2 Akorinto 11 – CCL & SZ-PL

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Akorinto 11:1-33

Paulo ndi Atumwi Onyenga

1Ndikukhulupirira kuti mupirira nako pangʼono kupusa kwanga. Chonde tandipirirani! 2Nsanje imene ndimakuchitirani ndi yofanana ndi ya Mulungu. Ndinakulonjezani mwamuna mmodzi yekha, mwamunayo ndiye Khristu, kuti ndidzakuperekeni inuyo kwa Iyeyo monga namwali wangwiro. 3Koma ndikuopa kuti monga Hava ananyengedwa ndi kuchenjera kwa njoka, mitima yanunso ingasocheretsedwe kuleka nʼkudzipereka moona mtima ndi modzipereka kwenikweni kwa Khristu. 4Pakuti ngati wina abwera kwa inu nalalikira Yesu wina wosiyana ndi Yesu amene tinamulalikira, kapena ngati mulandira mzimu wina wosiyana ndi Mzimu amene munalandira, kapena uthenga wabwino wina wosiyana ndi umene munawuvomereza, inuyo mumangolandira mosavuta.

5Komatu sindikuganiza kuti ndine wotsika kwambiri kwa “atumwi apamwamba.” 6Mwina ndikhoza kukhala wosaphunzitsidwa kayankhulidwe, koma ndili ndi chidziwitso. Izi tinakufotokozerani momveka bwinobwino. 7Kodi linali tchimo kwa ine kudzichepetsa nʼcholinga chakuti ndikukwezeni pamene ndinkalalikira Uthenga Wabwino wa Mulungu kwa inu mwaulere? 8Ndinkalanda mipingo ina pomalandira thandizo kwa iwo kuti ndikutumikireni. 9Ndipo pamene ndinali pakati panu, nditasowa kanthu, sindinalemetse munthu aliyense, pakuti abale ena amene anachokera ku Makedoniya anandipatsa zonse zimene ndinkazisowa. Ndayesetsa kuti ndisakhale cholemetsa kwa inu mʼnjira ina iliyonse, ndipo ndidzapitiriza kutero. 10Kunena moona mtima molingana ndi chilungamo cha Khristu chimene chili mwa ine, palibe amene angandiletse kudzitamandira mʼzigawo za ku Akaya. 11Nʼchifukwa chiyani ndikutero? Kodi nʼchifukwa choti sindikukondani? Mulungu akudziwa kuti ndimakukondani!

12Ndipo ndipitiriza kuchita zomwe ndikuchitazi nʼcholinga chakuti ndisapereke mpata kwa amene akufuna kupezera mwayi woti afanane nafe pa zinthu zimene iwowo amadzitamandira. 13Pakuti anthu oterewa ndi atumwi onama, antchito achinyengo, odzizimbayitsa ngati atumwi a Khristu. 14Sizododometsa zimenezi, pakuti Satana mwini amadzizimbayitsa kuoneka ngati mngelo wowunikira anthu. 15Nʼzosadabwitsa tsono ngati atumiki ake akudzizimbayitsa ngati otumikira chilungamo. Matsiriziro awo adzalandira zoyenerana ndi ntchito zawo.

Paulo Anyadira Mazunzo Ake

16Ndibwereze kunena kuti, wina aliyense asandiyese chitsiru. Koma ngati mutero, mundilandire monga mmene mukhoza kulandirira chitsiru, kuti ndinyadirepo pangʼono. 17Kudzinyadira kwangaku, sindikuyankhula monga mmene Ambuye akufunira koma ngati chitsiru. 18Popeza ambiri akudzitama monga dziko lapansi limachitira, inenso ndidzitamanso. 19Inu mumalolera kukhala ndi zitsiru mokondwera chifukwa mumati ndinu anzeru! 20Kunena zoona mumangololera aliyense; amene amakusandutsani akapolo, kapena amene amakudyerani masuku pamutu, kapena amene amakupezererani, kapena amene amadzitukumula, kapena amene amakumenyani khofi. 21Ndikuvomera mwamanyazi kuti ife sitinali olimba mtima kuti nʼkuchita zinthu zimenezi.

