提多書 3 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

提多書 3:1-15

專心行善

1你要提醒眾人順服執政掌權者,遵守法令,隨時準備做善事。 2不要毀謗,不要爭吵,要謙和、恭敬地對待每一個人。 3從前我們也愚蠢、悖逆、易受迷惑,受各種私慾和享樂的驅使,心裡充滿了嫉妒和惡念,令人憎惡,也彼此憎恨。 4但我們的救主上帝向人彰顯了祂的恩慈和仁愛, 5藉著重生之洗和聖靈的更新拯救了我們,這並非因為我們有義行,而是因為祂的憐憫。 6上帝藉著我們的救主耶穌基督把聖靈豐豐富富地澆灌在我們身上。 7這樣,我們既然靠著祂的恩典而被稱為義人,就可以成為後嗣,有永生的盼望。 8以上這些話是可信的,希望你認真教導,使信上帝的人專心行善。這都是造福眾人的美事。

9要避免愚昧的爭論、有關家譜的辯駁和律法上的爭執,因為這些毫無益處。 10對於製造分裂的人,警告過一兩次後,要和他斷絕來往。 11因為你知道這種人已經背道犯罪,自定己罪。

信末的囑咐與問候

12我會派亞提馬或者推基古去見你。到時候,你要立刻到尼哥波立來見我,因為我決定在那裡過冬。 13你要為西納律師和亞波羅送行,盡力幫助他們,讓他們路上一無所缺。 14我們的弟兄姊妹也要學習行善,供應有急需的人,免得毫無貢獻。

15這裡的弟兄姊妹都問候你,也請你問候那些因信仰而愛我們的人。

願恩典常與你們眾人同在!

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Tito 3:1-15

Kuchita Ntchito Zabwino

1Uwakumbutse anthu kuti azigonjera oweruza ndi olamulira, aziwamvera ndi kukhala okonzeka kuchita chilichonse chabwino. 2Asamachitire chipongwe aliyense, asamakangane, akhale ofatsa ndipo oganizira ena, ndipo nthawi zonse akhale aulemu kwa anthu onse.

3Nthawi ina tinali opusa, osamvera, onamizidwa ndi omangidwa ndi zilakolako ndi zokondweretsa zamitundumitundu. Tinkakhala moyo wadumbo ndi wakaduka, odedwa ndiponso odana wina ndi mnzake. 4Koma kukoma mtima ndi chikondi cha Mulungu Mpulumutsi wathu chitaonekera, 5Iye anatipulumutsa, osati chifukwa cha ntchito zathu zolungama zimene tinachita koma chifukwa cha chifundo chake. Anatipulumutsa potisambitsa, kutibadwitsa kwatsopano ndi kutikonzanso mwa Mzimu Woyera 6amene anatipatsa mowolowamanja kudzera mwa Yesu Khristu Mpulumutsi wathu, 7kuti titalungamitsidwa mwachisomo chake, tikhale olowamʼmalo okhala ndi chiyembekezo cha moyo wosatha. 8Mawuwa ndi okhulupirika ndipo ine ndikufuna kuti iwe utsindike zinthu izi, kuti amene akhulupirira Mulungu adzipereke kuchita ntchito zabwino. Zinthu izi ndi zabwino kwambiri ndi zopindulitsa kwa aliyense.

9Koma upewe kufufuzafufuza zopusa, kuwerengawerenga mndandanda wa mibado ya makolo, mikangano ndi mitsutso pa za Malamulo, chifukwa zimenezi ndi zosapindulitsa ndi zopanda pake. 10Munthu woyambitsa mipatuko umuchenjeze koyamba, ndiponso umuchenjeze kachiwiri. Kenaka umupewe. 11Iwe udziwe kuti munthu wotero ngosokoneza ndi wochimwa, ndipo akudzitsutsa yekha.

Mawu Otsiriza

12Ndikadzamutuma Artema kapena Tukiko kwanuko, udzayesetse kundipeza ku Nikapoli, chifukwa ndatsimikiza kukhala kumeneko pa nthawi yozizira. 13Uyesetse chilichonse ungathe kuthandiza Zena katswiri wa malamulo ndi Apolo, kuti apitirize ulendo wawo, ndipo uwonetsetse asasowe kanthu. 14Anthu athu aphunzire kudzipereka pogwira ntchito zabwino, nʼcholinga chakuti athandize zinthu zimene zikufunika msangamsanga. Ndipo asakhale moyo osapindulitsa.

15Onse amene ali ndi ine akupereka moni. Upereke moni kwa amene amatikonda ife mʼchikhulupiriro.

Chisomo chikhale ndi inu nonse.