詩篇 102 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

詩篇 102:1-28

第 102 篇

患難中的祈禱

受苦之人的禱告,在疲憊不堪時向耶和華的傾訴。

1耶和華啊,求你聽我的禱告,

垂聽我的呼求!

2我在危難的時候,

求你不要掩面不理我。

求你垂聽我的呼求,

趕快應允我。

3我的年日如煙消散,

我全身如火焚燒。

4我的心被摧殘,如草枯萎,

以致我不思飲食。

5我因哀歎而瘦骨嶙峋。

6我就像曠野中的鴞鳥,

又像廢墟中的貓頭鷹。

7我無法入睡,

我就像屋頂上一隻孤伶伶的麻雀。

8我的仇敵終日辱罵我,

嘲笑我的用我的名字咒詛人。

9我以爐灰為食物,

眼淚拌著水喝,

10因為你向我大發烈怒,

把我抓起來丟在一邊。

11我的生命就像黃昏的影子,

又如枯乾的草芥。

12耶和華啊!唯有你永遠做王,

你的大名萬代長存。

13你必憐憫錫安

因為現在是你恩待她的時候了,時候到了。

14你的僕人們喜愛城中的石頭,

憐惜城中的塵土。

15列國敬畏耶和華的名,

世上的君王都因祂的榮耀而戰抖。

16因為耶和華必重建錫安

帶著榮耀顯現。

17祂必垂聽窮人的禱告,

不藐視他們的祈求。

18要為後代記下這一切,

好讓將來的人讚美耶和華。

19耶和華從至高的聖所俯視人間,

從天上察看大地,

20要垂聽被囚之人的哀歎,

釋放被判死刑的人。

21-22這樣,萬族萬國聚集、敬拜

耶和華時,

人們必在錫安傳揚祂的名,

耶路撒冷讚美祂。

23祂使我未老先衰,

縮短了我的歲月。

24我說:「我的上帝啊,

你世代長存,

求你不要叫我中年早逝。

25太初你奠立大地的根基,

親手創造諸天。

26天地都要消亡,

但你永遠長存。

天地都會像外衣漸漸破舊,

你必更換天地,如同更換衣服,

天地都要消逝。

27但你永遠不變,

你的年日永無窮盡。

28你僕人的後代必生生不息,

在你面前安然居住。」

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 102:1-28

Salimo 102

Pemphero la munthu wosautsidwa, pamene walefuka, nakhuthulira pamaso pa Yehova kulira kwakeko.

1Yehova imvani pemphero langa;

kulira kwanga kopempha thandizo kufike kwa Inu.

2Musandibisire nkhope yanu

pamene ndili pa msautso.

Munditcherere khutu;

pamene ndiyitana ndiyankheni msanga.

3Pakuti masiku anga akupita ngati utsi;

mafupa anga akunyeka ngati nkhuni zoyaka.

4Mtima wanga wakanthidwa ndipo ukufota ngati udzu;

ndipo ndimayiwala kudya chakudya changa.

5Chifukwa cha kubuwula kwanga kofuwula

ndatsala chikopa ndi mafupa okhaokha.

6Ndili ngati kadzidzi wa ku chipululu,

monga kadzidzi pakati pa mabwinja.

7Ndimagona osapeza tulo; ndakhala

ngati mbalame yokhala yokha pa denga.

8Tsiku lonse adani anga amandichita chipongwe;

iwo amene amandinyoza, amagwiritsa ntchito dzina langa ngati temberero.

9Pakuti ndimadya phulusa ngati chakudya changa

ndi kusakaniza chakumwa changa ndi misozi

10chifukwa cha ukali wanu waukulu,

popeza Inu mwandinyamula ndi kunditayira kumbali.

11Masiku anga ali ngati mthunzi wa kumadzulo;

Ine ndikufota ngati udzu.

12Koma Inu Yehova, muli pa mpando wanu waufumu kwamuyaya;

kudziwika kwanu ndi kokhazikika ku mibado yonse.

13Inu mudzadzuka ndi kuchitira chifundo Ziyoni

pakuti ndi nthawi yoti muonetse kukoma mtima kwanu pa iyeyo;

nthawi yoyikika yafika.

14Pakuti miyala yake ndi yokondedwa kwa atumiki anu;

fumbi lake lokha limawachititsa kuti amve chisoni.

15Mitundu ya anthu idzaopa dzina la Yehova,

mafumu onse a dziko lapansi adzalemekeza ulemerero wanu.

16Pakuti Yehova adzamanganso Ziyoni

ndi kuonekera mu ulemerero wake.

17Iye adzayankha pemphero la anthu otayika;

sadzanyoza kupempha kwawo.

18Zimenezi zilembedwe chifukwa cha mibado ya mʼtsogolo,

kuti anthu amene sanabadwe adzatamande Yehova:

19“Yehova anayangʼana pansi kuchokera ku malo ake opatulika mmwamba,

kuchokera kumwamba anayangʼana dziko lapansi,

20kuti amve kubuwula kwa anthu a mʼndende,

kuti apulumutse amene anayenera kuphedwa.”

21Kotero dzina la Yehova lidzalengezedwa mu Ziyoni

ndi matamando ake mu Yerusalemu,

22pamene mitundu ya anthu ndi maufumu

adzasonkhana kuti alambire Yehova.

23Iye anathyola mphamvu zanga pa nthawi ya moyo wanga;

Iyeyo anafupikitsa masiku anga.

24Choncho Ine ndinati:

“Musandichotse, Inu Mulungu wanga, pakati pa masiku a moyo wanga;

zaka zanu zimakhalabe pa mibado yonse.

25Pachiyambi Inu munakhazikitsa maziko a dziko lapansi

ndipo mayiko akumwamba ndi ntchito ya manja anu.

26Izi zidzatha, koma Inu mudzakhalapo;

zidzatha ngati chovala.

Mudzazisintha ngati chovala

ndipo zidzatayidwa.

27Koma Inu simusintha,

ndipo zaka zanu sizidzatha.

28Ana a atumiki anu adzakhala pamaso panu;

zidzukulu zawo zidzakhazikika pamaso panu.”