箴言 1 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

箴言 1:1-33

箴言的價值

1這是大衛的兒子以色列所羅門的箴言。

2為使人認識智慧和教誨,

領悟真知灼見;

3為使人接受勸誡,

為人處事仁義、公平、正直;

4使愚昧人明智,

使青年有知識和明辨力;

5使智者聽了長學問,

明哲聽了得指引;

6使人領悟箴言和比喻,

明白智者的話和謎語。

7知識始於敬畏耶和華,

愚人輕視智慧和教誨。

8孩子啊,

你要聽從父親的教誨,

不可背棄母親的訓言。

9因為這要作你頭上的華冠,

頸上的項鏈。

10孩子啊,惡人若引誘你,

千萬不要聽從。

11他們若說:「跟我們來吧,

我們去埋伏殺人,

暗害無辜者取樂;

12我們要像陰間一樣生吞他們,

整個吞沒他們,

使他們如墜入墳墓的人;

13我們必得到各樣寶物,

把戰利品裝滿我們的房屋。

14跟我們一起幹吧,

大家有福同享!」

15孩子啊,

不要走他們的道,

切莫行他們的路。

16因為他們奔向罪惡,

急速地去殺人流血。

17在飛鳥眼前設網羅,徒勞無功。

18他們埋伏,卻自流己血;

他們伏擊,卻自害己命。

19這就是貪愛不義之財者的結局,

不義之財終要奪去他們的性命。

智慧的勸誡

20智慧在大街上高喊,

在廣場上揚聲,

21在熱鬧的市集宣告,

在城門口演說:

22「你們愚昧人喜愛愚昧,

嘲諷者以嘲弄為樂,

無知者厭惡知識,

要到什麼時候呢?

23你們若因我的責備而回轉,

我就向你們顯明我的旨意1·23 我就向你們顯明我的旨意」希伯來文是「我就將我的靈澆灌你們」。

叫你們明白我的話語。

24我呼喚你們,

你們卻充耳不聞;

我向你們招手,

你們卻視若無睹。

25你們漠視我的勸誡,

不接受我的責備。

26因此,

你們遭遇災難時,

我必發笑;

驚恐臨到你們時,

我必嗤笑——

27那時,恐懼如風暴襲擊你們,

災難如旋風臨到你們,

憂愁和苦難吞沒你們。

28你們呼求我,

我也不回答;

你們懇切地尋找我,

卻找不到。

29因為你們厭惡知識,

不願意敬畏耶和華,

30不接受我的勸誡,

又藐視我的責備。

31所以,你們必自食其果,

因自己的惡謀而吃盡苦頭。

32愚昧人背離正道,

自招滅亡;

愚頑人逍遙自在,

毀掉自己。

33然而,那聽從我的必安然居住,

得享安寧,

不怕災禍。」

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Miyambo 1:1-33

Mawu Oyamba: Cholinga ndi Mutu

1Iyi ndi miyambi ya Solomoni mwana wa Davide, mfumu ya Israeli:

2Ndi yothandiza kuti munthu adziwe nzeru ndi malangizo;

kuti amvetse mawu a matanthauzo ozama;

3kuti alandire malangizo othandiza kuti achite zinthu mwanzeru,

akhale wangwiro, wachilungamo ndiponso wosakondera.

4Ndi yothandiza munthu wamba kuti aphunzire nzeru za kuchenjera,

achinyamata kudziwa zinthu bwino ndi kulingalira.

5Munthu wanzeru amvetse bwino miyamboyi kuti awonjezere kuphunzira kwake,

ndi munthu womvetsa zinthu bwino apatepo luso,

6kuti azimvetsa miyambi ndi mafanizo,

mawu a anthu anzeru ndi mikuluwiko.

7Kuopa Yehova ndiye chiyambi cha nzeru.

Zitsiru zimanyoza nzeru ndi malangizo.

Malangizo kuti Asunge Nzeru

Malangizo kwa Achinyamata

8Mwana wanga, mvera malangizo a abambo ako

ndipo usakane mawu okuwongolera a amayi ako.

9Ali ngati sangamutu yokongola ya maluwa pamutu pako

ndiponso ali ngati mkanda mʼkhosi mwako.

10Mwana wanga, ngati anthu oyipa afuna kukukopa

usamawamvere.

11Akadzati, “Tiye kuno;

tikabisale kuti tiphe anthu,

tikabisalire anthu osalakwa;

12tiwameze amoyo ngati manda,

ndi athunthu ngati anthu otsikira mʼdzenje.

13Motero tidzapeza zinthu zosiyanasiyana zamtengowapatali

ndi kudzaza nyumba zathu ndi zolanda;

14Bwera, chita nafe maere,

ndipo tidzagawana chuma chathu tonse.”

15Mwana wanga, usayende nawo pamodzi,

usatsagane nawo mʼnjira zawozo.

16Iwowatu amangofuna zoyipa zokhazokha,

amathamangira kukhetsa magazi.

17Nʼkopanda phindu kutchera msampha

mbalame zikuona!

18Koma anthu amenewa amangobisalira miyoyo yawo yomwe;

amangodzitchera okha msampha!

19Awa ndiwo mathero a anthu opeza chuma mwankhanza;

chumacho chimapha mwiniwake.

Chenjezo Pomwe Tikana Nzeru

20Nzeru ikufuwula mu msewu,

ikuyankhula mokweza mawu mʼmisika;

21ikufuwula pa mphambano ya misewu,

ikuyankhula pa zipata za mzinda kuti,

22“Kodi inu anthu osachangamukanu, mudzakondwera ndi kusachangamuka mpaka liti?

Nanga anthu onyogodola adzakondabe kunyogodola mpaka liti?

Kapena opusa adzadana ndi nzeru mpaka liti?

23Tamverani mawu anga a chidzudzulo.

Ine ndikukuwuzani maganizo anga

ndi kukudziwitsani mawu anga.

24Popeza ndinakuyitanani koma inu munakana kumvera.

Ndinayesa kukuthandizani koma panalibe amene anasamala.

25Uphungu wanga munawunyoza.

Kudzudzula kwanga simunakusamale.

26Ndiye inenso ndidzakusekani mukadzakhala mʼmavuto;

ndidzakunyogodolani chikadzakugwerani chimene mumachiopacho.

27Chiwonongeko chikadzakugwerani ngati namondwe,

tsoka likadzakufikirani ngati kamvuluvulu,

mavuto ndi masautso akadzakugwerani.

28“Tsono mudzandiyitana koma sindidzayankha;

mudzandifunafuna, koma simudzandipeza.

29Popeza iwo anadana ndi chidziwitso

ndipo sanasankhe kuopa Yehova,

30popeza iwo sanasamale malangizo anga

ndipo ananyoza chidzudzulo changa.

31Tsono adzadya zipatso zoyenera mayendedwe awo

ndi kukhuta ndi ntchito zimene anachita kwa ena.

32Pakuti anthu osachangamuka amaphedwa chifukwa cha kusochera kwawo,

ndipo zitsiru zimadziwononga zokha chifukwa cha mphwayi zawo.

33Koma aliyense wondimvera adzakhala mwa bata;

adzakhala mosatekeseka posaopa chilichonse.”