列王紀上 6 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

列王紀上 6:1-38

建造聖殿

1所羅門在做以色列王的第四年二月,即西弗月,開始為耶和華建殿。那時正是以色列人離開埃及後第四百八十年。 2所羅門王為耶和華建造的殿長二十七米,寬九米,高十三米半。 3殿前的門廊和殿一樣寬九米,深四米半。 4殿有精緻的窗戶。 5靠殿牆、圍著外殿和內殿又造了三層廂房, 6底層寬二點二五米,中層寬二點七米,上層寬三點一米。廂房的橫樑都搭在殿牆突出的地方,免得插入殿牆。 7建殿的石頭都在採石場鑿好了,建殿的時候聽不到錘子、斧頭或其他鐵器的響聲。

8底層廂房的進口在殿的南面,沿著一道螺旋樓梯可以通到第二層和第三層。 9殿建成後,殿頂裝上香柏木的梁木和木板。 10靠著殿牆所造的廂房每一層高二點二五米,用香柏木的梁木與殿牆接連起來。

耶和華的約

11耶和華對所羅門說: 12「關於你所建的這殿,若你遵行我的律例,順從我的典章,謹守我的一切誡命,我必實現我對你父親大衛的應許。 13我必住在以色列人當中,不拋棄我的以色列子民。」

14所羅門建造的殿落成了。 15殿裡的牆壁和天花板都鋪上了香柏木,地面都鋪上了松木板。 16在殿的後部,從地面至天花板用香柏木板隔出長九米的內殿,就是至聖所。 17在至聖所外面是外殿,長十八米。 18殿內全部鋪上香柏木,不露一點石頭,香柏木上刻著野瓜和花朵的圖案。 19殿的至聖所用來安放耶和華的約櫃。 20至聖所長、寬和高都是九米,裡面全貼上純金,香柏木造的祭壇也包上純金。 21殿內全部貼上純金,至聖所前面有金鏈攔著。 22殿內都貼上純金,至聖所內的祭壇也都包上純金。

23至聖所裡面放著兩個橄欖木造的基路伯天使,各高四米半, 24各有兩個二點二五米長的翅膀,雙翅展開,兩翅尖相距四點五米。 25兩個基路伯的大小和形狀一模一樣, 26高度都是四點五米。 27他將兩個基路伯安在至聖所內,兩個基路伯展開翅膀,各有一個翅膀在至聖所的中央相接,另一個翅膀的尖端觸到牆壁。 28這兩個基路伯天使也包上金。

29內殿和外殿的牆壁都刻上基路伯天使、棕樹和花朵的圖案, 30地板是鋪金的。 31至聖所的門、門楣和門柱都是橄欖木造的,門柱呈五角形。 32兩扇用橄欖木造的門上都刻著基路伯天使、棕樹和花朵的圖案,並包上金。 33外殿的四角形門柱也是用橄欖木造的, 34兩扇門是松木造的,每一扇門都分為可折疊的兩片, 35上面刻著基路伯天使、棕樹和花朵的圖案,並包上金。 36內院的牆是由三層鑿好的石頭和一層香柏木建的。

37耶和華的殿在所羅門執政第四年的西弗月奠基, 38在他執政的第十一年的布勒月,即八月全部按規格建成,歷經七年。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Mafumu 6:1-38

Solomoni Amanga Nyumba ya Mulungu

1Patapita zaka 480 Aisraeli atatuluka mʼdziko la Igupto, chaka chachinayi cha ulamuliro wa Solomoni mu Israeli, mwezi wa Zivi, umene ndi mwezi wachiwiri, Solomoni anayamba kumanga Nyumba ya Yehova.

2Nyumba imene Solomoni anamangira Yehova mulitali mwake inali mamita 27, mulifupi mwake inali mamita asanu ndi anayi, ndipo msinkhu wake unali mamita 13 ndi theka. 3Chipinda chakubwalo mʼmbali mwake chinali mamita asanu ndi anayi kulingana ndi mulifupi mwa Nyumbayo ndipo kutalika kwake kunali kwa mamita anayi ndi theka. 4Anapanga mazenera amene maferemu ake anali olowa mʼkati mwa makoma a Nyumbayo. 5Mʼmbali mwa makoma a Nyumba yayikulu ndi chipinda chopatulika chamʼkati, anamanga zipinda zosanjikizana, mozungulira. 6Chipinda chapansi, mulifupi mwake chinali mamita awiri, chipinda chapakati mulifupi mwake chinali mamita awiri ndi theka ndipo chipinda chapamwamba penipeni mulifupi mwake chinali mamita atatu. Iye anapanga zinthu zosongoka kunja kwa khoma la kunja kuzungulira Nyumbayo kuti asamapise kanthu pa makoma a Nyumba ya Mulungu.

7Poyimanga Nyumbayo, anagwiritsa ntchito miyala yosemeratu, ndipo pogwira ntchitoyo sipanamveke nyundo, nkhwangwa kapena chida china chilichonse.

8Chipata cholowera ku chipinda chapansi chinali mbali ya kummwera kwa Nyumbayo. Panali makwerero okwerera ku chipinda chapakati ndiponso chipinda cha pamwamba. 9Choncho anamanga Nyumbayo mpaka kuyimaliza ndipo denga lake linali la mitanda ndi matabwa a mkungudza. 10Msinkhu wa chipinda chilichonse unali mamita awiri, ndipo anazilumukiza ku Nyumbayo ndi mitanda yamkungudza.

