2 Akorinto 13 – CCL & SZ-PL

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Akorinto 13:1-14

Mawu Otsiriza ndi Ochenjeza

1Uwu ndi ulendo wachitatu ndikubwera kudzakuyenderani. “Nkhani itsimikizike ndi umboni wa anthu awiri kapena atatu.” 2Ndinakuchenjezani kale pamene ndinali nanu ulendo wachiwiri uja. Tsopano ndikubwereza ndisanafike. Ndikabweranso sindidzachitira chifundo amene anachimwa poyamba paja kapena wina aliyense amene anachimwa, 3popeza mufuna chitsimikizo chakuti Khristu akuyankhula kudzera mwa ine. Iye siwofowoka pofuna kuchita nanu koma ndi wamphamvu pakati panu. 4Pofuna kutsimikizira, anapachikidwa ali wofowoka koma ali ndi moyo mwamphamvu ya Mulungu. Chomwechonso, ife ndife ofowoka mwa Iye, koma tidzakhala ndi moyo pamodzi naye ndi mphamvu ya Mulungu, potumikira pakati panu.

5Tadzisanthulani nokha kuti muone ngati muli mʼchikhulupiriro; dziyeseni nokha. Kodi simuzindikira kuti Khristu Yesu ali mwa inu, ngati si choncho mwalephera mayesowa? 6Ndipo ndikhulupirira kuti mudzazindikira kuti ife sitinalephere mayesowo. 7Tsopano tikupemphera kwa Mulungu kuti musadzachite kanthu kena kalikonse kolakwa. Osati chifukwa choti anthu aone kuti ife tapambana mayesowo koma kuti mudzachite zokhoza ngakhale anthu atamationa ngati olephera. 8Pakuti sitingachite chilichonse chotsutsana ndi choonadi, koma chokhacho chovomerezana ndi choonadi. 9Ife timasangalala kuti pamene tafowoka, inu muli amphamvu; ndipo pemphero lathu ndi lakuti mukhale angwiro. 10Nʼchifukwa chake ndimalemba zinthu zoterezi pamene ndili kutali, kuti ndikabwera ndisadzagwiritse ntchito ulamuliro wanga mokalipa, uwu ndi ulamuliro umene Ambuye anandipatsa kuti ndikukuzeni inu osati kukuwonongani.

Malonje Otsiriza

11Potsiriza abale, ndikuti tsalani bwino. Yesetsani kukhala angwiro, mvetsetsani pempho langa, khalani a mtima umodzi, khalani mwamtendere. Ndipo Mulungu wachikondi ndi mtendere adzakhala nanu.

12Lonjeranani ndi mpsopsono wachiyero. 13Anthu onse a Mulungu akupereka moni.

14Chisomo cha Ambuye Yesu Khristu, ndi chikondi cha Mulungu, ndi chiyanjano cha Mzimu Woyera zikhale ndi inu nonse.

Słowo Życia

2 Koryntian 13:1-13

Ostatnie ostrzeżenia

1Teraz, gdy wybieram się do was po raz trzeci, zapowiadam, że osądzę winnych na podstawie zgodnych oskarżeń dwóch lub trzech świadków. 2Podczas mojej ostatniej wizyty u was ostrzegałem tych, którzy grzeszą. Teraz ponownie ich ostrzegam, a także wszystkich innych: Tym razem nie będę łagodny!

3Domagacie się, żeby przemówił przeze mnie Chrystus? On nie jest wobec was bezradny, ale działa z całą mocą! 4Umarł na krzyżu jako słaby człowiek, ale teraz żyje dzięki mocy Boga. My również doświadczamy tej słabości, ale zobaczycie, że dzięki mocy Boga będziemy razem z Nim żyć!

Sprawdzajcie samych siebie

5Poddawajcie więc samych siebie próbie. Zadajcie sobie pytanie: „Czy moja wiara jest autentyczna i czy Jezus Chrystus jest obecny w moim życiu?”. Ufam, że przejdziecie ten test. 6Mam również nadzieję, iż dostrzeżecie Jezusa także w naszym życiu. 7Modlimy się do Boga, abyście nie mieli nic wspólnego ze złem. A nie czynimy tego po to, aby zdobyć dobrą opinię. Pragniemy raczej, aby wasze postępowanie było tak doskonałe, że na waszym tle my będziemy wyglądać jak słabeusze. 8Wszystko, co robimy, służy prawdzie, i nie czynimy niczego, co mogłoby jej zaszkodzić. 9Dlatego ogromnie cieszymy się, gdy jesteście mocni—choć sami już nie mamy sił. Modlimy się też o waszą duchową dojrzałość.

10Piszę o tym teraz w nadziei, że gdy do was przybędę, nie będę musiał być wobec was surowy. Pan przekazał mi bowiem władzę po to, aby wzmacniać wiarę innych wierzących, a nie rujnować ją.

Końcowe pozdrowienia

11Przyjaciele, kończąc ten list, życzę wam, abyście się radowali, dojrzewali duchowo, zachęcali się nawzajem, byli jednomyślni i żyli w zgodzie. Niech Bóg, który obdarza ludzi miłością i pokojem, będzie z wami!

12Wszyscy święci, którzy są ze mną, proszą o przekazanie wam ich pozdrowień. Przekażcie je sobie nawzajem!

13Niech Jezus, nasz Pan, obdarza was swoją łaską! Niech Bóg obdarza was swą miłością! A Duch Święty niech pomoże wam tworzyć wspólnotę z innymi wierzącymi!