1 Mafumu 16 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Mafumu 16:1-34

1Ndipo Yehova anayankhula kudzera mwa Yehu mwana wa Hanani, mawu odzudzula Baasa kuti, 2“Ine ndinakukuza kuchokera pa fumbi ndipo ndinakupanga kuti ukhale mtsogoleri wa anthu anga Aisraeli, koma iwe wakhala ukuyenda mʼnjira za Yeroboamu ndi kuchimwitsa anthu anga Aisraeli naputa mkwiyo wanga chifukwa cha machimo awo. 3Taonani, Ine ndatsala pangʼono kuwononga Baasa pamodzi ndi nyumba yake, ndipo ndidzachitira nyumba yake zimene ndinachita pa nyumba ya Yeroboamu mwana wa Nebati. 4Agalu adzadya aliyense wa banja la Baasa amene adzafere mu mzinda, ndipo mbalame za mu mlengalenga zidzadya iwo amene adzafere kuthengo.”

5Tsono ntchito zina za Baasa ndi zamphamvu zake zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli? 6Baasa anamwalira nayikidwa mʼmanda amene anayikidwa makolo ake ku Tiriza. Ndipo Ela mwana wake anakhala mfumu mʼmalo mwake.

7Komatu Yehova anayankhula kwa Baasa pamodzi ndi banja lake lonse kudzera mwa mneneri Yehu mwana wa Hanani, chifukwa cha zoyipa zonse zimene iye anachita pamaso pa Yehova, kukwiyitsa Yehovayo nakhala ngati nyumba ya Yeroboamu ndiponso chifukwa anawonongeratu banja la Yeroboamu.

Ela Mfumu ya Israeli

8Mʼchaka cha 26 cha ufumu wa Asa mfumu ya Yuda, Ela mwana wa Baasa anakhala mfumu ya Israeli, ndipo analamulira ku Tiriza zaka ziwiri.

9Zimuri, mmodzi mwa akuluakulu ake, amene ankalamulira theka la magaleta ake, anamuchitira chiwembu. Nthawi imeneyi Ela anali ku Tiriza, akumwa koledzera nako mʼnyumba ya Ariza, munthu amene ankayangʼanira nyumba yaufumu ku Tiriza. 10Zimuri anadzalowa, namukantha ndi kumupha mʼchaka cha 27 cha Asa mfumu ya Yuda. Ndipo Zimuriyo anakhala mfumu mʼmalo mwake.

11Zimuri atangoyamba kulamulira, anapha banja lonse la Baasa. Sanasiyepo munthu wamwamuna ndi mmodzi yemwe, wachibale kapena bwenzi lake. 12Choncho Zimuri anawononga banja lonse la Baasa, molingana ndi mawu amene Yehova anayankhula motsutsa Baasa kudzera mwa mneneri Yehu, 13chifukwa cha machimo onse amene Baasa ndi mwana wake Ela anachita nachimwitsa Israeli, anakwiyitsa Yehova, Mulungu wa Israeli ndi mafano awo osapindulitsa.

14Tsono ntchito zina za Ela ndi zina zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?

Zimuri Mfumu ya Israeli

15Mʼchaka cha 27 cha Asa mfumu ya Yuda, Zimuri analamulira ku Tiriza masiku asanu ndi awiri. Gulu la ankhondo linali litamanga misasa pafupi ndi Gibetoni, mzinda wa Afilisti. 16Ankhondo amene anali ku misasa atamva kuti Zimuri wachita chiwembu ndi kupha mfumu, tsiku lomwelo ku misasako anasankha Omuri, mkulu wa ankhondo kukhala mfumu ya Israeli. 17Tsono Omuri ndi Aisraeli onse amene anali naye anachoka ku Gibetoni ndi kukazinga Mzinda wa Tiriza. 18Zimuri ataona kuti mzinda walandidwa, anathawira ku nsanja ya nyumba ya mfumu ndipo anatentha nyumbayo iye ali momwemo. Kotero iyeyo anafa, 19chifukwa cha machimo amene iye anachita, kuchita zoyipa pamaso pa Yehova ndi kuyenda mʼnjira za Yeroboamu, nachimwitsa nazo Aisraeli.

20Tsono ntchito zina za Zimuri ndi chiwembu chake chimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?

