歷代志下 1 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

歷代志下 1:1-17

所羅門王求智慧

1大衛的兒子所羅門鞏固了自己的王位。因為他的上帝耶和華與他同在,使他極其偉大。

2所羅門召集所有以色列人,包括千夫長、百夫長、審判官、首領和族長, 3與他們一起去基遍的邱壇,因為那裡有上帝的會幕,是耶和華的僕人摩西在曠野製造的。 4大衛已經把上帝的約櫃從基列·耶琳搬到耶路撒冷,因為他在那裡為約櫃搭了一個帳篷。 5戶珥的孫子、烏利的兒子比撒列造的銅壇在基遍耶和華的會幕前,所羅門和會眾就在那裡求問耶和華。 6所羅門上到耶和華會幕前的銅壇那裡,獻上一千頭祭牲作為燔祭。

7當天晚上,上帝向所羅門顯現,問他:「你要我給你什麼?只管求吧。」 8所羅門回答說:「你厚待我父大衛,並讓我繼位。 9耶和華上帝啊,求你成就你給我父大衛的應許。你立我為王,使我統治這多如地上塵土的百姓。 10現在,求你賜我智慧和知識以帶領他們。不然,誰能治理這麼多的百姓呢?」 11上帝對所羅門說:「你既然有此心願,不為自己求富貴、資財、尊榮、長壽,也沒有求滅絕你的敵人,只求智慧和知識以治理我的子民——我交在你王權之下的百姓, 12我必賜你智慧和知識,並且我還要賜你空前絕後的富貴、資財和尊榮。」

13於是,所羅門基遍邱壇的會幕前回到耶路撒冷治理以色列

所羅門王的兵力和財富

14所羅門組建了戰車和騎兵,有一千四百輛戰車、一萬二千名騎兵,駐紮在屯車城和他所在的耶路撒冷15王使耶路撒冷的金銀多如石頭,使香柏木多如丘陵的無花果樹。 16所羅門的馬匹都是由王室商隊從埃及古厄按定價買來的。 17他們從埃及買來的車馬,每輛車六百塊銀子,每匹馬一百五十塊銀子,他們也把車馬賣給人諸王和亞蘭諸王。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Mbiri 1:1-17

Solomoni Apempha Nzeru

1Solomoni mwana wa Davide anakhazikika molimbika mu ufumu wake, pakuti Yehova Mulungu wake anali naye ndipo anamukweza kwambiri.

2Tsono Solomoni anayankhula kwa Aisraeli onse, olamulira a anthu 1,000, olamulira a anthu 100, oweruza ndiponso kwa atsogoleri onse a Israeli ndi atsogoleri amabanja. 3Solomoni pamodzi ndi gulu lonse la anthu anapita ku malo ofunika kwambiri pachipembedzo ku Gibiyoni. Tenti ya msonkhano ya Mulungu inali kumeneko, imene Mose mtumiki wa Yehova anayipanga mʼchipululu muja. 4Davide anabweretsa Bokosi la Mulungu kuchokera ku Kiriyati Yearimu, ndi kulikhazika kumalo kumene analikonzera popeza analimangira tenti mu Yerusalemu. 5Koma guwa lansembe lamkuwa limene Bezaleli mwana wa Uri, mwana wa Huri analipanga linali ku Gibiyoni kutsogolo kwa tenti ya Yehova. Kotero kuti Solomoni ndi gulu lonse anakapembedza kumeneko. 6Solomoni anapita pamene panali guwa lansembe lamkuwa pamaso pa Yehova mu tenti ya msonkhano ndipo anapereka nsembe zopsereza 1,000.

7Usiku umenewo Mulungu anaonekera kwa Solomoni ndipo anati kwa iye, “Pempha chilichonse chimene ukufuna ndipo ndidzakupatsa.”

8Solomoni anayankha Mulungu kuti, “Inu munaonetsa kukoma mtima kwakukulu kwa Davide abambo anga ndipo mwayika ine kukhala mfumu mʼmalo mwake. 9Tsopano Inu Yehova Mulungu, lolani kuti lonjezo lanu kwa abambo anga Davide likwaniritsidwe, pakuti mwandiyika kukhala mfumu ya anthu anu amene ndi ochuluka ngati fumbi la pa dziko lapansi. 10Mundipatse nzeru ndi luntha zolamulira anthu awa, pakuti ndani amene angathe kulamulira anthu anu ochulukawa?”

11Mulungu anati kwa Solomoni, “Popeza izi ndi zokhumba za mtima wako ndipo sunapemphe katundu, chuma kapena ulemu, kapena imfa ya adani ako, ndiponso poti sunapemphe moyo wautali koma nzeru ndi luntha kuti ulamulire anthu anga amene Ine ndakuyika kukhala mfumu yawo, 12Ine ndidzakupatsa nzeru ndi chidziwitso. Ndipo ndidzakupatsanso katundu, chuma ndi ulemu, zinthu zoti palibe mfumu imene inali nazo iwe usanakhalepo ndipo palibe wina amene adzakhale nazo iweyo ukadzafa.”

13Kotero Solomoni anabwerera ku Yerusalemu kuchoka kumalo opembedzerako a ku Gibiyoni, ku tenti ya msonkhano ndipo analamulira Israeli.

14Solomoni anasonkhanitsa magaleta ndi akavalo; anali ndi magaleta 1,400 ndi akavalo 12,000, amene anawayika mʼmizinda yosungira magaleta ndipo ena anali ndi iye mu Yerusalemu. 15Mfumu inasandutsa siliva ndi golide kukhala ngati miyala wamba mu Yerusalemu. Inasandutsanso mkungudza kukhala wochuluka ngati mitengo ya mkuyu ya ku zigwa. 16Solomoni amagula akavalo ku Igupto ndi Kuwe pakuti anthu amalonda a mfumu amakawagula ku Kuwe. 17Anthu ankagula galeta ku Igupto pa mtengo wa masekeli asiliva 600 ndipo kavalo pa mtengo wa ndalama zasiliva 150. Iwo ankazigulitsanso kwa mafumu onse a Ahiti ndi a Aramu.