提多書 2 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

提多書 2:1-15

教導純正的教義

1你的教導要符合純正的教義。 2勸年長的男子要節制、莊重、自律,有全備的信心、愛心和耐心。 3勸年長的婦女要過敬虔的生活,不說長道短,不做酒的奴隸,要以身作則。 4這樣,她們就能教導年輕的婦女愛丈夫、愛兒女、 5自制、貞潔,持家、和善、順服丈夫,免得上帝的道被人毀謗。

6勸勉年輕的男子要自制。 7你自己要在各樣的善行上作眾人的榜樣,在教導上要誠懇、認真、 8言語純全、無可指責,讓那些反對的人無話可說、自覺羞愧。

9勸勉作奴僕的要凡事順服主人,讓主人滿意,不頂撞主人, 10不偷拿主人的東西,為人要忠信可靠,好凡事尊崇我們救主上帝的教導。

11因為上帝拯救世人的恩典已經顯明了, 12這恩典教導我們除掉不敬虔的心和世俗的私慾,在今世過自律、公義、敬畏上帝的生活, 13懷著美好的盼望等候耶穌基督——我們偉大的上帝和救主的榮耀顯現。 14主耶穌為我們犧牲自己,要救贖我們脫離一切罪惡,並潔淨我們,使我們作祂的子民,成為熱心行善的人。

15你要講明這些事,運用各樣權柄勸勉人、責備人,別讓人輕看你。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Tito 2:1-15

Malangizo Osiyanasiyana

1Koma iwe uziphunzitsa zogwirizana ndi chiphunzitso choona. 2Phunzitsa amuna achikulire kuti akhale osaledzera, aulemu wawo, odziletsa, okhwima mʼchikhulupiriro, mʼchikondi ndi mʼkupirira.

3Chimodzimodzinso, phunzitsa amayi achikulire kuti akhale aulemu mʼmakhalidwe awo, asakhale osinjirira anzawo kapena zidakwa, koma akhale alangizi abwino. 4Tsono atha kulangiza amayi achichepere kukonda amuna awo ndi ana awo. 5Kuwaphunzitsa kukhala odziletsa ndi oyera mtima, osamala bwino mabanja awo, okoma mtima, ndi ogonjera amuna awo. Choncho palibe amene adzanyoze mawu a Mulungu.

6Momwemonso, uwalimbikitse amuna achichepere kuti akhale odziletsa. 7Pa zonse iwe mwini ukhale chitsanzo pa ntchito zabwino. Pa chiphunzitso chako uwonetsa kuona mtima ndi kutsimikiza mtima kwako. 8Phunzitsa choonadi kuti anthu asapeze chokutsutsa, motero wotsutsana nawe adzachita manyazi chifukwa adzasowa kanthu koyipa kuti atinenere.

9Phunzitsa akapolo kuti azigonjera ambuye awo mu zinthu zonse ndi kuwakondweretsa. Asamatsutsane nawo 10kapena kumawabera, koma adzionetse kuti ndi odalirika, motero pa zochita zawo zonse adzaonetsa ubwino wa chiphunzitso cha Mulungu, Mpulumutsi wathu.

11Pakuti chisomo cha Mulungu chimene chimapulumutsa chaonekera kwa anthu onse. 12Chisomo chimatiphunzitsa kukana moyo osalemekeza Mulungu komanso zilakolako za dziko lapansi. Ndipo chimatiphunzitsa kukhala moyo odziletsa, olungama ndi opembedza Mulungu nthawi ino, 13pamene tikudikira chiyembekezo chodala; kuonekera kwa ulemerero wa Mulungu wathu wamkulu ndi Mpulumutsi, Yesu Khristu, 14amene anadzipereka yekha chifukwa cha ife kutiwombola ku zoyipa zonse ndi kudziyeretsera yekha anthu amene ndi akeake, achangu pa ntchito yabwino.

15Tsono zimenezi ndi zinthu zomwe uyenera kuphunzitsa. Uziwalimbikitsa anthu ndi kuwatsutsa komwe. Uzichita zimenezi ndi ulamuliro wonse. Wina aliyense asakupeputse ayi.