詩篇 90 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

詩篇 90:1-17

卷四:詩篇90—106

第 90 篇

上帝與世人

上帝的僕人摩西的祈禱。

1主啊,

你是我們世世代代的居所。

2群山尚未誕生,

大地和世界還未形成,

從亙古到永遠,你是上帝。

3你叫人歸回塵土,

說:「世人啊,歸回塵土吧。」

4在你眼中,

千年如一日,又如夜裡的一更。

5你像急流一般把世人沖走,

叫他們如夢消逝。

他們像清晨的嫩草,

6清晨還生機盎然,

傍晚就凋謝枯萎。

7你的怒氣使我們滅亡,

你的憤怒使我們戰抖。

8你知道我們的罪惡,

對我們隱秘的罪瞭若指掌。

9我們活在你的烈怒之下,

一生就像一聲歎息飛逝而去。

10我們一生七十歲,

強壯的可活八十歲,

但人生最美好的時光也充滿勞苦和愁煩,

生命轉瞬即逝,

我們便如飛而去。

11誰明白你憤怒的威力?

有誰因為明白你的烈怒而對你心存敬畏呢?

12求你教導我們明白人生有限,

使我們做有智慧的人。

13耶和華啊,我還要苦候多久呢?

求你憐憫你的僕人。

14求你在清晨以慈愛來滿足我們,

使我們一生歡喜歌唱。

15你使我們先前經歷了多少苦難和不幸的歲月,

求你也賜給我們多少歡樂的歲月。

16求你讓僕人們看見你的作為,

讓我們的後代看見你的威榮。

17願主——我們的上帝恩待我們,

使我們所做的亨通,

使我們所做的亨通。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 90:1-17

BUKU LACHINAYI

Masalimo 90–106

Salimo 90

Pemphero la Mose munthu wa Mulungu.

1Ambuye, mwakhala muli malo athu okhalamo

pa mibado yonse.

2Mapiri asanabadwe,

musanalenge nʼkomwe dziko lapansi ndi dziko lonse,

kuyambira muyaya mpaka muyaya Inu ndinu Mulungu.

3Inu mumabwezera anthu ku fumbi,

mumati, “Bwerera ku fumbi iwe mwana wa munthu.”

4Pakuti zaka 1,000 pamaso panu

zili ngati tsiku limene lapita

kapena ngati kamphindi ka usiku.

5Inu mumasesa anthu mʼtulo ta imfa,

iwo ali ngati udzu watsopano wa mmawa,

6ngakhale kuti mmawa umaphuka watsopano,

pofika madzulo wauma ndi kufota.

7Ife tathedwa ndi mkwiyo wanu;

ndipo taopsezedwa ndi kuyipidwa kwanu.

8Mwayika mphulupulu zathu pamaso panu,

machimo athu obisika poonekera pamaso panu.

9Masiku athu onse amatha ali pansi pa ukali wanu;

timatsiriza zaka zathu ndi kubuwula.

10Kuchuluka kwa masiku athu ndi 70,

kapena 80 ngati tili ndi mphamvu;

komabe zaka zonsezi ndi za mavuto ndi nkhawa,

zimatha mofulumira ndipo ife timawulukira kutali.

11Kodi ndani amadziwa mphamvu ya mkwiyo wanu?

Pakuti ukali wanu ndi waukulu ngati ulemu umene uyenera Inu.

12Tiphunzitseni kuwerenga masiku athu molondola,

kuti tikhale ndi mtima wanzeru.

13Lezani mtima Inu Yehova! Kodi mudzatikwiyira mpaka liti?

Achitireni chifundo atumiki anu.

14Mutikhutitse mmawa ndi chikondi chanu chosatha,

kuti tiyimbe ndi chimwemwe ndi kukhala okondwa masiku athu onse.

15Tisangalatseni masiku ambiri monga masiku amene mwatisautsa,

kwa zaka zambiri monga momwe tinaonera mavuto.

16Ntchito zanu zionetsedwe kwa atumiki anu,

kukongola kwanu kwa ana awo.

17Kukoma mtima kwa Ambuye Mulungu wathu kukhale pa ife;

tikhazikitsireni ntchito ya manja athu;

inde, khazikitsani ntchito ya manja athu.