撒母耳記下 8 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

撒母耳記下 8:1-18

大衛戰勝敵人

1後來大衛打敗並征服了非利士人,奪取了他們的都城。 2他又打敗了摩押人,讓他們並排躺在地上,然後用繩子去量,每兩繩之內的人都要被殺掉,第三繩的人留下性命。從此,摩押人臣服於大衛,向他進貢。

3利合的兒子瑣巴哈大底謝出來要恢復他在幼發拉底河一帶的勢力,大衛打敗了他, 4俘獲一千七百名騎兵和兩萬名步兵,砍斷拉戰車的馬匹的蹄筋,只留下夠拉一百輛戰車的馬匹。 5大馬士革亞蘭人前來支援瑣巴哈大底謝大衛殺了他們兩萬二千人, 6還派軍駐守亞蘭國的大馬士革亞蘭人臣服大衛,向他進貢。耶和華使大衛無往而不勝。 7大衛奪走哈大底謝侍從的金盾牌,帶回耶路撒冷8又從哈大底謝統治的比他比羅他兩座城中奪走大量的銅。 9哈馬陀以聽說大衛打敗哈大底謝全軍, 10就派兒子約蘭帶著許多金銀銅器去朝見大衛王,向他請安,祝賀他打敗了哈大底謝。因為陀以常常和哈大底謝交戰。 11-12大衛王把這些器皿和他征服亞蘭人、摩押人、亞捫人、非利士人、亞瑪力人和利合的兒子瑣巴哈大底謝時所得的金銀都分別出來,奉獻給耶和華。 13大衛在鹽谷殺了一萬八千亞蘭人,聲威大振。 14他又在以東全境設駐軍,以東人都臣服於他。耶和華使他無往而不勝。

15大衛統治全以色列,他秉公行義治理百姓。 16那時,洗魯雅的兒子約押做元帥,亞希律的兒子約沙法做史官, 17亞希突的兒子撒督亞比亞他的兒子亞希米勒做祭司長,西萊雅做書記, 18耶何耶大的兒子比拿雅統管基利提人和比利提人。大衛的眾子都做首領。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Samueli 8:1-18

Kupambana kwa Davide pa Nkhondo

1Patapita nthawi, Davide anagonjetsa Afilisti ndi kuwapambana ndipo analanda Metegi Ama kuchoka mʼmanja mwa Afilistiwo.

2Davide anagonjetsanso Amowabu. Iye anawalamula kuti agone pansi mʼmizere itatu pa gulu lililonse ndipo anawayeza ndi chingwe. Pa gulu lililonse ankapha anthu amene anali pa mizere iwiri yoyamba, kusiyapo mzere wachitatu. Kotero Amowabu anakhala pansi pa ulamuliro wa Davide ndipo ankapereka msonkho.

3Komanso Davide anagonjetsa Hadadezeri mwana wa Rehobu, mfumu ya Zoba, pamene anapita kukakhazikitsa ulamuliro wake mʼmbali mwa mtsinje wa Yufurate. 4Davide analanda magaleta 1,000, anthu 7,000 okwera magaleta pamodzi ndi asilikali oyenda pansi 20,000. Iye anadula mitsempha ya akavalo onse okoka magaleta, koma anasiyapo akavalo 100 okha.

5Aramu wa ku Damasiko atabwera kudzathandiza Hadadezeri mfumu ya Zoba, Davide anakantha asilikali 22,000. 6Iye anakhazikitsa maboma mu ufumu wa Aramu wa ku Damasiko, ndipo Aaramu anakhala pansi pa ulamuliro wake ndipo ankapereka msonkho. Yehova ankamupatsa chipambano Davide kulikonse kumene ankapita.

7Davide anatenga zishango zagolide za akuluakulu ankhondo a Hadadezeri ndi kubwera nazo ku Yerusalemu. 8Mfumu Davide inatenga mkuwa wambiri kuchokera ku Beta ndi Berotai, mizinda ya Hadadezeri.

9Tou, mfumu ya Hamati atamva kuti Davide wagonjetsa gulu lonse lankhondo la Hadadezeri, 10anatumiza mwana wake Yoramu kwa mfumu Davide kukamulonjera ndi kukamuyamikira chifukwa cha kupambana kwake pa nkhondo yake ndi Hadadezeriyo, amene analinso pa nkhondo ndi Tou. Yoramu anabweretsa ziwiya zasiliva, zagolide ndi zamkuwa.

11Mfumu Davide inapereka zinthu zimenezi kwa Yehova, monga anachitira ndi siliva ndi golide zochokera ku mayiko onse amene anawagonjetsa: 12Edomu ndi Mowabu, Aamoni ndi Afilisti, ndi Aamaleki. Iye anaperekanso zolanda ku nkhondo zochokera kwa Hadadezeri mwana wa Rehobu, mfumu ya Zoba.

13Ndipo Davide anatchuka atabwera kokakantha Aedomu 18,000 mu Chigwa cha Mchere.

14Iye anayika maboma mʼdera lonse la Edomu, ndipo Aedomu onse anakhala pansi pa Davide. Yehova ankapambanitsa Davide kulikonse kumene ankapita.

Akuluakulu a Davide

15Davide analamulira dziko lonse la Israeli ndipo ankachita zonse mwachilungamo ndi molondola pamaso pa anthu ake onse. 16Yowabu mwana wa Zeruya anali mkulu wa ankhondo; Yehosafati mwana wa Ahiludi anali mlembi wa zochitika. 17Zadoki mwana wa Ahitubi ndi Ahimeleki mwana wa Abiatara anali ansembe; Seraya anali mlembi; 18Benaya mwana wa Yehoyada anali mtsogoleri wa Akereti ndi Apeleti; ndipo ana a Davide anali ansembe.