2 Mafumu 1 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Mafumu 1:1-18

Yehova Alanga Ahaziya

1Atamwalira Ahabu, Mowabu anawukira Israeli. 2Ndipo Ahaziya anagwa kuchokera pa khonde la chipinda chake chammwamba ku Samariya, ndipo anavulala kwambiri. Choncho iye anatuma amithenga nawawuza kuti, “Pitani mukafunse kwa Baala-zebubu, mulungu wa ku Ekroni, ngati ndichire matendawa.”

3Koma mngelo wa Yehova anawuza Eliya wa ku Tisibe kuti, “Nyamuka, pita ukakumane ndi amithenga a mfumu ya ku Samariya ndipo ukawafunse kuti, ‘Kodi popeza kulibe Mulungu ku Israeli, nʼchifukwa chake inu mukupita kukafunsa nzeru kwa Baala-zebubu, mulungu wa ku Ekroni?’ 4Tsono Yehova akuti, ‘Iweyo sudzadzuka pa bedi wagonapo. Udzafa ndithu!’ ” Ndipo Eliya ananyamuka.

5Amithenga aja atabwerera kwa mfumu, mfumuyo inawafunsa kuti, “Chifukwa chiyani mwabwerera?”

6Iwo anayankha kuti, “Munthu wina anabwera kudzakumana nafe, ndipo anatiwuza kuti, bwererani kwa mfumu imene inakutumani ndipo mukayiwuze kuti, ‘Yehova akuti, kodi popeza kulibe Mulungu ku Israeli, nʼchifukwa chake mukupita kukafunsa nzeru kwa Baala-zebubu, mulungu wa ku Ekroni? Tsono sudzadzuka pa bedi wagonapo. Udzafa ndithu!’ ”

7Mfumu inafunsa amithengawo kuti, “Kodi munthu amene anabwera kudzakumana nanuyo ndi kukuwuzani zimenezi amaoneka bwanji?”

8Iwo anayankha kuti, “Munthuyo anavala zovala zaubweya ndi lamba wachikopa mʼchiwuno mwake.”

Mfumu inati, “Munthu ameneyo ndi Eliya wa ku Tisibe.”

9Pamenepo mfumu inatuma mtsogoleri wa ankhondo ndi anthu ake makumi asanu kwa Eliya. Mtsogoleriyo anapita kwa Eliya, amene anali atakhala pamwamba pa phiri, ndipo anati, “Munthu wa Mulungu, mfumu ikuti, ‘Tsikani!’ ”

10Eliya anayankha mtsogoleriyo kuti, “Ngati ndine munthu wa Mulungu, moto utsike kuchokera kumwamba, ukupsereze iwe pamodzi ndi anthu makumi asanu akowo!” Pomwepo moto unatsikadi kuchokera kumwamba ndipo unapsereza mtsogoleriyo pamodzi ndi anthu akewo.

11Zitachitika izi, mfumu inatumanso mtsogoleri wina pamodzi ndi asilikali ake makumi asanu. Mtsogoleriyo anati kwa Eliya, “Munthu wa Mulungu, zimene mfumu ikunena ndi izi, ‘Tsikani msangamsanga!’ ”

12Eliya anayankha kuti, “Ngati ndine munthu wa Mulungu, moto utsike kuchokera kumwamba, ukupsereze iwe pamodzi ndi anthu ako makumi asanuwo!” Pomwepo moto unatsikadi kuchokera kumwamba ndipo unapsereza mtsogoleriyo pamodzi ndi anthu akewo.

13Ndipo mfumu inatumanso mtsogoleri wachitatu pamodzi ndi asilikali ake makumi asanu. Mtsogoleri wachitatuyu anakwera pa phiripo ndi kugwada pamaso pa Eliya. Iye anayankhula mopemba kuti, “Munthu wa Mulungu, chonde musandiwononge ineyo pamodzi ndi atumiki makumi asanu anuwa! 14Taonani, moto unatsika kuchokera kumwamba ndi kupsereza atsogoleri awiri pamodzi ndi anthu awo onse. Koma tsopano musawononge moyo wanga!”

