民數記 24 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

民數記 24:1-25

巴蘭第三次預言

1巴蘭見耶和華樂意賜福給以色列人,就不再像先前兩次那樣去求兆頭,而是面向曠野, 2舉目四望,看見以色列人按支派紮營。上帝的靈降在他身上, 3他便吟詩預言說:

比珥之子巴蘭的預言,

是眼睛明亮者的話,

4他得聽上帝之言,

俯伏在地,

得見全能者的異象。

5雅各啊,

你的帳篷何等華美!

以色列啊,

你的居所何等佳美!

6像連綿的山谷,

河畔的園子;

又如耶和華栽種的沉香,

水邊的香柏樹。

7他們沐浴充沛的甘霖,

撒種於濕潤的沃土。

他們的君王高過亞甲

國度名震四方。

8上帝把他們帶出埃及

24·8 」有古卷作「他們」。的力量如野牛之角。

他們要吞滅敵國,

打碎敵人的骨頭,

用利箭射穿仇敵。

9他們蹲伏如雄獅,

躺臥如母獅,誰敢招惹?

祝福他們的人有福了!

咒詛他們的人有禍了!」

10巴勒聽了大怒,用力擊掌,對巴蘭說:「我請你來咒詛我的仇敵,你竟三次祝福他們。 11現在快回家去吧!我說過要給你重賞,但耶和華不讓你得到。」 12巴蘭說:「我不是對你派來的使臣說過嗎? 13就是你把滿屋的金銀都給我,我也不能違背耶和華的命令、憑自己的意思行事——無論好事壞事。我只能說耶和華讓我說的話。 14現在我要回本族去了。但我要告訴你日後以色列人會怎樣對待你的人民。」

巴蘭第四次預言

15巴蘭吟詩預言說:

比珥之子巴蘭的預言,

是眼睛明亮者的話,

16他得聽上帝之言,

明白至高者的旨意,

俯伏在地,

得見全能者的異象。

17我所見的尚未發生,

我目睹的關乎將來。

一顆星要從雅各家升起,

一位君王要從以色列興起。

他要打爛摩押的前額,

擊碎舍特人的頭顱。

18他必征服以東

佔領敵疆西珥

以色列必勇往直前。

19雅各的後裔必掌權,

消滅城中的餘民。」

巴蘭最後的預言

20巴蘭觀看亞瑪力人,並以詩歌預言說:

亞瑪力原是列國之首,

但他的結局卻是滅亡。」

21巴蘭又觀看基尼人,並以詩歌預言說:

「雖然你的居所堅固,

你的巢築在峭壁,

22但你必遭滅頂,

亞述擄去。」

23巴蘭又以詩歌預言說:

「唉!若非上帝許可,

誰能存活呢?

24船隻從基提駛來,

征服亞述希伯

但他也要滅亡。」

25說完,巴蘭動身返回家鄉,巴勒也回去了。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Numeri 24:1-25

1Tsopano Balaamu ataona kuti kunakomera Yehova kudalitsa Israeli, sanapitenso ku mawula monga ankachitira kale, koma kuyangʼana ku chipululu. 2Balaamu atayangʼana, anaona Aisraeli atamanga misasa yawo fuko ndi fuko. Pamenepo mzimu wa Mulungu unabwera pa iye 3ndipo ananena uthenga wake:

“Uthenga wa Balaamu mwana wa Beori,

uthenga wa amene diso lake ndi lotsekuka,

4uthenga wa amene amamva mawu a Mulungu,

yemwe amaona masomphenya wochokera kwa Wamphamvuzonse,

yemwe amagwa chafufumimba, koma maso ake ali chipenyere:

5“Matenti ako ndi okongola kwambiri iwe Yakobo,

misasa yako, iwe Israeli!

6“Monga zigwa zotambalala,

monga minda mʼmbali mwa mtsinje,

monga aloe wodzalidwa ndi Yehova,

monga mikungudza mʼmbali mwa madzi.

