2 Mafumu 1 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Mafumu 1:1-18

Yehova Alanga Ahaziya

1Atamwalira Ahabu, Mowabu anawukira Israeli. 2Ndipo Ahaziya anagwa kuchokera pa khonde la chipinda chake chammwamba ku Samariya, ndipo anavulala kwambiri. Choncho iye anatuma amithenga nawawuza kuti, “Pitani mukafunse kwa Baala-zebubu, mulungu wa ku Ekroni, ngati ndichire matendawa.”

3Koma mngelo wa Yehova anawuza Eliya wa ku Tisibe kuti, “Nyamuka, pita ukakumane ndi amithenga a mfumu ya ku Samariya ndipo ukawafunse kuti, ‘Kodi popeza kulibe Mulungu ku Israeli, nʼchifukwa chake inu mukupita kukafunsa nzeru kwa Baala-zebubu, mulungu wa ku Ekroni?’ 4Tsono Yehova akuti, ‘Iweyo sudzadzuka pa bedi wagonapo. Udzafa ndithu!’ ” Ndipo Eliya ananyamuka.

5Amithenga aja atabwerera kwa mfumu, mfumuyo inawafunsa kuti, “Chifukwa chiyani mwabwerera?”

6Iwo anayankha kuti, “Munthu wina anabwera kudzakumana nafe, ndipo anatiwuza kuti, bwererani kwa mfumu imene inakutumani ndipo mukayiwuze kuti, ‘Yehova akuti, kodi popeza kulibe Mulungu ku Israeli, nʼchifukwa chake mukupita kukafunsa nzeru kwa Baala-zebubu, mulungu wa ku Ekroni? Tsono sudzadzuka pa bedi wagonapo. Udzafa ndithu!’ ”

7Mfumu inafunsa amithengawo kuti, “Kodi munthu amene anabwera kudzakumana nanuyo ndi kukuwuzani zimenezi amaoneka bwanji?”

8Iwo anayankha kuti, “Munthuyo anavala zovala zaubweya ndi lamba wachikopa mʼchiwuno mwake.”

Mfumu inati, “Munthu ameneyo ndi Eliya wa ku Tisibe.”

9Pamenepo mfumu inatuma mtsogoleri wa ankhondo ndi anthu ake makumi asanu kwa Eliya. Mtsogoleriyo anapita kwa Eliya, amene anali atakhala pamwamba pa phiri, ndipo anati, “Munthu wa Mulungu, mfumu ikuti, ‘Tsikani!’ ”

10Eliya anayankha mtsogoleriyo kuti, “Ngati ndine munthu wa Mulungu, moto utsike kuchokera kumwamba, ukupsereze iwe pamodzi ndi anthu makumi asanu akowo!” Pomwepo moto unatsikadi kuchokera kumwamba ndipo unapsereza mtsogoleriyo pamodzi ndi anthu akewo.

11Zitachitika izi, mfumu inatumanso mtsogoleri wina pamodzi ndi asilikali ake makumi asanu. Mtsogoleriyo anati kwa Eliya, “Munthu wa Mulungu, zimene mfumu ikunena ndi izi, ‘Tsikani msangamsanga!’ ”

12Eliya anayankha kuti, “Ngati ndine munthu wa Mulungu, moto utsike kuchokera kumwamba, ukupsereze iwe pamodzi ndi anthu ako makumi asanuwo!” Pomwepo moto unatsikadi kuchokera kumwamba ndipo unapsereza mtsogoleriyo pamodzi ndi anthu akewo.

13Ndipo mfumu inatumanso mtsogoleri wachitatu pamodzi ndi asilikali ake makumi asanu. Mtsogoleri wachitatuyu anakwera pa phiripo ndi kugwada pamaso pa Eliya. Iye anayankhula mopemba kuti, “Munthu wa Mulungu, chonde musandiwononge ineyo pamodzi ndi atumiki makumi asanu anuwa! 14Taonani, moto unatsika kuchokera kumwamba ndi kupsereza atsogoleri awiri pamodzi ndi anthu awo onse. Koma tsopano musawononge moyo wanga!”

15Mngelo wa Yehova anati kwa Eliya, “Pita naye, usamuope.” Choncho Eliya ananyamuka natsika naye limodzi kupita kwa mfumu.

