2 Akorinto 12 – CCL & SZ-PL

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Akorinto 12:1-21

Masomphenya a Paulo ndi Minga ya Mʼthupi Mwake

1Ndiyenera kupitiriza kudzitamandira. Ngakhale palibe choti ndipindule, ndipitiriza kufotokoza za masomphenya ndi mavumbulutso ochokera kwa Ambuye. 2Ndikudziwa munthu mwa Khristu amene zaka khumi ndi zinayi zapitazo anatengedwa kupita kumwamba kwachitatu. Sindikudziwa ngati zinachitika ali mʼthupi kapena ayi, zimenezo akudziwa ndi Mulungu. 3Ndipo ndikumudziwa munthu ameneyu. Sindikudziwa ngati zinachitika mʼthupi kapena ayi, zimenezo akudziwa ndi Mulungu. 4Munthuyu anatengedwa kupita ku paradizo. Ndipo anamva zinthu zosatheka kuneneka, zinthu zimene munthu saloledwa kunena. 5Ndidzatamanda za munthu ngati ameneyu, koma sindidzadzitamandira ine mwini kupatula za kufowoka kwanga. 6Ngakhale nditafuna kudzitamandira, sindingakhale chitsiru, chifukwa ndikunena zoona. Koma ndimapewa kuti pasapezeke munthu wondiganizira moposera chimene ndili chifukwa cha zimene ndimachita kapena kuyankhula, 7kapena chifukwa cha mavumbulutso aakulu kuposa awa. Choncho, kuti ndisadzitukumule, ndinayikidwa minga mʼthupi langa, wamthenga wa Satana, kuti adzindizunza. 8Katatu konse ndinapempha Ambuye kuti andichotsere. 9Koma anandiwuza kuti, “Chisomo changa ndi chokukwanira, pakuti mphamvu zanga zimaoneka kwathunthu mwa munthu wofowoka.” Choncho ndidzadzitamandira mokondwera chifukwa cha zofowoka zanga, kuti mʼkutero mphamvu ya Khristu ikhale pa ine. 10Tsono, chifukwa cha Khristu, ndimakondwera pamene ndili wofowoka, pamene akundinyoza, pamene ndikumva zowawa, ndi pamene akundizunza ndi kundisautsa. Pakuti pamene ndili wofowoka ndiye kuti ndili wamphamvu.

Paulo Akhudzidwa ndi Akorinto

11Ndadzisandutsa wopusa, koma inu mwandichititsa zimenezi. Ndinu amene munayenera kundichitira umboni. Ngakhale kuti sindine kanthu, koma sindine wochepetsetsa kwa “atumwi apamwamba” aja. 12Ndinapirira pokuonetserani zizindikiro za mtumwi weniweni, pochita pakati panu zizindikiro, zodabwitsa ndi ntchito zamphamvu. 13Kodi inu munaoneka ochepa motani ku mipingo ina, kupatula kuti sindinali cholemetsa kwa inu? Mundikhululukire cholakwa chimenechi!

14Ndakonzeka tsopano kudzakuyenderani kachitatu, ndipo sindidzakhala cholemetsa kwa inu chifukwa ndikungofuna inuyo osati zinthu zanu. Pakuti ana sasamalira makolo koma makolo ndiwo asamalira ana. 15Motero ndidzakondwera kukupatsani zanga zonse zimene ndili nazo ndi kudziperekanso ine mwini chifukwa cha inu. Kodi ine ndikamakukondani kwambiri chotere, inuyo mudzandikonda pangʼono? 16Ena mwa inu amavomereza kuti sindinali cholemetsa. Komabe ena amaganiza kuti ndine wochenjera, ndipo ndinakuchenjererani. 17Kodi ndinakudyerani masuku pamutu kudzera mwa wina aliyense amene ndinamutumiza kwa inu? 18Ndinamupempha Tito kuti abwere kwanuko ndipo ndinamutumiza pamodzi ndi mʼbale wathu. Kodi kapena Tito anakudyerani masuku pamutu? Kodi iye ndi ine sitinachite zinthu mofanana ndi Mzimu mmodzi yemweyo?

19Kodi mukuyesa kuti nthawi yonseyi takhala tikudzitchinjiriza tokha? Takhala tikuyankhula pamaso pa Mulungu monga anthu amene ali mwa Khristu; ndipo abwenzi okondedwa, chilichonse chimene timachita ndi chofuna kukulimbikitsani. 20Pakuti ndikuona kuti pamene ndibwera sindidzakupezani monga mmene ndikufunira kuti muzikhalira, ndipo simungadzandione monga mmene mukufunira kundionera. Ndikuopa kuti pangadzakhale mkangano, nsanje, kupserana mitima, kugawikana, ugogodi, miseche, kudzitukumula ndi chisokonezo. 21Ndikuopa kuti pamene ndidzabwerenso, Mulungu adzandichepetsa pamaso panu, ndipo ndidzamva chisoni ndi ambiri amene anachimwa kale ndipo sanalape zonyansa, zachigololo ndi zilakolako zoyipa zimene anachita.

