1 Yohane 5 – CCL & NSP

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Yohane 5:1-21

Chikhulupiriro mwa Mwana wa Mulungu

1Aliyense amene amakhulupirira kuti Yesu ndi Khristu, iyeyo ndi mwana wa Mulungu, ndipo aliyense amene amakonda Atate amakondanso Mwana wake. 2Chodziwira kuti timakonda ana a Mulungu nʼchakuti timakonda Mulungu ndi kusunga malamulo ake. 3Pakuti kukonda Mulungu ndiye kusunga malamulo ake. Ndipo malamulo ake siwolemetsa, 4chifukwa aliyense amene ndi mwana wa Mulungu amagonjetsa dziko lapansi. Chikhulupiriro chathu ndicho timagonjetsera dziko lapansi. 5Ndani amagonjetsa dziko lapansi? Yekhayo amene amakhulupirira kuti Yesu ndi Mwana wa Mulungu.

6Uyu ndiye anabwera mwa madzi ndi magazi, ndiye Yesu Khristu. Sanabwere mwa madzi okha, koma mwa madzi ndi magazi. Ndipo ndi Mzimu Woyera amene akuchitira umboni, chifukwa Mzimu Woyera ndi choonadi. 7Pakuti pali atatu amene amachitira umboni. 8Mzimu Woyera, madzi ndi magazi; ndipo atatu amavomerezana. 9Timalandira umboni wa anthu, koma umboni wa Mulungu ndi wopambana. Umboniwo ndi umene anachitira Mwana wake. 10Aliyense amene amakhulupirira Mwana wa Mulungu ali nawo umboniwu mu mtima mwake, koma aliyense amene sanakhulupirire Mulungu amayesa kuti Mulunguyo ndi wonama, chifukwa sanakhulupirire umboni umene Mulungu anachitira wa Mwana wake. 11Ndipo umboniwo ndi uwu: Mulungu anatipatsa moyo wosatha, ndipo moyowu uli mwa Mwana wake. 12Iye amene ali ndi Mwana ali ndi moyo, amene alibe Mwana wa Mulungu alibe moyo.

Mawu Otsiriza

13Ine ndikulemba zimenezi kwa inu, amene mwakhulupirira dzina la Mwana wa Mulungu kuti mudziwe kuti muli ndi moyo wosatha. 14Ife timalimba mtima tikamafika pamaso pa Mulungu, popeza kuti ngati tipempha kanthu kalikonse monga mwa chifuniro chake, amatimvera. 15Ndipo ngati tikudziwa kuti amatimvera, chilichonse chimene timapempha, tikudziwanso kuti tili nacho chimene tamupempha Iye.

16Ngati wina aona mʼbale wake akuchita tchimo losadzetsa imfa, apemphere ndipo Mulungu adzamupatsa moyo mʼbale wakeyo. Ndikunena za ochita tchimo losadzetsa imfa. Pali tchimo lodzetsa imfa. Ine sindikunena kuti apemphere ayi. 17Chilichonse chosalungama ndi tchimo ndipo pali tchimo losadzetsa imfa.

18Tikudziwa kuti aliyense amene ndi mwana wa Mulungu sachimwirachimwirabe. Yesu, Mwana wa Mulungu, amamusunga ndipo woyipa uja sangamukhudze. 19Tikudziwa kuti ndife ana a Mulungu ndi kuti dziko lonse lapansi lili pansi pa ulamuliro wa woyipayo. 20Tikudziwa kuti Mwana wa Mulungu anafika ndipo anatipatsa nzeru, kuti timudziwe Iye amene ali woona. Ndipo ife tili mwa Iye amene ndi woona, Mwana wake, Yesu Khristu. Iye ndi Mulungu woona ndi moyo wosatha.

21Ana okondedwa, dzisungeni bwino, osapembedza mafano.

New Serbian Translation

1. Јованова 5:1-21

Победоносна вера у Христа

1Свако ко верује да је Исус Христос, рођен је од Бога, и свако ко воли Оца, воли и оног који је рођен од њега. 2А да смо деца Божија, знамо по томе што волимо Бога и држимо се његових заповести. 3Љубав према Богу значи ово: држати његове заповести. Његове заповести нису тешке, 4јер сви који су рођени од Бога побеђују свет. А ово је средство наше победе: наша вера. 5Ко побеђује свет, ако не онај који верује да је Исус Син Божији?

6Он, Исус Христос, је онај који је дошао водом и крвљу. Не само водом, него водом и крвљу. А сам Дух сведочи о овоме, јер Дух је истина. 7Тако, имамо три сведока: 8Духа, воду и крв; а ово троје се слажу. 9Ако верујемо људском сведочанству, знајмо да је Божије сведочанство веће. Ово је Божије сведочанство којим је Бог потврдио свога Сина: 10ко верује у Сина Божијега има ово сведочанство у свом срцу, а ко не верује Богу, прави од њега лажљивца, јер није поверовао сведочанству којим је Бог потврдио свога Сина. 11Ово је сведочанство: Бог нам је дао живот вечни и овај живот је у његовом Сину. 12Ко има Сина има живот, а ко нема Сина Божијег, нема живота.

Вечни живот

13Ово сам написао вама који верујете у Сина Божијег, да знате да имате вечни живот. 14Ово је поуздање које имамо у њега: он нас слуша штогод да затражимо по његовој вољи. 15А ако знамо да нас слуша што год затражимо, онда знамо да већ имамо оно што смо тражили од њега.

Рођени од Бога не остаје у греху

16Ако неко види свога брата да чини грех који не води у смрт, нека моли за њега и Бог ће му дати живот. То је за оне који не чине смртни грех. Међутим, постоји грех који води у смрт. За такав грех не кажем да се моли. 17Свака је неправда грех, али постоји грех који не води у смрт.

18Знамо да свако ко је од Бога рођен не живи грешно, јер га онај који је рођен од Бога чува, и Зли га се не дотиче. 19Ми знамо да смо од Бога, а да је сав свет у власти Злога. 20Али знамо да је Син Божији дошао и дао нам разум да упознамо Истинитога. А ми смо у Истинитом – у његовом Сину Исусу Христу. Он је истински Бог и вечни живот.

21Дечице, чувајте се идола!