16Eliya anawuza mfumu kuti, “Yehova akuti, ‘Chifukwa chiyani munatumiza amithenga kwa Baala-zebubu, mulungu wa ku Ekroni, kukafunsa ngati muti muchire? Kodi mu Israeli mulibe Mulungu woti nʼkukuyankhani funso lanu? Choncho, popeza mwachita izi, simudzadzuka pamene mwagonapo; mudzafa ndithu.’ ” 17Motero Ahaziya anafadi, monga mwa mawu a Yehova amene Eliya anayankhula.

Tsono popeza Ahaziya analibe mwana, Yoramu analowa ufumu mʼmalo mwake mʼchaka chachiwiri cha Yehoramu mwana wa Yehosafati mfumu ya ku Yuda. 18Ntchito zina zonse zimene Ahaziya anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a ku Israeli?

New International Reader’s Version

2 Kings 1:1-18

The Lord Judges Ahaziah

1After King Ahab died, Moab refused to remain under Israel’s control. 2Ahaziah had fallen through the window of his upstairs room in Samaria. He had hurt himself. So he sent messengers to ask the god named Baal-Zebub for advice. Baal-Zebub was the god of the city of Ekron. Ahaziah said to the messengers, “Go and ask Baal-Zebub whether I will get well again.”

3But the angel of the Lord spoke to Elijah, who was from Tishbe. The angel said, “Go up to see the messengers of Ahaziah, the king of Samaria. Tell them, ‘You are on your way to ask Baal-Zebub for advice. He is the god of Ekron. Are you going there to pray to that god? Do you think there is no God in Israel?’ 4The Lord says to Ahaziah, ‘You will never leave the bed you are lying on. You can be sure that you will die!’ ” So Elijah went to see the messengers.

5They returned to the king. He asked them, “Why have you come back?”

6“A man met us on our way there,” they replied. “He said to us, ‘Go back to the king who sent you. Tell him, “The Lord says, ‘You are sending messengers to ask Baal-Zebub for advice. He is the god of Ekron. Are you going there to pray to that god? Do you think there is no God in Israel? You will never leave the bed you are lying on. You can be sure that you will die!’ ” ’ ”

7The king asked the messengers, “What kind of man came to see you? Who told you these things?”

8They replied, “He was wearing clothes made out of hair. He had a leather belt around his waist.”

The king said, “That was Elijah from Tishbe.”

9Then Ahaziah sent a captain to Elijah. The captain had his group of 50 fighting men with him. Elijah was sitting on top of a hill. The captain went up to him. He said to Elijah, “Man of God, the king says, ‘Come down!’ ”

10Elijah answered the captain, “If I’m really a man of God, may fire come down from heaven! May it burn up you and your 50 men!” Then fire came down from heaven. It burned up the captain and his men.

11After that happened, the king sent another captain to Elijah. The captain had his 50 men with him. He said to Elijah, “Man of God, the king says, ‘Come down at once!’ ”

12Elijah replied, “If I’m really a man of God, may fire come down from heaven! May it burn up you and your 50 men!” Then the fire of God came down from heaven. It burned up the captain and his 50 men.

13So the king sent a third captain with his 50 men. The captain went up to Elijah. He fell on his knees in front of him. “Man of God,” he begged, “please have respect for my life! Please have respect for the lives of these 50 men! 14Fire has come down from heaven. It has burned up the first two captains and all their men. But please have respect for my life!”

15The angel of the Lord said to Elijah, “Go down along with him. Don’t be afraid of him.” So Elijah got up and went down to the king with the captain.

16Elijah told the king, “The Lord says, ‘You have sent messengers to ask Baal-Zebub for advice. He is the god of Ekron. Did you go there to pray to that god for advice? Do you think there is no God in Israel? You will never leave the bed you are lying on. You can be sure that you will die!’ ” 17So King Ahaziah died. It happened just as the Lord had said it would. He had spoken that message through Elijah.

Ahaziah didn’t have any sons. So Joram, his younger brother, became the next king after him. It was the second year of Jehoram, the king of Judah. Jehoram was the son of Jehoshaphat. 18All the other events of Ahaziah’s rule are written down. Everything he did is written in the official records of the kings of Israel.