1 Mafumu 17 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Mafumu 17:1-24

Makwangwala Adyetsa Eliya

1Ndipo mneneri Eliya wa ku Tisibe ku Giliyadi, anati kwa Ahabu, “Pali Yehova wamoyo, Mulungu wa Israeli, amene ndimamutumikira, sipadzakhala mame kapena mvula zaka zikubwerazi, pokhapokha ine nditanena.”

2Pamenepo Yehova anayankhula ndi Eliya kuti, 3“Choka kuno, upite kummawa, ukabisale mʼmbali mwa mtsinje wa Keriti, pafupi ndi Yorodani. 4Uzikamwa mu mtsinjemo, ndipo ndalamula makwangwala kuti azikakudyetsa kumeneko.”

5Choncho Eliya anachita zomwe Yehova anamuwuza. Anapita ku mtsinje wa Keriti, pafupi ndi Yorodani, nakakhala kumeneko. 6Makwangwala ankabweretsera buledi ndi nyama mmawa ndi madzulo, ndipo ankamwa mu mtsinjemo.

Mayi Wamasiye wa ku Zarefati

7Patapita masiku, mtsinjewo unaphwa chifukwa mvula sinagwe mʼdzikomo. 8Yehova anayankhula naye kuti, 9“Nyamuka tsopano, pita ku Zarefati ku Sidoni ndipo ukakhale kumeneko. Ndalamula mkazi wamasiye wa kumeneko kuti azikakudyetsa.” 10Choncho iye ananyamuka napita ku Zarefati. Atafika pa chipata cha mzindawo, taonani mkazi wamasiye amatola nkhuni. Anamuyitana ndi kumuwuza kuti, “Patseni madzi pangʼono mʼchikho kuti ndimwe.” 11Mayi wamasiye uja ankapita kukatunga madzi, Eliya anamuyitananso namuwuza kuti, “Chonde munditengerekonso buledi.”

12Iye anayankha kuti “Pali Yehova Mulungu wanu wamoyo, ine ndilibe chakudya china chilichonse, koma kaufa pangʼono mʼmbiya ndi mafuta pangʼono mʼbotolo. Ine ndikutola tinkhuni tochepa kuti ndipite nato ku nyumba ndi kukaphika chakudya changa ndi cha mwana wanga, kuti tikadye kenaka tife.”

13Eliya anati kwa iye, “Musachite mantha. Pitani mukachite monga mwaneneramo. Koma poyamba mundipangire kachakudya pangʼono kuchokera pa ufa umene muli nawo ndi kubwera nako kwa ine, ndipo kenaka mukaphike choti mudye inuyo ndi mwana wanuyo. 14Pakuti Yehova Mulungu wa Israeli akuti, ‘Ufa umene uli mʼmbiyamo sudzatha ndipo mafuta amene ali mʼbotolomo sadzathanso mpaka tsiku limene Yehova adzagwetse mvula pa dziko lapansi.’ ”

15Mayi wamasiyeyo anapita nakachita zimene Eliya anamuwuza. Choncho panali chakudya cha Eliya, mayiyo pamodzi ndi banja lake lonse chimene anadya masiku ambiri. 16Pakuti ufa umene unali mʼmbiya sunathe ndiponso mafuta amene anali mʼbotolo sanathe, monga momwe ananenera Yehova kudzera mwa Eliya.

17Tsiku lina mwana wake wa mkazi wamasiye uja, mwini nyumbayo, anadwala. Matenda ananka nakulirakulirabe, ndipo kenaka analeka kupuma. 18Mayiyo anati kwa Eliya, “Kodi ndakulakwirani chiyani, inu munthu wa Mulungu? Kodi munabwera kuno kudzandikumbutsa tchimo langa ndi kudzandiphera mwana wanga?”

19Eliya anayankha kuti, “Patseni mwana wanuyo.” Iye anatenga mwanayo mʼmanja mwa mayiyo napita naye mʼchipinda chapamwamba, kumene Eliyayo amagona, namugoneka pa bedi lake. 20Kenaka Eliya anafuwula kwa Yehova nati, “Inu Yehova Mulungu wanga, kodi mwabweretsanso choyipa chotere pa mkazi wamasiye amene ine ndikukhala naye, pakuchititsa kuti mwana wake afe?” 21Pamenepo Eliya anakumbatira mwanayo katatu ndi kufuwula kwa Yehova kuti, “Inu Yehova Mulungu wanga, mubwezereni mwanayu moyo wake!”