Ndikuyankhula ngati chitsiru kuti chimene wina aliyense akhoza kudzitama nacho, Inenso ndikhoza kudzitama nachonso. 22Kodi iwo ndi Ahebri? Inenso ndine Mhebri. Kodi iwo ndi Aisraeli? Inenso ndine Mwisraeli. Kodi iwo ndi zidzukulu za Abrahamu? Inenso ndine mdzukulu wa Abrahamu. 23Kodi iwo ndi atumiki a Khristu? Ndikuyankhula ngati wamisala. Ine ndine woposa iwowo. Ndagwira ntchito kwambiri kupambana iwo, ndakhala ndikuyikidwa mʼndende kawirikawiri, ndakwapulidwapo kwambiri, kawirikawiri ndinali pafupi kufa. 24Andikwapulapo kasanu zikoti zija za Ayuda, makumi anayi kuchotsapo chimodzi. 25Katatu anandimenya ndi ndodo. Kamodzi anandigendapo miyala. Katatu sitima yathu ya panyanja inasweka, ndipo ndinakhala usiku ndi usana ndi kuyandama pa nyanja. 26Ndakhala ndikuyenda maulendo ataliatali. Moyo wanga wakhala ukukumana ndi zoopsa pa mitsinje, zoopsa za achifwamba, zoopsa zochokera kwa abale anga Ayuda, zoopsa zochokera kwa anthu akunja. Ndinakumana ndi zoopsa mʼmizinda, mʼmidzi, pa nyanja, ndi pakati pa abale onyenga. 27Ndakhala ndikugwira ntchito molimbika ndipo kawirikawiri ndakhala ndikuchezera usiku wonse osagona. Ndakhala ndikumva njala ndi ludzu ndipo kawirikawiri ndakhala wopanda chakudya. Ndakhala ndi kuzizidwa ndi wosowa zovala. 28Kuwonjezera pa zonsezi, tsiku ndi tsiku ndimakhala pa chipsinjo cha nkhawa ya mipingo yonse. 29Ndani ali wofowoka, ine wosakhala naye mʼkufowoka kwakeko? Ndani amene mnzake amuchimwitsa, ine wosavutika mu mtima?

30Ngati nʼkoyenera kudzitamandira, ndidzadzitamandira pa zinthu zimene zimaonetsa kufowoka kwanga. 31Mulungu, Atate a Ambuye Yesu, amene tiyenera kumutamanda nthawi zonse, akudziwa kuti sindikunama. 32Ku Damasiko, bwanamkubwa woyimira Mfumu Areta, anayika alonda kuzungulira mzinda wonse kuti andigwire. 33Koma abale anandiyika mʼdengu nanditsitsira pa chipupa kudzera pa zenera la mpandawo, motero ndinapulumuka mʼmanja mwake.

Słowo Życia

2 Koryntian 11:1-33

Paweł i fałszywi apostołowie

1Znieście trochę szaleństwa z mojej strony, proszę—wiem, że to zrobicie. 2Jestem o was zazdrosny—tak jak Bóg. To ja „zaręczyłem” was z Chrystusem i chcę postawić was przed Nim jako nieskazitelnie czystą narzeczoną. 3Obawiam się jednak, że ktoś odciąga was od pełnego poddania się Panu—podobnie jak przebiegły wąż zwiódł w raju Ewę. 4Przychodzą do was bowiem ludzie, którzy mówią o Jezusie, nie jest to jednak Jezus, o którym my wam opowiadaliśmy. Przyjmujecie też jakiegoś ducha, nie jest to jednak Duch Święty, którego otrzymaliście od Boga. Chętnie słuchacie również dobrej nowiny, ale nie jest to ta sama nowina, którą słyszeliście od nas. 5Nie uważam jednak, aby ci „superapostołowie” byli lepsi ode mnie. 6Może i jestem kiepskim mówcą, ale przynajmniej wiem, o czym mówię. Wy zaś doskonale wiecie, że jestem wobec was zupełnie szczery.

