1 Yohane 4 – CCL & NSP

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Yohane 4:1-21

Kuyesa Mizimu

1Anzanga okondedwa, musakhulupirire mzimu uliwonse, koma yesani mizimu ngati ikuchokera kwa Mulungu, chifukwa aneneri onama ambiri afalikira mʼdziko lapansi. 2Mungathe kuzindikira Mzimu wa Mulungu motere: Mzimu uliwonse umene umavomereza kuti Yesu Khristu anabwera mʼthupi, ndi wochokera kwa Mulungu, 3koma mzimu uliwonse umene suvomereza Yesu, siwochokera kwa Mulungu. Uwu ndi mzimu wa wokana Khristu umene munawumva kuti ukubwera ndipo ngakhale tsopano wabwera kale mʼdziko lapansi.

4Inu ana okondedwa, ndinu ochokera kwa Mulungu ndipo mwawagonjetsa aneneri onyengawa, chifukwa Iye amene ali mwa inu ndi wamkulu kuposa amene ali mʼdziko lapansi. 5Aneneri onyengawa ndi ochokera mʼdziko lapansi, nʼchifukwa chake amayankhula za dziko lapansi, ndipo dziko lapansi limawamvera. 6Ife ndi ochokera kwa Mulungu, ndipo aliyense amene amadziwa Mulungu amamvera zimene timayankhula. Koma aliyense amene sachokera kwa Mulungu samvera zimene timayankhula. Mmenemu ndiye mmene timasiyanitsira pakati pa mzimu wachoonadi ndi Mzimu wachinyengo.

Mulungu ndiye Chikondi

7Anzanga okondedwa, tiyeni tikondane wina ndi mnzake, pakuti chikondi chimachokera kwa Mulungu. Aliyense amene ali ndi chikondi ndi mwana wa Mulungu ndipo amadziwa Mulungu. 8Aliyense amene alibe chikondi sadziwa Mulungu, chifukwa Mulungu ndiye chikondi. 9Mmene Mulungu anaonetsera chikondi chake pakati pathu ndi umu: Iye anatumiza Mwana wake mmodzi yekha ku dziko lapansi kuti mwa Iyeyo tikhale ndi moyo. 10Chikondi ndi ichi: osati kuti ife ndife amene tinamukonda Mulungu, koma kuti Iyeyo ndiye amene anatikonda ndipo anatumiza Mwana wake kuti akhale nsembe yopepesera machimo athu. 11Anzanga okondedwa, popeza Mulungu anatikonda chotere, ifenso tiyenera kukondana wina ndi mnzake. 12Palibe amene anaonapo Mulungu, koma tikakondana wina ndi mnzake, ndiye kuti Mulungu amakhala mwa ife ndipo chikondi chake chafika pachimake penipeni mwa ife.

13Ife tikudziwa kuti timakhala mwa Iye ndipo Iyeyo amakhala mwa ife chifukwa anatipatsa Mzimu wake. 14Ndipo taona ndipo tikuchitira umboni, kuti Atate anatuma Mwana wake kuti akhale Mpulumutsi wa dziko lapansi. 15Ngati aliyense avomereza kuti Yesu ndi Mwana wa Mulungu, Mulungu amakhala mwa iye ndipo iyeyo amakhala mwa Mulungu. 16Tikudziwa ndipo timadalira chikondi chimene Mulungu ali nacho pa ife.

Mulungu ndiye chikondi. Aliyense amene amakhala moyo wachikondi, ali mwa Mulungu ndipo Mulungu amakhala mwa iye. 17Chikondi chafika pachimake penipeni pakati pathu, kotero kuti pa tsiku lachiweruzo tidzakhala olimba mtima chifukwa mʼdziko lapansi moyo wathu uli ngati wa Khristu. 18Mulibe mantha mʼchikondi. Koma chikondi ndi changwiro chimachotsa mantha, chifukwa mantha amabwera chifukwa choopa chilango. Munthu amene ali ndi mantha, chikondi chake sichangwiro.

19Ife timakonda Mulungu chifukwa ndiye anayamba kutikonda. 20Ngati wina anena kuti, “Ine ndimakonda Mulungu,” koma namadana ndi mʼbale wake ndi wabodza ameneyo. Pakuti aliyense amene sakonda mʼbale wake, amene akumuona, sangathenso kukonda Mulungu amene sanamuone. 21Ndipo Iye anatipatsa lamulo lakuti: Aliyense amene amakonda Mulungu ayenera kukondanso mʼbale wake.

New Serbian Translation

1. Јованова 4:1-21

Духове треба проверавати

1Вољени моји, не верујте сваком духу, него проверавајте духове долазе ли од Бога, јер је много лажних пророка изашло у свет. 2По овоме се познаје онај који има Божијег Духа: свако ко исповеда да је Исус Христос дошао у телу, долази од Бога, 3а сваки дух који не признаје Исуса не долази од Бога. Тај има духа антихристовог, за којега сте чули да ће доћи, и већ сада је у свету.

4Дечице, ви сте од Бога и већ сте надвладали такве. Наиме, моћнији је онај који је у вама, него онај који је у свету. 5Они су од света, па зато говоре оно што од света потиче, и свет их слуша. 6Али ми смо од Бога. Ко познаје Бога, нас слуша, а ко није од Бога, не слуша нас. По томе препознајемо Духа истине и духа заблуде.

Бог је љубав

7Вољени моји, волимо једни друге, јер љубав долази од Бога. Свако ко воли, од Бога је рођен и познаје Бога. 8Ко не воли, није познао Бога, јер Бог је љубав. 9Бог је показао своју љубав према нама тако што је послао у свет свога јединорођенога Сина да бисмо ми имали живот његовим посредством. 10Ово је љубав: нисмо ми заволели Бога, него је Бог заволео нас и послао свога Сина да буде жртва за опроштење наших греха. 11Вољени моји, ако нас је Бог толико заволео и ми смо дужни да волимо једни друге. 12Бога нико никада није видео, али ако волимо једни друге, Бог остаје у нама, те љубав његова у нама бива савршена.

13По овоме знамо да остајемо у њему и он у нама: дао нам је свога Духа. 14А ми смо видели да је Отац послао Сина да буде Спаситељ света. 15Ко исповеди да је Исус Син Божији, Бог остаје у њему и он у Богу. 16И ми смо упознали љубав коју Бог има према нама и поверовали у њу.

Бог је љубав и ко живи у љубави, Бог остаје у њему и он у Богу. 17Љубав је међу нама дошла до савршенства, да бисмо имали поуздање на Судњи дан. Јер, какав је он, такви смо и ми на овом свету. 18У љубави нема страха. Савршена љубав изгони страх, јер страх претпоставља казну. Ко год страхује, није дошао до савршенства у љубави.

19Ми волимо, јер је он први заволео нас. 20Ако неко каже: „Волим Бога!“, а мрзи свога брата, лажљивац је. Ко не воли свога брата којега види, не може волети ни Бога којега не види. 21Ову заповест имамо од њега: ко воли Бога, да воли и свога брата.