民數記 25 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

民數記 25:1-18

以色列人被誘犯罪

1以色列人駐紮在什亭期間,有些人與摩押女子行淫。 2那些女子邀他們參加祭祀,他們吃了祭物,並跪拜她們的神明, 3結果使以色列巴力·毗珥苟合。耶和華大怒, 4摩西說:「把為首的人都抓起來,當著我的面在大白天處死他們,以消除我對以色列人的怒氣。」 5於是,摩西以色列的審判官說:「你們各自把權下與巴力·毗珥苟合的人處死。」

6摩西以色列全體會眾正在會幕門口痛哭的時候,有個以色列人當著他們的面把一個米甸女子帶進自家的帳篷。 7亞倫祭司的孫子、以利亞撒的兒子非尼哈看見了,便起身離開會眾,拿著矛槍, 8跟著進入那人的帳篷,一槍刺透那對男女的腹部。以色列人當中的瘟疫馬上止住了, 9但已有兩萬四千人死於瘟疫。

10耶和華對摩西說: 11亞倫祭司的孫子、以利亞撒的兒子非尼哈消了我對以色列人的怒氣。因為在會眾中他與我一樣痛恨不貞,我才沒有在烈怒中消滅他們。 12你告訴他,我要賜給他平安的約, 13使他和他的後代憑此約可以永遠做祭司,因為他為我除掉了不貞之人,為以色列人贖了罪。」

14米甸女子一同被殺的以色列人名叫心利,是撒路的兒子,是西緬支派的一個族長。 15被殺的米甸女子名叫哥斯比,她父親蘇珥米甸人的一個族長。 16耶和華對摩西說: 17「你要攻打米甸人,擊殺他們。 18因為他們心存敵意,在毗珥陷害你們,他們的姊妹——米甸首領的女兒哥斯比誘惑你們,她在毗珥事件招來瘟疫之日被殺。」

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Numeri 25:1-18

Aisraeli Achita Chigololo

1Aisraeli akukhala ku Sitimu, anayamba kuchita chigololo ndi akazi a ku Mowabu, 2amene ankawayitana ku nsembe za milungu yawo. Anthuwo anadya chakudya chopereka kwa milungu ndi kupembedza milunguyo. 3Motero Aisraeli anapembedza nawo Baala-Peori ndipo Yehova anawapsera mtima kwambiri.

4Pamenepo Yehova anawuza Mose kuti, “Tenga atsogoleri onse a anthu awa, uwaphe poyera, pamaso pa Yehova kuti mkwiyo waukulu wa Yehova uchoke pa Israeli.”

5Choncho Mose anawuza oweruza a Israeli kuti, “Aliyense wa inu ayenera kupha anthu ake amene anapembedza nawo Baala-Peori.”

6Kenaka mwamuna wina wa ku Israeli anabweretsa ku banja lake mkazi wa Chimidiyani pamaso pa Mose ndi anthu onse a Israeli pamene ankalira pa khomo la tenti ya msonkhano. 7Finehasi mwana wa Eliezara, mwana wa wansembe Aaroni ataona izi, anachoka pa msonkhanowo, natenga mkondo mʼdzanja lake. 8Ndipo anatsatira Mwisraeliyu mpaka mʼtenti yake. Anasolola mkondowo ndi kubaya awiriwo kupyola Mwisraeliyo mpaka mʼthupi la mkaziyo. Pamenepo mliri unaleka pakati pa Aisraeli. 9Pa mliriwo, anthu okwana 24,000 anafa.

10Yehova anawuza Mose kuti, 11“Finehasi mwana wa Eliezara, mwana wa wansembe Aaroni wabweza mkwiyo wanga pa Aisraeli chifukwa sanalole kuti wina aliyense apembedze mulungu wina koma Ine ndekha. Nʼchifukwa chake sindinawawononge mu mkwiyo wanga. 12Tsono muwuze kuti ndikhazikitsa pangano langa la mtendere ndi iye. 13Ndikupangana naye pangano la unsembe wosatha, iyeyo pamodzi ndi zidzukulu zake zonse, chifukwa sanalole kuti anthu awukire Ine Mulungu, ndipo anachita ntchito yopepesera machimo Aisraeli.”

14Dzina la Mwisraeli yemwe anaphedwa ndi mkazi wa Chimidiyani anali Zimuri mwana wa Salu, mtsogoleri wa banja la Simeoni. 15Ndipo dzina la mkazi wa Chimidiyani, yemwe anaphedwayo, linali Kozibi mwana wa Zuri, mtsogoleri wa fuko la ku Midiyaniko.

16Yehova anawuza Mose kuti, 17“Amidiyani ndi adani anu ndipo uwaphe, 18chifukwa ankakuonani inu ngati adani awo pamene anakupusitsani pa nkhani ya ku Peori, ndiponso za mlongo wawo Kozibi, mwana wamkazi wa mtsogoleri wa Amidiyani, mkazi yemwe anaphedwa pamene mliri unabwera chifukwa cha zimene zinachitika ku Peori.”