7Czy postąpiłem źle, gdy za darmo—poświęcając siebie, a dbając tylko o wasze dobro—głosiłem wam dobrą nowinę od Boga? 8„Wykorzystywałem” inne kościoły, aby mieć pieniądze na pracę wśród was. 9Będąc z wami, miałem finansowe trudności, ale nie byłem obciążeniem dla kogokolwiek z was. Pomogli mi bowiem wierzący z Macedonii, którzy do mnie przyszli. Nigdy nie byłem więc dla was ciężarem—i nigdy nie będę! 10Tak jak pewne jest to, że mówię ludziom prawdę o Chrystusie, tak pewne jest to, że nikt w całej Achai nie znajdzie powodu, do odebrania mi satysfakcji z tego, że bezinteresownie służyłem Panu. 11Czy to znaczy, że was nie kocham? O nie! Bóg dobrze zna moją miłość do was!

12Pracuję dla Pana bezinteresownie. I nadal będę to robił! W ten sposób wytrącam argumenty z ręki tych, którzy przechwalają się, twierdząc, że pracują dokładnie tak, jak my. 13W rzeczywistości są jednak fałszywymi apostołami i nieuczciwymi ludźmi, podszywającymi się tylko pod apostołów Chrystusa. 14Nie powinno was to dziwić. Skoro sam szatan podszywa się pod anioła światłości, 15również jego wysłannicy udają, że czynią to, co prawe. W końcu jednak spotka ich kara, na jaką zasłużyli.

Paweł dumny z cierpień

16Przypominam: Nie traktujcie mnie jak szaleńca. A nawet jeśli uważacie mnie za takiego, mimo wszystko posłuchajcie, gdy będę się trochę przechwalał. 17Te moje słowa i myśli nie są od Pana—są to słowa człowieka, który przez chwilę zdobył się na szaleństwo. 18Skoro inni przechwalają się swoimi dokonaniami, ja również będę się chwalił. 19Przecież jesteście mądrzy, a mimo to chętnie słuchacie głupców. 20Nie razi was to, że ktoś was zniewala, wykorzystuje, zabiera to, co wasze, traktuje was z góry, a nawet znieważa i policzkuje. 21Tak, muszę przyznać, że jesteśmy słabi, bo nie potrafimy zachowywać się jak ci, którzy tak z wami postępują…

Skoro jednak oni się przechwalają, to również ja—zdobywszy się na to szaleństwo—będę to czynił. 22Są Hebrajczykami? Ja także. Izraelitami? Ja również. Są potomkami Abrahama? Ja też. 23Służą Chrystusowi? Odpowiem jak szalony: Ja też i to o wiele bardziej! Z powodu Chrystusa znosiłem bowiem o wiele więcej trudności niż oni. Za głoszenie dobrej nowiny byłem aresztowany i bity. Wielokrotnie też narażałem życie. 24Żydowscy przywódcy pięć razy wymierzyli mi karę trzydziestu dziewięciu batów. 25Trzykrotnie zostałem pobity, raz obrzucony kamieniami, trzy razy przeżyłem katastrofy morskie, z czego raz całą dobę spędziłem na morzu jako rozbitek. 26Odbyłem wiele uciążliwych podróży, byłem narażony na niebezpieczeństwa na rzekach, niebezpieczeństwa ze strony bandytów a także moich własnych rodaków oraz pogan. Niebezpieczeństwa czyhały na mnie także w miastach, na pustkowiu i na morzu. Zagrożenie stanowili również ludzie podszywający się pod wierzących. 27Doświadczyłem też wielu innych rzeczy: ciężkiej pracy, zmęczenia, bezsennych nocy, głodu i pragnienia. Często chodziłem z pustym żołądkiem i drżałem z zimna, nie miałem bowiem ciepłych ubrań. 28Poza tym wszystkim, zawsze towarzyszy mi troska o kościoły. 29Jeśli ktoś opada z sił, ja również słabnę. Jeśli ktoś upada, płonę ze wstydu.

30Jeżeli więc już naprawdę mam się czymś chwalić, to niech to będą moje słabości. 31Bóg—Ojciec Jezusa Chrystusa, naszego Pana—któremu należy się wieczna chwała, wie, że nie kłamię. 32W Damaszku, gubernator podległy królowi Aretasowi postawił straże w bramach miasta i kazał mnie aresztować, 33lecz udało mi się uciec—spuszczono mnie bowiem w koszu przez otwór w murze otaczającym miasto.