Omuri Mfumu ya Israeli

21Pambuyo pake Aisraeli anagawikana pakati: theka linatsatira Tibini mwana wa Ginati kuti limulonge ufumu, ndipo theka lina linatsatira Omuri. 22Koma anthu otsatira Omuri anali amphamvu kupambana amene ankatsatira Tibini mwana wa Ginati. Choncho Tibini anafa ndipo Omuri anakhala mfumu.

23Mʼchaka cha 31 cha Asa mfumu ya Yuda, Omuri anakhala mfumu ya Israeli, ndipo analamulira zaka 12 ndi miyezi isanu ndi umodzi ku Tiriza. 24Iye anagula phiri la Samariya kwa Semeri pa mtengo wa ndalama 6,000 za siliva ndipo pa phiripo anamangapo mzinda, nawutcha Samariya, potsata dzina la Semeri, dzina la mwini wakale wa phirilo.

25Koma Omuri anachita zoyipa pamaso pa Yehova ndipo anachimwa kuposa mafumu ena onse amene analipo iye asanakhale mfumu. 26Pakuti iye anayenda mʼnjira zonse za Yeroboamu mwana wa Nebati, ndipo tchimo lake anachimwitsa nalo Aisraeli, nakwiyitsa Yehova Mulungu wa Israeli ndi mafano awo opandapake.

27Tsono ntchito zina za Omuri ndi zamphamvu zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli? 28Choncho Omuri anamwalira nayikidwa mʼmanda amene anayikidwa makolo ake ku Samariya. Ndipo Ahabu mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.

Ahabu Akhala Mfumu ya Israeli

29Mʼchaka cha 38 cha ufumu wa Asa, mfumu ya Yuda, Ahabu mwana wa Omuri anakhala mfumu ya Israeli nalamulira Israeli ku Samariya zaka 22. 30Ahabu mwana wa Omuri anachita zoyipa zambiri pamaso pa Yehova kupambana mafumu onse akale. 31Iye sanachiyese ngati chinthu chochepa chabe kuchita machimo a Yeroboamu mwana wa Nebati, koma anakwatiranso Yezebeli, mwana wa Etibaala mfumu ya Asidoni, nayamba kutumikira Baala ndi kumupembedza. 32Iye anapangira Baala guwa lansembe mʼnyumba ya Baala imene anamanga ku Samariya. 33Ahabu anapanganso fano la Asera ndi kukwiyitsa kwambiri Yehova Mulungu wa Israeli, kupambana mafumu onse a Israeli amene analipo iye asanakhale mfumu.

34Pa nthawi ya Ahabu, Hiyeli wa ku Beteli anamanganso mzinda wa Yeriko. Pa nthawi yomanga maziko ake, mwana wake woyamba wa mwamuna, Abiramu anamwalira, ndipo pa nthawi yomanga zipata zake, mwana wa mngʼono wa mwamuna Segubu, anamwaliranso. Izi zinachitika monga momwe Yehova ananenera kudzera mwa Yoswa mwana wa Nuni.

New International Reader’s Version

1 Kings 16:1-34

1The Lord’s message about Baasha came to Jehu, the son of Hanani. Here is what the Lord said about Baasha. 2“I lifted you up from the dust. I appointed you king over my people Israel. But you lived the way Jeroboam had lived. You also caused my people Israel to sin. And their sins made me very angry. 3So I am about to destroy you, Baasha, and your royal house. I will make your house like the royal house of Jeroboam, the son of Nebat. 4Some of the people who belong to you will die in the city. Dogs will eat them up. Others will die in the country. The birds will eat them.”

5The other events of Baasha’s rule are written down. What he did and what he accomplished are written in the official records of the kings of Israel. 6Baasha joined the members of his family who had already died. He was buried in Tirzah. Baasha’s son Elah became the next king after him.

7The Lord’s message came through the prophet Jehu, the son of Hanani. It was against Baasha and his royal house. Baasha had done all kinds of evil things in the sight of the Lord. Baasha had also destroyed the royal house of Jeroboam. What Baasha did had made the Lord very angry. So Baasha had become as sinful as the royal house of Jeroboam had been.

Elah King of Israel

8Elah became king of Israel. It was in the 26th year that Asa was king of Judah. Elah ruled in Tirzah for two years. He was the son of Baasha.

