歷代志上 28 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

歷代志上 28:1-21

大衛對所羅門的囑咐

1大衛以色列的眾首領到耶路撒冷。於是,各支派的首領、各班將領、千夫長、百夫長、負責王和王子的財產及牲畜的官員、宮廷侍臣、顯貴和勇士都來了, 2大衛王站起來說:「我的弟兄,我的人民啊,請聽我說。我本想建造一座殿宇安放耶和華的約櫃,作我們上帝的腳凳,我已準備好建造的材料。 3但上帝對我說,『你不可為我的名建造殿宇,因為你是個戰士,曾流過人的血。』 4以色列的上帝耶和華從我父親家中揀選我做以色列的王,直到永遠。因為祂揀選了猶大支派做首領;在猶大支派中,祂揀選了我父親家;在我父親的眾子中,祂喜悅我,立我做以色列的王。 5耶和華賜給我許多兒子,祂在我眾子中揀選了所羅門,讓他坐以色列的王位,治理耶和華的國。 6耶和華對我說,『你兒子所羅門必建造我的殿宇和庭院,因為我揀選他做我的兒子,我也必做他的父親。 7倘若他像今天一樣繼續堅守我的誡命和典章,我必使他的國度永遠穩固。』 8現在,當著耶和華的會眾——全體以色列人的面,趁著我們的上帝在垂聽,你們要謹遵你們的上帝耶和華的一切誡命,以便你們可以擁有這片佳美之地,並且把它傳給你們的子孫作永遠的產業。

9「我兒所羅門啊,你要認識你父親的上帝耶和華,誠心樂意地事奉祂,因為祂洞察人心,知道人一切的心思意念。倘若你尋求祂,祂必讓你尋見;倘若你背棄祂,祂必永遠丟棄你。 10現在你要謹慎,因為耶和華揀選你來建造殿宇作聖所。你要堅定不移地去做。」

11大衛將殿的走廊、房舍、庫房、樓房、內室和安放施恩座的聖所的圖樣都交給所羅門12又將心裡構想的耶和華殿的院子、四周的房屋、殿的庫房和聖物庫房的圖樣都交給他。 13大衛還讓他知道祭司和利未人的班次、耶和華殿裡各樣的工作及一切所需的器皿, 14製造各種金器銀器所需金銀的分量—— 15金燈臺和金燈的分量,銀燈臺和銀燈的分量——按每座燈臺的用途酌定金銀的分量, 16放供餅的金桌子的分量,銀桌子的分量, 17純金的叉子、碗、瓶的分量,每個金碗和銀碗的分量, 18純金香壇的分量,以及在施恩座上展開翅膀遮蓋耶和華約櫃的基路伯天使的樣式。 19大衛說:「以上這一切都是耶和華親手指示我的,讓我明白工作的細節。」

20大衛又對兒子所羅門說:「你要堅定勇敢地去做!不要懼怕,也不要驚慌,因為我的上帝耶和華必不撇下你,也不丟棄你,祂必與你同在,直到聖殿的一切工作完畢。 21你看,在上帝殿裡司職的各班祭司和利未人已準備就緒,又有各種能工巧匠樂意在各種工作上幫你,眾首領和百姓都聽你調遣。」

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Mbiri 28:1-21

Ndondomeko ya Kamangidwe ka Nyumba ya Mulungu

1Davide anayitana akuluakulu onse a Israeli kuti asonkhane ku Yerusalemu: akuluakulu a mafuko, olamulira magulu a ntchito ya mfumu, olamulira ankhondo 1,000, ndi olamulira ankhondo 100, ndiponso akuluakulu onse osunga katundu ndi ziweto za mfumu ndi ana ake, pamodzinso ndi akuluakulu a ku nyumba yaufumu, anthu amphamvu ndi asilikali onse olimba mtima.

2Mfumu Davide inayimirira ndipo inati: “Tamverani abale anga ndi anthu anga. Ine ndinali ndi maganizo omanga nyumba monga malo okhalamo Bokosi la Chipangano la Yehova, malo oyikapo mapazi a Mulungu wathu, ndipo ndinakonza ndondomeko yomangira nyumbayo.” 3Koma Mulungu anati kwa ine, “Usandimangire nyumba chifukwa ndiwe munthu wankhondo ndipo wakhala ukukhetsa magazi.”