22Yehova anamva kufuwula kwa Eliya, ndipo moyo wa mwanayo unabwerera mwa iye ndipo anatsitsimuka. 23Eliya ananyamula mwanayo natsika naye kuchoka mʼchipinda chapamwamba chija nalowa naye mʼnyumba. Anamupereka kwa amayi ake ndipo anati, “Taonani, mwana wanu ali ndi moyo!”

24Pamenepo mayiyo anati kwa Eliya, “Tsopano ndadziwa kuti ndinu munthu wa Mulungu ndipo mawu a Yehova amene mumayankhula ndi owona.”

New International Reader’s Version

1 Kings 17:1-24

Elijah Announces No Dew or Rain

1Elijah was from Tishbe in the land of Gilead. He said to Ahab, “I serve the Lord. He is the God of Israel. You can be sure that he lives. And you can be just as sure that there won’t be any dew or rain on the whole land. There won’t be any during the next few years. It won’t come until I say so.”

Elijah Is Fed by Ravens

2Then a message came to Elijah from the Lord. He said, 3“Leave this place. Go east and hide in the Kerith Valley. It is east of the Jordan River. 4You will drink water from the brook. I have directed some ravens to supply you with food there.”

5So Elijah did what the Lord had told him to do. He went to the Kerith Valley. It was east of the Jordan River. He stayed there. 6The ravens brought him bread and meat in the morning. They also brought him bread and meat in the evening. He drank water from the brook.

Elijah and the Widow at Zarephath

7Some time later the brook dried up. It hadn’t rained in the land for quite a while. 8A message came to Elijah from the Lord. He said, 9“Go right away to Zarephath in the region of Sidon. Stay there. I have directed a widow there to supply you with food.” 10So Elijah went to Zarephath. He came to the town gate. A widow was there gathering sticks. He called out to her. He asked, “Would you bring me a little water in a jar? I need a drink.” 11She went to get the water. Then he called out to her, “Please bring me a piece of bread too.”

12“I don’t have any bread,” she replied. “And that’s just as sure as the Lord your God is alive. All I have is a small amount of flour in a jar and a little olive oil in a jug. I’m gathering a few sticks to take home. I’ll make one last meal for myself and my son. We’ll eat it. After that, we’ll die.”

13Elijah said to her, “Don’t be afraid. Go home. Do what you have said. But first make a small loaf of bread for me. Make it out of what you have. Bring it to me. Then make some for yourself and your son. 14The Lord is the God of Israel. He says, ‘The jar of flour will not be used up. The jug will always have oil in it. You will have flour and oil until the day the Lord sends rain on the land.’ ”

15She went away and did what Elijah had told her to do. So Elijah had food every day. There was also food for the woman and her family. 16The jar of flour wasn’t used up. The jug always had oil in it. That’s what the Lord had said would happen. He had spoken that message through Elijah.

17Some time later the son of the woman who owned the house became sick. He got worse and worse. Finally he stopped breathing. 18The woman said to Elijah, “You are a man of God. What do you have against me? Did you come to bring my sin out into the open? Did you come to kill my son?”

19“Give me your son,” Elijah replied. He took him from her arms. He carried him to the upstairs room where he was staying. He put him down on his bed. 20Then Elijah cried out to the Lord. He said, “Lord my God, I’m staying with this widow. Have you brought pain and sorrow even to her? Have you caused her son to die?” 21Then he lay down on the boy three times. He cried out to the Lord. He said, “Lord my God, give this boy’s life back to him!”

22The Lord answered Elijah’s prayer. He gave the boy’s life back to him. So the boy lived. 23Elijah picked up the boy. He carried him down from the upstairs room into the house. He gave him to his mother. He said, “Look! Your son is alive!”

24Then the woman said to Elijah, “Now I know that you are a man of God. I know that the message you have brought from the Lord is true.”