詩篇 103 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

詩篇 103:1-22

第 103 篇

上帝的慈愛

大衛的詩。

1我的心啊,要稱頌耶和華,

我要全心全意地稱頌祂的聖名。

2我的心啊,要稱頌耶和華,

不要忘記祂的一切恩惠。

3祂赦免我一切的罪惡,

醫治我一切的疾病。

4祂救贖我的生命脫離死亡,

以慈愛和憐憫環繞我。

5祂以美物滿足我的願望,

使我如鷹一般恢復青春。

6耶和華為一切受欺壓的人伸張正義,主持公道。

7祂讓摩西明白自己的旨意,

以色列人彰顯自己的作為。

8耶和華有憐憫和恩典,

不輕易發怒,充滿慈愛。

9祂不永久責備人,

也不永遠懷怒。

10祂沒有按我們的過犯對待我們,

也沒有照我們的罪惡懲罰我們。

11因為天離地有多高,

祂對敬畏祂之人的愛也多大!

12東離西有多遠,

祂叫我們的過犯離我們也多遠!

13耶和華憐愛敬畏祂的人,

如同慈父憐愛自己的兒女。

14因為祂知道我們的本源,

顧念我們不過是塵土。

15世人的年日如同草芥,

如野地茂盛的花,

16一經風吹,便無影無蹤,

永遠消逝。

17耶和華永永遠遠愛敬畏祂的人,

以公義待他們的子子孫孫,

18就是那些守祂的約、

一心遵行祂命令的人。

19耶和華在天上設立了寶座,

祂的王權無所不及。

20聽從耶和華的命令、遵行祂吩咐的大能天使啊,

你們要稱頌祂!

21事奉耶和華、遵從祂旨意的天軍啊,

你們要稱頌祂!

22耶和華所造的萬物啊,

要在祂掌管的各處稱頌祂。

我的心啊,要稱頌耶和華!

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 103:1-22

Salimo 103

Salimo la Davide.

1Tamanda Yehova, iwe moyo wanga;

ndi zonse zamʼkati mwanga zitamande dzina lake loyera.

2Tamanda Yehova, iwe moyo wanga,

ndipo usayiwale zabwino zake zonse.

3Amene amakhululuka machimo ako onse

ndi kuchiritsa nthenda zako zonse,

4amene awombola moyo wako ku dzenje

ndi kukuveka chikondi ndi chifundo chake ngati chipewa chaufumu,

5amene akwaniritsa zokhumba zako ndi zinthu zabwino,

kotero kuti umakhala wamphamvu zatsopano ngati mphungu.

6Yehova amachita chilungamo

ndipo amaweruza molungama onse opsinjika.

7Iye anadziwitsa Mose njira zake,

ntchito zake kwa Aisraeli.

8Yehova ndi wachifundo ndi wokoma mtima,

wosakwiya msanga ndi wachikondi chochuluka.

9Iye sadzatsutsa nthawi zonse,

kapena kusunga mkwiyo wake kwamuyaya;

10satichitira molingana ndi machimo athu,

kapena kutibwezera molingana ndi mphulupulu zathu.

11Pakuti monga kumwamba kuli kutali ndi dziko lapansi,

koteronso chikondi chake nʼchachikulu kwa iwo amene amamuopa;

12monga kummawa kutalikirana ndi kumadzulo,

koteronso Iye watichotsera mphulupulu zathu kuti zikhale kutali nafe.

13Monga bambo amachitira chifundo ana ake,

choncho Yehova ali ndi chifundo ndi iwo amene amamuopa;

14pakuti Iye amadziwa momwe tinawumbidwira,

amakumbukira kuti ndife fumbi.

15Kunena za munthu, masiku ake ali ngati udzu,

amaphuka ngati duwa la mʼmunda;

16koma mphepo imawombapo ndipo silionekanso

ndipo malo ake sakumbukirikanso.

17Koma kuchokera muyaya mpaka muyaya

chikondi cha Yehova chili ndi iwo amene amamuopa,

ndi chilungamo chake chili ndi ana a ana awo;

18iwo amene amasunga pangano lake

ndi kukumbukira kumvera malangizo ake.

19Yehova wakhazikitsa mpando wake waufumu mmwamba

ndipo ufumu wake umalamulira onse.

20Tamandani Yehova, inu angelo ake,

amphamvu inu amene mumachita zimene amalamula,

amene mumamvera mawu ake.

21Tamandani Yehova, zolengedwa zonse zakumwamba,

inu atumiki ake amene mumachita chifuniro chake.

22Tamandani Yehova, ntchito yake yonse

kulikonse mu ulamuliro wake.

Tamanda Yehova, iwe moyo wanga.