2 Timoteyo 3 – CCL & CRO

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Timoteyo 3:1-17

Zoopsa za Mʼmasiku Otsiriza

1Koma dziwa izi: Mʼmasiku otsiriza kudzafika nthawi zoopsa kwambiri. 2Anthu adzakhala odzikonda, okonda ndalama, odzitama, onyada, achipongwe, osamvera makolo awo, osayamika, wopanda chiyero. 3Adzakhala wopanda chikondi, osakhululuka, osinjirira, osadziletsa, ankhanza, osakonda zabwino, 4opereka anzawo kwa adani awo, osaopa zoyipa, odzitukumula, okonda zowasangalatsa mʼmalo mokonda Mulungu. 5Adzakhala ndi maonekedwe achipembedzo koma mphamvu yake ndi kumayikana. Anthu amenewa uziwapewa.

6Iwowa ndi anthu aja amene amayendayenda mʼmakomo a anthu nʼkumanyenga akazi ofowoka mʼmaganizo, olemedwa ndi machimo ndiponso otengeka ndi zilakolako zoyipa zamitundumitundu, 7amaphunzira nthawi zonse koma samatha kuzindikira choonadi. 8Monga momwe Yanesi ndi Yambere anawukira Mose, momwemonso anthu amenewa amawukira choonadi. Nzeru zawo ndi zowonongeka ndipo pa za chikhulupiriro, ndi okanidwa. 9Koma sadzapita nazo patali kwambiri zimenezi, pakuti anthu onse adzaona kupusa kwawo monga anachitira Yanesi ndi Yambere.

Paulo Alimbikitsa Timoteyo

10Tsono iwe, umadziwa zonse zimene ndimaphunzitsa, makhalidwe anga, cholinga changa, chikhulupiriro changa, kuleza mtima kwanga, chikondi changa, ndi kupirira kwanga, 11mazunzo anga, masautso anga, monga zinandichitikira ku Antiokeya, ku Ikoniya ndi ku Lusitra. Ndinazunzika kwambiri. Koma Ambuye anandipulumutsa pa zonsezi. 12Kunena zoona, munthu aliyense amene akufuna kukhala moyo wolemekeza Mulungu mwa Khristu Yesu, adzazunzikadi, 13pomwe anthu oyipa ndi onyenga adzanka nayipirayipira, kunamiza ena, iwo nʼkumanamizidwanso. 14Koma iwe pitiriza zimene waziphunzira ndi kuzivomereza, chifukwa ukudziwa amene anakuphunzitsa zimenezi. 15Kuyambira uli wamngʼono wakhala ukudziwa Malemba Oyera, amene akhoza kukupatsa nzeru zokupulumutsa kudzera mʼchikhulupiriro cha mwa Yesu Khristu. 16Malemba onse anawalembetsa ndi Mulungu, ndipo othandiza pophunzitsa, podzudzula, pokonza cholakwika ndi polangiza za chilungamo 17kuti munthu wa Mulungu akonzekere bwino lomwe kugwira ntchito iliyonse yabwino.

Knijga O Kristu

2 Timoteju 3:1-17

Opasnosti u posljednjim vremenima

1I znaj, Timoteju, da će posljednja vremena biti teška 2jer će ljudi biti sebični i pohlepni za novcem. Bit će oholi i hvalisavci, rugat će se Bogu, bit će neposlušni roditeljima i nezahvalni. Ništa im neće biti sveto. 3Bit će tvrda srca i nikad ni u čemu neće popuštati drugima; bit će lažljivci i stvarat će nevolje, neobuzdano će živjeti. Bit će grubi i okrutni, izrugivat će se onima koji nastoje biti dobri. 4Izdavat će svoje prijatelje; to su usijane glave, nadmene i ohole, koje će više voljeti svjetovne užitke nego štovanje Boga. 5Zadržat će izvanjsko obličje pobožnosti, ali će se odreći njezine sile. Takvih se ljudi klonite.

6Takvi su oni koji se uvlače u kuće i pridobivaju ženice opterećene bremenom grijeha, kojima vladaju različite strasti. 7One uvijek uče, a nikako da spoznaju istinu. 8Ti se učitelji bore protiv istine kao što su se Janes i Jambres suprotstavili Mojsiju. To su ljudi pokvarena uma i nevaljane vjere. 9Ali neće više napredovati jer će svima postati jasno da su bezumnici, baš kao što se dogodilo Janesu i Jambresu.

Pavao zadužuje Timoteja

10Ali ti znaš što poučavam, kako živim i što mi je životni naum. Znaš moju vjeru i što sam sve propatio. Znaš moju ljubav i postojanost. 11Znaš kakva sam progonstva i patnje pretrpio u Antiohiji, u Ikoniju i Listri. Ali Gospodin me iz svih izbavio. 12A i svi koji hoće pobožno živjeti u Kristu Isusu bit će progonjeni. 13Zli će pak ljudi i varalice napredovati iz zla u gore. Varat će druge, ali će i sami biti prevareni.

14Ali ti ostani vjeran onome čemu si poučen. Znaš da u to možeš vjerovati jer znaš da možeš vjerovati onome tko te je poučio. 15Odmalena poznaješ Sveto pismo, koje ti je dalo mudrost da primiš spasenje po vjeri u Krista Isusa. 16Jer cijelo je Sveto pismo od Boga nadahnuto i korisno za poučavanje, za popravljanje i odgajanje u pravednosti. 17Bog nas kroz njega oprema da budemo sposobni za svako djelo ljubavi.