant: Heb. desirable 6The children also of Judah and the children of Jerusalem have ye sold unto the Grecians, that ye might remove them far from their border.3.6 the Grecians: Heb. the sons of the Grecians 7Behold, I will raise them out of the place whither ye have sold them, and will return your recompence upon your own head: 8And I will sell your sons and your daughters into the hand of the children of Judah, and they shall sell them to the Sabeans, to a people far off: for the LORD hath spoken it.

9¶ Proclaim ye this among the Gentiles; Prepare war, wake up the mighty men, let all the men of war draw near; let them come up:3.9 Prepare: Heb. Sanctify 10Beat your plowshares into swords, and your pruninghooks into spears: let the weak say, I am strong.3.10 pruninghooks: or, scythes 11Assemble yourselves, and come, all ye heathen, and gather yourselves together round about: thither cause thy mighty ones to come down, O LORD.3.11 cause…: or, the LORD shall bring down 12Let the heathen be wakened, and come up to the valley of Jehoshaphat: for there will I sit to judge all the heathen round about. 13Put ye in the sickle, for the harvest is ripe: come, get you down; for the press is full, the fats overflow; for their wickedness is great. 14Multitudes, multitudes in the valley of decision: for the day of the LORD is near in the valley of decision.3.14 decision: or, concision, or, threshing 15The sun and the moon shall be darkened, and the stars shall withdraw their shining. 16The LORD also shall roar out of Zion, and utter his voice from Jerusalem; and the heavens and the earth shall shake: but the LORD will be the hope of his people, and the strength of the children of Israel.3.16 hope: Heb. place of repair, or, harbour 17So shall ye know that I am the LORD your God dwelling in Zion, my holy mountain: then shall Jerusalem be holy, and there shall no strangers pass through her any more.3.17 holy: Heb. holiness

18¶ And it shall come to pass in that day, that the mountains shall drop down new wine, and the hills shall flow with milk, and all the rivers of Judah shall flow with waters, and a fountain shall come forth of the house of the LORD, and shall water the valley of Shittim.3.18 flow: Heb. go 19Egypt shall be a desolation, and Edom shall be a desolate wilderness, for the violence against the children of Judah, because they have shed innocent blood in their land. 20But Judah shall dwell for ever, and Jerusalem from generation to generation.3.20 dwell: or, abide 21For I will cleanse their blood that I have not cleansed: for the LORD dwelleth in Zion.3.21 for the…: or, even I the LORD that