7Madzi adzayenderera mʼmitsuko yake;

mbewu zake zidzakhala ndi madzi ambiri.

“Mfumu yake idzakhala yamphamvu kuposa Agagi;

ufumu wake udzakwezedwa.

8“Mulungu womutulutsa mʼdziko la Igupto

ali ndi mphamvu ngati za njati.

Amawononga mitundu yomuwukira

ndi kuphwanya mafupa awo,

amalasa ndi mivi yake.

9Monga mkango waumuna, amabisala nagona pansi,

monga mkango waukazi, adzamuputa ndani?

“Amene adalitsa iwe, adalitsike

ndipo amene atemberera iwe, atembereredwe!”

10Kenaka Balaki anakwiyira Balaamu. Anawomba mʼmanja ndi kunena naye kuti, “Ndinakuyitana kuti utemberere adani anga, koma taona, wawadalitsa katatu konseka. 11Tsopano choka msanga uzipita kwanu! Ndinanena kuti ndidzakulipira bwino kwambiri, koma Yehova sanafune kuti ulandire malipirowo.”

12Balaamu anayankha Balaki kuti, “Kodi sindinawawuze amithenga amene munawatumiza kwa ine, 13kuti ngakhale Balaki atandipatsa nyumba yake yaufumu yodzaza ndi siliva ndi golide sindingathe kuchita zinthu mwa ine ndekha, zabwino kapena zoyipa, kuposa lamulo la Yehova ndi kuti ndiyenera kunena zokhazo zimene Yehova akunena? 14Tsopano ndikupita kwa anthu anga, koma tabwerani ndikuchenjezeni zimene anthu awa adzachitira anthu anu masiku akubwerawa.”

Uthenga Wachinayi wa Balaamu

15Ndipo iye ananena uthenga wake nati,

“Uthenga wa Balaamu mwana wa Beori,

uthenga wa amene diso lake ndi lotsekuka.

16Uthenga wa amene amamva mawu a Mulungu,

amene ali ndi nzeru zochokera kwa Wammwambamwamba,

amene amaona masomphenya wochokera kwa Wamphamvuzonse,

amene amagwa chafufumimba koma diso lake lili lotsekuka:

17“Ndikumuona iye koma osati tsopano;

ndikumupenya iye koma osati pafupi.

Nyenyezi idzatuluka mwa Yakobo;

ndodo yaufumu idzatuluka mwa Israeli.

Iye adzagonjetsa Mowabu

ndi kugonjetsa ana onse a Seti.

18Edomu adzagonjetsedwa;

Seiri, mdani wake, adzawonongedwa

koma mphamvu za Israeli zidzachuluka.

19Wolamulira adzachokera mwa Yakobo

ndipo adzawononga otsala a mu mzindamo.”

Uthenga Wachisanu wa Balaamu

20Kenaka Balaamu anaona Aamaleki ndipo ananena uthenga wake uwu:

“Aamaleki anali oyamba mwa mitundu ya anthu

koma potsiriza pake adzawonongeka.”

Uthenga Wachisanu ndi Chimodzi wa Balaamu

21Kenaka anaonanso Akeni ndipo ananena uthenga wake,

“Malo amene mukukhalamo ndi otetezedwa,

chisa chanu chinayikidwa pa thanthwe;

22komabe inu Akeni mudzawonongedwa,

pamene Asuri adzakutengeni ukapolo.”

Uthenga Wachisanu ndi Chiwiri wa Balaamu

23Ndipo ananenanso uthenga wina kuti,

“Aa, ndani adzakhala ndi moyo Mulungu akachita zimenezi?

24Sitima zapamadzi zidzabwera kuchokera ku madooko a Kitimu;

kupondereza Asuri ndi Eberi,

koma iwonso adzawonongeka.”

25Pamenepo Balaamu ananyamuka ndi kubwerera kwawo ndipo Balaki anapitanso njira yake.