提摩太後書 1 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

提摩太後書 1:1-18

1保羅奉上帝的旨意,按照在基督耶穌裡所應許的生命作基督耶穌的使徒, 2寫信給我親愛的兒子提摩太

願父上帝和我們的主基督耶穌的恩典、憐憫和平安臨到你!

勉勵忠心事奉

3我日夜不停地為你禱告,對我效法祖先用清潔的良心事奉的上帝充滿了感恩。 4每逢想起你流淚的情形,我就渴望見你,好使我的心充滿喜樂。 5我記得你那真誠無偽的信心。你外祖母羅以和你母親友妮基首先有了這信心,我深信你也有。 6因此我提醒你,要把上帝在我把手按在你身上時賜給你的恩賜充分發揮出來。 7因為上帝賜給我們的不是懦弱的心,而是剛強、仁愛、自律的心。

8所以,你不要羞於為我們的主做見證,也不要以我這為主被囚的人為恥,要靠著上帝的能力和我一同為福音受苦。 9上帝拯救了我們,並呼召我們過聖潔的生活,不是因為我們的行為,而是出於祂的旨意和恩典。早在萬古以前,祂就在基督耶穌裡把這恩典賜給我們了, 10如今藉著我們救主基督耶穌的降世顯明了出來。基督已經消滅了死亡,藉著福音將不朽的生命彰顯了出來。

11我為了這福音受委派做傳道人、使徒和教師。 12我因此而遭受這些苦難,但我不以為恥,因為我知道我所信的是誰,也深信祂能保守祂所託付我的1·12 祂所託付我的」又可翻譯為「我所信託祂的」。,一直到那日1·12 那日」指保羅站在基督面前交帳的日子。13你要以在基督耶穌裡的信心和愛心,把從我這裡聽到的正確教導當作典範遵守, 14要靠著住在我們裡面的聖靈牢牢守住交託給你的美善之道。

15你知道幾乎所有亞細亞的人都離棄了我,其中包括腓吉路黑摩其尼16願主憐憫阿尼色弗一家人,他常常鼓勵我,不以我被囚禁為恥。 17他在羅馬的時候千方百計尋訪我的下落,直到找著我為止。 18你很清楚,他從前在以弗所怎樣在各個方面服侍我。願主再來時格外地憐憫他。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Timoteyo 1:1-18

1Paulo mtumwi wa Khristu Yesu mwa chifuniro cha Mulungu. Anandituma kuti ndilalike za lonjezo la moyo umene uli mwa Khristu Yesu.

2Kwa Timoteyo, mwana wanga wokondedwa:

Chisomo, chifundo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate ndi Ambuye athu Yesu Khristu.

Chilimbikitso Pokhala Wokhulupirika

3Ndikuyamika Mulungu amene ndimamutumikira ndi chikumbumtima chosatsutsika, monga momwe ankachitira makolo anga. Usiku ndi usana ndimakukumbukira mosalekeza mʼmapemphero anga. 4Ndikamakumbukira misozi yako, ndimalakalaka nditakuona kuti ndidzazidwe ndi chimwemwe. 5Ndakumbukira za chikhulupiriro chako choona chimene chinayamba mwa agogo ako a Loisi ndi mwa amayi ako Yunike ndipo ndikutsimikiza mtima kuti chilinso mwa iwe.

Kumvera Paulo ndi Uthenga Wabwino

6Nʼchifukwa chake ndikukukumbutsa kuti upemerere monga amachitira moto, mphatso imene Mulungu anakupatsa nditakusanjika manja. 7Pakuti Mzimu amene Mulungu anatipatsa, si Mzimu wotipatsa manyazi, koma Mzimu wotipatsa mphamvu, chikondi ndi kudzisunga.

8Choncho usachite manyazi kuchitira umboni Ambuye athu, kapena kuchita manyazi chifukwa cha ine wamʼndende. Koma umve nane zowawa chifukwa cha Uthenga Wabwino, mothandizidwa ndi mphamvu za Mulungu. 9Iye anatipulumutsa ndipo anatiyitanira ku moyo oyera mtima, osati chifukwa cha chilichonse chimene tinachita, koma chifukwa cha chikonzero ndi chisomo chake. Chisomo chimenechi anatipatsa ife mwa Khristu Yesu nthawi isanayambe. 10Koma tsopano Mulungu watiwululira kudzera mʼkuoneka kwa Mpulumutsi wathu, Khristu Yesu, amene anathetsa mphamvu za imfa ndipo mwa Uthenga Wabwino anaonetsa poyera moyo umene sungafe. 11Ine ndinasankhidwa kukhala wamthenga, ndi mtumwi ndi mphunzitsi wa Uthenga Wabwinowu. 12Nʼchifukwa chake ndikuvutika monga ndililimu. Komabe zimenezi sizikundichititsa manyazi, popeza ndikumudziwa amene ndamukhulupirira ndipo ndikutsimikiza mtima kuti akhoza kusamalira chimene ndinamusungitsa mpaka tsiku lijalo.

13Zimene unamva kwa ine, uzisunge kuti zikhale chitsanzo cha chiphunzitso choona, mwa chikhulupiriro ndi chikondi mwa Khristu Yesu. 14Samalira bwino zokoma zimene anakusungitsa. Uzisamalire mothandizidwa ndi Mzimu Woyera amene amakhala mwa ife.

Zitsanzo za Kusakhulupirika ndi Kukhulupirika

15Iwe udziwa kuti onse a mʼchigawo cha Asiya anandithawa, kuphatikizapo Fugelo ndi Herimogene omwe.

16Mulungu achitire chifundo banja lonse la Onesiforo chifukwa ankandisangalatsa kawirikawiri ndipo sankachita nane manyazi ngakhale ndinali womangidwa ndi maunyolo. 17Mʼmalo mwake, atangofika ku Roma, anandifunafuna ndipo anandipeza. 18Ambuye amulole kuti adzalandire chifundo kwa Ambuye pa tsiku lijalo! Ukudziwa bwino momwe iye anandithandizira mʼnjira zosiyanasiyana ku Efeso.