詩篇 89 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

詩篇 89:1-52

第 89 篇

永遠配受稱頌的上帝

以斯拉人以探的訓誨詩。

1我要永遠稱頌耶和華的慈愛!

我的口要傳揚你的信實直到萬代。

2我要讓人知道:

你的慈愛存到永遠,

你的信實與天同存。

3你曾說:

「我與我所揀選的人立了約,

向我的僕人大衛起了誓,

4『我要使你的後裔永遠坐在寶座上,世代為王。』」(細拉)

5耶和華啊,

諸天要頌揚你的奇妙,

眾聖者要讚美你的信實。

6天上有誰能與耶和華相比,

眾天使中誰能像祂?

7祂在眾聖者的會中大受敬畏,

祂的威嚴無與倫比。

8萬軍之上帝耶和華啊,

誰能像你能力偉大,信實無比?

9你掌管洶湧的大海,

平息驚濤駭浪。

10你擊碎海怪89·10 海怪」希伯來文是「拉哈伯」。

以大能的臂膀驅散仇敵。

11天地都屬於你,

世界和其中的一切都是你造的。

12你創造了南方和北方,

他泊山和黑門山都向你歡呼。

13你有大能的臂膀,

雙手充滿力量。

14你的寶座以公平和正義為根基,

你以慈愛和信實為先鋒。

15耶和華啊,

懂得向你歡呼的人有福了,

他們走在你的榮光之中。

16他們因你的名終日歡欣,

因你的公義而雀躍。

17你是他們的力量和榮耀,

你的恩惠使我們充滿力量。

18耶和華賜下保護我們的盾牌,

我們的王屬於以色列的聖者。

19你曾在異象中對你忠心的子民說:

「我已把力量賜給一位勇士,

已擢升我在民中揀選的人。

20我找到了我的僕人大衛

用我的聖油膏立他。

21我的手必扶持他,

我的臂膀必加給他力量。

22仇敵勝不過他,

惡人不能欺壓他。

23我要當著他的面擊垮他的敵人,

打倒恨他的人。

24我要以信實和慈愛待他,

他必因我的名而充滿力量。

25我要使他左手掌管大海,

右手統治江河。

26他要向我高呼,

『你是我的父親,我的上帝,

拯救我的磐石。』

27我要立他為我的長子,

使他做天下至尊的君王。

28我要永遠用慈愛待他,

我與他立的約永不更改。

29我要使他的後裔永無窮盡,

讓他的王位與天同存。

30如果他的後代背棄我的律法,

不遵行我的典章,

31觸犯我的律例,

不守我的誡命,

32我就會因他們的罪用杖懲罰他們,

用鞭子責打他們。

33但我不會收回我的慈愛,

也不會背棄我的信實。

34我必不毀約,也不食言。

35因我曾憑自己的聖潔向大衛起誓,

我絕無謊言。

36他的後裔必永無窮盡,

他的王位必在我面前如日長存,

37又如天上亙古不變的月亮,

永遠堅立。」(細拉)

38如今,你對你所膏立的王大發怒氣,丟棄了他。

39你廢棄與他所立的約,

把他的冠冕扔在塵土中。

40你攻破了他的城牆,

使他的堅壘淪為廢墟。

41路人都趁機劫掠他的財物,

鄰居都嘲笑他。

42你助長了他敵人的勢力,

使敵人洋洋得意。

43你使他的刀劍失去鋒芒,

你使他敗退沙場。

44你使他的威榮盡失,

王位傾覆。

45你使他未老先衰,

滿面羞愧。(細拉)

46耶和華啊,

你隱藏自己要到何時呢?

要到永遠嗎?

你的怒火要燒到何時呢?

47願你顧念我的生命何其短暫!

你創造的世人何其虛幻!

48誰能長生不死?

誰能救自己脫離死亡的權勢呢?(細拉)

49主啊,你從前憑自己的信實向大衛應許的慈愛在哪裡呢?

50主啊,求你顧念你僕人——我所受的羞辱,

我心中如何忍受列國的嘲笑。

51耶和華啊,

你的仇敵嘲笑你所膏立的王,

他們嘲笑他的一舉一動。

52耶和華永遠當受稱頌。

阿們!阿們!

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 89:1-52

Salimo 89

Ndakatulo ya Etani, wa banja la Ezara.

1Ndidzayimba za chikondi chachikulu cha Yehova kwamuyaya;

ndi pakamwa panga ndidzachititsa kuti kukhulupirika kwanu kudziwike ku mibado yonse.

2Ndidzalalikira kuti chikondi chanu chidzakhazikika mpaka muyaya,

kuti Inu munakhazikitsa kukhulupirika kwanu kumwamba kwenikweniko.

3Inu munati, “Ndachita pangano ndi wosankhidwa wanga,

ndalumbira kwa Davide mtumiki wanga kuti,

4‘Ndidzakhazikitsa zidzukulu zako mpaka muyaya.

Ndidzachititsa kuti mpando wako waufumu ukhazikike ku mibado yonse,’ ”

Sela.

5Mayiko akumwamba amatamanda zozizwitsa zanu Yehova,

kukhulupirika kwanunso, mu msonkhano wa oyera mtima anu.

6Pakuti ndani mu mlengalenga angalingane ndi Yehova?

Ndani wofanana ndi Yehova pakati pa zolengedwa zakumwamba?

7Mu msonkhano wa oyera mtima Mulungu amaopedwa kwambiri;

Iye ndiye wochititsa mantha kupambana onse amene amuzungulira.

8Inu Yehova Mulungu Wamphamvuzonse, ndani wofanana nanu?

Yehova ndinu wamphamvu ndipo kukhulupirika kwanu kwakuzungulirani.