15Mngelo wa Yehova anati kwa Eliya, “Pita naye, usamuope.” Choncho Eliya ananyamuka natsika naye limodzi kupita kwa mfumu.

16Eliya anawuza mfumu kuti, “Yehova akuti, ‘Chifukwa chiyani munatumiza amithenga kwa Baala-zebubu, mulungu wa ku Ekroni, kukafunsa ngati muti muchire? Kodi mu Israeli mulibe Mulungu woti nʼkukuyankhani funso lanu? Choncho, popeza mwachita izi, simudzadzuka pamene mwagonapo; mudzafa ndithu.’ ” 17Motero Ahaziya anafadi, monga mwa mawu a Yehova amene Eliya anayankhula.

Tsono popeza Ahaziya analibe mwana, Yoramu analowa ufumu mʼmalo mwake mʼchaka chachiwiri cha Yehoramu mwana wa Yehosafati mfumu ya ku Yuda. 18Ntchito zina zonse zimene Ahaziya anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a ku Israeli?

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

列王紀下 1:1-18

耶和華責備亞哈謝

1亞哈死後,摩押背叛以色列2一天,亞哈謝撒瑪利亞王宮的樓臺上掉下來,受了傷,就派使者去求問以革倫的神明巴力·西蔔,看自己能否痊癒。 3耶和華的天使對提斯比以利亞說:「你去截住撒瑪利亞王的使者,對他們說,『你們為什麼去求問以革倫的神明巴力·西蔔?難道以色列沒有上帝嗎?』 4因此耶和華說,『亞哈謝再也不能下床了,他必定死。』」以利亞就去了。

5以利亞將天使的話告訴王的使者後,他們便回去見王。王問他們:「你們為什麼這麼快就回來了?」 6他們答道:「有一個人在路上截住我們,要我們回來告訴你,耶和華對你說,『你差人去求問以革倫的神明巴力·西蔔,是因為以色列沒有上帝嗎?因此,你再也不能下床了,你必定死。』」 7王又問他們:「在路上截住你們、對你們說這些話的,是什麼樣的人?」 8他們答道:「那人身穿毛皮衣服,腰束皮帶。」王說:「他是提斯比以利亞。」

9於是,王派一個五十夫長率領五十人去找以利亞。那時,以利亞正坐在山頂上。五十夫長到了那裡,對他說:「上帝的僕人啊,王命令你下來。」 10以利亞說:「我若是上帝的僕人,願火從天降下燒死你和你的五十個部下。」火立刻從天降下,燒死了五十夫長和他的五十個部下。 11亞哈謝王又派一個五十夫長率領五十人去以利亞那裡,五十夫長對以利亞說:「上帝的僕人啊,王命令你馬上下來。」 12以利亞說:「我若是上帝的僕人,願火從天降下,燒死你和你的五十個部下。」上帝的火從天降下,燒死了五十夫長和他的五十個部下。

13王再次派一個五十夫長率領五十人前去。五十夫長上去,雙膝跪在以利亞面前,哀求道:「上帝的僕人啊,求你饒了我和你的五十名僕人的性命。 14前兩個五十夫長和他們的部下都被天上降下的火燒死了,現在求你饒我一命!」 15耶和華的天使對以利亞說:「不要害怕,跟他去吧!」以利亞就起來跟他去見王。 16以利亞對王說:「耶和華說,『你差人去求問以革倫的神明巴力·西蔔,是因為以色列沒有上帝可以求問嗎?因此,你再也不能下床了,你必定死。』」

17亞哈謝果然死了,正如耶和華藉以利亞所說的。他沒有兒子,他兄弟約蘭繼位,那年是猶大約沙法的兒子約蘭執政第二年。 18亞哈謝其他的事都記在以色列的列王史上。