列王紀上 5 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

列王紀上 5:1-18

預備建造聖殿

1泰爾希蘭素來與大衛修好,他聽說以色列人膏立了所羅門繼承大衛的王位,就遣使者來見所羅門2所羅門也派人去見希蘭,說: 3「你知道,我父大衛因周圍戰事連連,未能為他的上帝耶和華建殿,要等到耶和華使仇敵伏在他腳下後再建。 4現在我的上帝耶和華使我四境太平,內外無憂, 5我想為我的上帝耶和華建殿,因為耶和華曾對我父大衛說,『我必使你的兒子繼承你的王位,他必為我的名建殿。』 6請你命人為我砍伐黎巴嫩的香柏木。我會派人幫助你的人,並按你的要求付你的人工錢。因為你知道,我們沒有人像西頓人那樣善於砍伐樹木。」

7希蘭聽了所羅門的話後,非常高興,說:「今天當讚美耶和華!祂賜給大衛一個有智慧的兒子治理這偉大的民族。」 8他派人回覆所羅門說:「我已收到你派人帶來的口信。我一定會照你的心願提供香柏木和松木。 9我的工人會將這些木料從黎巴嫩紮成木筏,經海道運到你指定的地點。木筏拆散以後,你就可以點收了。你也要成全我的心願,供應我家食糧。」 10於是,希蘭供應所羅門需用的香柏木和松木, 11所羅門每年供應希蘭四百四十萬升麥子和四千四百升橄欖油。 12耶和華照著應許賜給所羅門智慧。他跟希蘭修好,締結盟約。

13所羅門王從以色列徵集了三萬勞工, 14派他們每月輪班到黎巴嫩工作,每班一萬人,在黎巴嫩一個月,在家兩個月。亞多尼蘭做他們的總管。 15所羅門又徵用了七萬名搬運工,八萬名在山上鑿石的匠人。 16此外,他還派了三千三百名監工,監督工人做工。 17他們按照王的命令在山上鑿出珍貴的巨石,用來作殿的根基。 18於是,所羅門希蘭的工匠及迦巴勒人鑿好石頭,備好木料,準備建殿。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Mafumu 5:1-18

Kukonzekera Kumanga Nyumba ya Mulungu

1Hiramu mfumu ya ku Turo atamva kuti Solomoni wadzozedwa kukhala mfumu mʼmalo mwa abambo ake Davide, anatumiza akazembe ake kwa Solomoni, chifukwa mfumu Hiramu inali pa ubale wabwino ndi Davide nthawi zonse. 2Solomoni anabweza mawu awa kwa Hiramu:

3“Inu mukudziwa kuti chifukwa cha nkhondo zimene zinkachokera ku mbali zonse kulimbana ndi abambo anga, iwo sanathe kumangira Nyumba Yehova Mulungu wawo, mpaka Yehova atawayika adani awo pansi pa ulamuliro wawo. 4Koma tsopano Yehova Mulungu wanga wandipatsa mtendere mbali zonse za dziko ndipo ndilibe mdani kapena chovuta chilichonse. 5Choncho ine ndikufuna kumangira nyumba Yehova Mulungu wanga, monga momwe Iye anawuzira abambo anga Davide kuti, ‘Mwana wako amene ndidzamukhazike pa mpando waufumu mʼmalo mwako ndiye adzandimangire Nyumba.’

6“Choncho lamulani kuti andidulire mikungudza ya ku Lebanoni. Anthu anga adzagwira ntchito imeneyo pamodzi ndi anthu anuwo, ndipo ine ndidzalipira anthu anuwo malipiro amene inu mungakhazikitse. Inu mukudziwa kuti ife tilibe anthu aluso locheka matabwa monga Asidoni.”

7Hiramu anakondwa kwambiri atamva uthenga wa Solomoni ndipo anati, “Lero Yehova atamandike chifukwa wapatsa Davide mwana wanzeru kuti alamulire mtundu waukuluwu.”

8Tsono Hiramu anabweza mawu awa kwa Solomoni:

“Ndalandira uthenga umene mwanditumizira ndipo ine ndidzachita zonse zimene mukufuna pokupatsani mitengo ya mkungudza ndi payini. 9Anthu anga adzatsika nayo kuchokera ku Lebanoni mpaka ku nyanja, ndipo adzayiyandamitsa pa nyanja mpaka ku malo amene munene. Kumeneko ndidzayimasula ndipo mudzayitenga. Ndipo inu mudzakwaniritsa chokhumba changa pondipatsa chakudya cha banja langa laufumu.”

10Motero Hiramu anapereka kwa Solomoni mitengo yonse ya mkungudza ndi payini imene ankayifuna, 11ndipo Solomoni anamupatsa Hiramu mitanga ya tirigu 20,000 ngati chakudya cha pa nyumba yake, kuwonjezera pa migolo ya mafuta a olivi yokwana 20,000. Solomoni anapitiriza kupereka zimenezi chaka ndi chaka. 12Yehova anamupatsa Solomoni nzeru monga momwe analonjezera. Panali ubale wa mtendere pakati pa Solomoni ndi Hiramu, ndipo awiriwa anachita pangano.

13Mfumu Solomoni inasonkhanitsa anthu ogwira ntchito ya thangata mʼdziko lonse la Israeli ndipo anthu athangatawo analipo 30,000. 14Iye ankatumiza anthu 10,000 ku Lebanoni pa mwezi mosinthanasinthana, kotero kuti ankakhala ku Lebanoniko mwezi umodzi ndipo kwawo ankakhalako miyezi iwiri. Adoniramu ndiye ankayangʼanira ogwira ntchito yathangatayo. 15Solomoni anali ndi anthu amtengatenga 70,000, anthu 80,000 osema miyala ku mapiri, 16ndi akapitawo 33,000 amene ankayangʼanira ntchitoyi ndiponso anthu ogwira ntchito zina. 17Molamulidwa ndi mfumu, anakumba ndi kusema miyala ikuluikulu kwambiri yoti akamangire maziko a Nyumba ya Mulungu. 18Amisiri a Solomoni ndi a Hiramu ndiponso anthu a ku Gebala anasema miyala ndi kukonza matabwa ndi miyala yomangira Nyumba ya Mulungu.