9Mumalamula nyanja ya mafunde awukali;

pamene mafunde ake awundana Inu mumawakhalitsa bata.

10Munaphwanya Rahabe monga munthu wophedwa;

ndi dzanja lanu lamphamvu munabalalitsa adani anu.

11Mayiko akumwamba ndi anu ndiponso dziko lapansi ndi lanu;

munapanga dziko lonse ndi zonse zili mʼmenemo.

12Munalenga Kumpoto ndi Kummwera;

Tabori ndi Herimoni akuyimba ndi chimwemwe pa dzina lanu.

13Mkono wanu ndi wamphamvu;

dzanja lanu ndi lamphamvu, dzanja lanu lamanja ndi lopambana.

14Chilungamo ndi chiweruzo cholungama ndiye maziko a mpando wanu waufumu;

chikondi ndi kukhulupirika zimayenda patsogolo panu.

15Ndi odala amene aphunzira kuyamika Inu,

amene amayenda mʼkuwunika kwa nkhope yanu Yehova.

16Amakondwera mʼdzina lanu tsiku lonse lathunthu;

amasangalala koposa mʼchilungamo chanu.

17Pakuti Inu ndiye ulemerero wawo ndi mphamvu yawo

ndipo mwa kukoma mtima kwanu Inu mumakweza nyanga yathu.

18Ndithudi, chishango chathu ndi cha Yehova,

Mfumu yathu kwa Woyerayo wa Israeli.

19Kale munayankhula mʼmasomphenya,

kwa anthu anu okhulupirika munati,

“Ndapatsa mphamvu wankhondo;

ndakweza mnyamata wochokera pakati pa anthu.

20Ndamupeza mtumiki wanga Davide;

ndamudzoza ndi mafuta opatulika.

21Dzanja langa lidzamuchirikiza;

zoonadi, mkono wanga udzamupatsa mphamvu.

22Adani sadzamulamula kuti apereke msonkho;

anthu oyipa sadzamusautsa.

23Ndidzaphwanya adani ake pamaso pake

ndi kukantha otsutsana naye.

24Chikondi changa chokhulupirika chidzakhala naye,

ndipo kudzera mʼdzina langa nyanga yake idzakwezedwa.

25Ndidzayika dzanja lake pa nyanja,

dzanja lake lamanja pa mitsinje.

26Iyeyo adzafuwula kwa Ine kuti, ‘Ndinu Atate anga,

Mulungu wanga, Thanthwe ndi Chipulumutso changa.’

27Ndidzamuyika kuti akhale mwana wanga woyamba kubadwa;

wokwezedwa kwambiri pakati pa mafumu a dziko lapansi.

28Ndidzamusungira chifundo changa kwamuyaya,

ndipo pangano langa ndi iye silidzatha.

29Ine ndidzakhazikitsa zidzukulu zake mpaka muyaya,

mpando wake waufumu ngati masiku a miyamba.

30“Ngati ana ake adzataya lamulo langa

ndi kusatsatira malangizo anga,

31ngati adzaswa malamulo anga

ndi kulephera kusunga ziphunzitso zanga,

32Ine ndidzalanga tchimo lawo ndi ndodo,

mphulupulu zawo powakwapula.

33Koma sindidzachotsa chikondi changa pa iye,

kapena kukhala wosakhulupirika kwa iyeyo.

34Sindidzaswa pangano langa

kapena kusintha zimene milomo yanga yayankhula.

35Ndinalumbira kamodzi mwa kuyera kwanga

ndipo sindidzanama kwa Davide,

36kuti zidzukulu zake zidzakhale kwamuyaya

ndipo mpando wake waufumu udzakhazikika pamaso panga ngati dzuwa;

37udzakhazikika kwamuyaya monga mwezi,

mboni yokhulupirika mʼmitambo.

Sela

38“Koma tsopano Inu mwamukana, mwamutaya,

mwamukwiyira kwambiri wodzozedwa wanu.

39Mwakana pangano ndi mtumiki wanu

ndipo mwadetsa mʼfumbi chipewa chake chaufumu.

40Inu mwagumula makoma ake onse

ndipo mwasandutsa bwinja malinga ake.

41Onse amene amadutsa amalanda zinthu zake;

iye wakhala chotonzedwa cha anansi ake.

42Mwakweza dzanja lamanja la adani ake;

mwachititsa kuti adani ake akondwere.

43Mwabunthitsa lupanga lake,

simunamuthandize pa nkhondo.

44Inu mwathetsa kukongola kwa ulemerero wake

ndipo mwagwetsa pansi mpando wake waufumu.

45Mwachepetsa masiku a unyamata wake;

mwamuphimba ndi chofunda chochititsa manyazi.

Sela

46“Mpaka liti Yehova? Kodi mudzadzibisa mpaka kalekale?

Mpaka liti ukali wanu udzayaka ngati moto?

47Kumbukirani kuti masiku a moyo wanga ndi ochepa

pakuti munalenga kwachabe anthu onse!

48Kodi ndi munthu uti angakhale ndi moyo ndi kusaona imfa?

Kapena kudzipulumutsa yekha ku mphamvu ya manda?

Sela

49Inu Ambuye kodi chili kuti chikondi chanu chachikulu choyamba chija,

chimene mwa kukhulupirika kwanu munalumbira kwa Davide?

50Kumbukirani, Ambuye momwe mtumiki wanu wanyozedwera,

momwe ndakhalira ndi kusunga mu mtima mwanga mawu a pangano a anthu a mitundu yonse,

51mawu achipongwe amene adani anu akhala akunyoza, Inu Yehova,

ndi mawu amene akhala akunyoza mayendedwe onse a wodzozedwa wanu.

52“Matamando akhale kwa Yehova mpaka muyaya!”

Ameni ndi Ameni.