Słowo Życia

2 Koryntian 12:1-21

Widzenie Pawła i jego cierń

1Przechwalanie się nie ma sensu, ale powiem wam jeszcze o widzeniach i objawieniach otrzymanych od Pana. 2Znam pewnego człowieka, wierzącego Chrystusowi, który czternaście lat temu został zabrany aż do trzeciego nieba. Nie wiem, czy fizycznie, czy tylko duchowo—to wie tylko Bóg. 3-4I znalazł się w raju—też nie wiem, czy było tam jego ciało, czy tylko duch; o tym wie jedynie Bóg. Będąc tam, człowiek ten usłyszał słowa tak zadziwiające, że nie wolno mu nawet o tym mówić. 5Z takiego przeżycia mógłbym być dumny, ale nie z mojej osoby! Chyba że z moich słabości… 6Jeśli więc zechcę się czymś szczycić, wcale nie będę szalony—przecież powiem tylko prawdę. Nie będę jednak tego robił, aby na tej podstawie nie uznano mnie za kogoś wielkiego. Wolałbym, aby ludzie oceniali mnie na podstawie tego, co widzą w moim życiu i słyszą z moich ust 7—nawet jeśli doznałem niezwykłych objawień.

Abym z ich powodu nie popadł w pychę, w moje ciało wbity został cierń. Jest on jakby wysłannikiem szatana, który mnie policzkuje i upokarza. 8Trzy razy prosiłem Pana, aby mnie od tego uwolnił. 9On jednak odpowiadał: „Ciesz się z tego, że doświadczyłeś mojej łaski. Moja moc staje się najbardziej widoczna wtedy, gdy jesteś słaby”. Dlatego najchętniej będę się szczycił swoją słabością—aby objawiała się we mnie moc Chrystusa. 10Cieszę się więc z mojej bezsilności, z obelg, z cierpień, prześladowań i trudności, które spotykają mnie z powodu posłuszeństwa Jezusowi. Gdy jestem bezsilny, wtedy bowiem jestem naprawdę mocny.

Troska Pawła o Koryntian

11Sprowokowaliście mnie, abym zachował się jak szaleniec. A to wy przecież powinniście mnie chwalić! Niczym bowiem nie ustępuję tym „superapostołom”, chociaż w rzeczywistości nic nie znaczę. 12Sami przecież doświadczyliście dowodów mojego apostolstwa—ogromnej wytrwałości, cudownych znaków i przejawów mocy Bożej. 13Chyba tylko pod tym względem jesteście gorsi od innych kościołów, że nie byłem dla was finansowym obciążeniem. Wybaczcie mi to uchybienie!

Zapowiedź następnych odwiedzin

14Już po raz trzeci wybieram się do was—i tym razem również nic nie będę was kosztować. Nie zależy mi bowiem na sobie samym, ale na was! Przecież to nie dzieci utrzymują rodziców, ale rodzice dzieci. 15Z ogromną przyjemnością będę więc was wspierał—a nawet samego siebie poświęcę dla dobra waszych dusz. Czy jednak okazując wam coraz więcej miłości, będę przez was coraz mniej kochany?

16Być może sądzicie, że chociaż nie byłem dla was finansowym ciężarem, to i tak w jakiś sposób sprytnie was wykorzystałem. 17A może wykorzystał was ktoś wysłany przeze mnie? 18Posłałem do was Tytusa i jeszcze jednego wierzącego. Nie powiecie chyba przecież, że to oni was oszukali? Czy nie przejawialiśmy—oni i my—tej samej postawy? Czy nie postępowaliśmy wśród was tak samo?

19Od dawna uważacie, że chcemy się przed wami bronić. Stojąc przed obliczem Boga i Chrystusa, zapewniamy was jednak, że wszystko, co czynimy, robimy wyłącznie dla waszego dobra. 20Mimo to, obawiam się, że gdy do was przybędę, nie spodoba mi się to, co zastanę. Wam zaś może nie spodobać się moja reakcja na to. Boję się, że znowu zobaczę wśród was kłótnie, zazdrość, gniew, rywalizację, pomówienia, plotki, zarozumialstwo oraz podziały. 21Obawiam się, że—widząc coś takiego—znów zostanę w waszej obecności upokorzony przez Boga i zasmucę się z powodu tych, którzy wcześniej żyli w grzechu i wciąż jeszcze nie porzucili rozwiązłości seksualnej.