11Yehova anayankhula ndi Solomoni kuti, 12“Kunena za Nyumba imene ukumangayi, ngati iwe udzamvera malangizo anga ndi kutsatira mawu anga, ngati udzasunga malamulo anga ndi kuwachita, Ine ndidzakwaniritsa zonse zomwe ndinalonjeza Davide abambo ako. 13Ndipo Ine ndidzakhazikika pakati pa ana a Israeli ndipo sindidzawasiya anthu anga Aisraeli.”

14Kotero Solomoni anamanga Nyumba ya Mulungu nayimaliza. 15Anakuta khoma la mʼkati mwake ndi matabwa a mkungudza, kuyambira pansi pa Nyumbayo mpaka ku denga ndipo pansi pa Nyumbayo anayalapo matabwa a payini. 16Kumbuyo kwa Nyumbayo anadula chipinda chachitali mamita asanu ndi anayi. Chipindachi anachimanga ndi matabwa a mkungudza kuyambira pansi mpaka ku denga kuti chikhale chipinda chopatulika chamʼkati mwa Nyumba ya Mulungu ngati Malo Wopatulika Kwambiri. 17Chipinda chachikulu chimene chinali kutsogolo kwa Malo Wopatulika Kwambiriwa, chinali mamita 18 mulitali mwake. 18Mʼkati mwa Nyumbayi munali matabwa a mkungudza, pamene anajambulapo zithunzi za zikho ndi maluwa. Paliponse panali mkungudza wokhawokha. Panalibe mwala uliwonse umene unkaonekera.

19Anakonza malo wopatulika mʼkati mwa Nyumbayi kuti ayikemo Bokosi la Chipangano cha Yehova. 20Malo wopatulika a mʼkatiwo anali a mamita asanu ndi anayi mulitali mwake, mulifupi mwake, ndi msinkhu wake. Anakuta mʼkati mwake ndi golide weniweni ndiponso anapanga guwa lansembe la matabwa a mkungudza. 21Solomoni anakutira golide weniweni mʼkati mwake mwa Nyumbayi, ndipo anayalika maunyolo a golide mopingasa kutsogolo kwa malo wopatulika amene anakutidwa ndi golide. 22Motero anakuta mʼkati monse ndi golide. Anakutanso ndi golide guwa lansembe la mʼkati mwa chipinda chopatulika.

23Mʼchipinda chopatulika cha mʼkati anapangamo akerubi awiri a mtengo wa olivi. Msinkhu wa kerubi aliyense unali mamita anayi ndi theka. 24Phiko limodzi la kerubi kutalika kwake kunali mamita awiri ndi theka, phiko linanso linali mamita awiri ndi theka, kutambasula mapiko awiriwo, kuchokera msonga ina mpaka msonga ina kutalika kwake kunali mamita anayi ndi theka. 25Kerubi wachiwiriyo msinkhu wake unalinso mamita anayi ndi theka, pakuti akerubi awiriwo anali a misinkhu yofanana ndi a mapangidwe ofanana. 26Msinkhu wa kerubi aliyense unali mamita anayi ndi theka. 27Solomoni anayika akerubiwo mʼchipinda cha mʼkati mwenimweni mwa Nyumba ya Mulungu, atatambasula mapiko awo. Phiko la kerubi wina limakhudza khoma lina, pamene phiko la winayo limakhudza khoma linanso ndipo mapiko awo amakhudzana pakati pa chipindacho. 28Akerubiwo anawakuta ndi golide.

29Pa makoma onse kuzungulira Nyumbayo, mʼzipinda za mʼkati ndi za kunja zomwe, anajambulapo akerubi, mitengo ya mgwalangwa ndi maluwa. 30Anayala golide pansi mu Nyumbamo mʼzipinda zamʼkati ndi zakunja zomwe.

31Ndipo pa khomo lolowera ku malo wopatulika amʼkati anapanga zitseko za mtengo wa olivi ndipo khonde lake linali ndi mbali zisanu. 32Ndipo pa zitseko ziwiri zija za mtengo wa olivi anajambulapo kerubi, mitengo ya mgwalangwa ndi maluwa ndipo anapaka golide akerubiwo ndi mitengo ya mgwalangwayo. 33Anapanganso chimodzimodzi mphuthu za mbali zinayi za mtengo wa olivi za pa khomo la Nyumbayo. 34Solomoni anapanganso zitseko ziwiri za payini. Chitseko chilichonse chinali ndi mbali ziwiri zotha kuzipinda. 35Pa zitsekozo anagobapo akerubi, mitengo ya mgwalangwa ndi maluwa wotambasuka ndipo zojambulazo anazikuta ndi golide wopyapyala.

36Ndipo anamanga bwalo la mʼkati lokhala ndi khoma lokhala ndi mizere itatu ya miyala yosema ndiponso mzere umodzi wa matabwa osemedwa a mkungudza.

37Maziko a Nyumba ya Yehova anamangidwa pa chaka chachinayi, mwezi wa Zivi. 38Pa chaka cha 11 mwezi wa Buli, mwezi wachisanu ndi chitatu, madera onse a Nyumba anatha kumangidwa monga momwe kunkafunikira. Anamanga Nyumbayo kwa zaka zisanu ndi ziwiri.