2 Timoteyo 4 – CCL & CRO

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Timoteyo 4:1-22

1Pamaso pa Mulungu ndi pamaso pa Khristu Yesu, amene adzaweruza amoyo ndi akufa omwe pamene adzaonekera ndi ufumu wake, ndikukulamula kuti: 2Lalikira Mawu; khala wokonzeka pa nthawi yake, ngakhale pamene si pa nthawi yake. Konza zolakwa zawo, dzudzula ndipo limbikitsa moleza mtima kwambiri ndi malangizo osamalitsa. 3Pakuti idzafika nthawi imene anthu adzakana chiphunzitso choona. Mʼmalo mwake, chifukwa chokhumba kumva zowakomera zokha, adzasonkhanitsa aphunzitsi ambiri omawawuza zimene iwo akufuna kumva. 4Sadzafuna kumva choona koma adzafuna kumva nthano chabe. 5Koma iwe, khala tcheru nthawi zonse, pirira mʼzovuta, gwira ntchito ya mlaliki, gwira ntchito zonse za utumiki wako.

6Pakuti moyo wanga wayamba kale kuthiridwa ngati nsembe, ndipo nthawi yakwana yoti ndinyamuke ulendo wanga. 7Ndamenya nkhondo yabwino, ndatsiriza bwino mpikisano wa liwiro ndipo ndasunga chikhulupiriro. 8Tsopano mphotho yanga ikundidikira imene ndi chipewa cha chilungamo, imene Ambuye, woweruza wolungama, adzandipatsa pa tsiku lijalo, osati ine ndekha komanso onse amene akufunitsitsa kubwera kwake.

Ndemanga ya Paulo

9Uyesetse kubwera kuno msanga. 10Paja Dema anandisiya chifukwa chokonda dziko lapansi lino, ndipo anapita ku Tesalonika. Kresike anapita ku Galatiya ndipo Tito anapita ku Dalimatiya. 11Ndatsala ndi Luka yekha basi. Mutenge Marko ndipo ubwere naye kuno, chifukwa amandithandiza mu utumiki wanga. 12Ndatumiza Tukiko ku Efeso. 13Pobwera, unditengere chofunda pamwamba chimene ndinachisiya kwa Kupro ku Trowa. Unditengerenso mabuku anga, makamaka aja azikopawa.

14Alekisandro, mmisiri wa zitsulo anandichitira zoyipa kwambiri. Ambuye adzamubwezera pa zimene anachita. 15Iwenso ukhale naye tcheru chifukwa anatsutsa kwambiri uthenga wathu.

16Podziteteza koyamba pa mlandu wanga, panalibe ndi mmodzi yemwe amene anandithandiza, koma aliyense anandithawa. Mulungu awakhululukire. 17Koma Ambuye anayima nane limodzi, ndipo anandipatsa mphamvu, kuti kudzera mwa ine, uthenga ulalikidwe kwambiri, ndikuti anthu a mitundu ina amve. Ndipo ndinalanditsidwa mʼkamwa mwa mkango. 18Ambuye adzandilanditsa ku chilichonse chofuna kundichita choyipa ndipo adzandisamalira bwino mpaka kundilowetsa chonse mu ufumu wake wakumwamba. Kwa Iye kukhale ulemerero mpaka muyaya.

Mawu Otsiriza

19Pereka moni kwa Prisila ndi Akura pamodzi ndi banja lonse la Onesiforo. 20Erasto anatsalira ku Korinto. Trofimo ndinamusiya akudwala ku Mileto. 21Uyesetse kubwera kuno nthawi yozizira isanafike. Eubulo akupereka moni, ndiponso Pude, Lino, Klaudiya ndi abale onse nawonso akupereka moni.

22Ambuye akhale ndi mzimu wako. Chisomo chikhale ndi inu nonse.

Knijga O Kristu

2 Timoteju 4:1-22

1Zaklinjem te pred Bogom i pred Kristom Isusom koji će doći suditi žive i mrtve, zaklinjem te njegovim dolaskom i njegovim kraljevstvom: 2uporno propovijedaj Božju riječ bila za to prigoda ili ne. Upozoravaj ljude na grijeh, strogo ih kori, ali ih i hrabri strpljivo ih poučavajući.

3Jer doći će vrijeme kad ljudi više neće htjeti slušati zdravo učenje. Povodit će se za vlastitim željama te sebi naći mnoštvo učitelja koji će im govoriti ono što će goditi njihovim ušima. 4Odvraćat će uho od istine te ići za bajkama.

5Ali ti budi u svemu trijezan. Podnesi patnje, propovijedaj Radosnu vijest. Ispuni u potpunosti dužnost koju ti je Bog dao.

Pavlove posljednje riječi

6A ja se već prinosim za žrtvu ljevanicu. Približio se trenutak moje smrti. 7Dobro sam se borio za svojega Gospodina, istrčao sam trku i ostao mu vjeran. 8Pripravljen mi je vijenac pravednosti koji će mi Gospodin, pravedni sudac, dati na dan svojega dolaska. Dat će ga svima koji s ljubavlju iščekuju njegov slavni dolazak.

9Požuri se što brže doći k meni. 10Dema me je zbog ljubavi prema ovome svijetu ostavio i otišao u Solun. Krescencije je otišao u Galaciju, a Tit u Dalmaciju. 11Sa mnom je još samo Luka. Povedi sa sobom Marka kad dođeš jer mi je koristan za služenje. 12Tihika sam poslao u Efez. 13Donesi mi, kad dođeš, kabanicu koju sam ostavio u Troadi kod Karpa. Donesi i knjige, osobito pergamene.

14Kovač Aleksandar mi je nanio mnogo zla. Gospodin će mu platiti prema njegovim djelima. 15I ti ga se čuvaj jer se jako protivio našemu propovijedanju.

16Kad su me prvi put izveli pred sud, nitko nije bio uz mene. Svi su me napustili. Neka im Bog to ne uračuna u krivnju! 17Ali Gospodin je bio sa mnom i dao mi je snage da propovijedam Radosnu vijest u svoj punini, da ju čuju svi pogani. Izbavio me iz lavljih ralja. 18Gospodin će me izbaviti od svakoga zlog napada i sačuvati me za svoje nebesko kraljevstvo. Neka mu je slava uvijeke. Amen.

Posljednji pozdravi

19Pozdravi Prisku i Akvilu te Oneziforove ukućane. 20Erast je ostao u Korintu, a Trofima sam bolesnoga u Miletu ostavio.

21Požuri da stigneš ovamo prije zime. Pozdravljaju te Eubul, Pudencije, Lino, Klaudija i sva braća i sestre.

22Neka Gospodin bude s tvojim duhom. Milost s vama!