9Zimri was one of Elah’s officials. He commanded half of Elah’s chariot drivers. He made plans against Elah. Elah was in Tirzah at the time. He was getting drunk in the home of Arza. Arza was in charge of the palace at Tirzah. 10Zimri came in. He struck Elah down and killed him. It was in the 27th year of Asa, the king of Judah. Zimri became the next king after Elah.

11As soon as Zimri was seated on the throne as king, he killed off Baasha’s whole family. He didn’t even spare one male. It didn’t matter whether it was a relative or a friend. 12So Zimri destroyed the whole family of Baasha. That’s what the Lord had said would happen. He had spoken against Baasha through Jehu the prophet. 13Baasha and his son Elah had committed all kinds of sin. They had also caused Israel to commit the same sins. So Israel made the Lord very angry. They did it by worshiping worthless statues of gods. The Lord is the God of Israel.

14The other events of Elah’s rule are written down. Everything he did is written in the official records of the kings of Israel.

Zimri King of Israel

15Zimri ruled in Tirzah for seven days. It was in the 27th year that Asa was king of Judah. The army of Israel had set up camp near Gibbethon. It was a Philistine town. 16The Israelites in the camp heard that Zimri had made plans against King Elah. They also heard that Zimri had murdered him. So they announced that Omri was king over Israel. He was the commander of the army. They made him king that day in the camp. 17Then Omri and all his men pulled back from Gibbethon. They marched to Tirzah and surrounded it. They attacked it and captured it. 18Zimri saw that they had taken over the city. So he went into the safest place in the royal palace. He set the palace on fire all around him. He died there 19because of the sins he had committed. He had done what was evil in the sight of the Lord. He had lived the way Jeroboam had lived. He had committed the same sin Jeroboam had caused Israel to commit.

20The other events of Zimri’s rule are written down. The way he turned against King Elah and killed him is written down. All these things are written in the official records of the kings of Israel.

Omri King of Israel

21The Israelites divided up into two groups. Half of them wanted Tibni to be king. He was the son of Ginath. The other half wanted Omri. 22But Omri’s followers were stronger than those of Tibni, the son of Ginath. So Tibni died. And Omri began to rule.

23Omri became king of Israel. It was in the 31st year that Asa was king of Judah. Omri ruled for 12 years. He ruled in Tirzah for six of those years. 24He bought the hill of Samaria from Shemer. He weighed out 150 pounds of silver for it. Then he built a city on the hill. He called it Samaria. He named it after Shemer. Shemer had owned the hill before him.

25But Omri did what was evil in the sight of the Lord. He sinned more than all the kings who had ruled before him. 26He lived the way Jeroboam, the son of Nebat, had lived. He committed the same sin Jeroboam had caused Israel to commit. Israel made the Lord very angry. They did it by worshiping worthless statues of gods. The Lord is the God of Israel.

27The other events of Omri’s rule are written down. Everything he did and the things he accomplished are written in the official records of the kings of Israel. 28Omri joined the members of his family who had already died. He was buried in Samaria. Omri’s son Ahab became the next king after him.

Ahab King of Israel

29Ahab became king of Israel. It was in the 38th year that Asa was king of Judah. Ahab ruled over Israel in Samaria for 22 years. He was the son of Omri. 30Ahab, the son of Omri, did what was evil in the sight of the Lord. He did more evil things than any of the kings who had ruled before him. 31He thought it was only a small thing to commit the sins Jeroboam, the son of Nebat, had committed. Ahab also married Jezebel. She was Ethbaal’s daughter. Ethbaal was king of the people of Sidon. Ahab began to serve the god named Baal and worship him. 32He set up an altar to honor Baal. He set it up in the temple of Baal that he built in Samaria. 33Ahab also made a pole used to worship the female god named Asherah. He made the Lord very angry. Ahab did more to make him angry than all the kings of Israel had done before him. The Lord is the God of Israel.

34In Ahab’s time, Hiel from Bethel rebuilt Jericho. When he laid its foundations, it cost him the life of his oldest son Abiram. When he set up its gates, it cost him the life of his youngest son Segub. That’s what the Lord had said would happen. He had spoken it through Joshua, the son of Nun.