4“Komabe Yehova Mulungu wa Israeli anasankha ine pakati pa onse a banja langa kukhala mfumu ya Israeli kwamuyaya. Iye anasankha Yuda kukhala mtsogoleri, ndipo pa banja la Yuda anasankha banja langa. Pakati pa ana aamuna a abambo anga, kunamukomera Iye kundikhazika mfumu ya Aisraeli onse. 5Pa ana anga ambiri onse amene Yehova wandipatsa, Iye wasankha mwana wanga Solomoni kuti akhale pa mpando waufumu wa ufumu wa Yehova kuti alamulire Israeli.” 6Yehova anati kwa ine, “Solomoni mwana wako ndiye amene adzamanga nyumba yanga ndi mabwalo anga, pakuti Ine ndamusankha kuti akhale mwana wanga ndipo Ine ndidzakhala abambo ake. 7Ine ndidzakhazikitsa ufumu wake kwamuyaya ngati iye saleka kutsatira malamulo ndi malangizo anga, monga momwe zikuchitikira leromu.”

8“Tsono lero ine ndikulamula inu pamaso pa Aisraeli onse ndi pa msonkhano wa Yehova, ndipo Mulungu wathu akumva: Mutsatire mosamala malamulo a Yehova Mulungu wathu, kuti dziko labwinoli likhale lanu ndi kuti mudzalipereke kwa zidzukulu zanu kukhala cholowa chawo kwamuyaya.”

9“Ndipo iwe mwana wanga Solomoni, umvere Mulungu wa abambo ako, umutumikire ndi mtima wodzipereka kwathunthu ndi mtima wako wonse, pakuti Yehova amasanthula mtima wa aliyense, ndipo amadziwa maganizo aliwonse a munthu. Ngati ufunafuna Yehova, Iye adzapezeka; koma ngati umutaya, Iye adzakukana kwamuyaya. 10Tsopano ganizira bwino, pakuti Yehova wakusankha iwe kuti umange Nyumba ya Mulungu monga malo ake opatulika. Khala wamphamvu ndipo ugwire ntchito.”

11Kotero Davide anapatsa Solomoni mwana wake mapulani a khonde la Nyumba ya Mulungu, nyumba zake, mosungiramo katundu, zipinda zake zamʼmwamba, zipinda zamʼkati ndi malo a nsembe zopepesera machimo. 12Iye anapatsa Solomoni mapulani a zonse zimene ankaziganizira za bwalo la Nyumba ya Yehova ndi zipinda zonse zozungulira, zipinda zosungiramo chuma cha Nyumba ya Mulungu ndi zinthu zoperekedwa kwa Yehova. 13Davide anamulangiza za magulu a ansembe ndi Alevi ndi ntchito yonse yotumikira mʼNyumba ya Yehova, komanso za zinthu zonse zogwirira ntchito potumikira. 14Iye anakonzeratu za kulemera kwa golide wopangira zida zonse zagolide zogwirira ntchito zosiyanasiyana, ndiponso kulemera kwa siliva wopangira zida zonse zasiliva zogwirira ntchito zosiyanasiyana: 15kulemera kwa golide wopangira choyikapo nyale chagolide ndi nyale zake; ndiponso kulemera kwa siliva wa choyikapo nyale chilichonse ndi nyale zake, molingana ndi kagwiritsidwe ka choyikapo nyale chilichonse; 16kulemera kwa golide wa tebulo iliyonse yoyikapo buledi wopatulika; kulemera kwa siliva wopangira matebulo asiliva; 17muyeso wa golide woyengeka bwino wopangira mafoloko, mbale ndi zotungira; muyeso wa golide wa beseni lililonse la siliva; 18ndiponso muyeso wa golide wabwino wopangira guwa la zofukiza. Davide anamupatsanso ndondomeko ya mapangidwe a galeta, akerubi agolide atatambasula mapiko awo kuphimba Bokosi la Chipangano la Yehova.

19Davide anati, “Zonsezi ndalemba kuchokera kwa Yehova, ndipo Iye wachita kuti ndimvetsetse zonse za mapulaniwa.”

20Davide anatinso kwa mwana wake Solomoni, “Khala wamphamvu ndi wolimba mtima ndipo uchite ntchitoyi. Usachite mantha kapena kutaya mtima pakuti Yehova Mulungu wanga ali nawe. Iye sadzakukhumudwitsa kapena kukusiya mpaka ntchito yonse ya Nyumba ya Mulungu itatha. 21Magulu a ansembe ndi Alevi ndi okonzeka kugwira ntchito ya Nyumba ya Mulungu, ndipo munthu waluso aliyense wodzipereka adzakuthandiza pa ntchito yonse. Akuluakulu ndi anthu onse adzamvera chilichonse chomwe udzalamula.”